Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Numeri 6:25 - Buku Lopatulika

Yehova awalitse nkhope yake pa iwe, nakuchitire chisomo;

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Yehova awalitse nkhope yake pa iwe, nakuchitire chisomo;

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Chauta akuyang'aneni mwachikondi ndipo akukomereni mtima.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yehova awalitse nkhope yake pa iwe, nakuchitira chisomo;

Onani mutuwo



Numeri 6:25
15 Mawu Ofanana  

Ndipo iye anatukula maso ake naona Benjamini mphwake, mwana wa amake, nati, Kodi uyu ndi mphwanu wamng'ono uja, amene munanena ndi ine uja? Ndipo iye anati, Mulungu akuchitire iwe ufulu, mwana wanga.


Muwalitse nkhope yanu pa mtumiki wanu; ndipo mundiphunzitse malemba anu.


Pakuti mumuikira madalitso kunthawi zonse; mumkondweretsa ndi chimwemwe pankhope panu.


Walitsani nkhope yanu pa mtumiki wanu, mundipulumutse ndi chifundo chanu.


Mwapatsa chimwemwe mumtima mwanga, chakuposa chao m'nyengo yakuchuluka dzinthu zao ndi vinyo wao.


Atichitire chifundo Mulungu, ndi kutidalitsa, atiwalitsire nkhope yake;


Mutibweze, Yehova Mulungu wa makamu; nimuwalitse nkhope yanu, ndipo tidzapulumuka.


Mulungu wa makamu, mutibweze; nimuwalitse nkhope yanu, ndipo tidzapulumuka.


Mundibwerere ine, ndi kundichitira chifundo; mpatseni mtumiki wanu mphamvu yanu, ndipo pulumutsani mwana wa mdzakazi wanu.


Ndipo Iye anati, Ndidzapititsa ukoma wanga wonse pamaso pako, ndipo ndidzatchula dzina la Yehova pamaso pako; ndipo ndidzachitira ufulu amene ndidzamchitira ufulu; ndi kuchitira chifundo amene ndidzamchitira chifundo.


Ndipo tsopano, Mulungu wathu, mumvere pemphero la mtumiki wanu, ndi mapembedzero ake, nimuwalitse nkhope yanu pamalo anu opatulika amene ali opasuka, chifukwa cha Ambuye.


Ndipo tsopano, mupepeze Mulungu, kuti atichitire chifundo; ichicho chichokera kwa inu; kodi Iye adzavomereza ena a inu? Ati Yehova wa makamu.


Chifukwa chilamulo chinapatsidwa mwa Mose; chisomo ndi choonadi zinadza mwa Yesu Khristu.


kwa onse a ku Roma, okondedwa a Mulungu, oitanidwa kuti akhale oyera mtima: Chisomo chikhale ndinu ndi mtendere wa kwa Mulungu Atate wathu, ndi Ambuye Yesu Khristu.