Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 4:4 - Buku Lopatulika

Chitani chinthenthe, ndipo musachimwe. Nenani mumtima mwanu pakama panu, ndipo mukhale chete.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Chitani chinthenthe, ndipo musachimwe. Nenani mumtima mwanu pakama panu, ndipo mukhale chete.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Opani Mulungu, ndipo musachimwe. Mukhale phee ndipo muganize zimenezi mu mtima pamene mukugona.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Kwiyani koma musachimwe; pamene muli pa mabedi anu, santhulani mitima yanu ndi kukhala chete. Sela

Onani mutuwo



Masalimo 4:4
17 Mawu Ofanana  

Koma kwa munthu anati, Taonani, kuopa Ambuye ndiko nzeru; ndi kupatukana nacho choipa ndiko luntha.


Nduna zinandilondola kopanda chifukwa; koma mtima wanga uchita nao mantha mau anu.


Ine ndinakuitanani, pakuti mudzandiyankha, Mulungu; tcherani khutu lanu kwa ine, imvani mau anga.


Tumikirani Yehova ndi mantha, ndipo kondwerani ndi chinthenthe.


Ambiri amati kwa moyo wanga, alibe chipulumutso mwa Mulungu.


Ndifuula kwa Yehova ndi mau anga, ndipo andiyankha m'phiri lake loyera.


Dziko lonse lapansi liope Yehova, ponse pali anthu achite mantha chifukwa cha Iye.


Khalani chete, ndipo dziwani kuti Ine ndine Mulungu, Ndidzabuka mwa amitundu, ndidzabuka padziko lapansi.


Pokumbukira Inu pa kama wanga, ndi kulingalira za Inu maulonda a usiku.


Ndikumbukira nyimbo yanga usiku; ndilingalira mumtima mwanga; mzimu wanga unasanthula.


Khwalala la oongoka mtima ndilo lakuti asiye zoipa; wosunga njira yake atchinjiriza moyo wake.


Mphulupulu iomboledwa ndi chifundo ndi ntheradi; apatuka pa zoipa poopa Yehova.


Usadziyese wekha wanzeru; opa Yehova, nupatuke pazoipa;


Kodi simundiopa Ine? Ati Yehova: simudzanthunthumira pamaso pa Ine, amene ndinaika mchenga chilekaniro cha nyanja, ndi lemba lamuyaya kuti isapitirirepo? Ndipo ngakhale mafunde ake achita gavigavi, alephera; ngakhale akokoma, sangathe kupitirirapo.


Koma Yehova ali mu Kachisi wake wopatulika; dziko lonse lapansi likhale chete pamaso pake.


Dziyeseni nokha, ngati muli m'chikhulupiriro, dzitsimikizeni nokha. Kapena simuzindikira kodi za inu nokha kuti Yesu Khristu ali mwa inu? Mukapanda kukhala osatsimikizidwa.


Kwiyani, koma musachimwe; dzuwa lisalowe muli chikwiyire,