Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Mateyu 10:21 - Buku Lopatulika

21 Ndipo mbale adzapereka mbale wake kuimfa, ndi atate mwana wake: ndipo ana adzatsutsa akuwabala, nadzawafetsa iwo.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

21 Ndipo mbale adzapereka mbale wake kuimfa, ndi atate mwana wake: ndipo ana adzatsutsa akuwabala, nadzawafetsa iwo.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

21 “Mbale azidzapereka mbale wake kuti aphedwe, bambo azidzapereka mwana wake. Ana adzaukira makolo ao, mpaka kuŵaphetsa.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

21 “Mʼbale adzapereka mʼbale kuti aphedwe ndi abambo mwana wawo: ndipo ana adzawukira makolo awo ndi kuwapereka kuti aphedwe.

Onani mutuwo Koperani




Mateyu 10:21
12 Mawu Ofanana  

Ndipo Davide ananena ndi Abisai ndi anyamata ake onse, Onani, mwana wanga wotuluka m'matumbo anga, alikufuna moyo wanga; koposa kotani nanga Mbenjamini uyu? Mlekeni, atukwane, pakuti Yehova anamuuza.


mabwenzi anga enieni onse anyansidwa nane; ndi onse ndakondana nao asandulika adani anga.


Ukhala, nuneneza mbale wako; usinjirira mwana wa mai wako.


Ndipo ndidzapikisanitsa Aejipito; ndipo adzamenyana wina ndi mbale wake, ndi wina ndi mnansi wake; mzinda kumenyana ndi mzinda, ndi ufumu kumenyana ndi ufumu.


Ndipo kudzachitika, akaneneranso wina, atate wake ndi mai wake ombala adzanena naye, Sudzakhala ndi moyo, pakuti unena bodza m'dzina la Yehova; ndipo atate wake ndi mai wake ombala adzamgwaza ponenera iye.


Ndipo pomwepo ambiri adzakhumudwa, nadzaperekana wina ndi mnzake, nadzadana wina ndi mnzake.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa