Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -

Masalimo 64 - Buku Lopatulika


Davide apempha Mulungu amtchinjirize pa omlalira
Kwa Mkulu wa Nyimbo. Salimo la Davide.

1 Imvani Mulungu, mau anga, m'kudandaula kwanga; sungani moyo wanga angandiopse mdani.

2 Ndibiseni pa upo wachinsinsi wa ochita zoipa; pa phokoso la ochita zopanda pake.

3 Amene anola lilime lao ngati lupanga, napiringidza mivi yao, ndiyo mau akuwawitsa;

4 kuponyera wangwiro mobisika: Amponyera modzidzimutsa, osaopa.

5 Alimbikitsana m'chinthu choipa; apangana za kutchera misampha mobisika; akuti, Adzaiona ndani?

6 Afunafuna zosalungama; kusanthula, asanthuladi mpaka kutha; chingakhale cha m'kati mwake mwa munthu, ndi mtima wozama.

7 Koma Mulungu adzawaponyera muvi; adzalaswa modzidzimutsa.

8 Adzawakhumudwitsa, lilime lao lidzawatsutsa; onse akuwaona adzawathawa.

9 Ndipo anthu onse adzachita mantha; nadzabukitsa chochita Mulungu, nadzasamalira ntchito yake.

10 Wolungama adzakondwera mwa Yehova, nadzakhulupirira Iye; ndipo oongoka mtima onse adzalemekeza.

Bible Society of Malawi

Bible Society of Malawi
Titsatireni:



Zotsatsa