Biblia Todo Logo
Mavesi a Baibulo
- Zotsatsa -


NDIME ZA MAUKWATI

NDIME ZA MAUKWATI

Ukwati ndi chinthu chopangidwa ndi Mulungu, kuti munthu asakhale yekha. Ndi ubale wapadera komanso wodabwitsa umene umafuna kudzipereka ndi kupirira. Monga ana a Mulungu tiyenera kusonyeza chikondi chake ndipo ukwati umatipatsa mwayi tsiku ndi tsiku wochisonyeza.

Tili ndi mavesi ambiri a m’Baibulo omatithandiza kukhazika bwino ukwati wathu ngati tiwatsatire. Chimodzi mwa zinthu zoyamba zimene Ambuye amatifunsa tikakwatirana, ndichokusiya abambo ndi amayi athu kuti tipange banja lathu, nyumba yathu yatsopano. Zoonadi, tiyenera kulemekeza makolo athu, koma zisankho zopangidwa tsopano ziyenera kukhala ndi mnzanu, banja lanu.

Ukwati uyenera kuperekedwa kwa Mulungu, aliyense ayenera kutenga udindo umene Mulungu wapereka mu mgwirizanowu, ndi kuika chikondi chanu m'manja mwa Mulungu, kulimbitsa chikondi chanu tsiku ndi tsiku ndi pemphero ndi mawu a Mulungu.

Ukwati ndi wa nthawi zonse, dongosolo limene Mulungu analipangira ukwati ndi la nthawi zonse, kusudzulana sikuli m'dongosolo lake, Mulungu amafuna kuti mukhale pamodzi mpaka imfa. Pali zinthu zoopsa monga kusakhulupirika kapena nkhanza, koma dongosolo loyambirira la Mulungu ndi lakuti mwamuna ndi mkazi akhale pamodzi mpaka imfa.




Aefeso 5:33

Komanso inu, yense pa yekha, yense akonde mkazi wake wa iye yekha, monga adzikonda yekha; ndipo mkaziyo akumbukire kuti aziopa mwamuna.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 18:22

Wopeza mkazi apeza chinthu chabwino; Yehova amkomera mtima.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Akolose 3:19

Amuna inu, kondani akazi anu, ndipo musawawire mtima iwo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 13:4

Ukwati uchitidwe ulemu ndi onse, ndi pogona pakhale posadetsedwa; pakuti adama ndi achigololo adzawaweruza Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 13:4-5

Chikondi chikhala chilezere, chili chokoma mtima; chikondi sichidukidwa; chikondi sichidziwa kudzitamanda, sichidzikuza, sichichita zosayenera, sichitsata za mwini yekha, sichipsa mtima, sichilingirira zoipa;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 31:10-11

Mkazi wangwiro ndani angampeze? Pakuti mtengo wake uposa ngale. Mtima wa mwamuna wake umkhulupirira, sadzasowa phindu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 7:3

Mwamunayo apereke kwa mkazi mangawa ake; koma modzimodzinso mkazi kwa mwamuna.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Genesis 2:24

Chifukwa chotero mwamuna adzasiya atate wake ndi amake nadzadziphatika kwa mkazi wake: ndipo adzakhala thupi limodzi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aefeso 5:25

Amuna inu, kondani akazi anu, monganso Khristu anakonda Mpingo, nadzipereka yekha m'malo mwake;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Petro 3:7

Momwemonso amuna inu, khalani nao monga mwa chidziwitso, ndi kuchitira mkazi ulemu, monga chotengera chochepa mphamvu, monganso wolowa nyumba pamodzi wa chisomo cha moyo, kuti mapemphero anu angaletsedwe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 11:11

Komanso mkazi sakhala wopanda mwamuna, kapena mwamuna wopanda mkazi, mwa Ambuye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aefeso 5:21

ndi kumverana wina ndi mnzake m'kuopa Khristu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 21:9

Kukhala pangodya ya tsindwi kufunika kuposa kukhala m'nyumba ndi mkazi wolongolola.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Petro 4:8

koposa zonse mukhale nacho chikondano chenicheni mwa inu nokha; pakuti chikondano chikwiriritsa unyinji wa machimo;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aefeso 4:2-3

ndi kuonetsera kudzichepetsa konse, ndi chifatso, ndi kuonetsera chipiriro, ndi kulolerana wina ndi mnzake, mwa chikondi; Koma inu simunaphunzira Khristu chotero, ngatitu mudamva Iye, ndipo munaphunzitsidwa mwa Iye, monga choonadi chili mwa Yesu; kuti muvule, kunena za makhalidwe anu oyamba, munthu wakale, wovunda potsata zilakolako za chinyengo; koma kuti mukonzeke, mukhale atsopano mu mzimu wa mtima wanu, nimuvale munthu watsopano, amene analengedwa monga mwa Mulungu, m'chilungamo, ndi m'chiyero cha choonadi. Mwa ichi, mutataya zonama, lankhulani zoona yense ndi mnzake; pakuti tili ziwalo wina ndi mnzake. Kwiyani, koma musachimwe; dzuwa lisalowe muli chikwiyire, ndiponso musampatse malo mdierekezi. Wakubayo asabenso; koma makamaka agwiritse ntchito, nagwire ntchito yokoma ndi manja ake, kuti akhale nacho chakuchereza wosowa. Nkhani yonse yovunda isatuluke m'kamwa mwanu, koma ngati pali ina yabwino kukumangirira monga mofunika ndiyo, kuti ipatse chisomo kwa iwo akumva. ndi kusamalitsa kusunga umodzi wa Mzimu mwa chimangiriro cha mtendere.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 127:3

Taonani, ana ndiwo cholandira cha kwa Yehova; chipatso cha m'mimba ndicho mphotho yake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Nyimbo ya Solomoni 1:15-16

Taona, wakongolatu, bwenzi langa; namwaliwe taona, wakongola, maso ako akunga a nkhunda. Taona, wakongolatu, bwenzi langa, mnyamatawe, inde, wakongoletsa; pogona pathu mpa msipu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 17:17

Bwenzi limakonda nthawi zonse; ndipo mbale anabadwira kuti akuthandize pooneka tsoka.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 10:24

ndipo tiganizirane wina ndi mnzake kuti tifulumizane ku chikondano ndi ntchito zabwino,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Nyimbo ya Solomoni 5:1

Ndalowa m'munda mwanga, mlongo wanga, mkwatibwi: Ndatchera mure wanga ndi zonunkhiritsa zanga; ndadya uchi wanga ndi chisa chake; ndamwa vinyo wanga ndi mkaka wanga. Idyani, atsamwalinu, imwani, mwetsani chikondi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 27:9

Mafuta ndi zonunkhira zikondweretsa mtima, ndi ubwino wa bwenzi uteronso pakupangira uphungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 128:3

Mkazi wako adzanga mpesa wopatsa m'mbali za nyumba yako; ana ako adzanga timitengo ta azitona pozinga podyera pako.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 10:12

Udani upikisanitsa; koma chikondi chikwirira zolakwa zonse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aefeso 6:1

Ananu, mverani akukubalani mwa Ambuye, pakuti ichi nchabwino.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Nyimbo ya Solomoni 3:4

Nditawapitirira pang'ono, ndinampeza amene moyo wanga umkonda: Ndinamgwiriziza, osamfumbatula, mpaka nditamlowetsa m'nyumba ya amai, ngakhale m'chipinda cha wondibala.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 13:13

Ndipo tsopano zitsala chikhulupiriro, chiyembekezo, chikondi, zitatu izi; koma chachikulu cha izi ndicho chikondi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aefeso 5:1-2

Chifukwa chake khalani akutsanza a Mulungu, monga ana okondedwa; kuyesera chokondweretsa Ambuye nchiyani; ndipo musayanjane nazo ntchito za mdima zosabala kanthu, koma makamakanso muzitsutse; pakuti zochitidwa nao m'tseri, kungakhale kuzinena kuchititsa manyazi. Koma zinthu zonse potsutsika ndi kuunika, zionekera; pakuti chonse chakuonetsa chili kuunika. Mwa ichi anena, Khala maso wogona iwe, nuuke kwa akufa, ndipo Khristu adzawala pa iwe. Potero, penyani bwino umo muyendera, si monga opanda nzeru, koma monga anzeru; akuchita machawi, popeza masiku ali oipa. Chifukwa chake musakhale opusa, koma dziwitsani chifuniro cha Ambuye nchiyani. Ndipo musaledzere naye vinyo, m'mene muli chitayiko; komatu mudzale naye Mzimu, ndi kudzilankhulira nokha ndi masalmo, ndi mayamiko, ndi nyimbo zauzimu, kuimbira ndi kuimba m'malimba Ambuye mumtima mwanu; ndipo yendani m'chikondi monganso Khristu anakukondani inu, nadzipereka yekha m'malo mwathu, chopereka ndi nsembe kwa Mulungu, ikhale fungo lonunkhira bwino.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Deuteronomo 24:5

Munthu akatenga mkazi watsopano, asatuluke nayo nkhondo, kapena asamchititse kanthu kalikonse; akhale waufulu kunyumba yake chaka chimodzi, nakondweretse mkazi adamtengayo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 22:6

Phunzitsa mwana poyamba njira yake; ndipo angakhale atakalamba sadzachokamo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 27:17

Chitsulo chinola chitsulo; chomwecho munthu anola nkhope ya mnzake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mlaliki 9:9

Khalani mokondwa ndi mkazi umkonda masiku onse a moyo wako wachabe, umene Mulungu wakupatsa pansi pano masiku ako onse achabe; pakuti ilo ndi gawo lako la m'moyo ndi m'ntchito zimene uvutika nazo pansi pano.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 13:10

Chikondano sichichitira mnzake choipa; chotero chikondanocho chili chokwanitsa lamulo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Nyimbo ya Solomoni 2:3

Ngati maula pakati pa mitengo ya m'nkhalango, momwemo wokondedwa wanga pakati pa ana amuna. Ndinakondwa pakukhala pa mthunzi wake, zipatso zake zinatsekemera m'kamwa mwanga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 15:7

Chifukwa chake mulandirane wina ndi mnzake, monganso Khristu anakulandirani inu, kukachitira Mulungu ulemerero.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Nyimbo ya Solomoni 4:12

Mlongo wanga, mkwatibwi ndiye munda wotsekedwa; ngati kasupe wotsekedwa, ndi chitsime chopikiza.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Nyimbo ya Solomoni 7:6

Ha, ndiwe wokongola ndi wofunika, bwenziwe, m'zokondweretsa!

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 24:3-4

Nzeru imangitsa nyumba; luntha liikhazikitsa. Ndinapita pa munda wa waulesi, polima mphesa munthu wosowa nzeru. Taonani, ponsepo panamera minga, ndi kuwirirapo khwisa; tchinga lake lamiyala ndi kupasuka. Pamenepo ndinayang'ana ndi kuganizira, ndinaona ndi kulandira mwambo. Tulo tapang'ono, kungoodzera pang'ono, kungomanga manja pang'ono m'kugona, ndipo umphawi wako udzafika ngati mbala; ndi kusauka kwako ngati munthu wachikopa. Kudziwa kudzaza zipinda zake ndi chuma chonse chofunika cha mtengo wake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Afilipi 4:5

Kufatsa kwanu kuzindikirike ndi anthu onse. Ambuye ali pafupi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 12:16

Mukhale ndi mtima umodzi wina ndi mnzake. Musasamalire zinthu zazikulu, koma phatikanani nao odzichepetsa. Musadziyesere anzeru mwa inu nokha.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 10:27

Ndipo iye anayankha nati, Uzikonda Ambuye Mulungu wako ndi mtima wako wonse, ndi moyo wako wonse, ndi mphamvu yako yonse, ndi nzeru zako zonse, ndi mnansi wako monga iwe mwini.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Genesis 3:16

Kwa mkaziyo ndipo anati, Ndidzachulukitsa kusauka kwako ndi potenga mimba pako; udzasauka pakubala: udzakhumba mwamuna wako, ndipo iye adzakulamulira iwe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Nyimbo ya Solomoni 2:4

Anandifikitsa kunyumba ya vinyo, mbendera yake yondizolimira inali chikondi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 16:14

Zanu zonse zichitike m'chikondi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Yohane 3:18

Tiana, tisakonde ndi mau, kapena ndi lilime, komatu ndi kuchita ndi m'choonadi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 14:19

Chifukwa chake tilondole zinthu za mtendere, ndi zinthu zakulimbikitsana wina ndi mnzake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Yohane 4:12

Palibe munthu adamuona Mulungu nthawi iliyonse; tikakondana wina ndi mnzake, Mulungu akhala mwa ife, ndi chikondi chake chikhala changwiro mwa ife;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 31:30

Kukongola kungonyenga, maonekedwe okoma ndi chabe; koma mkazi woopa Yehova adzatamandidwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Nyimbo ya Solomoni 8:10

Ndine khoma, mawere anga akunga nsanja zake: Pamaso pa mnyamatayo ndinafanana ngati wopeza mtendere.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 7:32-34

Koma ndifuna kuti mukhale osalabadira. Iye amene wosakwatira alabadira zinthu za Ambuye, kuti akondweretse Ambuye; koma iye wokwatira alabadira zinthu za dziko lapansi, kuti akondweretse mkazi wake. Ndi mkazi wokwatiwa ndi namwali asiyananso. Iye wosakwatiwa alabadira za Ambuye, kuti akhale woyera m'thupi ndi mumzimu; koma wokwatiwayo, alabadira za dziko lapansi, kuti akondweretse mwamunayo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Genesis 1:27

Mulungu ndipo adalenga munthu m'chifanizo chake, m'chifanizo cha Mulungu adamlenga iye; adalenga iwo mwamuna ndi mkazi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 11:3

Koma ndifuna kuti mudziwe, kuti mutu wa munthu yense ndiye Khristu; ndi mutu wa mkazi ndiye mwamuna; ndipo mutu wa Khristu ndiye Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Akorinto 13:11

Chotsalira, abale, kondwerani. Muchitidwe angwiro; mutonthozedwe; khalani a mtima umodzi, khalani mumtendere; ndipo Mulungu wa chikondi ndi mtendere akhale pamodzi ndi inu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Akolose 3:14

koma koposa izi zonse khalani nacho chikondano, ndicho chomangira cha mtima wamphumphu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Nyimbo ya Solomoni 1:16

Taona, wakongolatu, bwenzi langa, mnyamatawe, inde, wakongoletsa; pogona pathu mpa msipu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Nyimbo ya Solomoni 4:7

Wakongola monsemonse, wokondedwa wanga, namwaliwe, mulibe chilema mwa iwe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Genesis 1:28

Mulungu ndipo anadalitsa iwo, ndipo adati kwa iwo, Mubalane, muchuluke, mudzaze dziko lapansi, muligonjetse: mulamulire pa nsomba za m'nyanja, ndi pa mbalame za m'mlengalenga, ndi zamoyo zonse zakukwawa pa dziko lapansi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aefeso 5:22

Akazi inu, mverani amuna anu a inu eni, monga kumvera Ambuye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Akolose 3:18

Akazi inu, muzimvera amuna anu, monga kuyenera mwa Ambuye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 30:18-19

Zinthu zitatu zindithetsa nzeru, ngakhale zinai, sindizidziwa: Njira ya mphungu m'mlengalenga, njira ya njoka pamwala, njira ya ngalawa pakati pa nyanja, njira ya mwamuna ndi namwali.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Genesis 24:67

Ndipo Isaki anamlowetsa mkaziyo m'hema wa amake Sara, namtenga Rebeka, nakhala iye mkazi wake; ndipo anamkonda iye; ndipo Isaki anatonthozedwa mtima atafa amake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 19:6

Chotero kuti salinso awiri koma thupi limodzi. Chifukwa chake ichi chimene Mulungu anachimanga pamodzi, munthu asachilekanitse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 14:1

Mkazi yense wanzeru amanga banja lake; koma wopusa alipasula ndi manja ake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 12:10

M'chikondano cha anzanu wina ndi mnzake mukondane ndi chikondi chenicheni; mutsogolerane ndi kuchitira wina mnzake ulemu;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Petro 3:3-4

Amene kukometsera kwanu kusakhale kwa kunja, kuluka tsitsi ndi kuvala za golide, kapena kuvala chovala; koma kukhale munthu wobisika wamtima, m'chovala chosaola cha mzimu wofatsa ndi wachete, ndiwo wa mtengo wake wapatali pamaso pa Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 31:28-29

Anake adzanyamuka, nadzamutcha wodala; mwamuna wake namtama, nati, Ana akazi ambiri anachita mwangwiro, koma iwe uposa onsewo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 7:39

Mkazi amangika pokhala mwamuna wake ali ndi moyo; koma atamwalira mwamuna ali womasuka, kuti akwatiwe naye amene afuna, koma mwa Ambuye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 7:4

Mkazi alibe ulamuliro wa pa thupi lake la iye yekha, koma mwamuna ndiye; koma momwemonso mwamuna alibe ulamuliro wa pa thupi la iye yekha, koma mkazi ndiye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 12:4

Mkazi wodekha ndiye korona wa mwamuna wake; koma wochititsa manyazi akunga chovunditsa mafupa a mwamunayo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Nyimbo ya Solomoni 2:16

Wokondedwa wanga ndi wa ine, ine ndine wake: aweta zake pakati akakombo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 19:14

Nyumba ndi chuma ndizo cholowa cha atate; koma mkazi wanzeru achokera kwa Yehova.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Nyimbo ya Solomoni 4:9

Walanda mtima wanga, mlongo wanga, mkwatibwi; walanda mtima wanga ndi diso lako limodzi, ndi chinganga chimodzi cha pakhosi pako.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Petro 3:1

Momwemonso, akazi inu, mverani amuna anu a inu nokha; kuti, ngatinso ena samvera mau, akakodwe opanda mau mwa mayendedwe a akazi;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 5:18-19

Adalitsike kasupe wako; ukondwere ndi mkazi wokula nayo. Ngati mbawala yokonda ndi chinkhoma chachisomo, maere ake akukwanire nthawi zonse; ukodwe ndi chikondi chake osaleka.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Nyimbo ya Solomoni 1:2

Mnyamatayo andipsompsonetse ndi m'kamwa mwake; pakuti chikondi chako chiposa vinyo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aefeso 4:32

Koma mukhalirane okoma wina ndi mnzake, a mtima wachifundo, akukhululukirana nokha, monganso Mulungu mwa Khristu anakhululukira inu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Genesis 29:20

Ndipo Yakobo anamtumikira zaka zisanu ndi ziwiri chifukwa cha Rakele; koma zidamuonekera iye ngati masiku owerengeka chifukwa cha chikondi chimene anamkonda iye nacho.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 7:5

Musakanizana, koma ndi kuvomerezana kwanu ndiko, kwa nthawi, kuti mukadzipereke kwa kupemphera, nimukakhalenso pamodzi, kuti Satana angakuyeseni, chifukwa cha kusadziletsa kwanu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Nyimbo ya Solomoni 6:3

Ndine wake wa wokondedwa wanga, wokondedwa wanganso ndiye wa ine; aweta zake pakati pa akakombo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 31:25

Avala mphamvu ndi ulemu; nangoseka nthawi ya m'tsogolo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 7:10

Koma okwatitsidwawo ndiwalamulira, si ine ai, koma Ambuye, kuti mkazi asasiye mwamuna,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Petro 3:2

pakuona mayendedwe anu oyera ndi kuopa kwanu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Nyimbo ya Solomoni 8:6

Undilembe pamtima pako, mokhoma chizindikiro, nundikhomenso chizindikiro pamkono pako; pakuti chikondi chilimba ngati imfa; njiru imangouma ngati manda: Kung'anima kwake ndi kung'anima kwa moto, ngati mphezi ya Yehova.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 5:15

Imwa madzi a m'chitsime mwako, ndi madzi oyenda a m'kasupe mwako.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Timoteyo 5:8

Koma ngati wina sadzisungiratu mbumba yake ya iye yekha, makamaka iwo a m'banja lake, wakana chikhulupiriro iye, ndipo aipa koposa wosakhulupirira.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Afilipi 2:3

musachite kanthu monga mwa chotetana, kapena monga mwa ulemerero wopanda pake, komatu ndi kudzichepetsa mtima, yense ayese anzake omposa iye mwini;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 22:39

Ndipo lachiwiri lolingana nalo ndili, Uzikonda mnzako monga udzikonda iwe mwini.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Nyimbo ya Solomoni 7:10

Ndine wa wokondedwa wanga mnyamatayo, ndine amene andifunayo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Atesalonika 5:11

Mwa ichi chenjezanani, ndipo mangiriranani wina ndi mnzake, monganso mumachita.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Nyimbo ya Solomoni 5:16

M'kamwa mwake muli mokoma; inde, ndiye wokondweretsa ndithu. Ameneyu ndi wokondedwa wanga, ameneyu ndi bwenzi langa, ana akazi inu a ku Yerusalemu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Malaki 2:14

Koma mukuti, Chifukwa ninji? Chifukwa kuti Yehova anali mboni pakati pa iwe ndi mkazi wa ubwana wako, amene unamchitira chosakhulupirika, chinkana iye ndiye mnzako, mkazi wa pangano lako.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 27:15-16

Kudonthadontha tsiku lamvula, ndi mkazi wolongolola ali amodzimodzi. Wofuna kumletsayo afuna kuletsa mphepo; dzanja lake lamanja lingogwira mafuta.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Genesis 2:18

Yehova Mulungu ndipo anati, Si kwabwino kuti munthu akhale yekha; ndidzampangira womthangatira iye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 6:31

Ndipo monga mufuna inu kuti anthu adzakuchitirani inu, muwachitire iwo motero inu momwe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Nyimbo ya Solomoni 4:10

Ha, chikondi chako nchokongola, mlongo wanga, mkwatibwi! Kodi chikondi chako sichiposa vinyo? Kununkhira kwa mphoka yako ndi kuposa zonunkhiritsa za mitundumitundu!

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Nyimbo ya Solomoni 8:7

Madzi ambiri sangazimitse chikondi, ngakhale mitsinje yodzala kuchikokolola: Mwamuna akapereka katundu yense wa m'nyumba yake ngati sintho la chikondi, akanyozedwa ndithu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani

Pemphero kwa Mulungu

Mulungu wokhulupirika ndi woona, Ambuye Wamkulukulu! Ndikukutamandani chifukwa ndinu Wolungama, Woyera, woyenera kutamandidwa ndi kupembedzedwa konse. M'dzina la Yesu ndikupempherera, Mulungu, ndinu amene amatiisintha ndi kutitsogolera kuchokera ku ulemerero wina kupita ku wina, kuti tikhalire chitsanzo ndi umboni kwa mabanja ena amene akuyamba moyo wawo waukwati ndi kukhala onyamula ulemerero wanu. Ambuye, ndikupemphani kuti muwakwezere amuna utsogoleri kuti atsogolere bwino mabanja awo ndi nzeru zakumwamba, kuphunzitsa mabanja awo mawu a Mulungu ndi chitsogozo cha Mzimu Woyera wanu. Atate, munalenga mkazi ndi cholinga, kumpatsa mphamvu ndi ulamuliro pa mdima. Ambuye, tsiku lililonse akhale ndi kudzipereka kuti athetse ntchito zonse za thupi, mkangano ndi kupusa m'miyoyo yawo. Ndikudziwa Mulungu wanga kuti mukugwira ntchito m'mabanja, kuti amuna ndi akazi asanyengedwe ndi mawu okometsera a aliyense amene akufuna kuwalimbikitsa panjira yoipa kapena kuyesa kuwanyengerera. Mawu anu amati: “M’chikondi mulibe mantha; koma chikondi changwiro chimatulutsa mantha kunja; pakuti mantha ali nawo chilango. Ndipo iye amene ali ndi mantha sanakwaniridwe m’chikondi.” Ambuye, ndikupemphani kuti muyimitse pakamwa pa iwo amene akufuna kulowererapo kupyolera mu uphungu woipa, kugwiritsa ntchito zamatsenga, kapena kupyolera mu ziphunzitso zabodza kapena mawu otsutsana ndi banja limene munakhazikitsa. M'dzina la Yesu. Ameni.
Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa