Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Danieli 9:17 - Buku Lopatulika

17 Ndipo tsopano, Mulungu wathu, mumvere pemphero la mtumiki wanu, ndi mapembedzero ake, nimuwalitse nkhope yanu pamalo anu opatulika amene ali opasuka, chifukwa cha Ambuye.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

17 Ndipo tsopano, Mulungu wathu, mumvere pemphero la mtumiki wanu, ndi mapembedzero ake, nimuwalitse nkhope yanu pa malo anu opatulika amene ali opasuka, chifukwa cha Ambuye.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

17 “Tsopano Mulungu wathu, imvani mapemphero ndi zopempha za mtumiki wanu. Kuti anthu onse akudziweni kuti ndinu Ambuye, komerani mtima malo anu opatulika amene asanduka bwinja.

Onani mutuwo Koperani




Danieli 9:17
20 Mawu Ofanana  

Koma mucheukire pemphero la kapolo wanu, ndi pembedzero lake, Yehova Mulungu wanga, kumvera kulira ndi kupempha kwake kumene kapolo wanu apempha pamaso panu lero;


mutchere khutu, ndi maso anu atseguke kumvera pemphero la kapolo wanu, ndilipempha pamaso panu tsopano apa msana ndi usiku, kupempherera ana a Israele akapolo anu, ndi kuwulula zoipa za ana a Israele zimene tachimwira nazo Inu; inde tachimwa, ine ndi nyumba ya atate wanga.


Muwalitse nkhope yanu pa mtumiki wanu; ndipo mundiphunzitse malemba anu.


Ambiri amati, Adzationetsa chabwino ndani? Weramutsirani ife kuunika kwa nkhope yanu, Yehova.


Atichitire chifundo Mulungu, ndi kutidalitsa, atiwalitsire nkhope yake;


kuti njira yanu idziwike padziko lapansi, chipulumutso chanu mwa amitundu onse.


Nyamulani mapazi anu kukapenya mapasukidwe osatha, zoipa zonse adazichita mdani m'malo opatulika.


Mbusa wa Israele, tcherani khutu; inu wakutsogolera Yosefe ngati nkhosa; inu wokhala pa akerubi, walitsani.


Mutibweze, Yehova Mulungu wa makamu; nimuwalitse nkhope yanu, ndipo tidzapulumuka.


Mutibweze, Mulungu; nimuwalitse nkhope yanu, ndipo tidzapulumuka.


Yehova, Mulungu wa makamu, mudzakwiyira pemphero la anthu anu kufikira liti?


Mulungu wa makamu, mutibweze; nimuwalitse nkhope yanu, ndipo tidzapulumuka.


Chifukwa cha Ine ndekha, chifukwa cha Ine ndekha ndidzachita ichi, pakuti dzina langa lidetsedwerenji? Ndi ulemerero wanga sindidzaupereka kwa wina.


munamva mau anga; musabise khutu lanu popuma ndi pofuula ine.


paphiri la Ziyoni lopasukalo ankhandwe ayendapo.


Ambuye, imvani; Ambuye khululukirani; Ambuye, mverani nimuchite; musachedwa, chifukwa cha inu nokha, Mulungu wanga; pakuti mzinda wanu ndi anthu anu anatchedwa dzina lanu.


Kufikira tsopano simunapemphe kanthu m'dzina langa; pemphani, ndipo mudzalandira, kuti chimwemwe chanu chikwaniridwe.


Pakuti monga mawerengedwe a malonjezano a Mulungu ali mwa Iye eya; chifukwa chakenso ali mwa Iye Amen, kwa ulemerero wa Mulungu mwa ife.


Ndipo pamzinda sipafunika dzuwa, kapena mwezi wakuuwalira; pakuti ulemerero wa Mulungu uunikira umenewu, ndipo nyali yake ndiye Mwanawankhosa.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa