Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 92:4 - Buku Lopatulika

Popeza Inu, Yehova, munandikondweretsa ndi kuchita kwanu, ndidzafuula mokondwera pa ntchito ya manja anu.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Popeza Inu, Yehova, munandikondweretsa ndi kuchita kwanu, ndidzafuula mokondwera pa ntchito ya manja anu.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Inu Chauta, mwandisangalatsa ndi ntchito zanu. Motero ndikufuula ndi chimwemwe chifukwa cha zimene Inu mwachita.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Pakuti Inu mumandisangalatsa ndi ntchito zanu, Inu Yehova; Ine ndikuyimba mwachimwemwe pa ntchito ya manja anu.

Onani mutuwo



Masalimo 92:4
20 Mawu Ofanana  

Ulemerero wa Yehova ukhale kosatha; Yehova akondwere mu ntchito zake;


Pomlingirira Iye pandikonde; ndidzakondwera mwa Yehova.


Yehova anatichitira ife zazikulu; potero tikhala okondwera.


Ndikumbukira masiku a kale lomwe; zija mudazichita ndilingirirapo; ndikamba pandekha za ntchito ya manja anu.


Yamikani Yehova ndi zeze; muimbireni ndi chisakasa cha zingwe khumi.


Wolungama adzakondwera mwa Yehova, nadzakhulupirira Iye; ndipo oongoka mtima onse adzalemekeza.


Munamchititsa ufumu pa ntchito za manja anu; mudagonjetsa zonse pansi pa mapazi ake;


Chochita Inu chioneke kwa atumiki anu, ndi ulemerero wanu pa ana ao.


Pakuti Yehova atero, Imbirani Yakobo ndi kukondwa, fuulirani mtundu woposawo; lalikirani, yamikirani, ndi kuti, Yehova, mupulumutse anthu anu, ndi otsala a Israele.


ndipo mzimu wanga wakondwera mwa Mulungu Mpulumutsi wanga,


Ndipo inu tsono muli nacho chisoni tsopano lino, koma ndidzakuonaninso, ndipo mtima wanu udzakondwera, ndipo palibe wina adzachotsa kwa inu chimwemwe chanu.


Koma ayamikike Mulungu, amene atitsogolera m'chigonjetso mwa Khristu, namveketsa fungo la chidziwitso chake mwa ife pamalo ponse.


Kondwera pa iye, m'mwamba iwe, ndi oyera mtima, ndi atumwi, ndi aneneri inu; chifukwa Mulungu anauweruzira kuweruzidwa kwanu.