Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -

Masalimo 3 - Buku Lopatulika


Kukhulupirika kwa Mulungu
Salimo la Davide, muja anathawa Abisalomu mwana wake.

1 Yehova! Ha! Achuluka nanga akundisautsa ine! Akundiukira ine ndi ambiri.

2 Ambiri amati kwa moyo wanga, alibe chipulumutso mwa Mulungu.

3 Ndipo Inu Yehova, ndinu chikopa changa; ulemerero wanga, ndi wondiweramutsa mutu wanga.

4 Ndifuula kwa Yehova ndi mau anga, ndipo andiyankha m'phiri lake loyera.

5 Ndinagona ine pansi, ndinagona tulo; ndinauka; pakuti Yehova anandichirikiza.

6 Sindidzaopa unyinji wa anthu akundizinga ine.

7 Ukani Yehova; ndipulumutseni, Mulungu wanga! Pakuti mwapanda adani anga onse patsaya; mwawathyola mano oipawo.

8 Chipulumutso ncha Yehova; dalitso lanu likhale pa anthu anu.

Bible Society of Malawi

Bible Society of Malawi
Titsatireni:



Zotsatsa