Biblia Todo Logo
Mavesi a Baibulo

- Zotsatsa -



57 Mau a Mulungu Okhudza Yesu Khristu, Mwana wa Mulungu

57 Mau a Mulungu Okhudza Yesu Khristu, Mwana wa Mulungu

Mukayandikira Atate, mukuyandikiranso Mwana, chifukwa onse ndi mmodzi. Kale, chifukwa cha zolakwa zathu, tinali kutali ndi Atate; mkhalowu unatilenga kutali ndi iye.

Koma chikondi chake ndi chachikulu, ndipo chifundo chake n’chosatha, moti sanafune kukhala kutali nanu, cholengedwa chake chamtengo wapatali. Chifukwa cha chikondi chake chopanda malire, anatuma Mwana wake yekha kuti adzafere inu; mwana wopanda chilema, wopanda tchimo, wangwiro.

Iye anachita izi kuti pasakhale cholepheretsa inu kukapembedza dzina lake. Kuti mukafike kwa Atate, muyenera kudzera mwa Yesu, kumuzindikira ngati Mpulumutsi wokha komanso wokwanira. Ndipo magazi ake adzakutsukani ku zoipa zanu, ndipo mudzakhala mwana wa Mulungu.

Palibe chifukwa choti musayandikire kwa iye; chophimba chachotsedwa, ndipo tsopano muli ndi ufulu wokhala osangalala ndikukonda Mlengi wanu. Musaiwale Yesu pa moyo wanu wa tsiku ndi tsiku, yamikirani nsembe yake ndipo muzimufunafuna ndi mtima wanu wonse.

Musakhale popanda chisomo chake, musachoke pafupi naye, musatembenukire chisomo chabwino chomuchitira ichi chomwe chabwera pa moyo wanu kuti mukakhale ndi moyo. Koposa zonse, kondani Mulungu ndi mtima wanu wonse, ndipo yendani naye nthawi zonse. Pakuti pali Mulungu mmodzi, ndi mkhalapakati mmodzi pakati pa Mulungu ndi anthu, ndiye munthu, Khristu Yesu (1 Timoteo 2:5).




Yohane 15:1

Ine ndine mpesa weniweni, ndipo Atate wanga ndiye wam'munda.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 10:15

monga Atate andidziwa Ine, ndi Ine ndimdziwa Atate; ndipo nditaya moyo wanga chifukwa cha nkhosa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 14:31

koma kuti dziko lapansi lizindikire kuti ndikonda Atate, ndi kuti ndichita monga momwe Atate wandilamula. Nyamukani, tizimuka kuchokera kuno.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 6:38

Pakuti ndinatsika Kumwamba, si kuti ndichite chifuniro changa, koma chifuniro cha Iye amene anandituma Ine.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 16:28

Ndinatuluka mwa Atate, ndipo ndadza kudziko lapansi: ndilisiyanso dziko lapansi, ndipo ndipita kwa Atate.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 20:21

Chifukwa chake Yesu anatinso kwa iwo, Mtendere ukhale ndi inu; monga Atate wandituma Ine, Inenso ndituma inu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 6:37

Chinthu chonse chimene anandipatsa Ine Atate chidzadza kwa Ine; ndipo wakudza kwa Ine sindidzamtaya iye kunja.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 5:43

Ndadza Ine m'dzina la Atate wanga, ndipo simundilandira Ine; akadza wina m'dzina lake la iye mwini, iyeyu mudzamlandira.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 10:30

Ine ndi Atate ndife amodzi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 8:58

Yesu anati kwa iwo, Indetu, indetu, ndinena kwa inu, asanayambe kukhala Abrahamu ndipo Ine ndilipo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 5:19

Pamenepo Yesu anayankha nati kwa iwo, Indetu, indetu ndinena kwa inu, sangathe Mwana kuchita kanthu pa yekha, koma chimene aona Atate achichita, ndicho. Pakuti zimene Iye azichita, zomwezo Mwananso azichita momwemo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 3:22

ndipo Mzimu Woyera anatsika ndi maonekedwe a thupi lake ngati nkhunda, nadza pa Iye; ndipo munatuluka mau m'thambo, kuti, Iwe ndiwe Mwana wanga wokondedwa, mwa Iwe ndikondwera.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 3:16

