Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Genesis 49:18 - Buku Lopatulika

18 Ndadikira chipulumutso chanu, Yehova.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

18 Ndadikira chipulumutso chanu, Yehova.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

18 “Ndikuyembekeza chipulumutso chanu, Inu Chauta.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

18 “Ndikuyembekeza chipulumutso chanu Yehova.

Onani mutuwo Koperani




Genesis 49:18
32 Mawu Ofanana  

Dani adzakhala njoka m'khwalala, songo panjira, imene iluma zitendene za kavalo, kuti womkwera wake agwe chambuyo.


Ndinayembekeza chipulumutso chanu, Yehova, ndipo ndinachita malamulo anu.


Ndinakhumba chipulumutso chanu, Yehova; ndipo chilamulo chanu ndicho chondikondweretsa.


Ndipo chifundo chanu chindidzere, Yehova, ndi chipulumutso chanu, monga mwa mau anu.


Taonani, monga maso a anyamata ayang'anira dzanja la ambuye wao, monga maso a adzakazi ayang'anira dzanja la mbuye wao wamkazi: Momwemo maso athu ayang'anira Yehova Mulungu wathu, kufikira atichitira chifundo.


Ndilindira Yehova, moyo wanga ulindira, ndiyembekeza mau ake.


Mwenzi chipulumutso cha Israele chitachokera ku Ziyoni! Pakubweretsa Yehova anthu ake a m'nsinga, pamenepo adzakondwera Yakobo, nadzasekera Israele.


Kuyembekeza ndayembekeza Yehova; ndipo anandilola, namva kufuula kwanga.


Moyo wanga ukhalira chete Mulungu yekha; chipulumutso changa chifuma kwa Iye.


Moyo wanga, ukhalire chete Mulungu yekha; pakuti chiyembekezo changa chifuma kwa Iye.


Tionetseni chifundo chanu, Yehova, tipatseni chipulumutso chanu.


Yehova ndiye mphamvu yanga ndi nyimbo yanga, ndipo wakhala chipulumutso changa; ameneyo ndiye Mulungu wanga, ndidzamlemekeza; ndiye Mulungu wa kholo langa, ndidzamveketsa.


Wochimwa adzakankhidwa m'kuipa kwake; koma wolungama akhulupirirabe pomwalira.


Ndipo adzanena tsiku limenelo, Taonani, uyu ndiye Mulungu wathu; tamlindirira Iye, adzatipulumutsa; uyu ndiye Yehova, tamlindirira Iye, tidzakondwa ndi kusekerera m'chipulumutso chake.


Chifukwa chake Yehova adzadikira, kuti akukomereni mtima, ndipo chifukwa chake Iye adzakuzidwa, kuti akuchitireni inu chifundo; pakuti Yehova ndiye Mulungu wa chiweruziro; odala ali onse amene amdikira Iye.


Inu Yehova, mutikomere ife mtima; ife talindira Inu; mukhale dzanja lathu m'mawa ndi m'mawa, chipulumutso chathunso m'nthawi ya mavuto.


Chifukwa chake upereketu zikole kwa mbuyanga, mfumu ya Asiriya, ndipo ine ndidzakupatsa iwe akavalo zikwi ziwiri, ngati iwe udzaona okwerapo.


Ndipo ndidzalindira Yehova, amene wabisira a nyumba ya Yakobo nkhope yake, ndipo ndidzamyembekeza Iye.


Yehova akhalira wabwino omlindirira, ndi moyo womfunafuna.


Ndiye Mkanani, m'dzanja lake muli miyeso yonyenga, akonda kusautsa.


Koma ine, ndidzadikira Yehova; ndidzalindirira Mulungu wa chipulumutso changa; Mulungu wanga adzandimvera.


Ndipo adzabala mwana wamwamuna, ndipo udzamutcha dzina lake Yesu; pakuti Iyeyo adzapulumutsa anthu ake kumachimo ao.


anadzapo Yosefe wa ku Arimatea, mkulu wa milandu womveka, amene yekha analikuyembekezera Ufumu wa Mulungu; nalimba mtima nalowa kwa Pilato, napempha mtembo wake wa Yesu.


Ndipo mngelo anati kwa iye, Usaope, Maria; pakuti wapeza chisomo ndi Mulungu.


Ndipo onani, mu Yerusalemu munali munthu, dzina lake Simeoni; ndipo munthu uyu, wolungama mtima ndi wopemphera, analikulindira matonthozedwe a Israele; ndipo Mzimu Woyera anali pa iye.


chifukwa maso anga adaona chipulumutso chanu,


(amene sanavomereze kuweruza kwao ndi ntchito yao) wa ku Arimatea, mudzi wa Ayuda, ndiye woyembekezera Ufumu wa Mulungu,


Pakuti chiyembekezetso cha cholengedwa chilindira vumbulutso la ana a Mulungu.


Koma ngati tiyembekezera chimene sitichipenya, pomwepo tichilindirira ndi chipiriro.


Pakuti ife mwa Mzimu, kuchokera m'chikhulupiriro, tilindira chiyembekezo cha chilungamo.


ndi kulindirira Mwana wake achokere Kumwamba, amene anamuukitsa kwa akufa, Yesu, wotipulumutsa ife kumkwiyo ulinkudza.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa