Mavesi a Baibulo

- Zotsatsa -


NDIME ZA YESU

NDIME ZA YESU

Ndikufuna ndikuuzeni za Mpulumutsi wathu, Yesu. Iye ndiye amene anatifera ife pa mtanda chifukwa cha chikondi chake chachikulu. Ndi Mwana wokondedwa wa Mulungu, ndipo kudzera mwa Iye, tili ndi moyo wosatha. Taganizirani zimenezo, moyo wosatha chifukwa cha chikondi chake!

Yesu ndi Mfumu ya mafumu, Ambuye wa ambuye. Anavutika chifukwa cha machimo athu. Amafuna kuti mumuyandikire tsiku lililonse, kuti mumudziwe bwino, ndipo kuti mulankhule naye ngati mmene mungachitire ndi mnzanu wapamtima. Kodi mukuona chikondi chake chachikulu chimenecho?

Amakukondani kwambiri moti anasankha kufera inu. Monga momwe lemba la Luka 19:10 limati, “Pakuti Mwana wa Munthu anadza kufunafuna ndi kupulumutsa chotayika.” Tangoganizani, anabwera kudzakufunani inu!

Kudzera mwa Yesu yekha, tingapeze chipulumutso ndi moyo wosatha, ndikutuluka muukapolo wa dziko lapansi lino. Lemba la Machitidwe 4:12 limati, “Ndipo mulibe chipulumutso mwa wina aliyense; pakuti palibe dzina lina pansi pa thambo, lopatsidwa kwa anthu, limene tingapulumutsidwe nalo.” Palibe njira ina, Yesu ndiye njira yekha.




Aefeso 5:18

Ndipo musaledzere naye vinyo, m'mene muli chitayiko; komatu mudzale naye Mzimu,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mlaliki 9:7

Tiye, idya zakudya zako mokondwa, numwe vinyo wako mosekera mtima; pakuti Mulungu wavomerezeratu zochita zako.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Deuteronomo 32:14

mafuta a mkaka wang'ombe, ndi mkaka wankhosa, ndi mafuta a anaankhosa, ndi nkhosa zamphongo za mtundu wa ku Basani, ndi atonde, ndi impso zonenepa zatirigu; ndipo munamwa vinyo, mwazi wamphesa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Genesis 9:20-21

Ndipo anayamba Nowa kukhala munthu wakulima nthaka, ndipo analima munda wamphesa:namwa vinyo wake, naledzera; ndipo anali wamaliseche m'kati mwa hema wake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mlaliki 2:3

Ndinafuna mumtima mwanga kusangalatsa thupi langa ndi vinyo, mtima wanga ulikunditsogolera mwanzeru, ndi kugwira utsiru, kuti ndizindikire chabwinocho cha ana a anthu nchiyani chimene azichichita pansi pa thambo masiku onse a moyo wao.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Genesis 14:18

Ndipo Melkizedeki mfumu ya ku Salemu, anatuluka nao mkate ndi vinyo: iye ndiye wansembe wa Mulungu Wamkulukulu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Timoteyo 5:23

Usakhalenso wakumwa madzi okha, komatu uchite naye vinyo pang'ono, chifukwa cha mimba yako ndi zofooka zako zobwera kawirikawiri.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Genesis 27:37

Ndipo anayankha Isaki nati kwa Esau, Taona, ndamuyesa iye mkulu wako, ndi abale ake onse ndampatsa iye akhale akapolo ake; ndakhazikitsa iye ndi tirigu ndi vinyo; nanga pamenepo mwana wanga, ndidzakuchitira iwe chiyani?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Numeri 6:26

Yehova akweze nkhope yake pa iwe, nakupatse mtendere.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Eksodo 29:40

ndi pa mwanawankhosa mmodziyo pakhale limodzi la magawo khumi la ufa wosalala, wosanganiza ndi limodzi la magawo anai la hini wa mafuta opera; ndi limodzi la magawo anai la hini wa vinyo, likhale nsembe yothira.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Estere 5:6

Ndipo mfumu inati kwa Estere pa madyerero a vinyo, Pempho lanu nchiyani? Lidzaperekedwa kwa inu; mufunanji? Chidzachitika, kufikira limodzi la magawo awiri a ufumuwo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Levitiko 10:9

Usamamwa vinyo, kapena choledzeretsa, iwe ndi ana ako omwe, m'mene mulowa m'chihema chokomanako, kuti mungafe; likhale lemba losatha mwa mibadwo yanu;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Danieli 5:1

Mfumu Belisazara anakonzera anthu ake akulu chikwi chimodzi madyerero akulu, namwa vinyo pamaso pa chikwicho.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Levitiko 23:13

Ndipo nsembe yaufa yake ikhale awiri a magawo khumi a efa wa ufa wosalala wosanganiza ndi mafuta, ndiyo nsembe yamoto ya Yehova, ichite fungo lokoma; ndi nsembe yake yothira ikhale yavinyo, limodzi la magawo anai la hini.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Danieli 5:4

Anamwa vinyo, nalemekeza milungu yagolide, ndi yasiliva, yamkuwa, yachitsulo, yamtengo, ndi yamwala.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Numeri 6:3

azisala vinyo ndi kachasu; asamwe vinyo wosasa, kapena kachasu wosasa, kapena chakumwa chonse cha mphesa, asamwe; asadye mphesa zaziwisi kapena zouma.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Danieli 5:23

koma munadzikweza kutsutsana naye Ambuye wa Kumwamba; ndipo anabwera nazo zotengera za nyumba yake kwa inu; ndi inu ndi akulu anu, akazi anu ndi akazi anu ang'ono, mwamweramo vinyo; mwalemekezanso milungu yasiliva, ndi yagolide, yamkuwa, yachitsulo, yamtengo, ndi yamwala, imene siiona kapena kumva, kapena kudziwa; ndi Mulungu amene m'dzanja mwake muli mpweya wanu, ndi njira zanu zonse, yemweyo simunamchitira ulemu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Deuteronomo 14:26

ndipo mugule ndi ndalamazo chilichonse moyo wanu ukhumba, ng'ombe kapena nkhosa, kapena vinyo, kapena chakumwa cholimba, kapena chilichonse moyo wanu ukufunsani; nimudye pomwepo pamaso pa Yehova Mulungu wanu, ndi kukondwera, inu ndi a pabanja panu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Amosi 2:8

nagona pansi pa zofunda za chikole kumaguwa a nsembe ali onse, ndi m'nyumba ya Mulungu wao akumwa vinyo wa iwo olipitsidwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Amosi 6:6

akumwera vinyo m'zipanda, nadzidzoza ndi mafuta abwino oposa, osagwidwa chisoni ndi kuthyoka kwa Yosefe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 104:14-15

Ameretsa msipu ziudye ng'ombe, ndi zitsamba achite nazo munthu; natulutse chakudya chochokera m'nthaka;ndi vinyo wokondweretsa mtima wa munthu, ndi mafuta akunyezimiritsa nkhope yake, ndi mkate wakulimbitsa mtima wa munthu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Amosi 9:14

Ndipo ndidzabwezanso undende wa anthu anga Israele, ndipo adzamanganso mabwinja, ndi kukhala m'menemo; nadzaoka minda ya mipesa nadzamwa vinyo wake, nadzalima minda ndi kudya zipatso zake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 104:15

ndi vinyo wokondweretsa mtima wa munthu, ndi mafuta akunyezimiritsa nkhope yake, ndi mkate wakulimbitsa mtima wa munthu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 20:1

Vinyo achita chiphwete, chakumwa chaukali chisokosa; wosochera nazo alibe nzeru.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 3:9-10

Lemekeza Yehova ndi chuma chako, ndi zinthu zako zonse zoyambirira kucha;motero nkhokwe zako zidzangoti thee, mbiya zako zidzasefuka vinyo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 14:21

Kuli kwabwino kusadya nyama, kapena kusamwa vinyo, kapena kusachita chinthu chilichonse chakukhumudwitsa mbale wako.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 9:2

yaphera nyama yake, nisanganiza vinyo wake, nilongosolanso pa gome lake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Numeri 15:5

ndipo uzikonzera nsembe yopsereza kapena yophera, vinyo wa nsembe yothira, limodzi la magawo anai la hini, ukhale wa mwanawankhosa mmodzi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Deuteronomo 7:13

ndipo adzakukondani, ndi kukudalitsani, ndi kukuchulukitsani; adzadalitsanso zipatso za thupi lanu, ndi zipatso za nthaka yanu, tirigu wanu, ndi vinyo wanu, ndi mafuta anu, zoswana za ng'ombe zanu, ndi anaankhosa anu, m'dziko limene analumbirira makolo anu kuti adzakupatsani.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 23:30-35

Ngamene achedwa pali vinyo, napita kukafunafuna vinyo wosanganizidwa.Usayang'ane pavinyo alikufiira, alikung'azimira m'chikho, namweka mosalala.Pa chitsiriziro chake aluma ngati njoka, najompha ngati mamba.Maso ako adzaona zachilendo, mtima wako udzalankhula zokhota.Udzafanana ndi wina wogona pakati pa nyanja, pena wogona pa nsonga ya mlongoti wa ngalawa.Udzati, Anandimenya, osaphwetekedwa ine; anandikwapula, osamva ine; ndidzauka nthawi yanji? Ndidzafunafunanso vinyoyo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 27:34

anamwetsa Iye vinyo wosanganiza ndi ndulu; ndipo Iye, m'mene analawa, sanafune kumwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mlaliki 3:13

Ndiponso kuti munthu yense adye namwe naone zabwino m'ntchito zake zonse; ndiwo mtulo wa Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yoweli 3:18

Ndipo kudzachitika tsiku ilo mapiri adzakhetsa vinyo wozuna, ndi pazitunda padzayenda mkaka, ndi m'mitsinje yonse ya Yuda mudzayenda madzi; ndi madzi akasupe adzatuluka m'nyumba ya Yehova, nadzamwetsa madzi chigwa cha Sitimu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yeremiya 23:9

Za aneneri. Mtima wanga usweka m'kati mwanga, mafupa anga onse anthunthumira; ndinga munthu woledzera, ngati munthu amene vinyo anamposa; chifukwa cha Yehova, ndi chifukwa cha mau ake opatulika.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 22:20

Ndipo choteronso chikho, atatha mgonero, nanena, Chikho ichi ndi pangano latsopano m'mwazi wanga wothiridwa chifukwa cha inu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 55:1

Inu nonse, inu akumva ludzu, idzani kumadzi; ndi osowa ndalama idzani inu mugule mudye; inde idzani, mugule vinyo ndi mkaka opanda ndalama ndi opanda mtengo wake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Genesis 27:25

Ndipo iye anati, Usendere nayo kwa ine, ndidye nyama ya mwana wanga, kuti moyo wanga ukudalitse iwe. Ndipo anasendera nayo kwa iye, nadya iye; ndipo anamtengera vinyo, namwa iye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yeremiya 31:12

Ndipo adzadza nadzaimba pa msanje wa Ziyoni, nadzasonkhanira ku zokoma za Yehova, kutirigu, ndi kuvinyo, ndi mafuta, ndi kwa ana a zoweta zazing'ono ndi zazikulu; ndipo moyo wao udzakhala ngati munda wamichera; ndipo sadzakhalanso konse ndi chisoni.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 22:13

koma taonani, kukondwa, ndi kusekerera, ndi kupha ng'ombe, ndi kupha nkhosa, ndi kudya nyama, ndi kumwa vinyo; tiyeni tidye ndi kumwa, chifukwa mawa tidzafa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 25:6

Ndipo m'phiri limeneli Yehova wa makamu adzakonzera anthu ake onse phwando la zinthu zonona, phwando la vinyo wa pamitsokwe, la zinthu zonona za mafuta okhaokha, la vinyo wansenga wokuntha bwino.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 9:17

Kapena samathira vinyo watsopano m'matumba akale; akatero, matumba aphulika, ndi vinyo atayika, ndi matumba aonongeka; koma athira vinyo watsopano m'matumba atsopano, ndi zonse ziwiri zisungika.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 21:17

Wokonda zoseketsa adzasauka; wokonda vinyo ndi mafuta sadzalemera.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 26:29

Ndipo ndinena kwa inu, sindidzamwanso chipatso ichi champesa, kufikira tsiku limene ndidzamwa chatsopano, pamodzi ndi inu, mu Ufumu wa Atate wanga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ezekieli 44:21

Kungakhale kumwa vinyo, wansembe asamwe polowa kubwalo la m'katimo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Marko 2:22

Ndipo palibe munthu amatsanulira vinyo watsopano m'matumba akale: pena vinyo adzaphulitsa matumba, ndipo aonongeka vinyo, ndi matumba omwe: koma vinyo watsopano amatsanulira m'matumba atsopano.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Deuteronomo 29:6

Simunadya mkate, simunamwa vinyo kapena chakumwa cholimba; kuti mudziwe kuti Ine ndine Yehova Mulungu wanu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Marko 14:25

Ndipo ndinena nanu, Sindidzamwanso chipatso cha mpesa, kufikira tsiku lijalo, limene ndidzamwa icho chatsopano mu Ufumu wa Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 5:37-38

Ndipo palibe munthu atsanulira vinyo watsopano m'matumba akale; chifukwa ngati atero, vinyo watsopanoyo adzaphulitsa matumba, ndipo ameneyo adzatayika, ndi matumba adzaonongeka.Koma kuyenera kutsanulira vinyo watsopano m'matumba atsopano.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 7:34

Mwana wa Munthu wafika wakudya ndi wakumwa; ndipo munena, Onani, munthu wosusuka ndi wakumwaimwa vinyo, bwenzi la amisonkho ndi anthu ochimwa!

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 22:18

pakuti ndinena kwa inu, kuyambira tsopano Ine sindidzamwako chipatso cha mpesa, kufikira Ufumu wa Mulungu udzafika.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 2:1-11

Ndipo tsiku lachitatu panali ukwati m'Kana wa m'Galileya; ndipo amake wa Yesu anali komweko.Ndipo Yesu yemwe ndi ophunzira ake anaitanidwa kuukwatiwo.Ndipo pakutha vinyo, amake wa Yesu ananena naye, Alibe vinyo.Yesu nanena naye, Mkazi, ndili ndi chiyani ndi inu? Nthawi yanga siinafike.Amake ananena kwa atumiki, Chimene chilichonse akanena kwa inu, chitani.Ndipo panali pamenepo mitsuko yamiyala isanu ndi umodzi yoikidwako monga mwa mayeretsedwe a Ayuda, yonse ya miyeso iwiri kapena itatu.Yesu ananena nao, Dzazani mitsukoyo ndi madzi. Naidzaza, ndendende.Ndipo ananena nao, Tungani tsopano, mupite nao kwa mkulu wa phwando. Ndipo anapita nao.Koma pamene mkuluyo analawa madzi osanduka vinyowo, ndipo sanadziwe kumene anachokera (koma atumiki amene adatunga madzi anadziwa), mkuluyo anaitana mkwati,nanena naye, Munthu aliyense amayamba kuika vinyo wokoma; ndipo anthu atamwatu, pamenepo wina wosakoma; koma iwe wasunga vinyo wokoma kufikira tsopano lino.Chiyambi ichi cha zizindikiro zake Yesu anachita m'Kana wa m'Galileya naonetsera ulemerero wake; ndipo ophunzira ake anakhulupirira Iye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Machitidwe a Atumwi 2:13

Koma ena anawaseka, nanena kuti, Akhuta vinyo walero.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 10:21

Simungathe kumwera chikho cha Ambuye, ndi chikho cha ziwanda; simungathe kulandirako kugome la Ambuye, ndi kugome la ziwanda.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 11:25

Koteronso chikho, chitatha chakudya, ndi kuti, Chikho ichi ndi pangano latsopano m'mwazi wanga; chitani ichi, nthawi zonse mukamwa, chikhale chikumbukiro changa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Afilipi 1:11

odzala nacho chipatso cha chilungamo, chimene chili mwa Yesu Khristu, kuchitira Mulungu ulemerero ndi chiyamiko.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Tito 2:3

Momwemonso akazi okalamba akhale nao makhalidwe oyenera anthu oyera, osadierekeza, osakodwa nacho chikondi cha pavinyo, akuphunzitsa zokoma;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 13:10

Tili nalo guwa la nsembe, limene iwo akutumikira chihema alibe ulamuliro wa kudyako.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yakobo 3:11

Kodi kasupe atulutsira pa uno womwewo madzi okoma ndi owawa?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Agalatiya 5:19-21

Ndipo ntchito za thupi zionekera, ndizo dama, chodetsa, kukhumba zonyansa,kupembedza mafano, nyanga, madano, ndeu, kaduka, zopsa mtima, zotetana, magawano, mipatuko,njiru, kuledzera, mchezo, ndi zina zotere; zimene ndikuchenjezani nazo, monga ndachita, kuti iwo akuchitachita zotere sadzalowa Ufumu wa Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 16:5

Yehova ndiye gawo la cholowa changa ndi chikho changa, ndinu wondigwirira cholandira changa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 75:8

Pakuti m'dzanja la Yehova muli chikho; ndi vinyo wake achita thovu; chidzala ndi zosanganizira, ndipo atsanulako. Indedi, oipa onse a pa dziko lapansi adzamwa nadzagugudiza nsenga zake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 116:13

Ndidzanyamula chikho cha chipulumutso, ndipo ndidzaitanira dzina la Yehova.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 23:5

Mundiyalikira gome pamaso panga m'kuona kwa adani anga; mwandidzoza mutu wanga mafuta; chikho changa chisefuka.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 78:65-66

Pamenepo Ambuye anauka ngati wam'tulo; ngati chiphona chakuchita nthungululu ndi vinyo.Ndipo anapanda otsutsana naye kumbuyo; nawapereka akhale otonzeka kosatha.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 60:3

Mwaonetsa anthu anu zowawa, mwatimwetsa vinyo wotinjenjemeretsa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 69:12

Okhala pachipata akamba za ine; ndipo oledzera andiimba.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 31:6-7

Wofuna kufa umpatse chakumwa chaukali, ndi vinyo kwa owawa mtima;amwe, naiwale umphawi wake, osakumbukiranso vuto lake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 24:7

Vinyo watsopano alira, mpesa ulefuka, mitima yonse yokondwa iusa moyo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 55:2

Bwanji inu mulikutayira ndalama chinthu chosadya, ndi kutayira malipiro anu zosakhutitsa? Mverani Ine mosamalitsa, nimudye chimene chili chabwino, moyo wanu nukondwere ndi zonona.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yeremiya 35:5-6

ndipo ndinaika pamaso pa ana amuna a nyumba ya Arekabu mbale zodzala ndi vinyo, ndi zikho, ndipo ndinati kwa iwo, Imwani vinyo.Koma anati, Sitidzamwa vinyo; pakuti Yonadabu mwana wa Rekabu kholo lathu anatiuza ife, kuti, Musadzamwe vinyo, kapena inu, kapena ana anu, kumuyaya;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Maliro 3:15

Wandidzaza ndi zowawa, wandikhutitsa chivumulo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ezekieli 27:18

Damasiko anagulana nawe malonda chifukwa cha zambirizo udazipanga, chifukwa cha kuchuluka kwa chuma chilichonse, ndi vinyo wa ku Heliboni, ndi ubweya wa nkhosa woyera.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yoweli 1:5

Galamukani, oledzera inu, nimulire; bumani, nonse akumwa vinyo, chifukwa cha vinyo watsopano; pakuti waletsedwa pakamwa panu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mika 2:11

Munthu akayenda ndi mtima wachinyengo ndi kunama, ndi kuti, Ndidzanenera kwa iwe za vinyo ndi chakumwa chakuledzeretsa; iye ndiye mneneri wa anthu ake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Zekariya 10:7

Ndipo iwo a ku Efuremu adzakhala ngati ngwazi, ndi mtima wao udzakondwera ngati ndi vinyo; ndipo ana ao adzachiona nadzakondwera; mtima wao udzakondwerera mwa Yehova.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 11:19

Mwana wa Munthu anadza wakudya, ndi wakumwa, ndipo iwo amati, Onani munthu wakudyaidya ndi wakumwaimwa vinyo, bwenzi la amisonkho ndi ochimwa! Ndipo nzeru iyesedwa yolungama ndi ntchito zake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 26:27

Ndipo pamene anatenga chikho, anayamika, napatsa iwo, nanena, Mumwere ichi inu nonse,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Marko 14:23

Ndipo anatenga chikho, ndipo pamene adayamika, anapereka kwa iwo; ndipo iwo onse anamweramo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 1:15

Pakuti iye adzakhala wamkulu pamaso pa Ambuye, ndipo sadzamwa konse vinyo kapena kachasu; nadzadzazidwa ndi Mzimu Woyera, kuyambira asanabadwe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 10:34

nadza kwa iye, namanga mabala ake, nathirapo mafuta ndi vinyo; ndipo anamuika iye pa nyama yake ya iye yekha, nadza naye kunyumba ya alendo, namsungira.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 6:55

Pakuti thupi langa ndi chakudya ndithu, ndi mwazi wanga ndi chakumwa ndithu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 15:14

Koma ine ndekhanso, abale anga, nditsimikiza mtima za inu, kuti inu nokhanso muli odzala ndi ubwino, odzazidwa ndi kudziwitsa konse, ndi kukhoza kudandaulirana wina ndi mnzake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 11:21-22

pakuti pakudyaku yense athanga watenga mgonero wake wa yekha, ndipo wina ali ndi njala, ndi wina aledzera.Nanga mulibe nyumba za kudyeramo ndi kumweramo? Kapena kodi munyoza Mpingo wa Mulungu, ndi kunyoza iwo amene alibe kanthu? Ndidzanena chiyani kwa inu? Kodi ndidzatama inu m'menemo? Sindikutamani.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 10:16

Chikho cha dalitso chimene tidalitsa, sichili chiyanjano cha mwazi wa Khristu kodi? Mkate umene tinyema suli chiyanjano cha thupi la Khristu kodi?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Akorinto 5:14

Pakuti chikondi cha Khristu chitikakamiza; popeza taweruza chotero, kuti mmodzi adafera onse, chifukwa chake onse adafa;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Agalatiya 5:24

Koma iwo a Khristu Yesu adapachika thupi, ndi zokhumba zake, ndi zilakolako zake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Afilipi 2:1-2

Ngati tsono muli chitonthozo mwa Khristu, ngati chikhazikitso cha chikondi, ngati chiyanjano cha Mzimu, ngati phamphu, ndi zisoni,kwaniritsani chimwemwe changa, kuti mukalingalire mtima zomwezo, akukhala nacho chikondi chomwe, a moyo umodzi, olingalira mtima umodzi;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Akolose 3:16

Mau a Khristu akhalitse mwa inu chichulukire mu nzeru yonse, ndi kuphunzitsa ndi kuyambirirana eni okha ndi masalmo, ndi mayamiko ndi nyimbo zauzimu, ndi kuimbira Mulungu ndi chisomo mumtima mwanu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Atesalonika 5:6-8

chifukwa chake tsono tisagone monga otsalawo, komatu tidikire, ndipo tisaledzere.Pakuti iwo akugona agona usiku; ndi iwo akuledzera aledzera usiku.Koma ife popeza tili a usana tisaledzere, titavala chapachifuwa cha chikhulupiriro ndi chikondi; ndi chisoti chili chiyembekezo cha chipulumutso.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 5:14

Koma chakudya chotafuna chili cha anthu akulu misinkhu, amene mwa kuchita nazo anazoloweretsa zizindikiritso zao kusiyanitsa chabwino ndi choipa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yakobo 5:13-14

Kodi wina wa inu akumva zowawa? Apemphere. Kodi wina asekera? Aimbire.Pali wina kodi adwala mwa inu? Adziitanire akulu a Mpingo, ndipo apemphere pa iye, atamdzoza ndi mafuta m'dzina la Ambuye:

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Petro 4:3

Pakuti nthawi yapitayi idatifikira kuchita chifuno cha amitundu, poyendayenda ife m'kukhumba zonyansa, zilakolako, maledzero, madyerero, maimwaimwa, ndi kupembedza mafano kosaloleka;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Petro 2:13

ochitidwa zoipa kulipira kwa chosalungama; anthu akuyesera chowakondweretsa kudyerera usana; ndiwo mawanga ndi zilema, akudyerera m'madyerero achikondi ao, pamene akudya nanu;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 5:12

Pakuti Inu, Yehova, mudzadalitsa wolungamayo; mudzamtchinjiriza nacho chivomerezo ngati chikopa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 4:7

Nzeru ipambana, tatenga nzeru; m'kutenga kwako konseko utenge luntha.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 16:10

Ndipo chikondwero ndi msangalalo zachotsedwa m'munda wopatsa zipatso; ndi m'minda ya mipesa simudzakhala kuimba, ngakhale phokoso losangalala; palibe woponda adzaponda vinyo m'moponderamo; ndaleketsa mfuu wa masika amphesa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ezekieli 18:6

wosadya pamapiripo, wosakweza maso ake kumafano a nyumba ya Israele, wosaipsa mkazi wa mnansi wake, kapena kuyandikira mkazi ataoloka,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Amosi 9:13

Taonani, akudza masiku, ati Yehova, akuti wolima adzapezana ndi wodula, ndi woponda mphesa adzapezana ndi wofetsa, ndi mapiri adzakhetsa vinyo watsopano, ndi zitunda zonse zidzasungunuka.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mika 6:15

Udzafesa koma osacheka; udzaponda azitona koma osadzola mafuta; udzaponda mphesa koma osamwa vinyo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 5:6

Odala ali akumva njala ndi ludzu la chilungamo; chifukwa adzakhuta.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Marko 10:43-44

Koma mwa inu sikutero ai; koma amene aliyense afuna kukhala wamkulu mwa inu adzakhala mtumiki wanu;ndipo amene aliyense afuna kukhala woyamba mwa inu adzakhala kapolo wa onse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 14:12-14

Ndipo ananenanso kwa iye amene adamuitana, Pamene ukonza chakudya cha pausana kapena cha madzulo, usaitane abwenzi ako, kapena abale ako, kapena a fuko lako, kapena anansi ako eni chuma; kuti kapena iwonso angabwereze kuitana iwe, ndipo udzakhala nayo mphotho.Koma pamene ukonza phwando uitane aumphawi, opunduka, otsimphina, akhungu;ndipo udzakhala wodala; chifukwa iwo alibe chakubwezera iwe mphotho; pakuti idzabwezedwa mphotho pa kuuka kwa olungama.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 2:10

nanena naye, Munthu aliyense amayamba kuika vinyo wokoma; ndipo anthu atamwatu, pamenepo wina wosakoma; koma iwe wasunga vinyo wokoma kufikira tsopano lino.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 14:16

Chifukwa chake musalole chabwino chanu achisinjirire.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 6:12

Zinthu zonse ziloledwa kwa ine; koma si zonse zipindula. Zinthu zonse ziloledwa kwa ine, koma sindidzalamulidwa nacho chimodzi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Afilipi 4:8

Chotsalira, abale, zinthu zilizonse zoona, zilizonse zolemekezeka, zilizonse zolungama, zilizonse zoyera, zilizonse zokongola, zilizonse zimveka zokoma; ngati kuli chokoma mtima china, kapena chitamando china, zilingirireni izi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Timoteyo 6:10

Pakuti muzu wa zoipa zonse ndiwo chikondi cha pa ndalama; chimene ena pochikhumba, anasochera, nataya chikhulupiriro, nadzipyoza ndi zowawa zambiri.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Tito 1:7

Pakuti woyang'anira ayenera kukhala wopanda chilema, ngati mdindo wa Mulungu; wosati waliuma, wosapsa mtima msanga, wosati wachiwawa, wopanda ndeu, wosati wa chisiriro chonyansa;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 13:9

Musatengedwe ndi maphunzitso a mitundumitundu, ndi achilendo; pakuti nkokoma kuti mtima ukhazikike ndi chisomo; kosati ndi zakudya, zimene iwo adazitsata sanapindula nazo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yakobo 4:4

Akazi achigololo inu, kodi simudziwa kuti ubwenzi wa dziko lapansi uli udani ndi Mulungu? Potero, iye amene afuna kukhala bwenzi la dziko lapansi adziika mdani wa Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:103

Mau anu azunadi powalawa ine! Koposa uchi m'kamwa mwanga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 10:9

Woyenda moongoka amayenda osatekeseka; koma wokhotetsa njira zake adzadziwika.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mlaliki 10:19

Amaphikira zakudya kuti asekere, vinyo nakondweretsa moyo; ndipo ndalama zivomera zonse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 14:17

Pakuti ufumu wa Mulungu sukhala chakudya ndi chakumwa, koma chilungamo, ndi mtendere, ndi chimwemwe mwa Mzimu Woyera.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani

Pemphero kwa Mulungu

Ambuye Wopulumutsa! Lero ndikufuulirani ndipo ndikuyang'ana nkhope yanu kuti ndikupatseni ulemerero ndi ulemu. Ulemerero ndi ulemu wonse ndi wanu chifukwa cha nsembe yanu yotipulumutsira ife ndi mwazi wanu wopatulika wokhetsedwa pa mtanda wa pa Gologota. Zikomo chifukwa cha pangano latsopano, lomwe limandilola kulowa pamaso pa mpando wachifundo. Munatipulumutsa ku ulamuliro wa mdima, Yesu, Mwana wa Mulungu, mkhalapakati pakati pa Mulungu ndi anthu. Zikomo chifukwa chodzipereka nokha chifukwa cha chikondi chanu pa anthu, mukulipira mtengo wapatali chifukwa cha machimo athu. Mawu anu amati: "Mwa Iye tili ndi chiwombolo mwa mwazi wake, ndicho chikhululukiro cha machimo, monga mwa chuma cha chisomo chake." Zikomo chifukwa munavulala chifukwa cha kupanduka kwanga, munaphwanyidwa chifukwa cha machimo anga, ndipo chilango cha mtendere wanga chinali pa Inu. Ulemerero ndi ulemu wonse ndi wanu. M'dzina la Yesu. Ameni!
Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa