Biblia Todo Logo
Mavesi a Baibulo
- Zotsatsa -



65 Mau a Chipulumutso m’Chipangano Chakale

65 Mau a Chipulumutso m’Chipangano Chakale

Kuyambira pachiyambi pomwe Mulungu analenga zinthu zonse, wandionetsa ine chikondi chake chachikulu. Analenganso mwamuna ndi mkazi kuti akhale paubwenzi naye.

Ngakhale titachimwa, Mulungu m’chifundo chake anasankha kundikhululukira ine osandilola kuti nditayike. Kale, chikhululukiro cha Mulungu chinkafuna nsembe ya nyama yopanda chilema, ndipo kudzera m’nsembeyi Ambuye anakhazikitsanso pangano lake ndi Nowa, lonjeza kuti sadzawononganso dziko lapansi chifukwa cha kuipa kwa anthu.

Nthawi zonse, Mulungu amayesetsa kundiyendetsa ine kubwera kwa Iye. Koma ambiri anasiya malamulo a Mulungu ndipo anatayika.

Kale, Ambuye anathandiza anthu ndipo nthawi zonse anali nafe, akutionetsa momwe angatipulumutsire. M’Chipangano Chakale, anthu ankayembekezera Mesiya, ndipo Mulungu anakwaniritsa malonjezo ake ngakhale asanatumize Mpulumutsi wathu.

Monga mmene lemba la Genesis 49:18 limati, “Ndikuyembekezera chipulumutso chanu, Yehova.”




Genesis 49:18

Ndadikira chipulumutso chanu, Yehova.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Eksodo 14:13

Ndipo Mose ananena ndi anthu, Musaope, chilimikani, ndipo penyani chipulumutso cha Yehova, chimene adzakuchitirani lero; pakuti Aejipito mwawaona lerowa, simudzawaonanso konse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yobu 13:16

Iye adzakhalanso chipulumutso changa, pakuti wonyoza Mulungu sadzafika pamaso pake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Eksodo 15:2

Yehova ndiye mphamvu yanga ndi nyimbo yanga, ndipo wakhala chipulumutso changa; ameneyo ndiye Mulungu wanga, ndidzamlemekeza; ndiye Mulungu wa kholo langa, ndidzamveketsa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Samueli 2:1

Ndipo Hana anapemphera, nati, Mtima wanga umyuka mokondwera kwa Yehova, nyanga yanga yakwezeka mwa Yehova; pakamwa panga pakula kwa adani anga; popeza ndikondwera m'chipulumutso chanu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Samueli 11:13

Koma Saulo anati, Sadzaphedwa lero munthu; pakuti lero Yehova anachita chipulumutso mu Israele.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Samueli 19:5

popeza iye anataya moyo wake nakantha Mfilistiyo, ndipo Yehova anachitira Aisraele onse chipulumutso chachikulu, inu munachiona, nimunakondwera; tsono mudzachimwiranji mwazi wosalakwa, ndi kumupha Davide popanda chifukwa?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 25:5

Munditsogolere m'choonadi chanu, ndipo mundiphunzitse; pakuti Inu ndinu Mulungu wa chipulumutso changa; Inu ndikuyembekezerani tsiku lonseli.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mika 7:7

Koma ine, ndidzadikira Yehova; ndidzalindirira Mulungu wa chipulumutso changa; Mulungu wanga adzandimvera.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 80:19

Mutibweze, Yehova Mulungu wa makamu; nimuwalitse nkhope yanu, ndipo tidzapulumuka.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 33:22

Pakuti Yehova ndiye woweruza wathu, Yehova ndiye wotipatsa malamulo, Yehova ndiye mfumu yathu; Iye adzatipulumutsa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 62:7

Pa Mulungu pali chipulumutso changa ndi ulemerero wanga. Thanthwe la mphamvu yanga ndi pothawirapo panga mpa Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Genesis 3:15

ndipo ndidzaika udani pakati pa iwe ndi mkaziyo, ndi pakati pa mbeu yako ndi mbeu yake; ndipo idzalalira mutu wako, ndipo iwe udzalalira chitendeni chake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 34:17-18

Iwowo anaitana, ndipo Yehova anawamva, nawalanditsa kumasautso ao onse. Yehova ali pafupi ndi iwo a mtima wosweka, apulumutsa iwo a mzimu wolapadi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 62:1

Moyo wanga ukhalira chete Mulungu yekha; chipulumutso changa chifuma kwa Iye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Genesis 12:3

ndipo ndidzadalitsa amene akudalitsa iwe; ndi kutemberera iye amene akutemberera iwe; ndipo mwa iwe adzadalitsidwa mabanja onse a dziko lapansi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yeremiya 17:14

Mundichiritse ine, Yehova, ndipo ndidzachiritsidwa; mundipulumutse ine, ndipo ndidzapulumutsidwa; pakuti chilemekezo changa ndinu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 103:12

Monga kum'mawa kutanimpha ndi kumadzulo, momwemo anatisiyanitsira kutali zolakwa zathu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yobu 19:25

Koma ndidziwa kuti Mombolo wanga ali ndi moyo, nadzauka potsiriza pafumbi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 3:8

Chipulumutso ncha Yehova; dalitso lanu likhale pa anthu anu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 79:9

Tithandizeni Mulungu wa chipulumutso chathu, chifukwa cha ulemerero wa dzina lanu; ndipo tilanditseni, ndi kutifafanizira zoipa zathu, chifukwa cha dzina lanu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 68:19

Wolemekeza Ambuye, tsiku ndi tsiku atisenzera katundu, ndiye Mulungu wa chipulumutso chathu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yona 2:9

Koma ine ndidzakupherani Inu nsembe ndi mau akuyamika, ndidzakwaniritsa chowinda changa. Chipulumutso ncha Yehova.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Samueli 22:47

Yehova ali ndi moyo; ndipo lidalitsike thanthwe langa; ndipo akulitsidwe Mulungu wa thanthwe la chipulumutso changa;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 27:1

Yehova ndiye kuunika kwanga ndi chipulumutso changa; ndidzaopa yani? Yehova ndiye mphamvu ya moyo wanga; ndidzachita mantha ndi yani?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 62:1-2

Moyo wanga ukhalira chete Mulungu yekha; chipulumutso changa chifuma kwa Iye. Musakhulupirire kusautsa, ndipo musatama chifwamba; chikachuluka chuma musakhazikepo mitima yanu. Mulungu ananena kamodzi, ndinachimva kawiri, kuti mphamvu ndi yake ya Mulungu. Chifundonso ndi chanu, Ambuye, Chifukwa Inu mubwezera munthu aliyense monga mwa ntchito yake. Iye yekhayo ndiye thanthwe langa ndi chipulumutso changa; msanje wanga, sindidzagwedezeka kwakukulu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 12:2

Taonani, Mulungu ndiye chipulumutso changa; ndidzakhulupirira, sindidzaopa; pakuti Yehova Mwini ndiye mphamvu yanga ndi nyimbo yanga, Iye ndiye chipulumutso changa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 37:39

Koma chipulumutso cha olungama chidzera kwa Yehova, Iye ndiye mphamvu yao m'nyengo ya nsautso.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 12:1

Tsiku lomwelo udzati, Ndikuyamikani inu Yehova; pakuti ngakhale munandikwiyira, mkwiyo wanu wachoka, ndipo mutonthoza mtima wanga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 51:12

Mundibwezere chimwemwe cha chipulumutso chanu; ndipo mzimu wakulola undigwirizize.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 45:22

Yang'anani kwa Ine, mupulumutsidwe, inu malekezero onse a dziko; pakuti Ine ndine Mulungu, palibe wina.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ezekieli 18:30

Chifukwa chake ndidzakuweruzani inu, nyumba ya Israele, yense monga mwa njira zake, ati Ambuye Yehova. Bwererani, nimutembenukire kuleka zolakwa zanu zonse, ndipo simudzakhumudwa nazo, ndi kuonongeka nayo mphulupulu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 31:16

Walitsani nkhope yanu pa mtumiki wanu, mundipulumutse ndi chifundo chanu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 68:20

Mulungu akhala kwa ife Mulungu wa chipulumutso; ndipo Yehova Ambuye ali nazo zopulumutsira kuimfa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 25:9

Ndipo adzanena tsiku limenelo, Taonani, uyu ndiye Mulungu wathu; tamlindirira Iye, adzatipulumutsa; uyu ndiye Yehova, tamlindirira Iye, tidzakondwa ndi kusekerera m'chipulumutso chake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 37:39-40

Koma chipulumutso cha olungama chidzera kwa Yehova, Iye ndiye mphamvu yao m'nyengo ya nsautso. Udzikondweretsenso mwa Yehova; ndipo Iye adzakupatsa zokhumba mtima wako. Ndipo Yehova awathandiza, nawalanditsa; awalanditsa kwa oipa nawapulumutsa, chifukwa kuti anamkhulupirira Iye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 43:11

Ine, Inetu ndine Yehova; ndipo palibe Mpulumutsi, koma Ine ndekha.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 45:17

Koma Israele adzapulumutsidwa ndi Yehova ndi chipulumutso chosatha; inu simudzakhala ndi manyazi, pena kuthedwa nzeru kunthawi zosatha.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 46:4

ngakhale mpaka mudzakalamba Ine ndine, ndipo ngakhale mpaka tsitsi laimvi, Ine ndidzakusenzani inu; ndalenga, ndipo ndidzanyamula; inde, ndidzasenza, ndipo ndidzapulumutsa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yeremiya 3:22

Bwerani, ana inu obwerera, ndidzachiritsa mabwerero anu. Taonani, tadza kwa Inu; pakuti ndinu Yehova Mulungu wathu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ezekieli 36:26-27

Ndipo ndidzakupatsani mtima watsopano, ndi kulonga m'kati mwanu mzimu watsopano; ndipo ndidzachotsa mtima wamwala m'thupi, ndi kukupatsani mtima wamnofu. Ndipo ndidzaika mzimu wanga m'kati mwanu, ndi kukuyendetsani m'malemba anga; ndipo mudzasunga maweruzo anga ndi kuwachita.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 91:14-16

Popeza andikondadi ndidzampulumutsa; ndidzamkweza m'mwamba, popeza adziwa dzina langa. Adzandifuulira Ine ndipo ndidzamyankha; kunsautso ndidzakhala naye pamodzi; ndidzamlanditsa, ndi kumchitira ulemu. Ndidzamkhutitsa ndi masiku ambiri, ndi kumuonetsera chipulumutso changa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 118:14

Yehova ndiye mphamvu yanga ndi nyimbo yanga; ndipo anakhala chipulumutso changa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:81

Moyo wanga unakomoka ndi kukhumba chipulumutso chanu: Ndinayembekezera mau anu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 130:7-8

Israele, uyembekezere Yehova; chifukwa kwa Yehova kuli chifundo, kwaonso kuchulukira chiombolo. Ndipo adzaombola Israele ku mphulupulu zake zonse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 146:7

ndiye wakuchitira chiweruzo osautsika; ndiye wakupatsa anjala chakudya; Yehova amasula akaidi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 61:1

Mzimu wa Ambuye Yehova uli pa ine; pakuti Yehova wandidzoza ine ndilalikire mau abwino kwa ofatsa; Iye wanditumiza ndikamange osweka mtima, ndikalalikire kwa am'nsinga mamasulidwe, ndi kwa omangidwa kutsegulidwa kwa m'ndende;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mika 7:7-9

Koma ine, ndidzadikira Yehova; ndidzalindirira Mulungu wa chipulumutso changa; Mulungu wanga adzandimvera. Usandiseka, mdani wangawe; pakugwa ine ndidzaukanso; pokhala ine mumdima Yehova adzakhala kuunika kwanga. Ndidzasenza mkwiyo wa Yehova, chifukwa ndamchimwira, mpaka andinenera mlandu wanga, ndi kundiweruzira mlandu wanga; adzanditulutsira kwa kuunika, ndipo ndidzapenya chilungamo chake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Zekariya 9:9

Kondwera kwambiri, mwana wamkazi wa Ziyoni; fuula mwana wamkazi wa Yerusalemu; taona, Mfumu yako ikudza kwa iwe; ndiye wolungama, ndi mwini chipulumutso; wofatsa ndi wokwera pabulu, ndi mwana wamphongo wa bulu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mika 7:18-19

Ndani Mulungu wofanana ndi Inu, wakukhululukira mphulupulu, wakupitirira zolakwa za otsala a cholowa chake? Sasunga mkwiyo wake kunthawi yonse popeza akondwera nacho chifundo. Adzabwera, nadzatichitira nsoni; adzagonjetsa mphulupulu zathu; ndipo mudzataya zochimwa zao zonse m'nyanja yakuya.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Eksodo 14:13-14

Ndipo Mose ananena ndi anthu, Musaope, chilimikani, ndipo penyani chipulumutso cha Yehova, chimene adzakuchitirani lero; pakuti Aejipito mwawaona lerowa, simudzawaonanso konse. Yehova adzakugwirirani nkhondo, ndipo inu mudzakhala chete.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 34:22

Yehova aombola moyo wa anyamata ake, ndipo sadzawatsutsa kumlandu onse akukhulupirira Iye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 46:1

Mulungu ndiye pothawirapo pathu ndi mphamvu yathu, thandizo lopezekeratu m'masautso.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Deuteronomo 30:19-20

Ndichititsa mboni lero, kumwamba ndi dziko lapansi zitsutse inu; ndaika pamaso panu moyo ndi imfa, mdalitso ndi temberero; potero, sankhani moyo, kuti mukhale ndi moyo, inu ndi mbeu zanu; nimukabwerera kwa Yehova Mulungu wanu, ndi kumvera mau ake, monga mwa zonse ndikuuzani lero lino, inu ndi ana anu, ndi mtima wanu wonse, ndi moyo wanu wonse; kukonda Yehova Mulungu wanu, kumvera mau ake, ndi kummamatira Iye, pakuti Iye ndiye moyo wanu, ndi masiku anu ochuluka; kuti mukhale m'dziko limene Yehova analumbirira makolo anu, Abrahamu, Isaki, ndi Yakobo, kuwapatsa ili.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:41

Ndipo chifundo chanu chindidzere, Yehova, ndi chipulumutso chanu, monga mwa mau anu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 40:1-2

Mutonthoze, mutonthoze mtima wa anthu anga, ati Mulungu wanu. Taonani, Ambuye Yehova adzadza ngati wamphamvu, ndipo mkono wake udzalamulira; taonani, mphotho yake ili ndi Iye, ndipo chobwezera chake chili patsogolo pa Iye. Iye adzadyetsa zoweta zake ngati mbusa, nadzasonkhanitsa anaankhosa m'manja mwake, nadzawatengera pa chifuwa chake, ndipo adzatsogolera bwinobwino zimene ziyamwitsa. Ndani wayesa madzi m'dzanja lake, nayesa thambo ndi chikhato, ndi kudzaza fumbi la nthaka m'nsengwa, ndi kuyesa mapiri m'mbale zoyesera, ndi zitunda m'mulingo? Ndani anapangira mzimu wa Yehova, kapena kukhala phungu lake, ndi kumphunzitsa Iye? Iye anakhala upo ndi yani, ndipo ndani analangiza Iye ndi kumphunzitsa m'njira ya chiweruzo, ndi kumphunzitsa nzeru ndi kumuonetsa njira ya luntha? Taonani, amitundu akunga dontho la m'mtsuko, nawerengedwa ngati fumbi losalala la m'muyeso; taonani atukula zisumbu ngati kanthu kakang'ono. Ndipo Lebanoni sakwanira kutentha, ngakhale nyama zake sizikwanira nsembe yopsereza. Amitundu onse ali chabe pamaso pa Iye; awayesa ngati chinthu chachabe, ndi chopanda pake. Mudzafanizira Mulungu ndi yani tsopano, kapena kumyerekeza ndi chithunzithunzi chotani? Fano losema mmisiri analisungunula, ndipo wosula golide analikuta ndi golide, naliyengera maunyolo asiliva. Munene inu zotonthoza mtima kwa Yerusalemu, nimufuulire kwa iye, kuti nkhondo yake yatha, kuti kuipa kwake kwakhululukidwa; kuti iye walandira mowirikiza m'dzanja la Yehova, chifukwa cha machimo ake onse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 139:7

Ndidzapita kuti kuzembera mzimu wanu? Kapena ndidzathawira kuti kuzembera nkhope yanu?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 18:10

Dzina la Yehova ndilo nsanja yolimba; wolungama athamangiramo napulumuka.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 143:10

Mundiphunzitse chokonda Inu; popeza Inu ndinu Mulungu wanga; Mzimu wanu ndi wokoma; munditsogolere kuchidikha.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yoweli 2:32

Ndipo kudzachitika kuti aliyense adzaitana pa dzina la Yehova adzapulumutsidwa; pakuti m'phiri la Ziyoni ndi mu Yerusalemu mudzakhala chipulumutso, monga Yehova anatero, ndi mwa otsala amene Yehova adzawaitana.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Habakuku 3:18

koma ndidzakondwera mwa Yehova, ndidzasekerera mwa Mulungu wa chipulumutso changa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Zekariya 2:10-11

Imba, nukondwere, mwana wamkazi wa Ziyoni; pakuti taonani, ndilinkudza, ndipo ndidzakhala pakati pako, ati Yehova. Ndipo amitundu ambiri adzaphatikidwa kwa Yehova tsiku ilo, nadzakhala anthu anga; ndipo ndidzakhala pakati pako, ndipo udzadziwa kuti Yehova wa makamu anandituma kwa iwe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 59:1

Taonani, mkono wa Yehova sufupika, kuti sungathe kupulumutsa; khutu lake silili logontha, kuti silingamve;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 53:5-6

Koma Iye analasidwa chifukwa cha zolakwa zathu, natundudzidwa chifukwa cha mphulupulu zathu; chilango chotitengera ife mtendere chinamgwera Iye; ndipo ndi mikwingwirima yake ife tachiritsidwa. Tonse tasochera ngati nkhosa; tonse tayenda yense m'njira ya mwini yekha; ndipo Yehova anaika pa Iye mphulupulu ya ife tonse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani

Pemphero kwa Mulungu

Ambuye Wopulumutsa! Lero ndikufuulirani inu, ndikuyang'ana nkhope yanu kuti ndikuyamikireni chifukwa ndinu Mulungu wa chipulumutso changa, ndi amene mumayenda patsogolo panga ngati chimphona champhamvu, mukumenyera nkhondo zanga. Monga momwe munatulutsira Aisraeli m'dziko la udziko la Igupto ndi dzanja lanu lamphamvu ndi lotambasuka, zikomo Atate, chifukwa simuswa mawu anu ndi mapangano anu. Zikomo chifukwa cha lonjezo la Mpulumutsi ndi Munthu Womasula. Kuyambira kale lomwe dziko lisanakhaleko, munaganizira kale za chipulumutso cha anthu, pakuti monga momwe imfa inadzera mwa munthu mmodzi, chiukiriro nachonso chidzera mwa munthu mmodzi. Zikomo Atate chifukwa kumene uchimo unachuluka, chisomo chinachulukirapo. Mulungu wanga, ulemerero ndi ulemu zonse zikhale zanu. M'dzina la Yesu. Ameni.
Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa