Mavesi a Baibulo

Zotsatsa


Gulu Laling'ono

104 Mau a m'Baibulo Okhudza Kulamulira Mkwiyo

Ndikakhala ndi mtendere wa Mulungu mumtima mwanga, palibe malo a maganizo oipa. Ukali uli ndi mphamvu yowononga kulankhulana, kusokoneza ubale, komanso kusokoneza chimwemwe ndi thanzi la anthu ambiri.

N’zomvetsa chisoni kuti nthawi zambiri anthufe timapeza zifukwa zotsimikizira ukali wathu m’malo motenga udindo. Komabe, tingathe kuugonjetsa ukaliwu motsatira mfundo za m’Baibulo, poona Mulungu pakati pa mayesero, kupemphera nthawi zonse, ndi kudzipereka kwa Iye.

Mawu a Mulungu amatilimbikitsa kuti tione mayesero osiyanasiyana ngati chifukwa chachikulu cha chimwemwe, podziwa kuti mayesero a chikhulupiriro chathu amabala chipiriro. Ndipo chipirirocho chizigwira ntchito yake yonse mwa ife, kuti tikule bwino m’zonse, osasowa kanthu kalili konse (Yakobo 1:2-4).


Aefeso 4:26-27

Kwiyani, koma musachimwe; dzuwa lisalowe muli chikwiyire,

ndiponso musampatse malo mdierekezi.

Mutu    |  Mabaibulo
Aefeso 4:31

Chiwawo chonse, ndi kupsa mtima, ndi mkwiyo, ndi chiwawa, ndi mwano zichotsedwe kwa inu, ndiponso choipa chonse.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 11:23

Chifuniro cha olungama chifikitsa zabwino zokha; koma chiyembekezo cha oipa mkwiyo.

Mutu    |  Mabaibulo
Mlaliki 7:9

Usakangaze mumtima mwako kukwiya; pakuti mkwiyo ugona m'chifuwa cha zitsiru.

Mutu    |  Mabaibulo
Aefeso 4:31-32

Chiwawo chonse, ndi kupsa mtima, ndi mkwiyo, ndi chiwawa, ndi mwano zichotsedwe kwa inu, ndiponso choipa chonse.

Koma mukhalirane okoma wina ndi mnzake, a mtima wachifundo, akukhululukirana nokha, monganso Mulungu mwa Khristu anakhululukira inu.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 16:32

Wosakwiya msanga aposa wamphamvu; wolamulira mtima wake naposa wolanda mudzi.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 37:8

Leka kupsa mtima, nutaye mkwiyo; usavutike mtima ungachite choipa.

Mutu    |  Mabaibulo
Yakobo 1:19-20

Mudziwa, abale anga okondedwa, kuti munthu aliyense akhale wotchera khutu, wodekha polankhula, wodekha pakupsa mtima.

Muchiyese chimwemwe chokha, abale anga, m'mene mukugwa m'mayesero a mitundumitundu;

Pakuti mkwiyo wa munthu suchita chilungamo cha Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 15:1

Mayankhidwe ofatsa abweza mkwiyo; koma mau owawitsa aputa msunamo.

Mutu    |  Mabaibulo
Mlaliki 11:10

Chifukwa chake chotsani zopweteka m'mtima mwako, nulekanitse zoipa ndi thupi lako; pakuti ubwana ndi unyamata ngwa chabe.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 14:29

Wosakwiya msanga apambana kumvetsa; koma wansontho akuza utsiru.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 29:11

Chitsiru chivumbulutsa mkwiyo wake wonse; koma wanzeru auletsa nautontholetsa.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 15:18

Munthu wozaza aputa makani; koma wosakwiya msanga atonthoza makangano.

Mutu    |  Mabaibulo
2 Timoteyo 2:23-24

Koma mafunso opusa ndi opanda malango upewe, podziwa kuti abala ndeu.

Ndipo kapolo wa Ambuye sayenera kuchita ndeu, komatu akhale woyenera, waulere pa onse, wodziwa kuphunzitsa, woleza,

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 19:11

Kulingalira kwa munthu kuchedwetsa mkwiyo; ulemerero wake uli wakuti akhululukire cholakwa.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 19:19

Munthu waukali alipire mwini; pakuti ukampulumutsa udzateronso.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 20:3

Kuli ulemu kwa mwamuna kupewa ndeu; koma zitsiru zonse zimangokangana.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 17:27

Wopanda chikamwakamwa apambana kudziwa; ndipo wofatsa mtima ali wanzeru.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 21:23

Wosunga m'kamwa mwake ndi lilime lake asunga moyo wake kumavuto.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 22:24-25

Usayanjane ndi munthu wokwiya msanga; ngakhale kupita ndi mwamuna waukali;

kuti ungaphunzire mayendedwe ake, ndi kutengera moyo wako msampha.

Mutu    |  Mabaibulo
Aefeso 4:26

Kwiyani, koma musachimwe; dzuwa lisalowe muli chikwiyire,

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 25:28

Wosalamulira mtima wake akunga mudzi wopasuka wopanda linga.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 29:22

Mwamuna wamkwiyo aputa makangano; waukali achuluka zolakwa.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 5:22

koma Ine ndinena kwa inu, kuti yense wokwiyira mbale wake wopanda chifukwa adzakhala wopalamula mlandu; ndipo amene adzanena ndi mbale wake, Wopanda pake iwe, adzakhala wopalamula mlandu wa akulu: koma amene adzati, Chitsiru iwe: adzakhala wopalamula Gehena wamoto.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 5:44

koma Ine ndinena kwa inu, Kondanani nao adani anu, ndi kupempherera iwo akuzunza inu;

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 6:14-15

Pakuti ngati mukhululukira anthu zolakwa zao adzakhululukira inunso Atate wanu wa Kumwamba.

Koma ngati simukhululukira anthu zolakwa zao, Atate wanunso sadzakhululukira zolakwa zanu.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 7:12

Chifukwa chake zinthu zilizonse mukafuna kuti anthu achitire inu, inunso muwachitire iwo zotero; pakuti icho ndicho chilamulo ndi aneneri.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 18:21-22

Pamenepo Petro anadza, nati kwa Iye, Ambuye, mbale wanga adzandilakwira kangati, ndipo ine ndidzamkhululukira iye? Kufikira kasanu ndi kawiri kodi?

Yesu ananena kwa iye, Sindinena kwa iwe kufikira kasanu ndi kawiri, koma kufikira makumi asanu ndi awiri kubwerezedwa kasanu ndi kawiri.

Mutu    |  Mabaibulo
Marko 11:25

Ndipo pamene muimirira ndi kupemphera, khululukirani, ngati munthu wakulakwirani kanthu; kuti Atate wanunso ali Kumwamba akhululukire inu zolakwa zanu.

Mutu    |  Mabaibulo
Luka 6:27-28

Koma ndinena kwa inu akumva, Kondanani nao adani anu; chitirani zabwino iwo akuda inu,

dalitsani iwo akutemberera inu, pemphererani iwo akuchitira inu chipongwe.

Mutu    |  Mabaibulo
Luka 6:31

Ndipo monga mufuna inu kuti anthu adzakuchitirani inu, muwachitire iwo motero inu momwe.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 12:17-19

Musabwezere munthu aliyense choipa chosinthana ndi choipa. Ganiziranitu zinthu za ulemu pamaso pa anthu onse.

Ngati nkutheka, monga momwe mukhoza, khalani ndi mtendere ndi anthu onse.

Musabwezere choipa, okondedwa, koma patukani pamkwiyo; pakuti kwalembedwa, Kubwezera kuli kwanga, Ine ndidzabwezera, ati Ambuye.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 12:21

Musagonje kwa choipa, koma ndi chabwino gonjetsani choipa.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 13:10

Chikondano sichichitira mnzake choipa; chotero chikondanocho chili chokwanitsa lamulo.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Akorinto 13:4-5

Chikondi chikhala chilezere, chili chokoma mtima; chikondi sichidukidwa; chikondi sichidziwa kudzitamanda, sichidzikuza,

sichichita zosayenera, sichitsata za mwini yekha, sichipsa mtima, sichilingirira zoipa;

Mutu    |  Mabaibulo
2 Akorinto 10:3-5

Pakuti pakuyendayenda m'thupi, sitichita nkhondo monga mwa thupi,

(pakuti zida za nkhondo yathu sizili za thupi, koma zamphamvu mwa Mulungu zakupasula malinga);

ndi kugwetsa matsutsano, ndi chokwezeka chonse chimene chidzikweza pokana chidziwitso cha Mulungu, ndi kugonjetsa ganizo lonse kukumvera kwa Khristu;

Mutu    |  Mabaibulo
Agalatiya 5:19-21

Ndipo ntchito za thupi zionekera, ndizo dama, chodetsa, kukhumba zonyansa,

Taonani, ine Paulo ndinena ndi inu, kuti, ngati mulola akuduleni, Khristu simudzapindula naye kanthu.

kupembedza mafano, nyanga, madano, ndeu, kaduka, zopsa mtima, zotetana, magawano, mipatuko,

njiru, kuledzera, mchezo, ndi zina zotere; zimene ndikuchenjezani nazo, monga ndachita, kuti iwo akuchitachita zotere sadzalowa Ufumu wa Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo
Agalatiya 5:22-23

Koma chipatso cha Mzimu ndicho chikondi, chimwemwe, mtendere, kuleza mtima, chifundo, kukoma mtima, chikhulupiriro,

chifatso, chiletso; pokana zimenezi palibe lamulo.

Mutu    |  Mabaibulo
Aefeso 4:32

Koma mukhalirane okoma wina ndi mnzake, a mtima wachifundo, akukhululukirana nokha, monganso Mulungu mwa Khristu anakhululukira inu.

Mutu    |  Mabaibulo
Aefeso 5:1-2

Chifukwa chake khalani akutsanza a Mulungu, monga ana okondedwa;

kuyesera chokondweretsa Ambuye nchiyani;

ndipo musayanjane nazo ntchito za mdima zosabala kanthu, koma makamakanso muzitsutse;

pakuti zochitidwa nao m'tseri, kungakhale kuzinena kuchititsa manyazi.

Koma zinthu zonse potsutsika ndi kuunika, zionekera; pakuti chonse chakuonetsa chili kuunika.

Mwa ichi anena, Khala maso wogona iwe, nuuke kwa akufa, ndipo Khristu adzawala pa iwe.

Potero, penyani bwino umo muyendera, si monga opanda nzeru, koma monga anzeru;

akuchita machawi, popeza masiku ali oipa.

Chifukwa chake musakhale opusa, koma dziwitsani chifuniro cha Ambuye nchiyani.

Ndipo musaledzere naye vinyo, m'mene muli chitayiko; komatu mudzale naye Mzimu,

ndi kudzilankhulira nokha ndi masalmo, ndi mayamiko, ndi nyimbo zauzimu, kuimbira ndi kuimba m'malimba Ambuye mumtima mwanu;

ndipo yendani m'chikondi monganso Khristu anakukondani inu, nadzipereka yekha m'malo mwathu, chopereka ndi nsembe kwa Mulungu, ikhale fungo lonunkhira bwino.

Mutu    |  Mabaibulo
Afilipi 2:3-4

musachite kanthu monga mwa chotetana, kapena monga mwa ulemerero wopanda pake, komatu ndi kudzichepetsa mtima, yense ayese anzake omposa iye mwini;

pakuti chifukwa cha ntchito ya Khristu anafikira pafupi imfa, wosasamalira moyo wake, kuti akakwaniritse chiperewero cha utumiki wanu wa kwa ine.

munthu yense asapenyerere zake za iye yekha, koma yense apenyererenso za mnzake.

Mutu    |  Mabaibulo
Akolose 3:8

Koma tsopano tayani inunso zonsezi: mkwiyo, kupsa mtima, dumbo, mwano, zonyansa zotuluka m'kamwa mwanu:

Mutu    |  Mabaibulo
Akolose 3:12-13

Chifukwa chake valani, monga osankhika a Mulungu, oyera mtima ndi okondedwa, mtima wachifundo, kukoma mtima, kudzichepetsa, chifatso, kuleza mtima;

kulolerana wina ndi mnzake, ndi kukhululukirana eni okha, ngati wina ali nacho chifukwa pa mnzake; monganso Ambuye anakhululukira inu, teroni inunso;

Mutu    |  Mabaibulo
Akolose 3:15

Ndipo mtendere wa Khristu uchite ufumu m'mitima yanu, kulingakonso munaitanidwa m'thupi limodzi; ndipo khalani akuyamika.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Atesalonika 5:15

Penyani kuti wina asabwezere choipa womchitira choipa; komatu nthawi zonse mutsatire chokoma, kwa anzanu, ndi kwa onse.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Timoteyo 2:8

Chifukwa chake ndifuna kuti amunawo apemphere pamalo ponse, ndi kukweza manja oyera, opanda mkwiyo ndi makani.

Mutu    |  Mabaibulo
2 Timoteyo 2:24-25

Ndipo kapolo wa Ambuye sayenera kuchita ndeu, komatu akhale woyenera, waulere pa onse, wodziwa kuphunzitsa, woleza,

wolangiza iwo akutsutsana mofatsa; ngati kapena Mulungu awapatse iwo chitembenuziro, kukazindikira choonadi,

Mutu    |  Mabaibulo
Tito 3:2

asachitire mwano munthu aliyense, asakhale andeu, akhale aulere, naonetsere chifatso chonse pa anthu onse.

Mutu    |  Mabaibulo
Ahebri 10:30

pakuti timdziwa Iye amene anati, Kubwezera chilango nkwanga, Ine ndidzabwezera. Ndiponso, Ambuye adzaweruza anthu ake.

Mutu    |  Mabaibulo
Ahebri 12:14

Londolani mtendere ndi anthu onse, ndi chiyeretso chimene, akapanda ichi, palibe mmodzi adzaona Ambuye:

Mutu    |  Mabaibulo
Yakobo 3:17-18

Koma nzeru yochokera kumwamba iyamba kukhala yoyera, nikhalanso yamtendere, yaulere, yomvera bwino, yodzala chifundo ndi zipatso zabwino, yopanda tsankho, yosadzikometsera pamaso.

Ndipo chipatso cha chilungamo chifesedwa mumtendere kwa iwo akuchita mtendere.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Petro 2:1

Momwemo pakutaya choipa chonse, ndi chinyengo chonse, ndi maonekedwe onyenga, ndi kaduka, ndi masinjiriro onse,

Mutu    |  Mabaibulo
1 Petro 2:23

amene pochitidwa chipongwe sanabwezera chipongwe, pakumva zowawa, sanaopsa, koma anapereka mlandu kwa Iye woweruza kolungama;

Mutu    |  Mabaibulo
1 Petro 3:9

osabwezera choipa ndi choipa, kapena chipongwe ndi chipongwe, koma penatu madalitso; pakuti kudzatsata ichi mwaitanidwa, kuti mukalandire dalitso.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Petro 4:8

koposa zonse mukhale nacho chikondano chenicheni mwa inu nokha; pakuti chikondano chikwiriritsa unyinji wa machimo;

Mutu    |  Mabaibulo
1 Yohane 2:9

Iye amene anena kuti ali m'kuunika, namuda mbale wake, ali mumdima kufikira tsopano lino.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Yohane 2:11

Koma iye wakumuda mbale wake ali mumdima, nayenda mumdima, ndipo sadziwa kumene amukako, pakuti mdima wamdetsa maso ake.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Yohane 3:15

Yense wakudana ndi mbale wake ali wakupha munthu; ndipo mudziwa kuti wakupha munthu aliyense alibe moyo wosatha wakukhala mwa iye.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Yohane 4:7-8

Okondedwa, tikondane wina ndi mnzake: chifukwa kuti chikondi chichokera kwa Mulungu, ndipo yense amene akonda, abadwa kuchokera kwa Mulungu, namzindikira Mulungu.

Iye wosakonda sazindikira Mulungu; chifukwa Mulungu ndiye chikondi.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Yohane 4:20

Munthu akati, kuti, Ndikonda Mulungu, nadana naye mbale wake, ali wabodza: pakuti iye wosakonda mbale wake amene wamuona, sakhoza kukonda Mulungu amene sanamuona.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Yohane 5:16

Wina akaona mbale wake alikuchimwa tchimo losati la kuimfa, apemphere Mulungu, ndipo Iye adzampatsira moyo wa iwo akuchita machimo osati a kuimfa. Pali tchimo la kuimfa: za ililo sindinena kuti mupemphere.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 17:14

Chiyambi cha ndeu chifanana ndi kutsegulira madzi; tsono kupikisana kusanayambe tasiya makani.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 10:12

Udani upikisanitsa; koma chikondi chikwirira zolakwa zonse.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 4:4

Chitani chinthenthe, ndipo musachimwe. Nenani mumtima mwanu pakama panu, ndipo mukhale chete.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 103:8-9

Yehova ndiye wa nsoni zokoma ndi wachisomo, wosakwiya msanga, ndi wa chifundo chochuluka.

Sadzatsutsana nao nthawi zonse; ndipo sadzasunga mkwiyo wake kosatha.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 141:3

Muike mdindo pakamwa panga, Yehova; sungani pakhomo pa milomo yanga.

Mutu    |  Mabaibulo
Luka 17:3-4

Kadzichenjerani nokha; akachimwa mbale wako umdzudzule, akalapa, umkhululukire.

momwemo kudzakhala tsiku lakuvumbuluka Mwana wa Munthu.

Tsikulo iye amene adzakhala pamwamba pa chindwi, ndi akatundu ake m'nyumba, asatsike kuwatenga; ndipo iye amene ali m'munda modzimodzi asabwere ku zake za m'mbuyo.

Kumbukirani mkazi wa Loti.

Iye aliyense akafuna kusunga moyo wake adzautaya, koma iye aliyense akautaya, adzausunga.

Ndinena ndi inu, usiku womwewo adzakhala awiri pa kama mmodzi; mmodzi adzatengedwa, ndi wina adzasiyidwa.

Padzakhala akazi awiri akupera pamodzi, mmodzi adzatengedwa, ndi wina adzasiyidwa.

Ndipo anayankha nanena kwa Iye, Kuti, Ambuye? Ndipo anati kwa iwo, Pamene pali mtembo, pomweponso miimba idzasonkhanidwa.

Ndipo akakuchimwira kasanu ndi kawiri pa tsiku lake, nakakutembenukira kasanu ndi kawiri ndi kunena, Ndalapa ine; uzimkhululukira.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 5:3-4

Ndipo si chotero chokha, komanso tikondwera m'zisautso; podziwa ife kuti chisautso chichita chipiriro; ndi chipiriro chichita chizolowezi;

ndi chizolowezi chichita chiyembekezo:

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 8:28

Ndipo tidziwa kuti amene akonda Mulungu zinthu zonse zithandizana kuwachitira ubwino, ndiwo amene aitanidwa monga mwa kutsimikiza kwa mtima wake.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 14:19

Chifukwa chake tilondole zinthu za mtendere, ndi zinthu zakulimbikitsana wina ndi mnzake.

Mutu    |  Mabaibulo
2 Akorinto 5:18-19

Koma zinthu zonse zichokera kwa Mulungu amene anatiyanjanitsa kwa Iye yekha mwa Khristu, natipatsa utumiki wa chiyanjanitso;

ndiko kunena kuti Mulungu anali mwa Khristu, alinkuyanjanitsa dziko lapansi kwa Iye yekha, osawawerengera zolakwa zao; ndipo anaikiza kwa ife mau a chiyanjanitso.

Mutu    |  Mabaibulo
Agalatiya 6:1

Abale, ngatinso munthu agwidwa nako kulakwa kwakuti, inu auzimu, mubweze wotereyo mu mzimu wa chifatso; ndi kudzipenyerera wekha, ungayesedwe nawenso.

Mutu    |  Mabaibulo
Afilipi 4:5

Kufatsa kwanu kuzindikirike ndi anthu onse. Ambuye ali pafupi.

Mutu    |  Mabaibulo
Afilipi 4:7

Ndipo mtendere wa Mulungu wakupambana chidziwitso chonse, udzasunga mitima yanu ndi maganizo anu mwa Khristu Yesu.

Mutu    |  Mabaibulo
Ahebri 12:15

ndi kuyang'anira kuti pangakhale wina wakuperewera chisomo cha Mulungu, kuti ungapuke muzu wina wa kuwawa mtima ungavute inu, ndipo aunyinji angadetsedwe nao;

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 25:15

Chipiriro chipembedza mkulu; lilime lofatsa lithyola fupa.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 12:16

Mkwiyo wa chitsiru udziwika posachedwa; koma wanzeru amabisa manyazi.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 12:18

Alipo wonena mwansontho ngati kupyoza kwa lupanga; koma lilime la anzeru lilamitsa.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 16:24

Mau okoma ndiwo chisa cha uchi, otsekemera m'moyo ndi olamitsa mafupa.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 55:8-9

Pakuti maganizo anga sali maganizo anu, ngakhale njira zanu sizili njira zanga, ati Yehova.

Pakuti monga kumwamba kuli kutali ndi dziko lapansi, momwemo njira zanga zili zazitali kupambana njira zanu, ndi maganizo anga kupambana maganizo anu.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 8:5-6

Pakuti iwo amene ali monga mwa thupi asamalira zinthu za thupi; koma iwo amene ali monga mwa mzimu, asamalira zinthu za mzimu:

pakuti chisamaliro cha thupi chili imfa; koma chisamaliro cha mzimu chili moyo ndi mtendere.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Akorinto 13:7

chikwirira zinthu zonse, chikhulupirira zinthu zonse, chiyembekeza zinthu zonse, chipirira zinthu zonse.

Mutu    |  Mabaibulo
Aefeso 6:12

Chifukwa kuti kulimbana kwathu sitilimbana nao mwazi ndi thupi, komatu nao maukulu, ndi maulamuliro, ndi akuchita zolimbika a dziko lapansi a mdima uno, ndi auzimu a choipa m'zakumwamba.

Mutu    |  Mabaibulo
Afilipi 2:5

Mukhale nao mtima m'kati mwanu umene unalinso mwa Khristu Yesu,

Mutu    |  Mabaibulo
Ahebri 10:24

ndipo tiganizirane wina ndi mnzake kuti tifulumizane ku chikondano ndi ntchito zabwino,

Mutu    |  Mabaibulo
Ahebri 13:1

Chikondi cha pa abale chikhalebe.

Mutu    |  Mabaibulo
Yakobo 3:13-14

Ndani ali wanzeru, ndi waluso mwa inu? Aonetsere ndi mayendedwe ake abwino ntchito zake mu nzeru yofatsa.

Koma mukakhala nako kaduka kowawa, ndi chotetana m'mtima mwanu, musadzitamandira, ndipo musamanama potsutsana nacho choonadi.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 18:15

Ndipo ngati mbale wako akuchimwira iwe, pita, numlangize pa nokha iwe ndi iye; ngati akumvera iwe, wambweza mbale wako.

Mutu    |  Mabaibulo
Luka 6:36-37

Khalani inu achifundo monga Atate wanu ali wachifundo. Ndipo musamaweruza, ndipo simudzaweruzidwa.

Ndipo musawatsutsa, ndipo simudzamatsutsidwa. Khululukani, ndipo mudzakhululukidwa.

Mutu    |  Mabaibulo
Yohane 15:12

Lamulo langa ndi ili, kuti mukondane wina ndi mnzake, monga ndakonda inu.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 15:5

Ndipo Mulungu wa chipiriro ndi wa chitonthozo apatse inu kuti mukhale ndi mtima umodzi wina ndi mnzake, monga mwa Khristu Yesu;

Mutu    |  Mabaibulo
1 Akorinto 16:14

Zanu zonse zichitike m'chikondi.

Mutu    |  Mabaibulo
Aefeso 4:15

koma ndi kuchita zoona mwa chikondi tikakule m'zinthu zonse, kufikira Iye amene ali mutu ndiye Khristu;

Mutu    |  Mabaibulo
Afilipi 2:14

Chitani zonse kopanda madandaulo ndi makani,

Mutu    |  Mabaibulo
Akolose 3:16

Mau a Khristu akhalitse mwa inu chichulukire mu nzeru yonse, ndi kuphunzitsa ndi kuyambirirana eni okha ndi masalmo, ndi mayamiko ndi nyimbo zauzimu, ndi kuimbira Mulungu ndi chisomo mumtima mwanu.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Atesalonika 5:11

Mwa ichi chenjezanani, ndipo mangiriranani wina ndi mnzake, monganso mumachita.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Timoteyo 4:12

Munthu asapeputse ubwana wako; komatu khala chitsanzo kwa iwo okhulupirira, m'mau, m'mayendedwe, m'chikondi, m'chikhulupiriro, m'kuyera mtima.

Mutu    |  Mabaibulo
Ahebri 10:23-24

tigwiritse chivomerezo chosagwedera cha chiyembekezo chathu, pakuti wolonjezayo ali wokhulupirika;

ndipo tiganizirane wina ndi mnzake kuti tifulumizane ku chikondano ndi ntchito zabwino,

Mutu    |  Mabaibulo
Yakobo 5:9

Musaipidwe wina ndi mnzake, abale, kuti mungaweruzidwe. Taonani, woweruza aima pakhomo.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Petro 3:11

ndipo apatuke pachoipa, nachite chabwino; afunefune mtendere ndi kuulondola.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Petro 5:5-6

Momwemonso, anyamata inu, mverani akulu. Koma nonsenu muvale kudzichepetsa kuti mutumikirane; pakuti Mulungu akaniza odzikuza, koma apatsa chisomo kwa odzichepetsa.

Potero dzichepetseni pansi pa dzanja la mphamvu la Mulungu, kuti panthawi yake akakukwezeni;

Mutu    |  Mabaibulo
1 Yohane 4:18

Mulibe mantha m'chikondi; koma chikondi changwiro chitaya kunja mantha, popeza mantha ali nacho chilango, ndipo wamanthayo sakhala wangwiro m'chikondi.

Mutu    |  Mabaibulo
Chivumbulutso 21:4

ndipo adzawapukutira misozi yonse kuichotsa pamaso pao; ndipo sipadzakhalanso imfa; ndipo sipadzakhalanso maliro, kapena kulira, kapena chowawitsa; zoyambazo zapita.

Mutu    |  Mabaibulo
Aefeso 4:2

ndi kuonetsera kudzichepetsa konse, ndi chifatso, ndi kuonetsera chipiriro, ndi kulolerana wina ndi mnzake, mwa chikondi;

Mutu    |  Mabaibulo

Pemphero kwa Mulungu

Ambuye Mulungu wanga wamuyaya, wamphamvu ndi wamkulu, Inu nokha ndinu woyenera ulemerero ndi ulemu wonse! Atate Woyera, ndikubwerera kwa Inu chifukwa ndikudziwa kuti ndikufunika mphamvu yanu yobwezeretsa ndi kumasula. Ndikupempha kuti Mzimu Woyera wanu undipatse mphamvu ndi kudziletsa kuti ndipewe makambirano opanda pake omwe amangondipangitsa kutaya mtima chifukwa cha mkwiyo, zomwe zimapangitsa kuti pakhale mikangano yambiri m'moyo wanga ndi m'banja langa. Ndikudziwa kuti kudzera m'mawu anga ndi zochita zanga zoyipa ndawalasa anthu omwe ali pafupi nane ndipo pamapeto pake chomwe ndimachita ndikumva ndili ndi liwongo ndipo nthawi yomweyo ndikufesa mkwiyo, kupsa mtima ndi ululu. Ndithandizeni kuti ndisagonjedwe ndi maganizo ndi malingaliro anga, chifukwa, ndithudi, mawu anu amati: "Kwiyani, koma musachimwe; dzuwa lisalowe muli chikwiyire, kapena kupatsa Mdyerekezi malo." Ambuye, ndipatseni nzeru kuti ndizitsatira mawu anu ndipo kuti kukhalapo kwanu tsiku lililonse kulamulire moyo wanga. Ndikutsutsa mkwiyo, kupsa mtima ndi ukali. M'dzina la Yesu. Ameni.