Mika 7:10 - Buku Lopatulika10 Pamenepo mdani wanga adzachiona, ndi manyazi adzamkuta iye amene adati kwa ine, Ali kuti Yehova Mulungu wako? Maso anga adzamuona; tsopano adzampondereza ngati thope la m'miseu. Onani mutuwoChichewa Buku Lopatulika Bible 201410 Pamenepo mdani wanga adzachiona, ndi manyazi adzamkuta iye amene adati kwa ine, Ali kuti Yehova Mulungu wako? Maso anga adzamuona; tsopano adzampondereza ngati thope la m'miseu. Onani mutuwoBuku Loyera Catholic Edition - Chichewa10 Tsono adani athu adzaona zimenezi, ndipo manyazi adzaŵagwira anthu amene ankatifunsa kuti, “Ali kuti Chauta, Mulungu wanu?” Tidzaona kugonjetsedwa kwao, adzaponderezedwa ngati matope m'miseu. Onani mutuwoMawu a Mulungu mu Chichewa Chalero10 Ndipo mdani wanga adzaona zimenezi nadzagwidwa ndi manyazi, iye amene anandifunsa kuti, “Ali kuti Yehova Mulungu wako?” Ndidzaona kugonjetsedwa kwake ndi maso anga; ngakhale tsopano adzaponderezedwa ngati matope mʼmisewu. Onani mutuwo |
Mukavomereza tsono, pakumva mau a lipenga, chitoliro, zeze, sansi, chisakasa, ndi ngoli, ndi zoimbitsa zilizonse, kugwadira ndi kulambira fano ndinalipanga, chabwino; koma mukapanda kulambira, mudzaponyedwa nthawi yomweyi m'kati mwa ng'anjo yotentha yamoto; ndipo mulungu yemwe adzakulanditsani m'manja mwanga ndani?