Biblia Todo Logo
Mavesi a Baibulo
- Zotsatsa -


108 Mau a m'Baibulo Okhudza Kusowa Chidwi

108 Mau a m'Baibulo Okhudza Kusowa Chidwi

Ndikudziwa kuti nthawi zina mtima umangokhala chete, ngati ulibe mphamvu yokhudzidwa ndi zinthu zomwe zikuchitika pa moyo wa anthu ena, kapena ntchito zathu, kaya za Mulungu kapena za dziko. Mtima umenewu ndi wovuta, umakupangitsa kuti usamamve chisoni cha anthu ena, ngakhale akukumana ndi mavuto aakulu.

Ukakhala ndi mtima umenewu, umatha kutaya chilakolako cha zinthu zomwe unkazikonda kale, zomwe unkafuna kuchita. Umatha kungokhala chete, osafuna kuchita khama kuti ukwaniritse maloto ako. Umafika povomereza moyo wamba, osafuna kusintha kalikonse.

Koma dziwa ichi, sudzakhala ndi mtima umenewu mpaka kalekale. Yesu ali ndi mphamvu yoti akuthandize. Baibulo limatiuza kuti mwa Iye ndife opambana. Ngakhale utamva kuti suli ndi mphamvu zopitirira, Iye angakupatsenso mphamvu zoyimirira ndikupitiriza ulendo wako.

Ndikukulimbikitsa lero, muka, ukapemphere kwa Mulungu. Mukaimirire mwamphamvu pa cholinga chimene Mulungu anakupatsa. Kumbukira kuti ukhoza kuchita zonse mwa Khristu amene amakupatsa mphamvu.




Ahebri 6:12

kuti musakhale aulesi, koma akuwatsanza iwo amene alikulowa malonjezano mwa chikhulupiriro ndi kuleza mtima.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Chivumbulutso 3:15-16

Ndidziwa ntchito zako, kuti suli wozizira kapena wotentha: mwenzi utakhala wozizira kapena wotentha. Kotero, popeza uli wofunda, wosati wotentha kapena wozizira, ndidzakulavula m'kamwa mwanga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 12:11

musakhale aulesi m'machitidwe anu; khalani achangu mumzimu, tumikirani Ambuye;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Marko 6:52

pakuti sanazindikire za mikateyo, koma mitima yao inauma.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 1:32

Pakuti kubwerera m'mbuyo kwa achibwana kudzawapha; ndipo mphwai za opusa zidzawaononga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yakobo 4:17

Potero kwa iye amene adziwa kuchita bwino, ndipo sachita, kwa iye kuli tchimo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ezekieli 12:2

Wobadwa ndi munthu iwe, ukhala pakati pa nyumba yampanduko, yokhala nao maso akuonera, koma osaona; ndi makutu akumvera, koma osamva; pakuti iwo ndiwo nyumba yampanduko.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Agalatiya 6:9

Koma tisaleme pakuchita zabwino; pakuti pa nyengo yake tidzatuta tikapanda kufooka.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 6:6

Pita kunyerere, waulesi iwe, penya njira zao nuchenjere;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 15:58

Chifukwa chake, abale anga okondedwa, khalani okhazikika, osasunthika, akuchuluka mu ntchito ya Ambuye, nthawi zonse, podziwa kuti kuchititsa kwanu sikuli chabe mwa Ambuye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Atesalonika 3:10

Pakutinso pamene tinali nanu tidakulamulirani ichi, Ngati munthu safuna kugwira ntchito, asadyenso.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aefeso 5:15-16

Potero, penyani bwino umo muyendera, si monga opanda nzeru, koma monga anzeru; akuchita machawi, popeza masiku ali oipa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 18:9

Wogwira ntchito mwaulesi ndiye mbale wake wa wosakaza.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Timoteyo 1:6

Chifukwa chake ndikukumbutsa iwe ukoleze mphatso ya Mulungu, ili mwa iwe mwa kuika kwa manja anga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aefeso 5:16

akuchita machawi, popeza masiku ali oipa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 10:24-25

ndipo tiganizirane wina ndi mnzake kuti tifulumizane ku chikondano ndi ntchito zabwino, osaleka kusonkhana kwathu pamodzi, monga amachita ena, komatu tidandaulirane, ndiko koposa monga momwe muona tsiku lilikuyandika.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Atesalonika 3:10-12

Pakutinso pamene tinali nanu tidakulamulirani ichi, Ngati munthu safuna kugwira ntchito, asadyenso. Pakuti tikumva za ena mwa inu kuti ayenda dwakedwake, osagwira ntchito konse, koma ali ochita mwina ndi mwina. Koma oterewa tiwalamulira ndi kuwadandaulira mwa Ambuye Yesu Khristu, kuti agwire ntchito pokhala chete, nadye chakudya cha iwo okha.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 24:12

Ndipo chifukwa cha kuchuluka kwa kusaweruzika, chikondano cha anthu aunyinji chidzazilala.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Tito 2:14

amene anadzipereka yekha m'malo mwa ife, kuti akatiombole ife kuzoipa zonse, nakadziyeretsere yekha anthu akhale ake enieni, achangu pa ntchito zokoma.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 10:4-5

Wochita ndi dzanja laulesi amasauka; koma dzanja la akhama lilemeretsa. Wokolola m'malimwe ndi mwana wanzeru; koma wogona pakutula ndi mwana wochititsa manyazi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 12:3

Pakuti talingirirani Iye amene adapirira ndi ochimwa otsutsana naye kotere, kuti mungaleme ndi kukomoka m'moyo mwanu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 24:33-34

Tulo tapang'ono, kungoodzera pang'ono, kungomanga manja pang'ono m'kugona, ndipo umphawi wako udzafika ngati mbala; ndi kusauka kwako ngati munthu wachikopa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Agalatiya 5:7

Munathamanga bwino; anakuletsani ndani kuti musamvere choonadi?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Petro 1:5-8

Ndipo mwa ichi chomwe, pakutengeraponso changu chonse, muonjezerapo ukoma pa chikhulupiriro chanu, ndi paukoma chizindikiritso; ndi pachizindikiritso chodziletsa; ndi pachodziletsa chipiriro; ndi pachipiriro chipembedzo; ndi pachipembedzo chikondi cha pa abale; ndi pachikondi cha pa abale chikondi. Pakuti izi zikakhala ndi inu, ndipo zikachuluka, zidzachita kuti musakhale aulesi kapena opanda zipatso pa chizindikiritso cha Ambuye Yesu Khristu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 13:11

Ndipo chitani ichi, podziwa inu nyengo, kuti tsopano ndiyo nthawi yabwino yakuuka kutulo; pakuti tsopano chipulumutso chathu chili pafupi koposa pamene tinayamba kukhulupirira.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 25:26

Koma mbuye wake anayankha, nati kwa iye, Kapolo iwe woipa ndi waulesi, unadziwa kuti ndimatuta kumene sindinafesa, ndi kusonkhanitsa kumene sindinawaza;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Atesalonika 3:13

Koma inu, abale, musaleme pakuchita zabwino.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yakobo 2:17

Momwemonso chikhulupiriro, chikapanda kukhala nacho ntchito, chikhala chakufa m'kati mwakemo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Atesalonika 5:6

chifukwa chake tsono tisagone monga otsalawo, komatu tidikire, ndipo tisaledzere.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Petro 1:13

Mwa ichi, podzimanga m'chuuno, kunena za mtima wanu, mukhale odzisunga, nimuyembekeze konsekonse chisomo chilikutengedwa kudza nacho kwa inu m'vumbulutso la Yesu Khristu;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 12:35-36

Khalani odzimangira m'chuuno, ndipo nyali zanu zikhale zoyaka; ndipo inu nokha khalani ofanana ndi anthu oyembekezera mbuye wao, pamene ati abwera kuchokera kuukwati; kuti pakudza iye, nakagogoda, akamtsegulire pomwepo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Akolose 3:23-24

chilichonse mukachichita, gwirani ntchito mochokera mumtima, monga kwa Ambuye, osati kwa anthu ai; podziwa kuti mudzalandira kwa Ambuye mphotho ya cholowa; mutumikira Ambuye Khristu mwaukapolo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 12:1

Chifukwa chake ifenso, popeza tizingidwa nao mtambo waukulu wotere wa mboni, titaye cholemetsa chilichonse, ndi tchimoli limangotizinga, ndipo tithamange mwachipiriro makaniwo adatiikira, ndi kupenyerera woyambira ndi womaliza wa chikhulupiriro chathu,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 6:6-8

Pita kunyerere, waulesi iwe, penya njira zao nuchenjere; zilibe mfumu, ngakhale kapitao, ngakhale mkulu; koma zitengeratu zakudya zao m'malimwe; nizituta dzinthu zao m'masika.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 25:14-30

Pakuti monga munthu, wakunka ulendo, aitana akapolo ake, napereka kwa iwo chuma chake. Ndipo mmodzi anampatsa ndalama za matalente zisanu, ndi wina ziwiri, ndi wina imodzi; kwa iwo onse monga nzeru zao; namuka iye. Pomwepo uyo amene analandira matalente asanu, anapita kugula nazo malonda, napindulapo matalente ena asanu. Chimodzimodzi uyo wa awiriwo, anapindulapo ena awiri. Koma uyo amene analandira imodziyo anamuka, nakumba pansi, naibisa talente ya mbuye wake. Ndipo itapita nthawi yaikulu, anabwera mbuye wa akapolo awo, nawerengera nao pamodzi. Ndipo asanu a iwo anali opusa, ndi asanu anali ochenjera. Ndipo uyo amene adalandira matalente asanu anadza, ali nawo matalente ena asanu, nanena, Mbuye, munandipatsa matalente asanu, onani ndapindulapo matalente ena asanu. Mbuye wake anati kwa iye, Chabwino, kapolo iwe wabwino ndi wokhulupirika; unali wokhulupirika pa zinthu zazing'ono, ndidzakhazika iwe pa zinthu zambiri; lowa iwe m'chikondwerero cha mbuye wako. Ndipo wa matalente awiriwo anadzanso, nati, Mbuye, munandipatsa ine matalente awiri; onani, ndapindulapo matalente ena awiri. Mbuye wake anati kwa iye, Chabwino, kapolo iwe wabwino ndi wokhulupirika; unali wokhulupirika pa zinthu zazing'ono, ndidzakhazika iwe pa zinthu zambiri; lowa iwe m'chikondwerero cha mbuye wako. Ndipo uyonso amene analandira talente imodzi, anadza, nati, Mbuye, ndinakudziwani inu kuti ndinu munthu wouma mtima, wakututa kumene simunafesa, ndi wakusonkhanitsa kumene simunawaza; ndinaopa ine, ndinapita, ndinabisa pansi talente yanu: onani, siyi talente yanuyo. Koma mbuye wake anayankha, nati kwa iye, Kapolo iwe woipa ndi waulesi, unadziwa kuti ndimatuta kumene sindinafesa, ndi kusonkhanitsa kumene sindinawaza; chifukwa chake ukadapereka ndalama zanga kwa okongola ndalama, ndipo ine pobwera ndikadatenga zanga ndi phindu lake. Chifukwa chake chotsani kwa iye ndalamayo, muipatse kwa amene ali nazo ndalama khumi. Pakuti kwa yense amene ali nazo, kudzapatsidwa, ndipo iye adzakhala nazo zochuluka: koma kwa iye amene alibe, kudzachotsedwa, chingakhale chimene anali nacho. Pakuti opusawo, m'mene anatenga nyali zao, sanadzitengeranso mafuta; Ndipo ponyani kapoloyo wopanda pake kumdima wakunja; kumene kudzakhala kulira ndi kukukuta mano.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Akorinto 8:11

Koma tsopano tsirizani kuchitaku; kuti monga kunali chivomerezo cha kufunira, koteronso kukhale kutsiriza kwake m'chimene muli nacho.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:4

Inu munatilamulira, tisamalire malangizo anu ndi changu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 8:6

pakuti chisamaliro cha thupi chili imfa; koma chisamaliro cha mzimu chili moyo ndi mtendere.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 13:4

Moyo wa waulesi ukhumba osalandira kanthu; koma moyo wa akhama udzalemera.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Akolose 4:2

Chitani khama m'kupemphera, nimudikire momwemo ndi chiyamiko;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 3:12

Tapenyani, abale, kuti kapena ukakhale mwa wina wa inu mtima woipa wosakhulupirira, wakulekana ndi Mulungu wamoyo;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 5:6

Odala ali akumva njala ndi ludzu la chilungamo; chifukwa adzakhuta.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 21:36

Koma inu dikirani nyengo zonse, ndi kupemphera, kuti mukalimbike kupulumuka zonse zimene zidzachitika, ndi kuimirira pamaso pa Mwana wa Munthu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Petro 3:9

Ambuye sazengereza nalo lonjezano, monga ena achiyesa chizengerezo; komatu aleza mtima kwa inu, wosafuna kuti ena aonongeke, koma kuti onse afike kukulapa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aefeso 4:1

Ndikudandaulirani inu tsono, ine wandende mwa Ambuye, muyende koyenera maitanidwe amene munaitanidwa nao,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 42:1-2

Monga nswala ipuma wefuwefu kukhumba mitsinje; motero moyo wanga upuma wefuwefu kukhumba Inu, Mulungu. Adani anga andinyoza ndi kundithyola mafupa anga; pakunena ndine dzuwa lonse, Mulungu wako ali kuti? Udziweramiranji moyo wanga iwe? Ndi kuzingwa m'kati mwanga? Yembekeza Mulungu; pakuti ndidzamlemekeza tsopanonso, ndiye chipulumutso cha nkhope yanga ndi Mulungu wanga. Moyo wanga uli ndi ludzu la kwa Mulungu, la kwa Mulungu wamoyo. Ndikadze liti kuoneka pamaso pa Mulungu?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 12:2

Ndipo musafanizidwe ndi makhalidwe a pansi pano: koma mukhale osandulika, mwa kukonzanso kwa mtima wanu, kuti mukazindikire chimene chili chifuno cha Mulungu, chabwino, ndi chokondweretsa, ndi changwiro.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 19:15

Ulesi ugonetsa tulo tofa nato; ndipo moyo wamkhongono udzamva njala.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Afilipi 3:13-14

Abale, ine sindiwerengera ndekha kuti ndatha kuchigwira: koma chinthu chimodzi ndichichita; poiwaladi zam'mbuyo, ndi kutambalitsira zam'tsogolo, ndilondetsa polekezerapo, kutsatira mfupo wa maitanidwe akumwamba a Mulungu a mwa Khristu Yesu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 27:4

Chinthu chimodzi ndinachipempha kwa Yehova, ndidzachilondola ichi, Kuti ndikhalitse m'nyumba ya Yehova masiku onse a moyo wanga, kupenya kukongola kwake kwa Yehova ndi kufunsitsa m'Kachisi wake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 9:24-27

Kodi simudziwa kuti iwo akuchita makani a liwiro, athamangadi onse, koma mmodzi alandira mfupo? Motero thamangani, kuti mukalandire. Koma yense wakuyesetsana adzikanizira zonse. Ndipo iwowa atero kuti alandire korona wakuvunda; koma ife wosavunda. Chifukwa chake ine ndithamanga chotero, si monga chosinkhasinkha. Ndilimbana chotero, si monga ngati kupanda mlengalenga; koma ndipumpuntha thupi langa, ndipo ndiliyesa kapolo; kuti, kapena ngakhale ndalalikira kwa ena, ndingakhale wotayika ndekha.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Akorinto 5:9

Chifukwa chakenso tifunitsitsa, kapena kwathu kapena kwina, kukhala akumkondweretsa Iye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 10:4

Wochita ndi dzanja laulesi amasauka; koma dzanja la akhama lilemeretsa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 1:19-20

Ngati inu muli ofuna ndi omvera, mudzadya zabwino za dziko, Imvani, miyamba inu, tchera makutu, iwe dziko lapansi, chifukwa Yehova wanena, Ndakulitsa ndipo ndalera ana, ndipo iwo anandipandukira Ine. koma ngati mukana ndi kupanduka, mudzathedwa ndi lupanga; chifukwa m'kamwa mwa Yehova mwatero.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mlaliki 9:10

Chilichonse dzanja lako lichipeza kuchichita, uchichite ndi mphamvu yako; pakuti mulibe ntchito ngakhale kulingirira ngakhale kudziwa, ngakhale nzeru, kumanda ulikupitako.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 18:1

Ndipo anawanenera fanizo lakuti ayenera iwo kupemphera nthawi zonse, osafooka mtima;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Afilipi 4:13

Ndikhoza zonse mwa Iye wondipatsa mphamvuyo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 6:33

Koma muthange mwafuna Ufumu wake ndi chilungamo chake, ndipo zonse zimenezo zidzaonjezedwa kwa inu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Timoteyo 4:2

lalikira mau; chita nao pa nthawi yake, popanda nthawi yake; tsutsa, dzudzula, chenjeza, ndi kuleza mtima konse ndi chiphunzitso.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 63:1

Inu Mulungu, ndinu Mulungu wanga; ndidzakufunani m'matanda kucha. Moyo wanga ukumva ludzu la kwa Inu, thupi langa lilirira Inu, m'dziko louma ndi lotopetsa, lopanda madzi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 6:13

ndipo musapereke ziwalo zanu kuuchimo, zikhale zida za chosalungama; koma mudzipereke inu nokha kwa Mulungu, monga amoyo atatuluka mwa akufa, ndi ziwalo zanu kwa Mulungu zikhale zida za chilungamo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Petro 5:8

Khalani odzisungira, dikirani; mdani wanu mdierekezi, monga mkango wobuma, ayendayenda ndi kufunafuna wina akamlikwire:

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Afilipi 2:12-13

Potero, okondedwa anga, monga momwe mumvera nthawi zonse, posati pokhapokha pokhala ine ndilipo, komatu makamaka tsopano pokhala ine palibe, gwirani ntchito yake ya chipulumutso chanu ndi mantha, ndi kunthunthumira; pakuti wakuchita mwa inu kufuna ndi kuchita komwe, chifukwa cha kukoma mtima kwake, ndiye Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 12:1

Chifukwa chake ndikupemphani inu, abale, mwa zifundo za Mulungu, kuti mupereke matupi anu nsembe yamoyo, yopatulika, yokondweretsa Mulungu, ndiko kupembedza kwanu koyenera.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 25:1-13

Pomwepo Ufumu wa Kumwamba udzafanizidwa ndi anamwali khumi, amene anatenga nyali zao, natuluka kukakomana ndi mkwati. Ndipo pamene iwo analikumuka kukagula, mkwati anafika; ndipo okonzekawo analowa naye pamodzi muukwati; ndipo anatseka pakhomo. Koma pambuyo pake anadzanso anamwali enawo, nati, Mbuye, Mbuye, mutitsegulire ife. Koma iye anayankha nati, Indetu ndinena kwa inu, sindikudziwani. Chifukwa chake dikirani, pakuti simudziwa tsiku lake, kapena nthawi yake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Akolose 3:17

Ndipo chilichonse mukachichita m'mau kapena muntchito, chitani zonse m'dzina la Ambuye Yesu, ndi kuyamika Mulungu Atate mwa Iye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 15:5

Ine ndine mpesa, inu ndinu nthambi zake: wakukhala mwa Ine, ndi Ine mwa iye, ameneyo abala chipatso chambiri; pakuti kopanda Ine simungathe kuchita kanthu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Timoteyo 4:14-15

Usanyalapse mphatsoyo ili mwa iwe, yopatsidwa kwa iwe mwa chinenero, pamodzi ndi kuika kwa manja a akulu. Izi uzisamalitse; mu izi ukhale; kuti kukula mtima kwako kuonekere kwa onse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 40:31

koma iwo amene alindira Yehova adzatenganso mphamvu; adzauluka pamwamba ndi mapiko monga ziombankhanga; adzathamanga koma osalema; adzayenda koma osalefuka.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:2

Odala iwo akusunga mboni zake, akumfuna ndi mtima wonse;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 9:4

Tiyenera kugwira ntchito za Iye wondituma Ine, pokhala pali msana; ukudza usiku pamene palibe munthu angakhoze kugwira ntchito.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 5:5

ndipo chiyembekezo sichichititsa manyazi; chifukwa chikondi cha Mulungu chinatsanulidwa m'mitima mwathu mwa Mzimu Woyera, amene wapatsidwa kwa ife.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 4:11

Chifukwa chake tichite changu cha kulowa mpumulowo, kuti wina angagwe m'chitsanzo chomwe cha kusamvera.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Petro 2:2

lirani monga makanda alero mkaka woyenera, wopanda chinyengo, kuti mukakule nao kufikira chipulumutso;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 6:46

Ndipo munditchuliranji Ine, Ambuye, Ambuye, ndi kusachita zimene ndizinena?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 22:13

Waulesi ati, Pali mkango panjapo, ndidzaphedwa pamakwalalapo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 8:37

Koma m'zonsezi, ife tilakatu, mwa Iye amene anatikonda.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aefeso 3:16-19

kuti monga mwa chuma cha ulemerero wake akulimbikitseni inu ndi mphamvu mwa Mzimu wake, m'kati mwanu, kuti Khristu akhale chikhalire mwa chikhulupiriro m'mitima yanu; kuti, ozika mizu ndi otsendereka m'chikondi, mukakhozetu kuzindikira pamodzi ndi oyera mtima onse, kupingasa, ndi utali, ndi kukwera, ndi kuzama nchiyani; ndi kuzindikira chikondi cha Khristu, chakuposa mazindikiridwe, kuti mukadzazidwe kufikira chidzalo chonse cha Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 51:10-12

Mundilengere mtima woyera, Mulungu; mukonze mzimu wokhazikika m'kati mwanga. Musanditaye kundichotsa pamaso panu; musandichotsere Mzimu wanu Woyera. Mundibwezere chimwemwe cha chipulumutso chanu; ndipo mzimu wakulola undigwirizize.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Yohane 3:18

Tiana, tisakonde ndi mau, kapena ndi lilime, komatu ndi kuchita ndi m'choonadi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:10

Ndinakufunani ndi mtima wanga wonse; ndisasokere kusiyana nao malamulo anu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 69:9

Pakuti changu cha pa nyumba yanu chandidya; ndi zotonza za iwo otonza Inu zandigwera ine.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Timoteyo 3:5

akukhala nao maonekedwe a chipembedzo, koma mphamvu yake adaikana; kwa iwonso udzipatule.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 13:24

Yesetsani kulowa pa khomo lopapatiza; chifukwa anthu ambiri, ndikuuzani, adzafunafuna kulowamo, koma sadzakhoza.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 20:4

Waulesi salima chifukwa cha chisanu; adzapemphapempha m'masika osalandira kanthu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 7:21

Si yense wakunena kwa Ine, Ambuye, Ambuye, adzalowa mu Ufumu wa Kumwamba; koma wakuchitayo chifuniro cha Atate wanga wa Kumwamba.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 55:6

Funani Yehova popezeka Iye, itanani Iye pamene ali pafupi;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 4:23-24

Koma ikudza nthawi, ndipo tsopano ilipo, imene olambira oona adzalambira Atate mumzimu ndi m'choonadi; pakuti Atate afuna otere akhale olambira ake. Mulungu ndiye mzimu; ndipo omlambira Iye ayenera kumlambira mumzimu ndi m'choonadi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 13:12-14

Usiku wapita, ndi mbandakucha wayandikira; chifukwa chake tivule ntchito za mdima, ndipo tivale zida za kuunika. Tiyendeyende koyenera, monga usana; si m'madyerero ndi kuledzera ai, si m'chigololo ndi chonyansa ai, si mu ndeu ndi nkhwidzi ai. Koma valani inu Ambuye Yesu Khristu, ndipo musaganizire za thupi kuchita zofuna zake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aefeso 5:18

Ndipo musaledzere naye vinyo, m'mene muli chitayiko; komatu mudzale naye Mzimu,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Agalatiya 2:20

Ndinapachikidwa ndi Khristu; koma ndili ndi moyo; wosatinso ine ai, koma Khristu ali ndi moyo mwa ine; koma moyo umene ndili nao tsopano m'thupi, ndili nao m'chikhulupiriro cha Mwana wa Mulungu, amene anandikonda, nadzipereka yekha chifukwa cha ine.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 91:1

Iye amene akhala pansi m'ngaka yake ya Wam'mwambamwamba adzagonera mu mthunzi wa Wamphamvuyonse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 22:37-38

Ndipo Yesu anati kwa iye, Uzikonda Ambuye Mulungu wako ndi mtima wako wonse, ndi moyo wako wonse, ndi nzeru zako zonse. Ili ndilo lamulo lalikulu ndi loyamba.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Atesalonika 5:17

Pempherani kosaleka;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 15:19

Mayendedwe a waulesi akunga linga laminga, koma njira ya oongoka mtima iundidwa ngati mseu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 55:1

Inu nonse, inu akumva ludzu, idzani kumadzi; ndi osowa ndalama idzani inu mugule mudye; inde idzani, mugule vinyo ndi mkaka opanda ndalama ndi opanda mtengo wake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 12:9

Chikondano chikhale chopanda chinyengo. Dana nacho choipa; gwirizana nacho chabwino.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 7:35

Koma ichi ndinena mwa kupindula kwanu kwa inu nokha; sikuti ndikakutchereni msampha, koma kukuthandizani kuchita chimene chiyenera, ndi kutsata chitsatire Ambuye, opanda chocheukitsa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 51:1-2

Mundichitire ine chifundo, Mulungu, monga mwa kukoma mtima kwanu; monga mwa unyinji wa nsoni zokoma zanu mufafanize machimo anga. Mundilengere mtima woyera, Mulungu; mukonze mzimu wokhazikika m'kati mwanga. Musanditaye kundichotsa pamaso panu; musandichotsere Mzimu wanu Woyera. Mundibwezere chimwemwe cha chipulumutso chanu; ndipo mzimu wakulola undigwirizize. Pomwepo ndidzalangiza ochimwa njira zanu; ndipo olakwa adzabwera kwa Inu. Mundilanditse kumlandu wa mwazi, Mulungu, ndinu Mulungu wa chipulumutso changa; lilime langa lidzakweza nyimbo ya chilungamo chanu. Ambuye, tsegulani pa milomo yanga; ndipo pakamwa panga padzalalikira ulemekezo wanu. Pakuti simukondwera ndi nsembe, mwenzi nditapereka; nsembe yopsereza simuikonda. Nsembe za Mulungu ndizo mzimu wosweka; Inu, Mulungu, simudzaupeputsa mtima wosweka ndi wolapa. Chitirani Ziyoni chokoma monga mwa kukondwera kwanu; mumange malinga a miyala a Yerusalemu. Pamenepo mudzakondwera nazo nsembe zachilungamo, ndi nsembe yopsereza ndi yopsereza yathunthu; pamenepo adzapereka ng'ombe pa guwa lanu la nsembe. Mubwereze kunditsuka mphulupulu yanga, ndipo mundiyeretse kundichotsera choipa changa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Afilipi 1:6

pokhulupirira pamenepo, kuti Iye amene anayamba mwa inu ntchito yabwino, adzaitsiriza kufikira tsiku la Yesu Khristu;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 14:15

Ngati mukonda Ine, sungani malamulo anga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 35:3-4

Limbitsani manja opanda mphamvu, ndi kulimbitsa maondo a gwedegwede. Nenani kwa a mitima ya chinthenthe, Limbani, musaope; taonani, Mulungu wanu adza ndi kubwezera chilango, ndi mphotho ya Mulungu; Iye adzafika ndi kukupulumutsani.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 24:10

Ukalefuka tsiku la tsoka mphamvu yako ichepa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 84:2

Moyo wanga ulakalaka, inde ukomokanso ndi kufuna mabwalo a Yehova; mtima wanga ndi thupi langa zifuulira kwa Mulungu wamoyo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Deuteronomo 4:29

Koma mukafuna Yehova Mulungu wanu kumeneko, mudzampeza, ngati mumfunafuna ndi mtima wanu wonse ndi moyo wanu wonse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 11:12

Ndipo kuyambira masiku a Yohane Mbatizi, kufikira tsopano lino, Ufumu wa Kumwamba uli wokakamizidwa, ndipo okakamirawo aukwatula ndi mphamvu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yakobo 4:8

Yandikirani kwa Mulungu, ndipo adzayandikira kwa inu. Sambani m'manja, ochimwa inu; yeretsani mitima, a mitima iwiri inu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani

Pemphero kwa Mulungu

Mulungu wanga wodabwitsa ndi wamphamvu, wochita zodabwitsa ndi zozizwitsa, dzina lanu ndi lolungama chifukwa ndinu Woyera ndi wachifundo. M'mawa uliwonse mumandisonyeza kukhulupirika kwanu ndipo mumandisunga ine ndi moyo wanga, simundisiya nditagwa, chifukwa mumateteza mapazi anga kuti asapunthwe ndi miyala. Ndi mawu anu omwe amandipatsa mphamvu ndipo ndimayembekezera modalira chifukwa ndinu mthandizi wanga wofulumira ndipo mumabwera msanga kudzapulumutsa moyo wanga. Ambuye, mumandidziwa bwino kwambiri, mwawona kundinyamuka kwanga ndi kugona kwanga, palibe chomwe ndingabise pamaso panu. Lero ndikupemphani kuti mundithandize m'zofooka zanga, ndikufuna kuyenda nthawi zonse m'chifuniro chanu changwiro, ndichifukwa chake ndikufuna kuti mundinyamule Yesu, kuti muchotse m'moyo wanga chilichonse chomwe chimandiletsa kupita patsogolo ndipo mundisinthe kukhala cholengedwa chatsopano, mundipange monga momwe mulili inu. Musalole kuti ulesi undilekanitse ndi cholinga chanu chosatha, bwezeretsani mphamvu zanga ngati za njati, sinthani maganizo anga ndipo nthawi zonse mundipatse chifukwa chokhalira ndi moyo kuti palibe chomwe chinganditsekereze. Lero ndasankha kusiya ulesi, ndimauchotsa m'moyo wanga chifukwa Khristu anandiitana ku zinthu zazikulu chifukwa chake ndikulengeza kuti sindidzafa, koma ndidzakhala ndi moyo kuti ndinene zodabwitsa za Mulungu wanga! Aleluya! M'dzina la Yesu, Ameni.
Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa