Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -

Masalimo 63 - Buku Lopatulika


Mtima woliralira kuyanjana ndi Mulungu
Salimo la Davide; muja anakhala m'chipululu cha Yuda.

1 Inu Mulungu, ndinu Mulungu wanga; ndidzakufunani m'matanda kucha. Moyo wanga ukumva ludzu la kwa Inu, thupi langa lilirira Inu, m'dziko louma ndi lotopetsa, lopanda madzi.

2 Kuti ndione mphamvu yanu ndi ulemerero wanu, monga ndinakuonani m'malo oyera.

3 Pakuti chifundo chanu chiposa moyo makomedwe ake; milomo yanga idzakulemekezani.

4 Potero ndidzakuyamikani m'moyo mwanga; ndidzakweza manja anga m'dzina lanu.

5 Mudzakhutitsa moyo wanga ngati ndi mafuta ndi zonona; ndipo pakamwa panga ndidzakulemekezani ndi milomo yakufuula mokondwera.

6 Pokumbukira Inu pa kama wanga, ndi kulingalira za Inu maulonda a usiku.

7 Pakuti munakhala mthandizi wanga; ndipo ndidzafuula mokondwera mu mthunzi wa mapiko anu.

8 Moyo wanga uumirira Inu. Dzanja lamanja lanu lindigwiriziza.

9 Koma iwo amene afuna moyo wanga kuti auononge, adzalowa m'munsi mwake mwa dziko.

10 Adzawapereka kumphamvu ya lupanga; iwo adzakhala gawo la ankhandwe.

11 Koma mfumu idzakondwera mwa Mulungu; yense wakulumbirira iye adzatamandira; pakuti pakamwa pa iwo onena bodza padzatsekedwa.

Bible Society of Malawi

Bible Society of Malawi
Titsatireni:



Zotsatsa