Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 42:3 - Buku Lopatulika

Misozi yanga yakhala ngati chakudya changa, usana ndi usiku; pakunena iwo kwa ine dzuwa lonse, Mulungu wako ali kuti?

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Misozi yanga yakhala ngati chakudya changa, usana ndi usiku; pakunena iwo kwa ine dzuwa lonse, Mulungu wako ali kuti?

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Ntchito yanga ndi kulira usana ndi usiku, osalaŵa chakudya chilichonse. Ndipo anthu akhala akunena kuti, “Mulungu wako ali kuti?”

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Misozi yanga yakhala chakudya changa usana ndi usiku, pamene anthu akunena kwa ine tsiku lonse kuti, “Mulungu wako ali kuti?”

Onani mutuwo



Masalimo 42:3
16 Mawu Ofanana  

Kapena Yehova adzayang'anira chosayenerachi alikundichitira ine, ndipo Yehova adzandibwezera chabwino m'malo mwa kunditukwana kwa lero.


Pakuti ndadya mapulusa ngati mkate, ndi kusakaniza chomwera changa ndi misozi,


Aneneranji amitundu, Ali kuti Mulungu wao?


Nditambalitsira manja anga kwa Inu: Moyo wanga ulira Inu monga dziko lolira mvula.


Adadzitengera kwa Yehova; kuti adzampulumutsa, amlanditse tsopano popeza akondwera naye.


Ambiri amati kwa moyo wanga, alibe chipulumutso mwa Mulungu.


Adani anga andinyoza ndi kundithyola mafupa anga; pakunena ndine dzuwa lonse, Mulungu wako ali kuti?


Kuti ndione mphamvu yanu ndi ulemerero wanu, monga ndinakuonani m'malo oyera.


Anenerenji amitundu, Ali kuti Mulungu wao? Kubwezera chilango cha mwazi wa atumiki anu umene anaukhetsa kudziwike pakati pa amitundu pamaso pathu.


Ndipo anansi athu amene anatonza Inu muwabwezere chotonza chao, kasanu ndi kawiri kumtima kwao, Ambuye.


Munawadyetsa mkate wa misozi, ndipo munawamwetsa misozi yambiri.


Mbawanso inapeza nyumba, ndi namzeze chisa chake choikamo ana ake, pa maguwa a nsembe anu, Yehova wa makamu, mfumu yanga ndi Mulungu wanga.


Katatu m'chaka amuna onse azioneka pamaso pa Ambuye Yehova.


Ansembe, atumiki a Yehova, alire pakati pa khonde la pakhomo ndi guwa la nsembe, nanene, Alekeni anthu anu, Yehova, musapereka cholowa chanu achitonze, kuti amitundu awalamulire; adzaneneranji mwa anthu, Ali kuti Mulungu wao?


Pamenepo mdani wanga adzachiona, ndi manyazi adzamkuta iye amene adati kwa ine, Ali kuti Yehova Mulungu wako? Maso anga adzamuona; tsopano adzampondereza ngati thope la m'miseu.


Pakuti ndaniyo, wa zamoyo zonse adamva mau a Mulungu wamoyo wakunena ali pakati pa moto, monga ife nakhala ndi moyo?