Pakuti Mulungu anakonda dziko lapansi kotero, kuti anapatsa Mwana wake wobadwa yekha, kuti yense wakukhulupirira Iye asatayike, koma akhale nao moyo wosatha.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 5:23

kuti onse akalemekeze Mwana, monga alemekeza Atate. Wosalemekeza Mwana salemekeza Atate amene anamtuma Iye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 1:1

Pachiyambi panali Mau, ndipo Mau anali kwa Mulungu, ndipo Mau ndiye Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 1:23

Onani namwali adzaima, nadzabala mwana wamwamuna, ndipo adzamutcha dzina lake, Imanuele. Ndilo losandulika, Mulungu nafe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 14:20

Tsiku lomwelo mudzazindikira kuti ndili Ine mwa Atate wanga, ndi inu mwa Ine, ndi Ine mwa inu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 16:16

Ndipo Simoni Petro anayankha nati, Inu ndinu Khristu, Mwana wa Mulungu wamoyo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 3:17

ndipo onani, mau akuchokera kumiyamba akuti, Uyu ndiye mwana wanga wokondedwa, mwa Iyeyu ndikondwera.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Akorinto 1:3

Wolemekezeka Mulungu ndi Atate wa Ambuye wathu Yesu Khristu, Atate wa zifundo ndi Mulungu wa chitonthozo chonse,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 1:3

Chisomo kwa inu ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate wathu, ndi Ambuye Yesu Khristu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 15:10

Ngati musunga malamulo anga mudzakhala m'chikondi changa; monga Ine ndasunga malamulo a Atate wanga, ndipo ndikhala m'chikondi chake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Chivumbulutso 1:8

Ine ndine Alefa ndi Omega, ati Ambuye Mulungu, amene ali, amene adali, ndi amene alinkudza, Wamphamvuyonse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 5:20

Pakuti Atate akonda Mwana, namuonetsa zonse azichita yekha: ndipo adzamuonetsa ntchito zoposa izi, kuti mukazizwe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 16:15-16

Iye ananena kwa iwo, Koma inu mutani kuti Ine ndine yani? Ndipo Simoni Petro anayankha nati, Inu ndinu Khristu, Mwana wa Mulungu wamoyo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 5:17

Koma Yesu anayankha iwo, Atate wanga amagwira ntchito kufikira tsopano, Inenso ndigwira ntchito.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Tito 2:13

akulindira chiyembekezo chodala, ndi maonekedwe a ulemerero wa Mulungu wamkulu ndi Mpulumutsi wathu Yesu Khristu;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 24:49

Ndipo onani, Ine nditumiza pa inu lonjezano la Atate wanga; koma khalani inu m'mzinda muno, kufikira mwavekedwa ndi mphamvu yochokera Kumwamba.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 23:34

Ndipo Yesu ananena, Atate, muwakhululukire iwo, pakuti sadziwa chimene achita. Ndipo anagawana zovala zake, poyesa maere.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 1:14

Ndipo Mau anasandulika thupi, nakhazikika pakati pa ife, ndipo tinaona ulemerero wake, ulemerero wonga wa wobadwa yekha wa Atate, wodzala ndi chisomo ndi choonadi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 3:35

Atate akonda Mwana, nampatsa zinthu zonse m'dzanja lake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 2:49

Ndipo Iye anati kwa iwo, Kuli bwanji kuti munalikundifunafuna Ine? Simunadziwa kodi kuti kundiyenera Ine ndikhale m'zake za Atate wanga?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 1:2-3

koma pakutha pake pa masiku ano analankhula ndi ife ndi Mwana amene anamuika wolowa nyumba wa zonse, mwa Iyenso analenga maiko ndi am'mwamba omwe; ameneyo, pokhala ali chinyezimiro cha ulemerero wake, ndi chizindikiro chenicheni cha chikhalidwe chake, nanyamula zonse ndi mau a mphamvu yake, m'mene adachita chiyeretso cha zoipa, anakhala padzanja lamanja la Ukulu mu Mwamba,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 6:44

Kulibe mmodzi akhoza kudza kwa Ine koma ngati Atate wondituma Ine amkoka iye; ndipo Ine ndidzamuukitsa iye tsiku lomaliza.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Akolose 1:15-17

amene ali fanizo la Mulungu wosaonekayo, wobadwa woyamba wa chilengedwe chonse; pakuti mwa Iye, zinalengedwa zonse za m'mwamba, ndi za padziko, zooneka ndi zosaonekazo, kapena mipando yachifumu, kapena maufumu, kapena maukulu, kapena maulamuliro; zinthu zonse zinalengedwa mwa Iye ndi kwa Iye. Ndipo Iye ali woyamba wa zonse, ndipo zonse zigwirizana pamodzi mwa Iye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Akolose 1:15

amene ali fanizo la Mulungu wosaonekayo, wobadwa woyamba wa chilengedwe chonse;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 14:28

Mwamva kuti Ine ndinanena kwa inu, Ndimuka, ndipo ndidza kwa inu. Mukadandikonda Ine, mukadakondwera kuti ndipita kwa Atate; pakuti Atate ali wamkulu ndi Ine.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 1:4

amene anatsimikizidwa ndi mphamvu kuti ndiye Mwana wa Mulungu monga mwa Mzimu wa chiyero, ndi kuuka kwa akufa; ndiye Yesu Khristu Ambuye wathu;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 1:3-4

wakunena za Mwana wake, amene anabadwa, wa mbeu ya Davide, monga mwa thupi, akazitape, osinjirira, akumuda Mulungu, achipongwe, odzitama, amatukutuku, oyamba zoipa, osamvera akulu ao, opanda nzeru, osasunga mapangano, opanda chikondi cha chibadwidwe, opanda chifundo; amene ngakhale adziwa kuweruza kwake kwa Mulungu, kuti iwo amene achita zotere ayenera imfa, azichita iwo okha, ndiponso avomerezana ndi iwo akuzichita. amene anatsimikizidwa ndi mphamvu kuti ndiye Mwana wa Mulungu monga mwa Mzimu wa chiyero, ndi kuuka kwa akufa; ndiye Yesu Khristu Ambuye wathu;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 26:39

Ndipo anamuka patsogolo pang'ono, nagwa nkhope yake pansi, napemphera, nati, Atate ngati nkutheka, chikho ichi chindipitirire Ine; koma si monga ndifuna Ine, koma Inu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 14:6

Yesu ananena naye, Ine ndine njira, ndi choonadi, ndi moyo. Palibe munthu adza kwa Atate, koma mwa Ine.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Yohane 5:20

Ndipo tidziwa kuti Mwana wa Mulungu wafika, natipatsa ife chidziwitso, kuti tizindikire Woonayo, ndipo tili mwa Woonayo, mwa Mwana wake Yesu Khristu. Iye ndiye Mulungu woona ndi moyo wosatha.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Yohane 5:11-12

Ndipo uwu ndi umboniwo, kuti Mulungu anatipatsa ife moyo wosatha, ndipo moyo umene uli mwa Mwana wake. Iye wakukhala ndi Mwana ali nao moyo; wosakhala ndi Mwana wa Mulungu alibe moyo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Agalatiya 2:20

Ndinapachikidwa ndi Khristu; koma ndili ndi moyo; wosatinso ine ai, koma Khristu ali ndi moyo mwa ine; koma moyo umene ndili nao tsopano m'thupi, ndili nao m'chikhulupiriro cha Mwana wa Mulungu, amene anandikonda, nadzipereka yekha chifukwa cha ine.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 1:35

Ndipo mngelo anayankha, nati kwa iye, Mzimu Woyera adzafika pa iwe, ndi mphamvu ya Wamkulukulu idzakuphimba iwe: chifukwa chakenso Choyeracho chikadzabadwa, chidzatchedwa Mwana wa Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 5:18

Chifukwa cha ichi Ayuda anaonjeza kufuna kumupha, si chifukwa cha kuswa tsiku la Sabata kokha, komatu amatchanso Mulungu Atate wake wa Iye yekha; nadziyesera wolingana ndi Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Afilipi 2:6-7

ameneyo, pokhala nao maonekedwe a Mulungu, sanachiyese cholanda kukhala wofana ndi Mulungu, koma anadzikhuthula yekha, natenga maonekedwe a kapolo, nakhala m'mafanizidwe a anthu;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 9:6

Pakuti kwa ife mwana wakhanda wabadwa, kwa ife mwana wamwamuna wapatsidwa; ndipo ulamuliro udzakhala pa phewa lake, ndipo adzamutcha dzina lake Wodabwitsa, Wauphungu, Mulungu wamphamvu, Atate Wosatha, Kalonga wa mtendere.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 11:25-26

Yesu anati kwa iye, Ine ndine kuuka ndi moyo: wokhulupirira Ine, angakhale amwalira, adzakhala ndi moyo; ndipo yense wakukhala ndi moyo, nakhulupirira Ine, sadzamwalira nthawi yonse. Kodi ukhulupirira ichi?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 4:15

Pakuti sitili naye mkulu wa ansembe wosatha kumva chifundo ndi zofooka zathu; koma wayesedwa m'zonse monga momwe ife, koma wopanda uchimo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 8:32

Iye amene sanatimane Mwana wake wa Iye yekha, koma anampereka chifukwa cha ife tonse, adzalekeranji kutipatsanso ife zinthu zonse kwaulere pamodzi ndi Iye?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Machitidwe a Atumwi 4:12

Ndipo palibe chipulumutso mwa wina yense, pakuti palibe dzina lina pansi pa thambo la kumwamba, lopatsidwa mwa anthu, limene tiyenera kupulumutsidwa nalo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Petro 1:18-19

podziwa kuti simunaomboledwa ndi zovunda, golide ndi siliva, kusiyana nao makhalidwe anu achabe ochokera kwa makolo anu: koma ndi mwazi wa mtengo wake wapatali monga wa mwanawankhosa wopanda chilema, ndi wopanda banga, ndiwo mwazi wa Khristu:

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Petro 1:3

Wodalitsika Mulungu ndiye Atate wa Ambuye wathu Yesu Khristu, Iye amene, monga mwa chifundo chake chachikulu, anatibalanso ku chiyembekezo cha moyo, mwa kuuka kwa akufa kwa Yesu Khristu;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 8:12

Pamenepo Yesu analankhulanso nao, nanena, Ine ndine kuunika kwa dziko lapansi; iye wonditsata Ine sadzayenda mumdima, koma adzakhala nako kuunika kwa moyo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Chivumbulutso 22:13

Ine ndine Alefa ndi Omega, Woyamba ndi Wotsiriza, Chiyambi ndi Chitsiriziro.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani

Pemphero kwa Mulungu

Ambuye wanga wakumwamba, zikomo kwambiri chifukwa cha chikondi chanu chosatha ndipo mwanditulutsa mu mdima. Mwachita zinthu zazikulu pa ine, ndinu wodabwitsa ndipo nthawi zonse mumandikwana ndi ubwino wanu. Mtima wanga ukukuthokozani chifukwa cha zonse. Ndikudziwa kuti ndinu nokha njira, choonadi, ndi moyo, ndipo palibe afika kwa Atate koma kudzera mwa inu. Chonde, ndiphunzitseni kukhala nanu paubwenzi wolimba wachikondi ndi kudzipereka ngati mmene mulili ndi Atate. Zikomo Ambuye Yesu, chifukwa cha mawu anu, chifukwa mwalonjeza kuti tidzachita zinthu zazikulu m'dzina lanu. Mawu anu amati: “Tsiku limenelo mudzadziwa kuti Ine ndili mwa Atate, ndi inu muli mwa Ine, ndi Ine mwa inu.” Ambuye Yesu, zikomo pondibweretsa kwa Atate, ndithandizeni tsiku lililonse kuti ndikhale nanu paubwenzi wolimba ndi kukhala womvera ngati mmene munali kwa Atate, kuti nditsatire mawu anu ndi kukhala mmodzi ndi inu, monga inu ndi Atate muli mmodzi. Ulemerero ndi ulemu zonse zikhale kwa inu. M'dzina la Yesu. Ameni.
Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa