Mavesi a Baibulo

- Zotsatsa -


MAVESI ODALITSA

MAVESI ODALITSA

Pali anthu apadera amene Mulungu waika pa moyo wako, ndi anthu odalitsidwa ndi okondedwa, amene tikuwadalitsa m'dzina la Yesu. M'Baibulo muli mavesi ambiri oti tithokoze ndi kudalitsa miyoyo imeneyi.

Sitimadalitsa anthu okhawo, koma mabanja athu, dziko lathu, ndi abale athu mwa Khristu. “Yehova akudalitse, nakusunge; Yehova akuunikire nkhope yake pa iwe, nakuchitire chifundo; Yehova akweze nkhope yake pa iwe, nakupatsenso mtendere.” (Numeri 6:24-26)

Timadalitsanso abusa athu amene Mulungu amawagwiritsa ntchito. “Pakuti Inu, Yehova, mudzadalitsa wolungama; Mudzam'zungulira ndi chiyanjo chanu ngati ndi chishango.” (Salimo 5:12)

Sitiyenera kudalitsa okhawo atichitira zabwino, chifukwa Mulungu watilamula kuti tizidalitsa ngakhale atichitira zoipa. “Dalitsani iwo akutikuzunzani; dalitsani, musatemberere.” (Aroma 12:14)




Mateyu 25:35-40

pakuti ndinali ndi njala, ndipo munandipatsa Ine kudya; ndinali ndi ludzu, ndipo munandimwetsa Ine; ndinali mlendo, ndipo munachereza Ine;wamaliseche Ine, ndipo munandiveka; ndinadwala, ndipo munadza kucheza ndi Ine; ndinali m'nyumba yandende, ndipo munadza kwa Ine.Pomwepo olungama adzamyankha Iye kuti, Ambuye, tinakuonani Inu liti wanjala, ndi kukudyetsani? Kapena waludzu, ndi kukumwetsani?Ndipo tinaona Inu liti mlendo, ndi kukucherezani? Kapena wamaliseche, ndi kukuvekani?Ndipo tinakuonani Inu liti wodwala, kapena m'nyumba yandende, ndipo tinadza kwa Inu?Ndipo Mfumuyo idzayankha nidzati kwa iwo, Indetu ndinena kwa inu, Chifukwa munachitira ichi mmodzi wa abale anga, ngakhale ang'onong'ono awa, munandichitira ichi Ine.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 19:17

Wochitira waumphawi chifundo abwereka Yehova; adzambwezera chokoma chakecho.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 58:10

ndipo ngati upereka kwa wanjala chimene moyo wako umakhumba, ndi kukhutitsa moyo wovutidwa, pomwepo kuunika kwako kudzauka mumdima, ndipo usiku wako udzanga usana;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 82:3-4

Weruzani osauka ndi amasiye; weruzani molungama ozunzika ndi osowa.Pulumutsani osauka ndi aumphawi; alanditseni m'dzanja la oipa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Agalatiya 6:2

Nyamuliranani zothodwetsa, ndipo kotero mufitse chilamulo cha Khristu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 3:11

Koma iye anayankha nanena kwa iwo, Iye amene ali nao malaya awiri apatse kwa iye amene alibe; ndi iye amene ali nazo zakudya achite chomwecho.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 41:1-3

Wodala iye amene asamalira wosauka! Tsiku la tsoka Yehova adzampulumutsa.Yehova adzamsunga, nadzamsunga ndi moyo, ndipo adzadalitsika pa dziko lapansi, ndipo musampereke ku chifuniro cha adani ake.Yehova adzamgwiriziza pa kama wodwalira; podwala iye mukonza pogona pake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 12:13

Patsani zosowa oyera mtima; cherezani aulendo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 14:31

Wotsendereza aumphawi atonza Mlengi wake; koma wochitira wosauka chifundo amlemekeza.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Yohane 3:17-18

Koma iye amene ali nacho chuma cha dziko lapansi, naona mbale wake ali wosowa ndi kutsekereza chifundo chake pommana iye, nanga chikondi cha Mulungu chikhala mwa iye bwanji?Tiana, tisakonde ndi mau, kapena ndi lilime, komatu ndi kuchita ndi m'choonadi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 6:1-4

Yang'anirani kuti musachite zolungama zanu pamaso pa anthu kuti muonekere kwa iwo; pakuti ngati mutero mulibe mphotho ndi Atate wanu wa Kumwamba.Chifukwa chake pamene paliponse upatsa mphatso zachifundo, usamaomba lipenga patsogolo pako, monga amachita onyenga m'masunagoge, ndi m'makwalala, kotero kuti atamandidwe ndi anthu. Indetu ndinena kwa inu, Iwo alandiriratu mphotho zao.Koma iwe popatsa mphatso zachifundo, dzanja lako lamanzere lisadziwe chimene lichita dzanja lako lamanja;kotero kuti mphatso zako zachifundo zikhale zam'tseri; ndipo Atate wako wakuona m'tseri adzakubwezera iwe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yakobo 2:14-17

Chipindulo chake nchiyani, abale anga, munthu akanena, Ndili nacho chikhulupiriro, koma alibe ntchito? Kodi chikhulupirirocho chikhoza kumpulumutsa?Mbale kapena mlongo akakhala wausiwa, nichikamsowa chakudya cha tsiku lake,ndipo wina wa inu akanena nao, Mukani ndi mtendere, mukafunde ndi kukhuta; osawapatsa iwo zosowa za pathupi; kupindula kwake nchiyani?Momwemonso chikhulupiriro, chikapanda kukhala nacho ntchito, chikhala chakufa m'kati mwakemo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 10:33-34

Koma Msamariya wina ali pa ulendo wake anadza pali iye; ndipo pakumuona, anagwidwa chifundo,nadza kwa iye, namanga mabala ake, nathirapo mafuta ndi vinyo; ndipo anamuika iye pa nyama yake ya iye yekha, nadza naye kunyumba ya alendo, namsungira.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Machitidwe a Atumwi 20:35

M'zinthu zonse ndinakupatsani chitsanzo, chakuti pogwiritsa ntchito, kotero muyenera kuthandiza ofooka ndi kukumbuka mau a Ambuye Yesu, kuti anati yekha, Kupatsa kutidalitsa koposa kulandira.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Deuteronomo 15:7-8

Akakhala ndi inu munthu waumphawi, ndiye wina wa abale anu, m'umodzi wa midzi yanu, m'dziko limene Yehova Mulungu wanu akupatsani, musakhakala mtima wanu, kapena kuumitsa dzanja lanu kukaniza mbale wanu waumphawi;koma muzimtansira dzanja lanu ndithu ndi kumkongoletsa ndithu zofikira kusowa kwake, monga umo amasowa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 37:21

Woipa akongola, wosabweza, koma wolungama achitira chifundo, napereka.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Akorinto 9:6-7

Koma nditi ichi, kuti iye wakufesa mouma manja, mouma manjanso adzatuta. Ndipo iye wakufesa moolowa manja, moolowa manjanso adzatuta.Yense achite monga anatsimikiza mtima, si mwa chisoni kapena mokakamiza, pakuti Mulungu akonda wopereka mokondwerera.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 28:27

Wogawira aumphawi sadzasowa; koma wophimba maso ake adzatembereredwa kwambiri.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 58:6-7

Kodi kumeneku si kusala kudya kumene ndinakusankha: kumasula nsinga za zoipa, ndi kumasula zomanga goli, ndi kuleka otsenderezedwa amuke mfulu, ndi kuti muthyole magoli onse?Kodi si ndiko kupatsa chakudya chako kwa anjala, ndi kuti ubwere nao kunyumba kwako aumphawi otayika? Pakuona wamaliseche kuti umveke, ndi kuti usadzibisire wekha a chibale chako?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 5:42

Kwa iye wopempha iwe umpatse, ndipo kwa iye wofuna kukukongola usampotolokere.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 15:26-27

Pakuti kunakondweretsa a ku Masedoniya ndi Akaya kuchereza osauka a kwa oyera mtima a ku Yerusalemu.Pakuti kunakondweretsa iwo; ndiponso iwo ali amangawa ao. Pakuti ngati amitundu anagawana zinthu zao zauzimu, alinso amangawa akutumikira iwo ndi zinthu zathupi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 146:7-9

ndiye wakuchitira chiweruzo osautsika; ndiye wakupatsa anjala chakudya; Yehova amasula akaidi.Yehova apenyetsa osaona; Yehova aongoletsa onse owerama; Yehova akonda olungama.Yehova asunga alendo; agwiriziza mwana wamasiye ndi mkazi wamasiye; koma akhotetsa njira ya oipa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 14:13-14

Koma pamene ukonza phwando uitane aumphawi, opunduka, otsimphina, akhungu;ndipo udzakhala wodala; chifukwa iwo alibe chakubwezera iwe mphotho; pakuti idzabwezedwa mphotho pa kuuka kwa olungama.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Eksodo 22:25-27

Ukakongoletsa ndalama anthu anga osauka okhala nanu, usamkhalira ngati wangongole; usamwerengera phindu.Ukati ulandire chikole kaya chovala cha mnansi wako, koma polowa dzuwa uchibwezere kwa iye;popeza chofunda chake ndi ichi chokha, ndicho chovala cha pathupi pake; azifundira chiyani pogona? Ndipo kudzakhala kuti akandifuulira Ine, ndidzamva; pakuti Ine ndine wachisomo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 22:9

Mwini diso lamataya adzadala; pakuti apatsa osauka zakudya zake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Timoteyo 6:17-19

Lamulira iwo achuma m'nthawi yino ya pansi pano, kuti asadzikuze, kapena asayembekezere chuma chosadziwika kukhala kwake, koma Mulungu, amene atipatsa ife zonse kochulukira, kuti tikondwere nazo;kuti achite zabwino, nachuluke ndi ntchito zabwino, nakondwere kugawira ena, nayanjane;nadzikundikire okha maziko okoma ku nyengo ikudzayi, kuti akagwire moyo weniweniwo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:36

Lingitsani mtima wanga kumboni zanu, si ku chisiriro ai.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yakobo 1:27

Mapembedzedwe oyera ndi osadetsa pamaso pa Mulungu ndi Atate ndiwo: kucheza ndi ana amasiye ndi akazi amasiye m'chisautso chao, ndi kudzisungira mwini wosachitidwa mawanga ndi dziko lapansi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 112:5

Wodala munthu wakuchitira chifundo, nakongoletsa; adzalimbika nao mlandu wake poweruzidwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 10:42

Ndipo amene aliyense adzamwetsa mmodzi wa ang'ono awa chikho chokha cha madzi ozizira, pa dzina la wophunzira, indetu ndinena kwa inu, iye sadzataya mphotho yake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 58:7

Kodi si ndiko kupatsa chakudya chako kwa anjala, ndi kuti ubwere nao kunyumba kwako aumphawi otayika? Pakuona wamaliseche kuti umveke, ndi kuti usadzibisire wekha a chibale chako?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 31:20

Aolowera chikhato chake osauka; natambasulira aumphawi manja ake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 12:33-34

Gulitsani zinthu muli nazo, nimupatse mphatso zachifundo; mudzikonzere matumba a ndalama amene sakutha, chuma chosatha m'Mwamba, kumene mbala siziyandikira, ndipo njenjete siziononga.Pakuti kumene kuli chuma chanu, komweko kudzakhalanso mtima wanu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Deuteronomo 24:19-21

Mutasenga dzinthu zanu m'munda mwanu, ndipo mwaiwala mtolo m'mundamo, musabwererako kuutenga; ukhale wa mlendo, wa mwana wamasiye, ndi wa mkazi wamasiye; kuti Yehova Mulungu wanu akudalitseni m'ntchito zonse za manja anu. Mutagwedeza mtengo wanu wa azitona musayesenso nthambi mutatha nazo; akhale a mlendo, a mwana wamasiye, ndi a mkazi wamasiye.Mutatchera m'munda wanu wamphesa, musakunkha pambuyo panu; zikhale za mlendo, za mwana wamasiye, ndi za mkazi wamasiye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 12:10

M'chikondano cha anzanu wina ndi mnzake mukondane ndi chikondi chenicheni; mutsogolerane ndi kuchitira wina mnzake ulemu;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 24:1

Dziko lapansi nla Yehova ndi zodzala zake zomwe, dziko lokhalamo anthu ndi iwo okhala m'mwemo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mlaliki 11:1

Ponya zakudya zako pamadzi; udzazipeza popita masiku ambiri.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Akorinto 8:13-15

Pakuti sinditero kuti ena akamasuke, ndi inu musautsidwe;koma mwa kulingana kuchuluka kwanu kukwanire kusowa kwao nthawi ya makono ano, kutinso kuchuluka kwao kukwanire kusowa kwanu.Kuti pakhale chilingano; monga kwalembedwa, Wosonkhetsa chambiri sichinamtsalira; ndi iye wosonkhetsa pang'ono sichinamsowa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 7:12

Chifukwa chake zinthu zilizonse mukafuna kuti anthu achitire inu, inunso muwachitire iwo zotero; pakuti icho ndicho chilamulo ndi aneneri.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Agalatiya 2:10

pokhapo kuti tikumbukire aumphawi; ndicho chomwe ndinafulumira kuchichita.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 13:16

Koma musaiwale kuchitira chokoma ndi kugawira ena; pakuti nsembe zotere Mulungu akondwera nazo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 10:17-18

Yehova, mwamva chikhumbo cha ozunzika, mudzakhazikitsa mtima wao, mudzatchereza khutu lanu;kuti muweruze mlandu wa amasiye ndi wokhalira mphanthi, kuti munthu wa pa dziko lapansi angaonjeze kuopsa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 3:27

Oyenera kulandira zabwino usawamane; pokhoza dzanja lako kuwachitira zabwino.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 6:38

Patsani, ndipo kudzapatsidwa kwa inu; muyeso wabwino, wotsendereka, wokuchumuka, wosefukira, anthu adzakupatsani m'manja mwanu. Pakuti kudzayesedwa kwa inu ndi muyeso womwewo muyesa nao inu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Eksodo 23:10-11

Ndipo uzibzala m'munda mwako zaka zisanu ndi chimodzi, ndi kututa zipatso zako;koma chaka chachisanu ndi chiwiri uuleke, ugone; kuti aumphawi a anthu a mtundu wako adyemo, ndipo zotsalira nyama za kuthengo zizidye; momwemo uzichita ndi munda wako wamphesa, ndi munda wako wa azitona.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 146:9

Yehova asunga alendo; agwiriziza mwana wamasiye ndi mkazi wamasiye; koma akhotetsa njira ya oipa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 32:8

Koma mfulu aganizira zaufulu, nakhazikika m'zaufulu zomwe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Akorinto 9:8

Ndipo Mulungu akhoza kuchulukitsira chisomo chonse kwa inu; kuti inu, pokhala nacho chikwaniro chonse m'zinthu zonse, nthawi zonse, mukachulukire kuntchito yonse yabwino;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 5:16

Chomwecho muwalitse inu kuunika kwanu pamaso pa anthu, kuti pakuona ntchito zanu zabwino, alemekeze Atate wanu wa Kumwamba.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 13:10

Chikondano sichichitira mnzake choipa; chotero chikondanocho chili chokwanitsa lamulo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 69:33

Pakuti Yehova amvera aumphawi, ndipo sapeputsa am'ndende ake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 28:8

Wochulukitsa chuma chake, pokongoletsa ndi phindu, angokundikira yemwe achitira osauka chisoni.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Petro 4:10

monga yense walandira mphatso, mutumikirane nayo, ngati adindo okoma a chisomo cha mitundumitundu cha Mulungu;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 113:7-8

Amene autsa wosauka kumchotsa kufumbi, nakweza waumphawi kumchotsa kudzala.Kuti amkhalitse pamodzi ndi akulu, pamodzi ndi akulu a anthu ake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Deuteronomo 26:12-13

Mutatha kugawa magawo khumi, zobala zanu zonse chaka chachitatu, ndicho chaka chogawa magawo khumi, muzizipereka kwa Mlevi, kwa mlendo, kwa mwana wamasiye, ndi kwa mkazi wamasiye, kuti adye m'midzi mwanu, ndi kukhuta.Ndipo munene pamaso pa Yehova Mulungu wanu, Ndachotsa zopatulika m'nyumba mwanga, ndi kuzipereka kwa Mlevi, ndi kwa mlendo, ndi kwa mwana wamasiye, ndi kwa mkazi wamasiye, monga mwa lamulo lanu lonse munandilamulira ine; sindinalakwira malamulo anu, kapena kuwaiwala.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 58:9

Pamenepo udzaitana, ndipo Yehova adzayankha; udzafuula ndipo Iye adzati, Ndine pano. Ngati uchotsa pakati pa iwe goli, kukodolana moipa, ndi kulankhula moipa,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 25:40

Ndipo Mfumuyo idzayankha nidzati kwa iwo, Indetu ndinena kwa inu, Chifukwa munachitira ichi mmodzi wa abale anga, ngakhale ang'onong'ono awa, munandichitira ichi Ine.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 16:19

Kufatsa mtima ndi osauka kuposa kugawana zofunkha ndi onyada.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Agalatiya 6:9

Koma tisaleme pakuchita zabwino; pakuti pa nyengo yake tidzatuta tikapanda kufooka.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 15:1

Ndipo ife amene tili olimba tiyenera kunyamula zofooka za opanda mphamvu, ndi kusadzikondweretsa tokha.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Yohane 3:16-18

Umo tizindikira chikondi, popeza Iyeyu anapereka moyo wake chifukwa cha ife; ndipo ife tiyenera kupereka moyo wathu chifukwa cha abale.Koma iye amene ali nacho chuma cha dziko lapansi, naona mbale wake ali wosowa ndi kutsekereza chifundo chake pommana iye, nanga chikondi cha Mulungu chikhala mwa iye bwanji?Tiana, tisakonde ndi mau, kapena ndi lilime, komatu ndi kuchita ndi m'choonadi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 6:30

Munthu aliyense akakupempha kanthu, umpatse; ndi iye amene alanda zako, usazipemphanso.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Machitidwe a Atumwi 2:44-45

Ndipo onse akukhulupirira anali pamodzi, nakhala nazo zonse zodyerana.Ndipo zimene anali nazo, ndi chuma chao, anazigulitsa, nazigawira kwa onse, monga momwe yense anasowera.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 11:25

Mtima wa mataya udzalemera; wothirira madzi nayenso adzathiriridwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 41:17

Wosauka ndi wosowa afuna madzi, ndipo palibe, ndi lilime lao lilephera, chifukwa cha ludzu; Ine Yehova ndidzawayankha, Ine Mulungu wa Israele sindidzawasiya.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 12:5

Chifukwa cha kupasuka kwa ozunzika, chifukwa cha kuusa moyo kwa aumphawi, ndiuka tsopano, ati Yehova; ndidzamlonga mosungika muja alakalakamo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:69-70

Odzikuza anandipangira bodza: Ndidzasunga malangizo anu ndi mtima wanga wonse.Mtima wao unona ngati mafuta; koma ine ndikondwera nacho chilamulo chanu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 10:8

Chiritsani akudwala, ukitsani akufa, konzani akhate, tulutsani ziwanda: munalandira kwaulere, patsani kwaulere.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yakobo 2:15-16

Mbale kapena mlongo akakhala wausiwa, nichikamsowa chakudya cha tsiku lake,ndipo wina wa inu akanena nao, Mukani ndi mtendere, mukafunde ndi kukhuta; osawapatsa iwo zosowa za pathupi; kupindula kwake nchiyani?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 12:8

kapena iye wakudandaulira, kukudandaulirako; wakugawira achite ndi mtima woona; iye wakuweruza, aweruze ndi changu; iye wakuchita chifundo, achite ndi kukondwa mtima.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 18:22

Koma m'mene Yesu anamva, anati kwa iye, Usowa chinthu chimodzi: gulitsa zilizonse uli nazo, nugawire osauka; ndipo udzakhala nacho chuma chenicheni m'Mwamba; ndipo ukadze kuno, unditsate Ine.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 22:22-23

Usalande za waumphawi chifukwa ali waumphawi, ngakhale kutsendereza wosauka kubwalo.Pakuti Yehova adzanenera mlandu wao; omwe akwatula zao Iye adzakwatula moyo wao.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Machitidwe a Atumwi 10:4

Ndipo pompenyetsetsa iye ndi kuopa, anati, Nchiyani, Mbuye? Ndipo anati kwa iye, Mapemphero ako ndi zachifundo zako zinakwera zikhala chikumbutso pamaso pa Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 37:25

Ndinali mwana ndipo ndakalamba; ndipo sindinapenya wolungama wasiyidwa, kapena mbumba zake zilinkupempha chakudya.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Akorinto 9:11

polemeretsedwa inu m'zonse kukuolowa manja konse, kumene kuchita mwa ife chiyamiko cha kwa Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 5:7

Odala ali akuchitira chifundo; chifukwa adzalandira chifundo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 41:1

Wodala iye amene asamalira wosauka! Tsiku la tsoka Yehova adzampulumutsa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 58:11

ndipo Yehova adzakutsogolera posalekai, ndi kukhutitsa moyo wako m'chilala, ndi kulimbitsa mafupa ako; ndipo udzafanana ndi munda wothirira madzi, ndi kasupe wamadzi amene madzi ake saphwa konse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 21:13

Wotseka makutu ake polira waumphawi, nayenso adzalira koma osamvedwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 12:1-2

Chifukwa chake ndikupemphani inu, abale, mwa zifundo za Mulungu, kuti mupereke matupi anu nsembe yamoyo, yopatulika, yokondweretsa Mulungu, ndiko kupembedza kwanu koyenera.Ndipo musafanizidwe ndi makhalidwe a pansi pano: koma mukhale osandulika, mwa kukonzanso kwa mtima wanu, kuti mukazindikire chimene chili chifuno cha Mulungu, chabwino, ndi chokondweretsa, ndi changwiro.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Deuteronomo 15:10

Muzimpatsa ndithu, osawawa mtima wanu pompatsa; popeza, chifukwa cha ichi Yehova Mulungu wanu adzakudalitsani mu ntchito zanu zonse, ndi m'zonse muikapo dzanja lanu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 40:17

Ndipo ine ndine wozunzika ndi waumphawi; koma Ambuye andikumbukira ine. Inu ndinu mthandizi wanga, ndi Mpulumutsi wanga, musamachedwa, Mulungu wanga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 19:21

Yesu ananena naye, Ngati ufuna kukhala wangwiro, pita, kagulitse zomwe uli nazo, nupatse aumphawi, ndipo udzakhala ndi chuma Kumwamba; ndipo ukadze kuno, unditsate.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 29:7

Wolungama asamalira mlandu wa osauka; koma woipa alibe nzeru yakuudziwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Timoteyo 5:8

Koma ngati wina sadzisungiratu mbumba yake ya iye yekha, makamaka iwo a m'banja lake, wakana chikhulupiriro iye, ndipo aipa koposa wosakhulupirira.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 69:32-33

Ofatsa anachiona, nakondwera, ndipo inu, ofuna Mulungu, mtima wanu ukhale ndi moyo.Pakuti Yehova amvera aumphawi, ndipo sapeputsa am'ndende ake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Eksodo 22:21-24

Ndipo usasautsa mlendo kapena kumpsinja; pakuti munali alendo m'dziko la Ejipito.Musazunza mkazi wamasiye, kapena mwana wamasiye aliyense.Ukawazunza ndi kakuti konse, nakandilirira pang'ono ponse iwowa, ndidzamvadi kulira kwao;ndi mkwiyo wanga idzayaka, ndipo ndidzapha inu ndi lupanga; ndipo akazi anu adzakhala amasiye, ndi ana anu omwe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 107:9

Pakuti akhutitsa mtima wolakalaka, nadzaza mtima wanjala ndi zabwino.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 58:3

Amati, Bwanji ife tasala kudya, ndipo Inu simuona? Ndi bwanji ife tavutitsa moyo wathu, ndipo Inu simusamalira? Taonani, tsiku la kusala kudya kwanu inu mupeza kukondwerera kwanu, ndi kutsendereza antchito anu onse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 22:39

Ndipo lachiwiri lolingana nalo ndili, Uzikonda mnzako monga udzikonda iwe mwini.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 15:17

Kudya masamba, pali chikondano, kuposa ng'ombe yonenepa pali udani.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 84:11

Pakuti Yehova Mulungu ndiye dzuwa ndi chikopa; Yehova adzapatsa chifundo ndi ulemerero; sadzakaniza chokoma iwo akuyenda angwiro.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Agalatiya 6:10

Chifukwa chake, monga tili nayo nyengo, tichitire onse chokoma, koma makamaka iwo a pa banja la chikhulupiriro.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 112:9

Anagawagawa, anapatsa aumphawi; chilungamo chake chikhalitsa kosatha; nyanga yake idzakwezeka ndi ulemu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 21:26

Ena asirira modukidwa tsiku lonse; koma wolungama amapatsa osamana.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Eksodo 20:17

Usasirire nyumba yake ya mnzako, usasirire mkazi wake wa mnzako, kapena wantchito wake wa mwamuna, kapena wantchito wake wamkazi, kapena ng'ombe yake, kapena bulu wake, kapena kanthu kalikonse ka mnzako.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 106:4

Mundikumbukire, Yehova, monga momwe muvomerezana ndi anthu anu; mundionetsa chipulumutso chanu:

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 6:33

Koma muthange mwafuna Ufumu wake ndi chilungamo chake, ndipo zonse zimenezo zidzaonjezedwa kwa inu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 13:1-2

Chikondi cha pa abale chikhalebe.Musaiwale kuchereza alendo; pakuti mwa ichi ena anachereza angelo osachidziwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 25:4

Chifukwa Inu mwakhala linga la aumphawi, linga la osowa m'kuvutidwa kwake, pobisalira chimphepo, mthunzi wa pa dzuwa, pamene kuomba kwa akuopsa kufanana ndi chimphepo chakuomba tchemba.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 136:1-3

Yamikani Yehova pakuti ndiye wabwino; pakuti chifundo chake nchosatha.Yamikani Mulungu wa milungu; pakuti chifundo chake nchosatha.Yamikani Mbuye wa ambuye; pakuti chifundo chake nchosatha.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 82:3

Weruzani osauka ndi amasiye; weruzani molungama ozunzika ndi osowa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 61:1-3

Mzimu wa Ambuye Yehova uli pa ine; pakuti Yehova wandidzoza ine ndilalikire mau abwino kwa ofatsa; Iye wanditumiza ndikamange osweka mtima, ndikalalikire kwa am'nsinga mamasulidwe, ndi kwa omangidwa kutsegulidwa kwa m'ndende;ndikalalikire chaka chokomera Yehova, ndi tsiku lakubwezera la Mulungu wathu; ndikatonthoze mtima wa onse amene akulira maliro;ndikakonzere iwo amene alira maliro m'Ziyoni, ndi kuwapatsa chovala kokometsa m'malo mwa phulusa, mafuta akukondwa m'malo mwa maliro, chovala cha matamando m'malo mwa mzimu wopsinjika; kuti iwo atchedwe mitengo ya chilungamo yakuioka Yehova, kuti Iye alemekezedwe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 41:2

Yehova adzamsunga, nadzamsunga ndi moyo, ndipo adzadalitsika pa dziko lapansi, ndipo musampereke ku chifuniro cha adani ake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 18:5

Ndipo amene adzalandira kamwana kamodzi kotereka chifukwa cha dzina langa, alandira Ine;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 72:12-14

Pakuti adzapulumutsa waumphawi wofuulayo; ndi wozunzika amene alibe mthandizi.Adzachitira nsoni wosauka ndi waumphawi, nadzapulumutsa moyo wa aumphawi.Adzaombola moyo wao ku chinyengo ndi chiwawa; ndipo mwazi wao udzakhala wa mtengo pamaso pake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Deuteronomo 10:18

Aweruzira ana amasiye ndi mkazi wamasiye; ndipo akonda mlendo, ndi kumpatsa chakudya ndi chovala.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 147:9

Amene apatsa zoweta chakudya chao, ana a khungubwi alikulira.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 10:37

Ndipo anati, Iye wakumchitira chifundo. Ndipo Yesu anati kwa iye, Pita nuchite iwe momwemo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 56:10-11

Alonda ake ali akhungu, iwo onse ali opanda nzeru; iwo onse ali agalu achete, osatha kuuwa; kungolota, kugona pansi, kukonda kugona tulo.Inde agalu ali osusuka, sakhuta konse; amenewa ali abusa osazindikira; iwo onse atembenukira kunjira zao, yense kutsata phindu lake m'dera lake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 145:9

Yehova achitira chokoma onse; ndi nsoni zokoma zake zigwera ntchito zake zonse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 68:5

Mulungu, mokhala mwake moyera, ndiye Atate wa ana amasiye, ndi woweruza wa akazi amasiye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 12:15

Kondwani nao iwo akukondwera; lirani nao akulira.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 86:5

Pakuti Inu, Ambuye, ndinu wabwino, ndi wokhululukira, ndi wa chifundo chochulukira onse akuitana Inu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Machitidwe a Atumwi 4:32-35

Ndipo unyinji wa iwo akukhulupirira anali wa mtima umodzi ndi moyo umodzi; ndipo sananena mmodzi kuti kanthu ka chuma anali nacho ndi kake ka iye yekha; koma anali nazo zonse zodyerana.Ndipo atumwi anachita umboni ndi mphamvu yaikulu za kuuka kwa Ambuye Yesu; ndipo panali chisomo chachikulu pa iwo onse.Pakuti mwa iwo munalibe wosowa; pakuti onse amene anali nayo minda, kapena nyumba, anazigulitsa nabwera nao malonda ake a izo adazigulitsa,nawaika pa mapazi a atumwi; ndipo anagawira yense monga kusowa kwake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 58:7-8

Kodi si ndiko kupatsa chakudya chako kwa anjala, ndi kuti ubwere nao kunyumba kwako aumphawi otayika? Pakuona wamaliseche kuti umveke, ndi kuti usadzibisire wekha a chibale chako?Pomwepo kuunika kwako kudzawalitsa monga m'mawa, ndi kuchira kwako kudzaonekera msangamsanga; ndipo chilungamo chako chidzakutsogolera; ulemerero wa Yehova udzakhala wotchinjiriza pambuyo pako.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 11:24

Alipo wogawira, nangolemerabe; aliponso womana chomwe ayenera kupatsa nangosauka.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:132

Munditembenukire, ndi kundichitira chifundo, monga mumatero nao akukonda dzina lanu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 6:1

Yang'anirani kuti musachite zolungama zanu pamaso pa anthu kuti muonekere kwa iwo; pakuti ngati mutero mulibe mphotho ndi Atate wanu wa Kumwamba.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 130:7

Israele, uyembekezere Yehova; chifukwa kwa Yehova kuli chifundo, kwaonso kuchulukira chiombolo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 146:6

Amene analenga zakumwamba ndi dziko lapansi, nyanja ndi zonse zili m'mwemo. Ndiye wakusunga choonadi kosatha,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 113:7

Amene autsa wosauka kumchotsa kufumbi, nakweza waumphawi kumchotsa kudzala.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Afilipi 2:4

munthu yense asapenyerere zake za iye yekha, koma yense apenyererenso za mnzake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 116:5-6

Yehova ngwa chifundo ndi wolungama; ndi Mulungu wathu ngwa nsoni.Yehova asunga opusa; ndidafooka ine, koma anandipulumutsa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 68:10

Gulu lanu linakhala m'dziko muja. Mwa ukoma wanu munalikonzera ozunzika, Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 12:14

Munthu amakhuta zabwino ndi zipatso za m'kamwa mwake; zochita za manja ake zidzabwezedwa kwa iye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Yohane 3:17

Koma iye amene ali nacho chuma cha dziko lapansi, naona mbale wake ali wosowa ndi kutsekereza chifundo chake pommana iye, nanga chikondi cha Mulungu chikhala mwa iye bwanji?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 125:4

Chitirani chokoma, Yehova, iwo okhala okoma; iwo okhala oongoka mumtima mwao.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 15:25-27

Koma tsopano ndipita ku Yerusalemu, ndilikutumikira oyera mtima.Pakuti kunakondweretsa a ku Masedoniya ndi Akaya kuchereza osauka a kwa oyera mtima a ku Yerusalemu.Pakuti kunakondweretsa iwo; ndiponso iwo ali amangawa ao. Pakuti ngati amitundu anagawana zinthu zao zauzimu, alinso amangawa akutumikira iwo ndi zinthu zathupi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 29:14

Mfumu yolamulira osauka mwantheradi, mpando wake udzakhazikika kufikira nthawi zonse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Machitidwe a Atumwi 10:31

nati Kornelio, lamveka pemphero lako, ndi zopereka zachifundo zako zakumbukika pamaso pa Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 72:4

Adzaweruza ozunzika a mwa anthu, adzapulumutsa ana aumphawi, nadzaphwanya wosautsa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 14:19

Chifukwa chake tilondole zinthu za mtendere, ndi zinthu zakulimbikitsana wina ndi mnzake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 133:1-2

Onani, nkokoma ndi kokondweretsa ndithu kuti abale akhale pamodzi!Ndiko ngati mafuta a mtengo wake pamutu, akutsikira kundevu, inde kundevu za Aroni; akutsikira kumkawo wa zovala zake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Agalatiya 6:1

Abale, ngatinso munthu agwidwa nako kulakwa kwakuti, inu auzimu, mubweze wotereyo mu mzimu wa chifatso; ndi kudzipenyerera wekha, ungayesedwe nawenso.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 116:1-2

Ndimkonda, popeza Yehova amamva mau anga ndi kupemba kwanga.Popeza amanditcherera khutu lake, chifukwa chake ndidzaitanira Iye masiku anga onse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 103:1-5

Lemekeza Yehova, moyo wanga; ndi zonse za m'kati mwanga zilemekeze dzina lake loyera.Lemekeza Yehova, moyo wanga, ndi kusaiwala zokoma zake zonse atichitirazi:Amene akhululukira mphulupulu zako zonse; nachiritsa nthenda zako zonse;amene aombola moyo wako ungaonongeke; nakuveka korona wa chifundo ndi nsoni zokoma:Amene akhutitsa m'kamwa mwako ndi zabwino; nabweza ubwana wako unge mphungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani

Pemphero kwa Mulungu

Ambuye, inu ndinu Alfa ndi Omega! Atate, Mlengi wa thambo ndi dziko lapansi, ndinu woyamba ndi wotsiriza, chiyambi ndi chitsiriziro. Ndikubwera kwa inu kudzera mwa Ambuye wanga Yesu Khristu, ndikupempha kuti muteteze ndi kulimbitsa moyo wa mnzanga, mupatseni nzeru ndi luntha kuti asankhe zinthu zabwino, kuti ayende m'cholinga chimene munamupangira. Mulimbitseni, mutsitsimutseni mphamvu zake ndipo molimbikira mulimbitse chikhulupiriro chake, kotero kuti kukhalapo kwa Mzimu Woyera wanu kukhale patsogolo pa moyo wake ndi banja lake. Mawu anu amati: "Pakuti adzatumiza angelo ake kukutetezani m'njira zako zonse." Ambuye, pitirizani kumupatsa zonse zomfunika, mupatseni nzeru ndi kulimba mtima kuti agonjetse mantha ake ndipo athe kupambana mavuto aliwonse omwe akukumana nawo. Ndikulengeza kuti mukupita patsogolo pake ngati chimphona champhamvu, mukulimbana nkhondo zake zonse. Mumuteteze ku ziwembu zonse ndi misampha ya mdani. Zikomo, Ambuye, ulemerero ndi ulemu zonse zikhale kwa inu. M'dzina la Yesu. Ameni!
Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa