Mavesi a Baibulo

Zotsatsa


Gulu Laling'ono

NDIME ZA MULUNGU

Mulungu ndiye mlengi wako, mtetezi wako, wosamalira wako. Ndi wamphamvuzonse, wachifundo, wokhululuka, wabwino. Tingadziwe Mulungu kudzera m'mawu ake. Amakuikira mtima ndipo wakupangira dongosolo labwino pa moyo wako.

Amadziwa zonse zisanachitike. Ndi chikondi chosatha. Pakuti Ine Yehova ndine Mulungu wako, wakugwira dzanja lako lamanja, nanena ndi iwe, Usawopa; Ine ndikuthandiza. (Yesaya 41:13)

Choncho Mulungu nthawi zonse adzakhala nafe, timangofunika kumuyandikila. Iye ndiye mlengi ndi wosamalira zinthu zonse, amene anapulumutsa dziko kudzera mwa Mwana wake, Yesu Khristu.


Masalimo 50:14

Pereka kwa Mulungu nsembe yachiyamiko; numchitire Wam'mwambamwamba chowinda chako.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 100:1

Fuulirani kwa Yehova, inu, dziko lonse lapansi.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 47:7

Pakuti Mulungu ndiye mfumu ya dziko lonse lapansi; imbirani ndi chilangizo.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 67:3

Anthu akuyamikeni, Mulungu; anthu onse akuyamikeni.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 145:1

Ndidzakukwezani Mulungu wanga, Mfumu; ndipo ndidzalemekeza dzina lanu kunthawi za nthawi.

Mutu    |  Mabaibulo
Yeremiya 33:9

Ndipo ndidzayesa mudzi uno chifukwa cha kukondwa, ndi chiyamiko ndi ulemerero, pamaso pa amitundu onse a pa dziko lapansi, amene adzamva zabwino zonse ndidzawachitirazo, ndipo adzaopa nadzanthunthumira chifukwa cha zabwino zonse ndi mtendere wonse zimene ndidzauchitira.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:171

Milomo yanga itulutse chilemekezo; popeza mundiphunzitsa malemba anu.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Mbiri 16:25

Pakuti Yehova ali wamkulu, nayenera kulemekezedwa kwakukulu; ayenera amuope koposa milungu yonse.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 40:3

Ndipo anapatsa nyimbo yatsopano m'kamwa mwanga, chilemekezo cha kwa Mulungu wanga; ambiri adzachiona, nadzaopa, ndipo adzakhulupirira Yehova.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 34:1

Ndidzalemekeza Yehova nyengo zonse; kumlemekeza kwake kudzakhala m'kamwa mwanga kosalekeza.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 100:4

Lowani kuzipata zake ndi chiyamiko, ndi kumabwalo ake ndi chilemekezo: Myamikeni; lilemekezeni dzina lake.

Mutu    |  Mabaibulo
Ahebri 13:15

Potero mwa Iye tipereke chiperekere nsembe yakuyamika Mulungu, ndiyo chipatso cha milomo yovomereza dzina lake.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 147:7

Yamikani Yehova ndi kuthira mang'ombe; muimbireni Mulungu wathu zomlemekeza pazeze:

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 96:6

Pamaso pake pali ulemu ndi ukulu. M'malo opatulika mwake muli mphamvu ndi zochititsa kaso.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 96:4

Pakuti Yehova ndi wamkulu, nayenera kulemekezedwa kwakukulu; ayenera amuope koposa milungu yonse.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 75:9

Koma ine ndidzalalikira kosalekeza, ndidzaimbira zomlemekeza Mulungu wa Yakobo.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 95:6-7

Tiyeni, tipembedze tiwerame; tigwade pamaso pa Yehova, amene anatilenga.

Pakuti Iye ndiye Mulungu wathu, ndipo ife ndife anthu a pabusa pake, ndi nkhosa za m'dzanja mwake. Lero, mukamva mau ake!

Mutu    |  Mabaibulo
Yona 2:9

Koma ine ndidzakupherani Inu nsembe ndi mau akuyamika, ndidzakwaniritsa chowinda changa. Chipulumutso ncha Yehova.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 145:21

Pakamwa panga padzanena chilemekezo cha Yehova; ndi zinthu zonse zilemekeze dzina lake loyera kunthawi za nthawi.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Mbiri 16:27

Pamaso pake pali ulemu ndi ukulu, m'malo mwake muli mphamvu ndi chimwemwe.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 148:2

Mlemekezeni, angelo ake onse; mlemekezeni, makamu ake onse.

Mutu    |  Mabaibulo
Yohane 4:24

Mulungu ndiye mzimu; ndipo omlambira Iye ayenera kumlambira mumzimu ndi m'choonadi.

Mutu    |  Mabaibulo
Eksodo 15:11

Afanana ndi Inu ndani mwa milungu, Yehova? Afanana ndi Inu ndani, wolemekezedwa, woyera, woopsa pomyamika, wakuchita zozizwa?

Mutu    |  Mabaibulo
Eksodo 15:2

Yehova ndiye mphamvu yanga ndi nyimbo yanga, ndipo wakhala chipulumutso changa; ameneyo ndiye Mulungu wanga, ndidzamlemekeza; ndiye Mulungu wa kholo langa, ndidzamveketsa.

Mutu    |  Mabaibulo
Danieli 2:23

Ndikuyamikani ndi kukulemekezani Inu, Mulungu wa makolo anga, pakuti mwandipatsa nzeru ndi mphamvu; ndipo mwandidziwitsa tsopano ichi tachifuna kwa Inu; pakuti mwatidziwitsa mlandu wa mfumu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 150:6

Zonse zakupuma zilemekeze Yehova. Aleluya.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 35:28

Ndipo lilime langa lilalikire chilungamo chanu, ndi lemekezo lanu tsiku lonse.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 95:2

Tidze nacho chiyamiko pamaso pake, timfuulire Iye mokondwera ndi nyimbo.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 33:1

Fuulani mokondwera mwa Yehova, inu olungama mtima, oongoka mtima ayenera kulemekeza.

Mutu    |  Mabaibulo
Ahebri 2:12

Ndi kuti, Ndidzalalikira dzina lanu kwa abale anga, pakati pa Mpingo ndidzakuimbirani.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 145:3

Yehova ndi wamkulu, nayenera kulemekezedwa kwakukulu; ndi ukulu wake ngwosasanthulika.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 12:5

Muimbire Yehova; pakuti wachita zaulemerero; chidziwike ichi m'dziko lonse.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 29:2

Perekani kwa Yehova ulemerero wa dzina lake, gwadirani Yehova moyera ndi mokometsetsa.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 78:4

Sitidzazibisira ana ao, koma kufotokozera mbadwo ukudzawo zolemekeza za Yehova, ndi mphamvu yake, ndi zodabwitsa zake zimene anazichita.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Samueli 2:2

Palibe wina woyera ngati Yehova; palibe wina koma Inu nokha; palibenso thanthwe longa Mulungu wathu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 42:4

Ndidzikumbukira izi ndipo nditsanulira moyo wanga m'kati mwa ine, pakuti ndidafopita ndi unyinji wa anthu, ndinawatsogolera kunyumba ya Mulungu, ndi mau akuimbitsa ndi kuyamika, ndi unyinji wakusunga dzuwa lokondwera.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 100:2

Tumikirani Yehova ndi chikondwerero: Idzani pamaso pake ndi kumuimbira mokondwera.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 79:13

Potero ife anthu anu ndi nkhosa zapabusa panu tidzakuyamikani kosatha; tidzafotokozera chilemekezo chanu ku mibadwomibadwo.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 43:21

anthu amene ndinadzilengera ndekha, kuti aonetse matamando anga.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 22:25

Lemekezo langa lidzakhala la Inu mu msonkhano waukulu, zowinda zanga ndidzazichita pamaso pa iwo akumuopa Iye.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 9:11

Imbirani zoyamika Yehova, wokhala ku Ziyoni; lalikirani mwa anthu ntchito zake.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 12:1

Chifukwa chake ndikupemphani inu, abale, mwa zifundo za Mulungu, kuti mupereke matupi anu nsembe yamoyo, yopatulika, yokondweretsa Mulungu, ndiko kupembedza kwanu koyenera.

Mutu    |  Mabaibulo
Ahebri 12:28-29

Mwa ichi polandira ufumu wosagwedezeka, tikhale nacho chisomo, chimene tikatumikire nacho Mulungu momkondweretsa, ndi kumchitira ulemu ndi mantha.

Pakuti Mulungu wathu ndiye moto wonyeketsa.

Mutu    |  Mabaibulo
Chivumbulutso 19:5

Ndipo mau anachokera kumpando wachifumu, ndi kunena, Lemekezani Mulungu wathu akapolo ake onse akumuopa Iye, ang'ono ndi akulu.

Mutu    |  Mabaibulo
Luka 2:20

Ndipo abusawo anabwera, nalemekeza ndi kutamanda Mulungu pa zinthu zonse anazimva, naziona, monga kunalankhulidwa kwa iwo.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 116:17

Ndidzapereka kwa Inu nsembe yachiyamiko, ndipo ndidzaitanira dzina la Yehova.

Mutu    |  Mabaibulo
Akolose 3:16-17

Mau a Khristu akhalitse mwa inu chichulukire mu nzeru yonse, ndi kuphunzitsa ndi kuyambirirana eni okha ndi masalmo, ndi mayamiko ndi nyimbo zauzimu, ndi kuimbira Mulungu ndi chisomo mumtima mwanu.

Ndipo chilichonse mukachichita m'mau kapena muntchito, chitani zonse m'dzina la Ambuye Yesu, ndi kuyamika Mulungu Atate mwa Iye.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 4:10

Pomwepo Yesu ananena kwa iye, Choka Satana, pakuti kwalembedwa, Ambuye Mulungu wako udzamgwadira, ndipo Iye yekhayekha udzamlambira.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 86:9

Amitundu onse mudawalenga adzadza nadzagwada pamaso panu, Ambuye; nadzalemekeza dzina lanu.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Mbiri 16:29

Mchitireni Yehova ulemerero wa dzina lake; bwerani nacho chopereka, ndipo fikani pamaso pake; lambirani Yehova m'chiyero chokometsetsa.

Mutu    |  Mabaibulo
Eksodo 34:14

pakuti musalambira mulungu wina; popeza Yehova dzina lake ndiye Wansanje, ali Mulungu wansanje;

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 103:1

Lemekeza Yehova, moyo wanga; ndi zonse za m'kati mwanga zilemekeze dzina lake loyera.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 22:3

Koma Inu ndinu woyera, wakukhala m'malemekezo a Israele.

Mutu    |  Mabaibulo
Chivumbulutso 4:11

Muyenera inu, Ambuye wathu, ndi Mulungu wathu, kulandira ulemerero ndi ulemu ndi mphamvu; chifukwa mudalenga zonse, ndipo mwa chifuniro chanu zinakhala, nizinalengedwa.

Mutu    |  Mabaibulo
Afilipi 3:3

pakuti ife ndife mdulidwe, akutumikira popembedza ndi Mzimu wa Mulungu, nadzitamandira mwa Khristu Yesu, osakhulupirira m'thupi;

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 95:1-2

Tiyeni tiimbire Yehova mokondwera; tifuule kwa thanthwe la chipulumutso chathu.

Zaka makumi anai mbadwo uwu unandimvetsa chisoni, ndipo ndinati, Iwo ndiwo anthu osokerera mtima, ndipo sadziwa njira zanga.

Chifukwa chake ndinalumbira mu mkwiyo wanga, ngati adzalowa mpumulo wanga.

Tidze nacho chiyamiko pamaso pake, timfuulire Iye mokondwera ndi nyimbo.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Mbiri 29:11-12

Ukulu, ndi mphamvu, ndi ulemerero, ndi chipambano, ndi chifumu ndi zanu, Yehova; pakuti zonse zam'mwamba ndi pa dziko lapansi ndi zanu; ufumu ndi wanu, Yehova; ndipo mwakwezeka mutu wa pa zonse.

Zolemera ndi ulemu zifuma kwanu, ndipo muchita ufumu pa zonse, ndi m'dzanja mwanu muli mphamvu yaikulu; kukuza ndi kupatsa onse mphamvu kuli m'dzanja lanu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 5:7

Koma ine, mwa kuchuluka kwa chifundo chanu ndidzalowa m'nyumba yanu; ndidzagwada kuyang'ana Kachisi wanu woyera ndi kuopa Inu.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 15:9

Koma andilambira Ine kwachabe, ndi kuphunzitsa maphunzitso, malangizo a anthu.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 29:13

Ndipo Ambuye anati, Popeza anthu awa ayandikira ndi Ine ndi m'kamwa mwao, nandilemekeza ndi milomo yao, koma mtima wao uli kutali ndi Ine, ndi mantha ao akundiopa Ine, ndi lamulo la anthu analiphunzira;

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 37:4

Udzikondweretsenso mwa Yehova; ndipo Iye adzakupatsa zokhumba mtima wako.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:10-11

Ndinakufunani ndi mtima wanga wonse; ndisasokere kusiyana nao malamulo anu.

Ndizindikira koposa okalamba popeza ndinasunga malangizo anu.

Ndinaletsa mapazi anga njira iliyonse yaoipa, kuti ndisamalire mau anu.

Sindinapatukana nao maweruzo anu; pakuti Inu munandiphunzitsa.

Mau anu azunadi powalawa ine! Koposa uchi m'kamwa mwanga.

Malangizo anu andizindikiritsa; chifukwa chake ndidana nao mayendedwe onse achinyengo.

Mau anu ndiwo nyali ya ku mapazi anga, ndi kuunika kwa panjira panga.

Ndinalumbira, ndipo ndinatsimikiza mtima, kuti ndidzasamalira maweruzo anu olungama.

Ndazunzika kwambiri: Ndipatseni moyo, Yehova, monga mwa mau anu.

Landirani, Yehova, zopereka zaufulu za pakamwa panga, ndipo ndiphunzitseni maweruzo anu.

Moyo wanga ukhala m'dzanja langa chikhalire; koma sindiiwala chilamulo chanu.

Ndinawabisa mau anu mumtima mwanga, kuti ndisalakwire Inu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 138:1-2

Ndidzakuyamikani ndi mtima wanga wonse; ndidzaimba zakukulemekezani patsogolo pa milungu.

Ndidzagwadira kuloza ku Kachisi wanu woyera, ndi kuyamika dzina lanu, chifukwa cha chifundo chanu ndi choonadi chanu; popeza munakuzitsa mau anu koposa dzina lanu lonse.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 15:16

kuti ndikhale mtumiki wa Khristu Yesu kwa anthu amitundu, wakutumikira Uthenga Wabwino wa Mulungu, kuti kupereka kwake kwa anthu amitundu kulandirike, koyeretsedwa ndi Mzimu Woyera.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 47:6-7

Imbirani Mulungu, imbirani; imbirani mfumu yathu, imbirani.

Pakuti Mulungu ndiye mfumu ya dziko lonse lapansi; imbirani ndi chilangizo.

Mutu    |  Mabaibulo
Deuteronomo 6:13

Muziopa Yehova Mulungu wanu; ndi kutumikira Iyeyu; ndipo polumbira muzitchula dzina lake.

Mutu    |  Mabaibulo
Chivumbulutso 7:11-12

Ndipo angelo onse anaimirira pozinga mpando wachifumu, ndi akulu, ndi zamoyozo zinai; ndipo anagwa nkhope yao pansi kumpando wachifumu, nalambira Mulungu,

ndi kunena, Amen: Thamo ndi ulemerero, ndi nzeru, ndi chiyamiko, ndi ulemu, ndi chilimbiko, ndi mphamvu zikhale kwa Mulungu wathu kufikira nthawi za nthawi. Amen.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Akorinto 10:31

Chifukwa chake mungakhale mudya, mungakhale mumwa, mungakhale muchita kanthu kena, chitani zonse ku ulemerero wa Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 6:3

Ndipo wina anafuula kwa mnzake, nati, Woyera, Woyera, Woyera, Yehova wa makamu; dziko lonse lapansi ladzala ulemerero wake.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 63:1-3

Inu Mulungu, ndinu Mulungu wanga; ndidzakufunani m'matanda kucha. Moyo wanga ukumva ludzu la kwa Inu, thupi langa lilirira Inu, m'dziko louma ndi lotopetsa, lopanda madzi.

Adzawapereka kumphamvu ya lupanga; iwo adzakhala gawo la ankhandwe.

Koma mfumu idzakondwera mwa Mulungu; yense wakulumbirira iye adzatamandira; pakuti pakamwa pa iwo onena bodza padzatsekedwa.

Kuti ndione mphamvu yanu ndi ulemerero wanu, monga ndinakuonani m'malo oyera.

Pakuti chifundo chanu chiposa moyo makomedwe ake; milomo yanga idzakulemekezani.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 26:30

Ndipo pamene anaimba nyimbo, anatuluka kunka kuphiri la Azitona.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 69:30-31

Ndidzalemekeza dzina la Mulungu ndi kuliimbira, ndipo ndidzambukitsa ndi kumyamika.

Ndipo chidzakomera Yehova koposa ng'ombe, inde mphongo za nyanga ndi ziboda.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 95:3

Pakuti Yehova ndiye Mulungu wamkulu; ndi mfumu yaikulu yoposa milungu yonse.

Mutu    |  Mabaibulo
Luka 4:8

Ndipo Yesu anayankha, nati kwa iye, Kwalembedwa, kuti, Ambuye Mulungu wako uzimgwadira, ndipo Iye yekhayekha uzimtumikira.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 1:25

amenewo anasandutsa choonadi cha Mulungu chabodza napembedza, natumikira cholengedwa, ndi kusiya Wolengayo, ndiye wolemekezeka nthawi yosatha. Amen.

Mutu    |  Mabaibulo
Chivumbulutso 15:4

Ndani adzakhala wosaopa ndi wosalemekeza dzina lanu Ambuye? Chifukwa Inu nokha muli woyera; chifukwa mitundu yonse idzadza nidzalambira pamaso panu, popeza zolungama zanu zidaonetsedwa.

Mutu    |  Mabaibulo

Pemphero kwa Mulungu

Zikomo Ambuye, inu ndinu wochiritsa wanga, wopereka wanga, ndi mlonda wanga. Inu ndinu amene mumalowerera nkhondo zanga, ndi kunditsogolera kuchoka pa ulemerero kupita pa ulemerero. M'dzina lamphamvu la Yesu, ndimabwera kwa inu kukulambirani ndi kukudalitsani chifukwa cha chikondi chanu chachikulu ndi chifundo chanu chosatha. Mfumu yanga, ndikudalitsani ndi kukukwezani chifukwa mwandikhululukira, mwandipulumutsa, mwandiyang'ana ndi chisomo Mulungu. Inu mumachita zizindikiro kumwamba ndi pano padziko lapansi, munatsegula nyanja pakati. Aa wodalitsidwa, Woyera wa Israeli! Aa Mulungu wodalitsidwa pakati pa mitundu yonse, iwo akukutamandani ndi kudalitsa dzina lanu, lomwe lili pamwamba pa dzina lililonse ndi kulengeza kuti ndinu Mfumu yayikulu. Mulungu ndikupemphani kuti nthawi zonse chiyamiko chanu chikhale mkamwa mwanga nthawi zonse. Mawu anu amati: "Wodalitsika Mulungu ndi Atate wa Ambuye wathu Yesu Khristu, amene anatidalitsa ndi madalitso onse auzimu m'malo akumwamba mwa Khristu." Zikomo chifukwa chifundo chanu ndi cha mibadwo ndi mibadwo, inu ndinu Mulungu wanga, Mfumu yanga ndipo palibe chabwino kunja kwa inu. Inu ndinu mlengi wa kumwamba ndi dziko lapansi, dzina lanu lokha ndilo lokwezeka, onse oyera mtima anu atamande ndi kuimba ndi chimwemwe chifukwa ntchito zanu ndi zodabwitsa ndi zosawerengeka monga mchenga wa m'nyanja. M'dzina la Yesu. Ameni!