Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 11:2 - Buku Lopatulika

Pakuti, onani, oipa akoka uta, apiringidza muvi wao pansinga, kuwaponyera mumdima oongoka mtima.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Pakuti, onani, oipa akoka uta, apiringidza muvi wao pansinga, kuwaponyera mumdima oongoka mtima.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Taonani, anthu oipa akunga uta ndipo akwinja muvi pa nsinga, kuti alase anthu a mtima wolungama.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Pakuti taona oyipa akunga mauta awo; ayika bwino mivi yawo pa zingwe za uta, pobisala pawo kuti alase olungama mtima.

Onani mutuwo



Masalimo 11:2
18 Mawu Ofanana  

Podzikuza woipa apsereza waumphawi; agwe m'chiwembu anapanganacho.


Chitirani chokoma, Yehova, iwo okhala okoma; iwo okhala oongoka mumtima mwao.


Pamene mzimu wanga unakomoka m'kati mwanga, munadziwa njira yanga. M'njira ndiyendamo ananditchera msampha.


Pakuti mudzawabweza m'mbuyo, popiringidza m'nsinga zanu pankhope pao.


Sekerani mwa Yehova, ndimo kondwerani inu olungama mtima; ndipo fuulani mokondwera nonsenu oongoka mtima.


Oipa anasolola lupanga, nakoka uta wao; alikhe ozunzika ndi aumphawi, aphe amene ali oongoka m'njira.


Wolungama adzakondwera mwa Yehova, nadzakhulupirira Iye; ndipo oongoka mtima onse adzalemekeza.


Chikopa changa chili ndi Mulungu, wopulumutsa oongoka mtima.


Akapanda kutembenuka munthu, iye adzanola lupanga lake; wakoka uta wake, naupiringidza.


Pakuti chiweruzo chidzabwera kunka kuchilungamo, ndipo oongoka mtima onse adzachitsata.


Kuunika kufesekera wolungama, ndi chikondwerero oongoka mtima.


Ndipo apinda lilime lao ngati uta wao, liname; koma akula mphamvu m'dzikomo, koma si pachoonadi; pakuti alinkunkabe nachita zoipa, ndipo sandidziwa Ine, ati Yehova.


nakhala upo wakuti amgwire Yesu ndi chinyengo, namuphe.


Nati Saulo, Ndidzampatsa iye, kuti amkhalire msampha, ndi kuti dzanja la Afilisti limgwere. Chifukwa chake Saulo ananena ndi Davide, Lero udzakhala mkamwini wanga kachiwiri.


Ndipo Davide anadziwa kuti Saulo analikulingalira zomchitira zoipa; nati kwa Abiyatara wansembe, Bwera kuno ndi efodi.