Biblia Todo Logo
Mavesi a Baibulo

- Zotsatsa -


66 Mau a Mulungu Okhudza Chikondi Chake

66 Mau a Mulungu Okhudza Chikondi Chake

Chikondi cha Mulungu n’chodabwitsa kwambiri, choyera, changwiro, chopanda malire. Sichikufuna kubwezera chilichonse, chimakwirira zonse. Mulungu anakonda dziko kwambiri kotero kuti anatipereka Mwana wake yekhayo, kuti aliyense wokhulupirira Iye asatayike, koma akhale ndi moyo wosatha, monga mmene Yohane 3:16-18 amanenera.

Mulungu amandikonda ndi chikondi chopanda malire, chopanda kudzudzula, chopanda tsankho. Sandikonda chifukwa choti ndine wabwino kapena woyenera kukondedwa, amandikonda chifukwa ndili wamtengo wapatali kwa Iye. Ngakhale machimo anga, sandiipitsa, koma amandikhumbatira mobwerezabwereza. Amandikonda kwambiri moti anapereka zonse chifukwa cha ine, osayembekezera kuti ndingam’bwezere chilichonse.

Ngakhale akadziwa kuti ndingalakwe, anali atandikonderatu kale. Ndiye chifukwa chake ndiyenera kuyamikira chikondi chake, chifukwa ndi chinthu chabwino kwambiri chomwe chingandichitikire pa moyo wanga. Kudzera mwa Iye, ndimapeza mtendere, machiritso, kubwezeretsedwa, ndi ufulu.

Chikondi chake pa ine sichidzatha. M’mawa uliwonse amandiuza kuti “ndimakukonda”. Akayang’ana kumwamba amasekerera chifukwa cha ine, ndipo dzanja lake lamphamvu limandithandiza nthawi zonse, chifukwa anandisankha ine kuti ndichite zinthu zazikulu, ndipo sandikusiya. Chikondi chake sichitha, Iye ndi yemweyo masiku onse. Kukhulupirika kwake kumakhala kosatha.

Ndi chikondi chomwe timangolandira ndi kuchilandira, chodzaza chifundo ndi chisoni. Sachiganizira machimo athu, chifukwa amatikhululukira ndi kutilandira. Baibulo limatiuza kuti chikondi sichitha, chikondi ndiye maziko a moyo omwe tonse timafunikira.




1 Yohane 3:1

Taonani, chikondicho Atate watipatsa, kuti titchedwe ana a Mulungu; ndipo tili ife otere. Mwa ichi dziko lapansi silizindikira ife, popeza silimzindikira Iye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aefeso 1:5

Anatikonzeratu tilandiridwe ngati ana a Iye yekha mwa Yesu Khristu, monga umo kunakomera chifuniro chake,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 5:8

Koma Mulungu atsimikiza kwa ife chikondi chake cha mwini yekha m'menemo, kuti pokhala ife chikhalire ochimwa, Khristu adatifera ife.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 106:8

Koma anawapulumutsa chifukwa cha dzina lake, kuti adziwitse chimphamvu chake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 23:3

Atsitsimutsa moyo wanga; anditsogolera m'mabande a chilungamo, chifukwa cha dzina lake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Zefaniya 3:17

Yehova Mulungu wako ali pakati pako, wamphamvu wakupulumutsa; adzakondwera nawe ndi chimwemwe, adzakhala wopanda thamo m'chikondi chake; adzasekerera nawe ndi kuimbirapo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 5:5

ndipo chiyembekezo sichichititsa manyazi; chifukwa chikondi cha Mulungu chinatsanulidwa m'mitima mwathu mwa Mzimu Woyera, amene wapatsidwa kwa ife.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 8:39

ngakhale utali, ngakhale kuya, ngakhale cholengedwa china chilichonse, sichingadzakhoze kutisiyanitsa ife ndi chikondi cha Mulungu, chimene chili mwa Khristu Yesu Ambuye wathu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aefeso 2:4

koma Mulungu, wolemera chifundo, chifukwa cha chikondi chake chachikulu chimene anatikonda nacho,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Tito 3:4-5

Koma pamene kukoma mtima, ndi chikondi cha pa anthu, cha Mpulumutsi wathu Mulungu zidanoneka, zosati zochokera m'ntchito za m'chilungamo, zimene tidazichita ife, komatu monga mwa chifundo chake anatipulumutsa ife, mwa kutsuka kwa kubadwanso ndi makonzedwe a Mzimu Woyera,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Atesalonika 3:5

Ndipo Ambuye atsogolere bwino mitima yanu ilowe m'chikondi cha mulungu ndi m'chipiriro cha Khristu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 8:17

Akundikonda ndiwakonda; akundifunafuna adzandipeza.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yeremiya 31:3

Yehova anaonekera kwa ine kale, ndi kuti, Inde, ndakukonda iwe ndi chikondi chosatha; chifukwa chake ndakukoka iwe ndi kukukomera mtima.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 3:16

Pakuti Mulungu anakonda dziko lapansi kotero, kuti anapatsa Mwana wake wobadwa yekha, kuti yense wakukhulupirira Iye asatayike, koma akhale nao moyo wosatha.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 17:23

Ine mwa iwo, ndi Inu mwa Ine, kuti akhale angwiro mwa mmodzi; kuti dziko lapansi lizindikire kuti Inu munandituma Ine, nimunawakonda iwo, monga momwe munakonda Ine.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 14:23

Yesu anayankha nati kwa iye, Ngati wina akonda Ine, adzasunga mau anga; ndipo Atate wanga adzamkonda, ndipo tidzadza kwa iye, ndipo tidzayesa kwa iye mokhalamo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Yohane 4:19

Tikonda ife, chifukwa anayamba Iye kutikonda.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 8:37

Koma m'zonsezi, ife tilakatu, mwa Iye amene anatikonda.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Yohane 4:12

Palibe munthu adamuona Mulungu nthawi iliyonse; tikakondana wina ndi mnzake, Mulungu akhala mwa ife, ndi chikondi chake chikhala changwiro mwa ife;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Chivumbulutso 3:19

Onse amene ndiwakonda, ndiwadzudzula ndi kuwalanga; potero chita changu, nutembenuke mtima.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Yohane 4:10

Umo muli chikondi, sikuti ife tinakonda Mulungu, koma kuti Iye anatikonda ife, ndipo anatuma Mwana wake akhale chiombolo chifukwa cha machimo athu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Akorinto 8:9

Pakuti mudziwa chisomo cha Ambuye wathu Yesu Khristu, kuti, chifukwa cha inu anakhala wosauka, angakhale anali wolemera, kuti inu ndi kusauka kwake mukakhale olemera.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 94:18-19

Pamene ndinati, Literereka phazi langa, chifundo chanu, Yehova, chinandichirikiza. Pondichulukira zolingalira zanga m'kati mwanga, zotonthoza zanu zikondweretsa moyo wanga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Maliro 3:22-23

Chifukwa chakusathedwa ife ndicho chifundo cha Yehova, pakuti chisoni chake sichileka, chioneka chatsopano m'mawa ndi m'mawa; mukhulupirika ndithu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 16:27

pakuti Atate yekha akonda inu, chifukwa inu mwandikonda Ine, ndi kukhulupirira kuti Ine ndinatuluka kwa Atate.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 8:38-39

Pakuti ndakopeka mtima kuti ngakhale imfa, ngakhale moyo, ngakhale angelo, ngakhale maufumu, ngakhale zinthu zilipo, ngakhale zinthu zilinkudza, ngakhale zimphamvu, ngakhale utali, ngakhale kuya, ngakhale cholengedwa china chilichonse, sichingadzakhoze kutisiyanitsa ife ndi chikondi cha Mulungu, chimene chili mwa Khristu Yesu Ambuye wathu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Atesalonika 2:16

Ndipo Ambuye wathu Yesu Khristu, ndi Mulungu Atate wathu amene anatikonda natipatsa chisangalatso chosatha ndi chiyembekezo chokoma mwa chisomo,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Yohane 4:16

Ndipo ife tazindikira, ndipo takhulupirira chikondicho Mulungu ali nacho pa ife. Mulungu ndiye chikondi, ndipo iye amene akhala m'chikondi akhala mwa Mulungu, ndipo Mulungu akhala mwa iye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 3:3-4

Chifundo ndi choonadi zisakusiye; uzimange pakhosi pako; uzilembe pamtima pako; Usakangane ndi munthu chabe, ngati sanakuchitire choipa. Usachitire nsanje munthu wachiwawa; usasankhe njira yake iliyonse. Pakuti wamphulupulu anyansa Yehova; koma chinsinsi chake chili ndi oongoka. Yehova atemberera za m'nyumba ya woipa; koma adalitsa mokhalamo olungama. Anyozadi akunyoza, koma apatsa akufatsa chisomo. Anzeru adzalandira ulemu cholowa chao; koma opusa adzakweza manyazi. motero udzapeza chisomo ndi nzeru yabwino, pamaso pa Mulungu ndi anthu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 30:5

Pakuti mkwiyo wake ukhala kanthawi kokha; koma kuyanja kwake moyo wonse. Kulira kuchezera, koma mamawa kuli kufuula kokondwera.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 54:10

Pakuti mapiri adzachoka, ndi zitunda zidzasunthika; koma kukoma mtima kwanga sikudzakuchokera iwe, kapena kusunthika chipangano changa cha mtendere, ati Yehova amene wakuchitira iwe chifundo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 143:8

Mundimvetse chifundo chanu mamawa; popeza ndikhulupirira Inu: Mundidziwitse njira ndiyendemo; popeza ndikweza moyo wanga kwa Inu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 12:6

pakuti iye amene Ambuye amkonda amlanga, nakwapula mwana aliyense amlandira.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aefeso 5:2

ndipo yendani m'chikondi monganso Khristu anakukondani inu, nadzipereka yekha m'malo mwathu, chopereka ndi nsembe kwa Mulungu, ikhale fungo lonunkhira bwino.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 136:26

Yamikani Mulungu wa Kumwamba, pakuti chifundo chake nchosatha.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Deuteronomo 5:10

ndi kuchitira chifundo anthu zikwi, a iwo amene akondana ndi Ine nasunga malamulo anga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Deuteronomo 7:9

Chifukwa chake dziwani kuti Yehova Mulungu wanu ndiye Mulungu; ndiye Mulungu wokhulupirika, wakusunga chipangano ndi chifundo ndi iwo akumkonda ndi kusunga malamulo ake, kufikira mibadwo zikwi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 94:18

Pamene ndinati, Literereka phazi langa, chifundo chanu, Yehova, chinandichirikiza.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yuda 1:20

Koma inu, okondedwa, podzimangirira nokha pa chikhulupiriro chanu choyeretsetsa, ndi kupemphera mu Mzimu Woyera,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 57:10

Pakuti chifundo chanu nchachikulu kufikira m'mwamba, ndi choonadi chanu kufikira mitambo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aefeso 2:4-5

koma Mulungu, wolemera chifundo, chifukwa cha chikondi chake chachikulu chimene anatikonda nacho, tingakhale tinali akufa m'zolakwa zathu, anatipatsa moyo pamodzi ndi Khristu (muli opulumutsidwa ndi chisomo),

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Hoseya 14:4

Ndidzachiritsa kubwerera kwao, ndidzawakonda mwaufulu; pakuti mkwiyo wanga wamchokera.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 8:3

Koma ngati wina akonda Mulungu, yemweyu adziwika ndi Iye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 42:8

Koma usana Yehova adzalamulira chifundo chake, ndipo usiku nyimbo yake idzakhala ndi ine. Inde pemphero la kwa Mulungu wa moyo wanga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 2:9

koma monga kulembedwa, Zimene diso silinazione, ndi khutu silinazimve, nisizinalowe mu mtima wa munthu, zimene zilizonse Mulungu anakonzereratu iwo akumkonda Iye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 49:15

Kodi mkazi angaiwale mwana wake wa pabere, kuti iye sangachitire chifundo mwana wombala iye? Inde awa angaiwale, koma Ine sindingaiwale iwe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 3:12

pakuti Yehova adzudzula omwe awakonda; monga atate mwana amene akondwera naye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yobu 33:26

Apembedza Mulungu, ndipo amkomera mtima; m'mwemo aona nkhope yake mokondwera; ndipo ambwezera munthu chilungamo chake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 103:8

Yehova ndiye wa nsoni zokoma ndi wachisomo, wosakwiya msanga, ndi wa chifundo chochuluka.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Eksodo 20:6

ndi kuwachitira chifundo anthu zikwizikwi a iwo amene akondana ndi Ine, nasunga malamulo anga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Petro 5:7

ndi kutaya pa Iye nkhawa yanu yonse, pakuti Iye asamalira inu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 136:1

Yamikani Yehova pakuti ndiye wabwino; pakuti chifundo chake nchosatha.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aefeso 3:17-19

kuti Khristu akhale chikhalire mwa chikhulupiriro m'mitima yanu; kuti, ozika mizu ndi otsendereka m'chikondi, mukakhozetu kuzindikira pamodzi ndi oyera mtima onse, kupingasa, ndi utali, ndi kukwera, ndi kuzama nchiyani; ndi kuzindikira chikondi cha Khristu, chakuposa mazindikiridwe, kuti mukadzazidwe kufikira chidzalo chonse cha Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 145:9

Yehova achitira chokoma onse; ndi nsoni zokoma zake zigwera ntchito zake zonse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Agalatiya 2:20

Ndinapachikidwa ndi Khristu; koma ndili ndi moyo; wosatinso ine ai, koma Khristu ali ndi moyo mwa ine; koma moyo umene ndili nao tsopano m'thupi, ndili nao m'chikhulupiriro cha Mwana wa Mulungu, amene anandikonda, nadzipereka yekha chifukwa cha ine.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 8:32

Iye amene sanatimane Mwana wake wa Iye yekha, koma anampereka chifukwa cha ife tonse, adzalekeranji kutipatsanso ife zinthu zonse kwaulere pamodzi ndi Iye?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 86:15

Koma Inu, Ambuye, ndinu Mulungu wansoni ndi wachisomo, wopatsa mtima msanga, ndi wochulukira chifundo ndi choonadi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 136:23-24

Amene anatikumbukira popepuka ife; pakuti chifundo chake nchosatha. Natikwatula kwa otisautsa; pakuti chifundo chake nchosatha.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 63:9

M'mazunzo ao onse Iye anazunzidwa, ndipo mthenga wakuimirira pamaso pake anawapulumutsa; m'kukonda kwake ndi m'chisoni chake Iye anawaombola, nawabereka nawanyamula masiku onse akale.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 13:4-7

Chikondi chikhala chilezere, chili chokoma mtima; chikondi sichidukidwa; chikondi sichidziwa kudzitamanda, sichidzikuza, sichichita zosayenera, sichitsata za mwini yekha, sichipsa mtima, sichilingirira zoipa; sichikondwera ndi chinyengo, koma chikondwera ndi choonadi; chikwirira zinthu zonse, chikhulupirira zinthu zonse, chiyembekeza zinthu zonse, chipirira zinthu zonse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 36:7

Ha! Chifundo chanu, Mulungu, nchokondedwadi! Ndipo ana a anthu athawira kumthunzi wa mapiko anu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 15:9

Monga momwe Atate wandikonda Ine, Inenso ndakonda inu; khalani m'chikondi changa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 15:30

Ndipo ndikudandaulirani, abale, ndi Ambuye wathu Yesu Khristu, ndi chikondi cha Mzimu, kuti mudzalimbike pamodzi ndi ine m'mapemphero anu kwa Mulungu chifukwa cha ine;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Akolose 3:14

koma koposa izi zonse khalani nacho chikondano, ndicho chomangira cha mtima wamphumphu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Zekariya 2:8

Pakuti atero Yehova wa makamu: Utatha ulemererowo ananditumiza kwa amitundu amene anakufunkhani; pakuti iye wokhudza inu, akhudza mwana wa m'diso lake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani

Pemphero kwa Mulungu

Ambuye wanga wachifundo ndi wamphamvu! M'mawa uliwonse mumandionetsa chikondi chanu, mumandiuza kuti mumandikonda ndikatsegula maso anga ndi kuona thambo lalikulu labuluu, chikondi chanu chakhala chodzala m'moyo wanga, ndikukuthokozani chifukwa cha kukoma mtima kwanu, pakuti ndisanabadwe dziko, ndinali kale m'malingaliro mwanu, pakuti munakonda dziko kwambiri kotero kuti munapereka mwana wanu yekhayo kuti aliyense wokhulupirira iye asatayike koma akhale ndi moyo wosatha. Zikomo chifukwa chikondi chanu ndi changwiro, chokhazikika komanso chopanda malire. Munationetsa chikondi chanu ngakhale ine ndili wochimwa, Khristu anafera ine. Ndithandizeni kumvera mawu anu ndikuwatsatira, zikomo chifukwa chikondi chanu chathiridwa m'mitima yathu, kudzera mwa Mzimu Woyera. M'dzina la Yesu. Ameni.
Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa