Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -

Masalimo 21 - Buku Lopatulika


Davide ayamika Mulungu pa kugonjetsa adani
Kwa Mkulu wa Nyimbo. Salimo la Davide.

1 Yehova, adzasekera mfumu mu mphamvu yanu; adzakondwera kwakukulu m'chipulumutso chanu!

2 Mwampatsa iye chikhumbo cha mtima wake, ndipo simunakane pempho la milomo yake.

3 Pakuti mufika kwa iye ndi madalitso okoma; muika korona wa golide woyengetsa pamutu pake.

4 Anakupemphani moyo, mwampatsa iye; mwamtalikitsira masiku kunthawi za nthawi.

5 Ulemerero wake ngwaukulu mwa chipulumutso chanu; mumchitira iye ulemu ndi ukulu.

6 Pakuti mumuikira madalitso kunthawi zonse; mumkondweretsa ndi chimwemwe pankhope panu.

7 Pakuti mfumu akhulupirira Yehova, ndipo mwa chifundo cha Wam'mwambamwamba sadzagwedezeka iye.

8 Dzanja lanu lidzapeza adani anu onse, dzanja lanu lamanja lidzapeza iwo akuda Inu.

9 Mudzawaika ngati ng'anjo yamoto pa nyengo ya mkwiyo wanu. Yehova adzawatha m'kukwiya kwake, ndipo moto udzawanyeketsa.

10 Mudzaziononga zobala zao kuzichotsa padziko lapansi, ndi mbeu zao mwa ana a anthu.

11 Pakuti anakupangirani choipa, anapangana chiwembu, osakhoza kuchichita.

12 Pakuti mudzawabweza m'mbuyo, popiringidza m'nsinga zanu pankhope pao.

13 Kwezekani, Yehova, mu mphamvu yanu; potero tidzaimba ndi kulemekeza chilimbiko chanu.

Bible Society of Malawi

Bible Society of Malawi
Titsatireni:



Zotsatsa