Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -

Masalimo 125 - Buku Lopatulika


Okhulupirira Yehova akhazikika mtima
Nyimbo yokwerera.

1 Iwo akukhulupirira Yehova akunga phiri la Ziyoni, losasunthika, likhazikika kosatha.

2 Monga mapiri azinga Yerusalemu, momwemo Yehova azinga anthu ake, kuyambira tsopano kufikira nthawi zonse.

3 Pakuti ndodo yachifumu ya choipa siidzapumula pa gawo la olungama; kuti olungama asatulutse dzanja lao kuchita chosalungama.

4 Chitirani chokoma, Yehova, iwo okhala okoma; iwo okhala oongoka mumtima mwao.

5 Koma iwo akupatula kutsata njira zao zokhotakhota, Yehova adzawachotsa pamodzi ndi ochita zopanda pake. Mtendere ukhale pa Israele.

Bible Society of Malawi

Bible Society of Malawi
Titsatireni:



Zotsatsa