Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Masalimo 22:8 - Buku Lopatulika

8 Adadzitengera kwa Yehova; kuti adzampulumutsa, amlanditse tsopano popeza akondwera naye.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

8 Adadzitengera kwa Yehova; kuti adzampulumutsa, amlanditse tsopano popeza akondwera naye.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

8 Amati, “Unkadalira Chauta, Chauta yemweyo akupulumutse. Akulanditsetu tsono, popeza kuti amakukonda.”

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

8 “Iyeyu amadalira Yehova, musiyeni Yehovayo amulanditse. Musiyeni Yehova amupulumutse popeza amakondwera mwa Yehovayo.”

Onani mutuwo Koperani




Masalimo 22:8
17 Mawu Ofanana  

Inenso ndikadanena monga inu, moyo wanu ukadakhala m'malo mwa moyo wanga, ndikadalumikizanitsa mau akutsutsana nanu, ndi kukupukusirani mutu wanga.


Ndiwakhaliranso chotonza; pakundiona apukusa mutu.


Ananditulutsanso andifikitse motakasuka; anandilanditsa, pakuti anakondwera ndi ine.


Pereka njira yako kwa Yehova; khulupiriranso Iye, adzachichita.


Adani anga andinyoza ndi kundithyola mafupa anga; pakunena ndine dzuwa lonse, Mulungu wako ali kuti?


Umsenze Yehova nkhawa zako, ndipo Iye adzakugwiriziza, nthawi zonse sadzalola wolungama agwedezeke.


ndi kuti, Wamsiya Mulungu. Mlondoleni, mgwireni; popeza palibe wompulumutsa.


Popeza andikondadi ndidzampulumutsa; ndidzamkweza m'mwamba, popeza adziwa dzina langa.


Pereka zochita zako kwa Yehova, ndipo zolingalira zako zidzakhazikika.


Taona Mtumiki wanga, amene ndimgwiriziza; Wosankhika wanga, amene moyo wanga ukondwera naye; ndaika mzimu wanga pa Iye; Iye adzatulutsira amitundu chiweruziro.


Taona mnyamata wanga, amene ndinamsankha, wokondedwa wanga, amene moyo wanga ukondwera naye; pa Iye ndidzaika Mzimu wanga, ndipo Iye adzalalikira chiweruzo kwa akunja.


Akali chilankhulire, onani, mtambo wowala unawaphimba iwo: ndipo onani, mau ali kunena mumtambo, Uyu ndiye Mwana wanga wokondedwa, mwa iyeyu ndikondwera, mverani Iye.


ndipo onani, mau akuchokera kumiyamba akuti, Uyu ndiye mwana wanga wokondedwa, mwa Iyeyu ndikondwera.


Ndipo anthu anaima alikupenya. Ndi akulunso anamlalatira Iye, nanena, Anapulumutsa ena; adzipulumutse yekha ngati iye ndiye Khristu wa Mulungu, wosankhidwa wake.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa