Mavesi a Baibulo

- Zotsatsa -


Mavesi a Khrisimasi

Mavesi a Khrisimasi

Nthawi ya Khirisimasi ndi nthawi yabwino kwambiri yoti ndiganizire za chikondi chachikulu chimene Mulungu anationetsa potumiza Mwana wake Yesu padziko lapansi. Ndi nthawi yabwino yoti ndigawane uthenga umenewu ndi chikondi chimenechi ndi anthu amene ali pafupi nane.

Ndikukumbukira kuti Khirisimasi ndi imodzi mwa maholide ofunikira kwambiri amene timakondwerera monga Akhristu, pamodzi ndi Pasika ndi Pentekosti: Kubadwa kwa Yesu Khristu ku Betelehemu. Nthawi imeneyi nthawi zambiri ndimakhala wokonzeka kumva komanso kudziwa zomwe ndili nazo ndi zomwe ndikumva, ndikuyamikira Mulungu pa zonse zomwe wandipatsa chaka chino.

Pakuti mwana wabadwira ife, mwana wamkazi wapatsidwa ife; ulamuliro udzakhala pa phewa lake, ndipo adzatchedwa: Wodabwitsa Wopereka Malangizo, Mulungu Wamphamvu, Atate Wamuyaya, Kalonga wa Mtendere (Yesaya 9:6).

Chaka chino Khirisimasi, lonjezo la Mulungu lindilimbikitse kukhala moyo wosiyana, kuyamika mtengo wa magazi ake pa mtanda, kukana chilichonse cha dziko, ndipo mzimu wa ubwino ndi kuwolowa manja, wodzala ndi chikondi ndipo wodzala ndi chipiriro chimene ndinalandira pa Ubatizo, zikule mu ine.

Ndikukumbukira kuti kuti ndiyime bwino pa moyo wanga, ndiyimirire patsogolo pa Mulungu.




Luka 2:11

pakuti wakubadwirani inu lero, m'mudzi wa Davide, Mpulumutsi, amene ali Khristu Ambuye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 2:1-2

Ndipo pa kubadwa kwake kwa Yesu m'Betelehemu wa Yudeya m'masiku a Herode mfumu, onani, Anzeru a kum'mawa anafika ku Yerusalemu,nati, Ali kuti amene anabadwa mfumu ya Ayuda? Chifukwa tinaona nyenyezi yake kum'mawa, ndipo tinadzera kudzamlambira Iye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yeremiya 9:6

Ukhala pakati pa manyengo m'manyengo; akana kundidziwa, ati Yehova.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 2:6-7

Ndipo panali pokhala iwo komweko, masiku ake a kubala anakwanira.Ndipo iye anabala mwana wake wamwamuna woyamba; namkulunga Iye m'nsalu, namgoneka modyera ng'ombe, chifukwa kuti anasowa malo m'nyumba ya alendo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 2:4-5

Ndipo Yosefe yemwe anakwera kuchokera ku Galileya, kumudzi wa Nazarete, kunka ku Yudeya, kumudzi wa Davide, dzina lake Betelehemu, chifukwa iye anali wa banja ndi fuko lake la Davide;kukalembedwa iye mwini pamodzi ndi Maria, wopalidwa naye ubwenzi; ndi uyu anali ndi pakati.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 1:35

Ndipo mngelo anayankha, nati kwa iye, Mzimu Woyera adzafika pa iwe, ndi mphamvu ya Wamkulukulu idzakuphimba iwe: chifukwa chakenso Choyeracho chikadzabadwa, chidzatchedwa Mwana wa Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 1:30-31

Ndipo mngelo anati kwa iye, Usaope, Maria; pakuti wapeza chisomo ndi Mulungu.Ndipo taona, udzakhala ndi pakati, nudzabala mwana wamwamuna, nudzamutcha dzina lake Yesu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Marko 1:18

Ndipo pomwepo anasiya makoka ao, namtsata Iye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 1:21-23

Ndipo adzabala mwana wamwamuna, ndipo udzamutcha dzina lake Yesu; pakuti Iyeyo adzapulumutsa anthu ake kumachimo ao.Ndipo zonsezi zinakhala kuti chikachitidwe chonenedwa ndi Ambuye mwa mneneri, ndi kuti,Onani namwali adzaima, nadzabala mwana wamwamuna, ndipo adzamutcha dzina lake, Imanuele. Ndilo losandulika, Mulungu nafe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Agalatiya 4:4-5

koma pokwaniridwa nthawi, Mulungu anatuma Mwana wake, wobadwa ndi mkazi, wobadwa wakumvera lamulo,kuti akaombole iwo akumvera lamulo, kuti ife tikalandire umwana.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 2:7

Ndipo iye anabala mwana wake wamwamuna woyamba; namkulunga Iye m'nsalu, namgoneka modyera ng'ombe, chifukwa kuti anasowa malo m'nyumba ya alendo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 2:11

Ndipo pofika kunyumba anaona kamwanako ndi Maria amake, ndipo anagwa pansi namgwadira Iye; namasula chuma chao, nampatsa Iye mitulo, ndiyo golide ndi lubani ndi mure.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 1:14

Ndipo Mau anasandulika thupi, nakhazikika pakati pa ife, ndipo tinaona ulemerero wake, ulemerero wonga wa wobadwa yekha wa Atate, wodzala ndi chisomo ndi choonadi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 1:22-23

Ndipo zonsezi zinakhala kuti chikachitidwe chonenedwa ndi Ambuye mwa mneneri, ndi kuti,Onani namwali adzaima, nadzabala mwana wamwamuna, ndipo adzamutcha dzina lake, Imanuele. Ndilo losandulika, Mulungu nafe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 2:10-11

Ndipo mngelo anati kwa iwo, Musaope; pakuti onani, ndikuuzani inu uthenga wabwino wa chikondwero chachikulu, chimene chidzakhala kwa anthu onse;pakuti wakubadwirani inu lero, m'mudzi wa Davide, Mpulumutsi, amene ali Khristu Ambuye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 72:11

Inde mafumu onse adzamgwadira iye, amitundu onse adzamtumikira.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 9:6-7

Pakuti kwa ife mwana wakhanda wabadwa, kwa ife mwana wamwamuna wapatsidwa; ndipo ulamuliro udzakhala pa phewa lake, ndipo adzamutcha dzina lake Wodabwitsa, Wauphungu, Mulungu wamphamvu, Atate Wosatha, Kalonga wa mtendere.Za kuenjezera ulamuliro wake, ndi za mtendere sizidzatha pa mpando wachifumu wa Davide, ndi pa ufumu wake, kuukhazikitsa, ndi kuuchirikiza ndi chiweruziro ndi chilungamo kuyambira tsopano ndi kunkabe nthawi zonse. Changu cha Yehova wa makamu chidzachita zimenezi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 2:4-7

Ndipo Yosefe yemwe anakwera kuchokera ku Galileya, kumudzi wa Nazarete, kunka ku Yudeya, kumudzi wa Davide, dzina lake Betelehemu, chifukwa iye anali wa banja ndi fuko lake la Davide;kukalembedwa iye mwini pamodzi ndi Maria, wopalidwa naye ubwenzi; ndi uyu anali ndi pakati.Ndipo panali pokhala iwo komweko, masiku ake a kubala anakwanira.Ndipo iye anabala mwana wake wamwamuna woyamba; namkulunga Iye m'nsalu, namgoneka modyera ng'ombe, chifukwa kuti anasowa malo m'nyumba ya alendo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 2:13-14

Ndipo dzidzidzi panali pamodzi ndi mngeloyo ambirimbiri a gulu la Kumwamba, natamanda Mulungu, nanena, Ulemerero ukhale kwa Mulungu Kumwambamwamba, ndi mtendere pansi pano mwa anthu amene akondwera nao.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mika 5:2

Koma iwe, Betelehemu Efurata, ndiwe wamng'ono kuti ukhale mwa zikwi za Yuda, mwa iwe mudzanditulukira wina wakudzakhala woweruza m'Israele; matulukiro ake ndiwo a kale lomwe, kuyambira nthawi yosayamba.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 1:18-19

Ndipo kubadwa kwake kwa Yesu Khristu kunali kotere: Amai wake Maria anapalidwa ubwenzi ndi Yosefe, koma asanakomane iwowo, anapezedwa iye ali ndi pakati mwa Mzimu Woyera.Koma Yosefe, mwamuna wake, anali wolungama, ndiponso sanafune kunyazitsa iye, nayesa m'mtima kumleka iye m'tseri.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 2:8-12

Ndipo panali abusa m'dziko lomwelo, okhala kubusa ndi kuyang'anira zoweta zao usiku.Ndipo mngelo wa Ambuye anaimirira pa awo, ndi kuwala kwa Ambuye kunawaunikira kozungulira: ndipo anaopa ndi mantha akulu.Ndipo mngelo anati kwa iwo, Musaope; pakuti onani, ndikuuzani inu uthenga wabwino wa chikondwero chachikulu, chimene chidzakhala kwa anthu onse;pakuti wakubadwirani inu lero, m'mudzi wa Davide, Mpulumutsi, amene ali Khristu Ambuye.Ndipo ichi ndi chizindikiro kwa inu: Mudzapeza mwana wakhanda wokuta ndi nsalu atagona modyera.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 2:15-16

Ndipo panali, pamene angelo anachokera kwa iwo kunka Kumwamba, abusa anati wina ndi mnzake, Tipitiretu ku Betelehemu, tikaone chinthu ichi chidachitika, chimene Ambuye anatidziwitsira ife.Ndipo iwo anadza ndi changu, napeza Maria, ndi Yosefe, ndi mwana wakhanda atagona modyera.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 98:4-6

Fuulirani kwa Yehova, inu, dziko lonse lapansi; kuwitsani ndi kufuulira mokondwera; inde, imbirani zomlemekeza.Muimbireni Yehova zomlemekeza ndi zeze; ndi zeze ndi mau a salimo.Fuulani pamaso pa Mfumu Yehova, ndi mbetete ndi liu la lipenga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 11:1-2

Ndipo padzatuluka mphukira pa tsinde la Yese, ndi nthambi yotuluka m'mizu yake idzabala zipatso;Ndipo mzimu wa Yehova udzambalira iye mzimu wanzeru ndi wakuzindikira, mzimu wa uphungu ndi mphamvu, mzimu wakudziwa ndi wakuopa Yehova;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 1:31-33

Ndipo taona, udzakhala ndi pakati, nudzabala mwana wamwamuna, nudzamutcha dzina lake Yesu.Iye adzakhala wamkulu, nadzatchedwa Mwana wa Wamkulukulu: ndipo Ambuye Mulungu adzampatsa Iye mpando wachifumu wa Davide atate wake:ndipo Iye adzachita ufumu pa banja la Yakobo kunthawi zonse; ndipo ufumu wake sudzatha.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 2:9-11

Ndipo iwo, m'mene anamva mfumu, anamuka; ndipo onani, nyenyezi ija anaiona kum'mawa, inawatsogolera iwo, kufikira inadza niima pamwamba pomwe panali kamwanako.Ndipo iwo poona nyenyeziyo, anakondwera ndi kukondwera kwakukulu.Ndipo pofika kunyumba anaona kamwanako ndi Maria amake, ndipo anagwa pansi namgwadira Iye; namasula chuma chao, nampatsa Iye mitulo, ndiyo golide ndi lubani ndi mure.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 2:20

Ndipo abusawo anabwera, nalemekeza ndi kutamanda Mulungu pa zinthu zonse anazimva, naziona, monga kunalankhulidwa kwa iwo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 9:2

Anthu amene anayenda mumdima, aona kuwala kwakukulu; iwo amene anakhala m'dziko la mthunzi wa imfa, kuwala kwatulukira kwa iwo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 2:34-35

Ndipo Simeoni anawadalitsa, nati kwa Maria amake, Taona, Uyu waikidwa akhale kugwa ndi kunyamuka kwa anthu ambiri mwa Israele; ndipo akhale chizindikiro chakutsutsana nacho;eya, ndipo lupanga lidzakupyoza iwe moyo wako; kuti maganizo a m'mitima yambiri akaululidwe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 2:12

Ndipo iwo, pochenjezedwa m'kulota kuti asabwerere kwa Herode, anachoka kupita ku dziko lao pa njira ina.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 2:14-15

Popeza tsono ana ndiwo a mwazi ndi nyama, Iyenso momwemo adalawa nao makhalidwe omwewo kuti mwa imfa akamuononge iye amene anali nayo mphamvu ya imfa, ndiye mdierekezi;nakamasule iwo onse amene, chifukwa cha kuopa imfa, m'moyo wao wonse adamangidwa ukapolo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 96:1-3

Muimbireni Yehova nyimbo yatsopano; muimbireni Yehova, inu, dziko lonse lapansi.Muimbireni Yehova, lemekezani dzina lake; lalikirani chipulumutso chake tsiku ndi tsiku.Fotokozerani ulemerero wake mwa amitundu; zodabwitsa zake mwa mitundu yonse ya anthu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 3:16

Pakuti Mulungu anakonda dziko lapansi kotero, kuti anapatsa Mwana wake wobadwa yekha, kuti yense wakhulupirira Iye asatayike, koma akhale nao moyo wosatha.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 1:46-47

Ndipo Maria anati, Moyo wanga ulemekeza Ambuye,ndipo mzimu wanga wakondwera mwa Mulungu Mpulumutsi wanga,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 1:68-70

Wolemekezeka Ambuye, Mulungu wa Israele; chifukwa Iye anayang'ana, nachitira anthu ake chiombolo.Ndipo Iye anatikwezera ife nyanga ya chipulumutso, mwa fuko la Davide mwana wake.Monga Iye analankhula ndi m'kamwa mwa aneneri ake oyera mtima, akale lomwe,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 2:15

nakhalabe kumeneko kufikira atamwalira Herode; kuti chikachitidwe chonenedwa ndi Ambuye mwa mneneri kuti, Ndinaitana Mwana wanga atuluke m'Ejipito.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 60:1-3

Nyamuka, wala, pakuti kuunika kwako kwafika, ndi ulemerero wa Yehova wakutulukira.Pakuti taona, mdima udzaphimba dziko lapansi, ndi mdima wa bii mitundu ya anthu; koma Yehova adzakutulukira ndi ulemerero wake udzaoneka pa iwe.Ndipo amitundu adzafika kwa kuunika kwako, ndi mafumu kwa kuyera kwa kutuluka kwako.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 1:24-25

Ndipo Yosefe anauka tulo take, nachita monga anamuuza mngelo wa Ambuye, nadzitengera yekha mkazi wake;ndipo sanamdziwe iye kufikira atabala mwana wake; namutcha dzina lake Yesu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 1:76-79

Eya, ndipo iwetu kamwanawe, udzanenedwa mneneri wa Wamkulukulu; pakuti udzatsogolera Ambuye, kukonza njira zake.Kuwapatsa anthu ake adziwitse chipulumutso, ndi makhululukidwe a machimo ao,chifukwa cha mtima wachifundo wa Mulungu wathu. M'menemo mbandakucha wa kumwamba udzatichezera ife.Kuwalitsira iwo okhala mumdima ndi mthunzi wa imfa; kulunjikitsa mapazi athu mu njira ya mtendere.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 148:1-4

Aleluya. Lemekezani Yehova kochokera kumwamba; mlemekezeni m'misanje.Mlemekezeni, angelo ake onse; mlemekezeni, makamu ake onse.Mlemekezeni, dzuwa ndi mwezi; mlemekezeni, nyenyezi zonse zounikira.Mlemekezeni, m'mwambamwamba, ndi madzi inu, a pamwamba pa thambo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 15:12

Ndiponso, Yesaya ati, Padzali muzu wa Yese, ndi Iye amene aukira kuchita ufumu pa anthu amitundu; Iyeyo anthu amitundu adzamuyembekezera.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 2:25-30

Ndipo onani, m'Yerusalemu munali munthu, dzina lake Simeoni; ndipo munthu uyu, wolungama mtima ndi wopemphera, analikulindira matonthozedwe a Israele; ndipo Mzimu Woyera anali pa iye.Ndipo anamuululira Mzimu Woyera kuti sadzaona imfa, kufikira adzaona Khristu wake wa Ambuye.Ndipo iye analowa ku Kachisi ndi Mzimu: ndipo pamene atate ndi amake analowa ndi kamwanako Yesu, kudzamchitira Iye mwambo wa chilamulo,pomwepo iye anamlandira Iye m'manja mwake, nalemekeza Mulungu, nati,Tsopano, Ambuye, monga mwa mau anu aja, lolani ine, kapolo wanu, ndichoke mumtendere;chifukwa maso anga adaona chipulumutso chanu,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 1:17

Motero mibadwo yonse kuyambira pa Abrahamu kufikira kwa Davide ndiyo mibadwo khumi ndi inai; ndi kuyambira pa Davide kufikira pa kutengedwa kunka ku Babiloni mibadwo khumi ndi inai; ndi kuyambira pa kutengedwa kunka ku Babiloni kufikira kwa Khristu mibadwo khumi ndi inai.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 53:2

Pakuti ameneyo adzaphuka pamaso pake ngati mtengo wanthete, ndi ngati muzu womera m'nthaka youma; Iye alibe maonekedwe, pena kukongola; ndipo pamene timuona palibe kukongola kuti timkhumbe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 1:9

Uku ndiko kuunika kwenikweni, kumene kuunikira anthu onse akulowa m'dziko lapansi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 72:10-11

Mafumu a ku Tarisisi ndi ku Zisumbuzo adzabwera nacho chopereka; mafumu a ku Sheba ndi Seba adzadza nazo mphatso.Inde mafumu onse adzamgwadira iye, amitundu onse adzamtumikira.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 2:38

Ndipo iye anafikako pa nthawi yomweyo, navomerezanso kutama Mulungu, nalankhula za Iye kwa anthu onse akuyembekeza chiombolo cha Yerusalemu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 2:6

Ndipo iwe Betelehemu, dziko la Yudeya, sukhala konse wamng'onong'ono mwa akulu a Yudeya. Pakuti Wotsogolera adzachokera mwa iwe, amene adzaweta anthu anga Aisraele.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 110:1

Yehova ananena kwa Ambuye wanga, Khalani pa dzanja lamanja langa, kufikira nditaika adani anu chopondapo mapazi anu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 42:1

Taona Mtumiki wanga, amene ndimgwiriziza; Wosankhika wanga, amene moyo wanga ukondwera naye; ndaika mzimu wanga pa Iye; Iye adzatulutsira amitundu chiweruziro.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 8:32

Iye amene sanatimana Mwana wake wa Iye yekha, koma anampereka chifukwa cha ife tonse, adzalekeranji kutipatsanso ife zinthu zonse kwaulere pamodzi ndi Iye?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 5:14

Inu ndinu kuunika kwa dziko lapansi. Mudzi wokhazikika pamwamba pa phiri sungathe kubisika.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 1:28

Ndipo pakulowa mngelo anati kwa iye, Tikuoneni, wochitidwa chisomo, Ambuye ali ndi iwe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 2:20-21

nati, Tauka, nutenge kamwana ndi amake, nupite kudziko la Israele: chifukwa anafa uja wofuna moyo wake wa kamwanako.Ndipo anauka iye, natenga kamwana ndi amake, nalowa m'dziko la Israele.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 46:10

Khalani chete, ndipo dziwani kuti Ine ndine Mulungu, Ndidzabuka mwa amitundu, ndidzabuka pa dziko lapansi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 100:1-5

Fuulirani kwa Yehova, inu, dziko lonse lapansi. Tumikirani Yehova ndi chikondwerero: Idzani pamaso pake ndi kumuimbira mokondwera.Dziwani kuti Yehova ndiye Mulungu; Iyeyu anatilenga, ndipo ife ndife ake; ndife anthu ake ndi nkhosa zapabusa pake.Lowani kuzipata zake ndi chiyamiko, ndi kumabwalo ake ndi chilemekezo: Myamikeni; lilemekezeni dzina lake.Pakuti Yehova ndiye wabwino; chifundo chake chimanka muyaya; ndi chikhulupiriko chake ku mibadwomibadwo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 49:6

inde, ati, Chili chinthu chopepuka ndithu kuti Iwe ukhale mtumiki wanga wakuutsa mafuko a Yakobo, ndi kubwezera osungika a Israele; ndidzakupatsanso ukhale kuunika kwa amitundu, kuti ukhale chipulumutso changa mpaka ku malekezero a dziko lapansi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 2:7-8

Pomwepo Herode anawaitana Anzeruwo m'tseri, nafunsitsa iwo nthawi yake idaoneka nyenyeziyo.Nawatumiza ku Betelehemu, nati, Yendani mufunitsitse za kamwanako; ndipo pamene mudzampeza, mundibwezere mau, kuti inenso ndidzadze kudzamlambira Iye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 1:49-50

Chifukwa Iye Wamphamvuyo anandichitira ine zazikulu; ndipo dzina lake lili loyera.Ndipo chifundo chake chifikira anthu a mibadwomibadwo pa iwo amene amuopa Iye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 5:8

Koma Mulungu atsimikiza kwa ife chikondi chake cha mwini yekha m'menemo, kuti pokhala ife chikhalire ochimwa, Khristu adatifera ife.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Afilipi 2:7-8

koma anadzikhuthula yekha, natenga maonekedwe a kapolo, nakhala m'mafanizidwe a anthu;ndipo popezedwa m'maonekedwe ngati munthu, anadzichepetsa yekha, nakhala womvera kufikira imfa, ndiyo imfa ya pamtanda.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 100:4

Lowani kuzipata zake ndi chiyamiko, ndi kumabwalo ake ndi chilemekezo: Myamikeni; lilemekezeni dzina lake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 60:6

Gulu la ngamira lidzakukuta, ngamira zazing'ono za Midiyani ndi Efa; iwo onsewo adzachokera ku Sheba adzabwera nazo golide ndi lubani; ndipo adzalalikira matamando a Yehova.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 1:23

Onani namwali adzaima, nadzabala mwana wamwamuna, ndipo adzamutcha dzina lake, Imanuele. Ndilo losandulika, Mulungu nafe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 2:30-32

chifukwa maso anga adaona chipulumutso chanu, chimene munakonza pamaso pa anthu onse,kuunika kukhale chivumbulutso cha kwa anthu a mitundu, ndi ulemerero wa anthu anu Israele.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 113:3

Chitulukire dzuwa kufikira kulowa kwake lilemekezedwe dzina la Yehova.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 8:12

Pamenepo Yesu analankhulanso nao, nanena, Ine ndine kuunika kwa dziko lapansi; iye wonditsata Ine sadzayenda mumdima, koma adzakhala nako kuunika kwa moyo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 19:1

Zakumwamba zimalalikira ulemerero wa Mulungu; ndipo thambo lionetsa ntchito ya manja ake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Agalatiya 3:26-27

Pakuti inu nonse muli ana a Mulungu, mwa chikhulupiriro cha mwa Khristu Yesu.Pakuti nonse amene munabatizidwa kwa Khristu mudavala Khristu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 2:1-3

Ndipo kunali masiku aja, kuti lamulo linatuluka kwa Kaisara Augusto kuti dziko lonse lokhalamo anthu lilembedwe;ndiko kulembera koyamba pokhala Kwirinio kazembe wa Siriya.Ndipo onse anamuka kulembedwa, munthu aliyense kumudzi wake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 89:27

Inde ndidzamuyesa mwana wanga woyamba, womveka wa mafumu a pa dziko lapansi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 28:19

Chifukwa chake mukani, phunzitsani anthu a mitundu yonse, ndi kuwabatiza iwo m'dzina la Atate, ndi la Mwana, ndi la Mzimu Woyera:

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 53:5

Koma Iye analasidwa chifukwa cha zolakwa zathu, natundudzidwa chifukwa cha mphulupulu zathu; chilango chotitengera ife mtendere chinamgwera Iye; ndipo ndi mikwingwirima yake ife tachiritsidwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 14:6

Yesu ananena naye, Ine ndine njira, ndi choonadi, ndi moyo. Palibe munthu adza kwa Atate, koma mwa Ine.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 1:54-55

Anathangatira Israele mnyamata wake, kuti akakumbukire chifundo,(Monga analankhula kwa makolo athu) kwa Abrahamu ndi kwa mbeu yake kunthawi yonse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 2:3

Ndipo Herode mfumuyo pakumva ichi anavutika, ndi Yerusalemu yense pamodzi naye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 4:7

Mwapatsa chimwemwe mumtima mwanga, chakuposa chao m'nyengo yakuchuluka dzinthu zao ndi vinyo wao.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 61:1

Mzimu wa Ambuye Yehova uli pa ine; pakuti Yehova wandidzoza ine ndilalikire mau abwino kwa ofatsa; Iye wanditumiza ndikamange osweka mtima, ndikalalikire kwa am'nsinga mamasulidwe, ndi kwa omangidwa kutsegulidwa kwa m'ndende;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 1:79

Kuwalitsira iwo okhala mumdima ndi mthunzi wa imfa; kulunjikitsa mapazi athu mu njira ya mtendere.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 15:13

Ndipo Mulungu wa chiyembekezo adzaze inu ndi chimwemwe chonse ndi mtendere m'kukhulupirira, kuti mukachuluke ndi chiyembekezo, mu mphamvu ya Mzimu Woyera.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 136:1-3

Yamikani Yehova pakuti ndiye wabwino; pakuti chifundo chake nchosatha.Yamikani Mulungu wa milungu; pakuti chifundo chake nchosatha.Yamikani Mbuye wa ambuye; pakuti chifundo chake nchosatha.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 23:1

Yehova ndiye mbusa wanga; sindidzasowa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 12:2

Taonani, Mulungu ndiye chipulumutso changa; ndidzakhulupirira, sindidzaopa; pakuti Yehova Mwini ndiye mphamvu yanga ndi nyimbo yanga, Iye ndiye chipulumutso changa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 2:14

Ulemerero ukhale kwa Mulungu Kumwambamwamba, ndi mtendere pansi pano mwa anthu amene akondwera nao.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 2:10

Ndipo iwo poona nyenyeziyo, anakondwera ndi kukondwera kwakukulu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 68:19

Wolemekeza Ambuye, tsiku ndi tsiku atisenzera katundu, ndiye Mulungu wa chipulumutso chathu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Afilipi 4:4

Kondwerani mwa Ambuye nthawi zonse: ndibwerezanso kutero, kondwerani.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 52:7

Ha, akongolatu pamapiri mapazi a iye amene adza ndi uthenga wabwino, amene abukitsa mtendere, amene adza ndi uthenga wabwino wa zinthu zabwino, amene abukitsa chipulumutso; amene ati kwa Ziyoni, Mulungu wako ndi mfumu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 10:15

Ndipo adzalalikira bwanji, ngati satumidwa? Monganso kwalembedwa, Okometsetsa ndithu ali mapazi a iwo akulalikira Uthenga Wabwino wa zinthu zabwino.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Agalatiya 4:6

Ndipo popeza muli ana, Mulungu anatumiza Mzimu wa Mwana wake alowe m'mitima yathu, wofuula Abba! Atate!

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 1:20

Koma pakusinkhasinkha iye zinthu izi, onani, mngelo wa Ambuye anaonekera kwa iye m'kulota, nanena, Yosefe, mwana wa Davide, usaope kudzitengera wekha Maria mkazi wako; pakuti icho cholandiridwa mwa iye chili cha Mzimu Woyera.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 37:4

Udzikondweretsenso mwa Yehova; ndipo Iye adzakupatsa zokhumba mtima wako.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 3:6

ndipo anthu onse adzaona chipulumutso cha Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 96:10

Nenani mwa amitundu, Yehova achita ufumu; dziko lokhalamo anthu lomwe likhazikika kuti silingagwedezeke; adzaweruza mitundu ya anthu molunjika.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 1:12

Koma onse amene anamlandira Iye, kwa iwo anapatsa mphamvu yakukhala ana a Mulungu, kwa iwotu, akukhulupirira dzina lake;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 148:1-5

Aleluya. Lemekezani Yehova kochokera kumwamba; mlemekezeni m'misanje.Mlemekezeni, angelo ake onse; mlemekezeni, makamu ake onse.Mlemekezeni, dzuwa ndi mwezi; mlemekezeni, nyenyezi zonse zounikira.Mlemekezeni, m'mwambamwamba, ndi madzi inu, a pamwamba pa thambo.Alemekeze dzina la Yehova; popeza analamulira, ndipo zinalengedwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 5:9

Odala ali akuchita mtendere; chifukwa adzatchedwa ana a Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 12:10

M'chikondano cha anzanu wina ndi mnzake mukondane ndi chikondi chenicheni; mutsogolerane ndi kuchitira wina mnzake ulemu;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 18:28

Pakuti Inu muyatsa nyali yanga; Yehova, Mulungu wanga, aunikira mdima wanga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Afilipi 1:3-5

Ndiyamika Mulungu wanga pokumbukira inu ponse;nthawi zonse m'pembedzero langa lonse la kwa inu nonse ndichita pembedzerolo ndi kukondwera,chifukwa cha chiyanjano chanu chakuthandizira Uthenga Wabwino, kuyambira tsiku loyambalo, kufikira tsopano lino;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 60:1-2

Nyamuka, wala, pakuti kuunika kwako kwafika, ndi ulemerero wa Yehova wakutulukira.Pakuti taona, mdima udzaphimba dziko lapansi, ndi mdima wa bii mitundu ya anthu; koma Yehova adzakutulukira ndi ulemerero wake udzaoneka pa iwe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Yohane 1:9

Ngati tivomereza machimo athu, ali wokhulupirika ndi wolungama Iye, kuti atikhululukire machimo athu, ndi kutisambitsa kutichotsera chosalungama chilichonse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 1:78-79

chifukwa cha mtima wachifundo wa Mulungu wathu. M'menemo mbandakucha wa kumwamba udzatichezera ife.Kuwalitsira iwo okhala mumdima ndi mthunzi wa imfa; kulunjikitsa mapazi athu mu njira ya mtendere.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 1:1

Buku la kubadwa kwa Yesu Khristu, mwana wa Davide, mwana wa Abrahamu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 7:14

Chifukwa chake Ambuye mwini yekha adzakupatsani inu chizindikiro; taonani namwali adzaima, nadzabala mwana wamwamuna, nadzamutcha dzina lake Imanuele.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 126:3

Yehova anatichitira ife zazikulu; potero tikhala okondwera.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Habakuku 3:18

koma ndidzakondwera mwa Yehova, ndidzasekerera mwa Mulungu wa chipulumutso changa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 1:14

Ndipo udzakhala nako kukondwera ndi msangalalo; ndipo anthu ambiri adzakondwera pa kubadwa kwake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 1:46-48

Ndipo Maria anati, Moyo wanga ulemekeza Ambuye,ndipo mzimu wanga wakondwera mwa Mulungu Mpulumutsi wanga,chifukwa Iye anayang'anira umphawi wa mdzakazi wake; pakuti taonani, kuyambira tsopano, anthu a mibadwo yonse adzanditchula ine wodala.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 1:21

Ndipo adzabala mwana wamwamuna, ndipo udzamutcha dzina lake Yesu; pakuti Iyeyo adzapulumutsa anthu ake kumachimo ao.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 2:10

Ndipo mngelo anati kwa iwo, Musaope; pakuti onani, ndikuuzani inu uthenga wabwino wa chikondwero chachikulu, chimene chidzakhala kwa anthu onse;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 9:6

Pakuti kwa ife mwana wakhanda wabadwa, kwa ife mwana wamwamuna wapatsidwa; ndipo ulamuliro udzakhala pa phewa lake, ndipo adzamutcha dzina lake Wodabwitsa, Wauphungu, Mulungu wamphamvu, Atate Wosatha, Kalonga wa mtendere.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani

Pemphero kwa Mulungu

Ambuye Mulungu Wamphamvuyonse, ulemerero ndi ulemu zikhale kwa Inu! Mulungu wanga wakumwamba, m'dzina la Yesu ndikupemphani chikhululukiro cha machimo anga ndipo ndikukuthankani Atate, chifukwa munandinikonda kwambiri kotero kuti munatumiza Mwana wanu kuti ine ndikhale ndi moyo wopanda uchimo ndi imfa. Ambuye wanga, ndikuyang'ana mumtima mwanga ndipo sindipeza mawu okwanira othandizira kufotokoza momwe ndikusangalalira kukhala ndi banja langa kukumbukira zomwe munachita pa mtanda. Inu, Mulungu wachikondi munatumiza Yesu pamene sitinali oyenera ngakhale pang'ono kuti muchotse madothi a m'miyoyo yathu omwe sitingathe kuyeretsa tokha, ndikukuthankani kwambiri chifukwa cha Yesu. Atate wokondedzeka, dzina lanu ndi loyenera kutamandidwa konse ndipo chimwemwe changa ndi mphamvu yanu Ambuye. Zikomo Yesu, chifukwa chobweretsa chikondi cha Mulungu padziko lapansi ndikutivumbula zinsinsi za Atate, zikomo chifukwa cha kukhalapo kwanu m'moyo wanga ndi m'banja langa. Popanda Inu ndikanatayika ndipo pamaso panu ndikuvomereza, chifukwa Inu ndinu wokhulupirika ndi wowona, simundisiya ndipo simutopa kundifuna. Ndikupemphani kuti mundidzaze ndi chisomo chanu champhamvu ndi kundisintha kukhala dalitso kwa ena nthawi ino ndi moyo wanga wonse, Mzimu Woyera limbikitsani mumtima mwanga nsembe imene Yesu anapereka kuti mundisinthe kufikira nditafika pa msinkhu wa munthu wangwiro. M'dzina la Yesu. Ameni!
Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa