Biblia Todo Logo
Mavesi a Baibulo
- Zotsatsa -


48 Mau a m'Baibulo Okhudza Zivomerezi ndi Chivomezi

48 Mau a m'Baibulo Okhudza Zivomerezi ndi Chivomezi

Ndikufuna ndikuuzeni anzanga, mwina mukudziwa nkhani ya Adamu ndi Eva, momwe anachimwira Mulungu. Chifukwa cha zimenezi, dziko lathu lino linaledzera. Baibulo limatiuza mu Genesis 3:17 kuti Mulungu anauza Adamu kuti, "Popeza wamvera mkazi wako, nudya zipatso za mtengo umene ndinakuletsa, dziko lapansi lidzatembereredwa chifukwa cha iwe; udzadya zipatso zake ndi zowawa masiku onse a moyo wako."

Kumbukirani kuti Mulungu analenga dziko lino labwino kwambiri. Pa tsiku lachisanu ndi chimodzi la chilengedwe, zonse zinali zabwino kwambiri. Koma uchimo unabweretsa temberero ndi matenda. Zinthu ngati zivomerezi zimatipatsa chenjezo. Zimatiwonetsa kuti ufumu wa Khristu ukubwera, ndipo tiyenera kulapa machimo athu ndi mtima wonse.

Ngati sitilapa, tidzatayika miyoyo yathu ndi kukhala pamalo okhetsa mano ndi kulira kwamuyaya. Mulungu akufuna kuti tisinthe miyoyo yathu, tisiye zoyipa ndi machimo, ndi kukhala oyera mtima. Tiyeni timvere mawu a Mulungu ndikukhala moyo woyenera.




Luka 21:11

ndipo kudzakhala zivomezi zazikulu, ndi njala ndi miliri m'malo akutiakuti, ndipo kudzakhala zoopsa ndi zizindikiro zazikulu zakumwamba.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Marko 13:8

Pakuti mtundu wa anthu udzayambana ndi mtundu wina, ndipo ufumu ndi ufumu unzake: padzakhala zivomezi m'malo m'malo; padzakhala njala; izi ndi zoyambira za zowawa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 29:6

Ndipo Yehova wa makamu adzamzonda ndi bingu, ndi chivomezi, ndi mkokomo waukulu, kamvulumvulu, ndi mkuntho, ndi lawi la moto wonyambita.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Eksodo 19:18

Ndipo phiri la Sinai linafuka monsemo, popeza Yehova anatsikira m'moto pamenepo; ndi utsi wake unakwera ngati utsi wa m'ng'anjo, ndi phiri lonse linagwedezeka kwambiri.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Mafumu 19:11-12

Ndipo Iye anati, Tuluka, nuime paphiri lino pamaso pa Yehova. Ndipo taonani, Yehova anapitapo, ndi mphepo yaikulu ndi yamphamvu inang'amba mapiri, niphwanya matanthwe pamaso pa Yehova; koma Yehova sanakhale m'mphepomo. Itapita mphepoyo kunali chivomezi; komanso Yehova sanali m'chivomezicho. Chitaleka chivomezi panali moto; koma Yehova sanali m'motomo. Utaleka moto panali bata la kamphepo kayaziyazi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 27:54

Ndipo anali naye akudikira Yesu, anaona chivomezi, ndi zinthu zimene zinachitidwa, anaopa kwambiri, nanena, Indedi Uyu ndiye Mwana wa Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 18:7

Pamenepo linagwedezeka, ndi kutenthemera dziko lapansi, ndi maziko a mapiri ananjenjemera nagwedezeka, pakuti anakwiya Iyeyo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Machitidwe a Atumwi 16:26

ndipo mwadzidzidzi panali chivomezi chachikulu, chotero kuti maziko a ndende anagwedezeka: pomwepo pamakomo ponse panatseguka; ndi maunyolo a onse anamasuka.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 28:2

Ndipo onani, panali chivomezi chachikulu; pakuti mngelo wa Ambuye anatsika Kumwamba, nafika kukunkhuniza mwalawo, nakhala pamwamba pake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Chivumbulutso 11:19

Ndipo anatsegulidwa Kachisi wa Mulungu amene ali mu Mwamba; ndipo linaoneka likasa la chipangano chake, mu Kachisi mwake, ndipo panali mphezi, ndi mau, ndi mabingu, ndi chivomezi, ndi matalala aakulu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 24:7

Pakuti mtundu umodzi wa anthu udzaukirana ndi mtundu wina, ndi ufumu ndi ufumu wina; ndipo kudzakhala njala ndi zivomezi m'malo akutiakuti.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 46:2-3

Chifukwa chake sitidzachita mantha, lingakhale lisandulika dziko lapansi, angakhale mapiri asunthika, nakhala m'kati mwa nyanja. Chinkana madzi ake akokoma, nachita thovu, nagwedezeka mapiri ndi kudzala kwake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Chivumbulutso 6:12

Ndipo ndinaona pamene anamasula chizindikiro chachisanu ndi chimodzi, ndipo panali chivomezi chachikulu; ndi dzuwa lidada bii longa chiguduli cha ubweya ndi mwezi wonse unakhala ngati mwazi;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 24:19-20

Dziko lapansi lasweka ndithu, dziko lapansi lasungunukadi, dziko lapansi lili kugwedezeka kopambana. Ndipo padzakhala monga ndi anthu, moteronso ndi ansembe; monga ndi mtumiki, moteronso ndi mbuyake; monga ndi mdzakazi, moteronso ndi mbuyake wamkazi; monga ndi wogula, moteronso ndi wogulitsa; monga ndi wobwereka, moteronso ndi wombwereka; monga ndi wotenga phindu, moteronso ndi wombwezera phindu kwa iye. Dziko lapansi lidzachita dzandidzandi, ngati munthu woledzera, ndi kunjenjemera, ngati chilindo; ndi kulakwa kwake kudzalilemera, ndipo lidzagwa losaukanso.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 24:20

Dziko lapansi lidzachita dzandidzandi, ngati munthu woledzera, ndi kunjenjemera, ngati chilindo; ndi kulakwa kwake kudzalilemera, ndipo lidzagwa losaukanso.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 46:2

Chifukwa chake sitidzachita mantha, lingakhale lisandulika dziko lapansi, angakhale mapiri asunthika, nakhala m'kati mwa nyanja.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Chivumbulutso 11:13

Ndipo panthawipo panali chivomezi chachikulu, ndipo limodzi la magawo khumi a mzinda lidagwa; ndipo anaphedwa m'chivomezicho anthu zikwi zisanu ndi ziwiri; ndipo otsalawo anakhala amantha, napatsa ulemerero kwa Mulungu wa mu Mwamba.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Chivumbulutso 16:18

ndipo panakhala mphezi, ndi mau, ndi mabingu; ndipo panali chivomezi chachikulu chotero sichinaoneke chiyambire anthu padziko, chivomezi cholimba chotero, chachikulu chotero.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 54:10

Pakuti mapiri adzachoka, ndi zitunda zidzasunthika; koma kukoma mtima kwanga sikudzakuchokera iwe, kapena kusunthika chipangano changa cha mtendere, ati Yehova amene wakuchitira iwe chifundo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ezekieli 38:19

Pakuti ndanena mu nsanje yanga, ndi m'moto wa kuzaza kwanga, Zoonadi tsiku ilo kudzakhala kugwedezeka kwakukulu m'dziko la Israele;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 13:13

Chifukwa chake ndidzanthunthumiritsa miyamba, ndipo dziko lapansi lidzagwedezeka kuchokera m'malo ake, m'mkwiyo wa Yehova wa makamu, tsiku la mkwiyo wake waukali.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yeremiya 10:10

Koma Yehova ndiye Mulungu woona; ndiye Mulungu wamoyo, mfumu yamuyaya; pa mkwiyo wake dziko lapansi lidzanthunthumira, ndi amitundu sangapirire ukali wake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yoweli 3:16

Ndipo Yehova adzadzuma ali ku Ziyoni, ndi kumveketsa mau ake ali ku Yerusalemu; ndi thambo ndi dziko lapansi zidzagwedezeka; koma Yehova adzakhala chopulumukirako anthu adzakhala chopulumukirako anthu ake, ndi linga la ana a Israele.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Samueli 14:15

Ndipo kunali kunthunthumira kuzithando, kuthengoko, ndi pakati pa anthu onse; a ku kaboma ndi owawanya omwe ananthunthumira; ndi dziko linagwedezeka; chomwecho kunali kunthunthumira kwakukulu koposa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ezekieli 38:19-20

Pakuti ndanena mu nsanje yanga, ndi m'moto wa kuzaza kwanga, Zoonadi tsiku ilo kudzakhala kugwedezeka kwakukulu m'dziko la Israele; Wobadwa ndi munthu iwe, lozetsa nkhope yako kwa Gogi, wa kudziko la Magogi, ndiye mfumu yaikulu ya Meseki ndi Tubala; nunenere motsutsana naye, motero kuti nsomba za m'nyanja, ndi mbalame za m'mlengalenga, ndi nyama zakuthengo, ndi zokwawa zonse zakukwawa pansi, ndi anthu onse akukhala padziko, zidzanjenjemera pamaso panga; ndi mapiri adzagwetsedwa, ndi potsetsereka padzagumuka, ndi makoma onse adzagwa pansi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ezekieli 38:20

motero kuti nsomba za m'nyanja, ndi mbalame za m'mlengalenga, ndi nyama zakuthengo, ndi zokwawa zonse zakukwawa pansi, ndi anthu onse akukhala padziko, zidzanjenjemera pamaso panga; ndi mapiri adzagwetsedwa, ndi potsetsereka padzagumuka, ndi makoma onse adzagwa pansi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Amosi 1:1

Mau a Amosi, amene anali mwa oweta ng'ombe a ku Tekowa, ndiwo amene anawaona za Israele masiku a Uziya mfumu ya Yuda, ndi masiku a Yerobowamu mwana wa Yowasi mfumu ya Israele, zitatsala zaka ziwiri chisanafike chivomezi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Nahumu 1:5

Mapiri agwedezeka chifukwa cha Iye, ndi zitunda zisungunuka; ndi dziko lapansi likwezeka pamaso pake, ndi maiko ndi onse okhala m'mwemo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Amosi 8:8

Kodi dziko silidzanjenjemera chifukwa cha ichi, ndi kulira aliyense wokhalamo? Inde lidzakwera lonseli ngati madzi a m'mtsinje; lidzagwezeka, ndi kutsikanso ngati mtsinje wa Ejipito.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Zekariya 14:4

Ndi mapazi ake adzaponda tsiku lomwelo paphiri la Azitona, lili pandunji pa Yerusalemu kum'mawa, ndi phiri la Azitona lidzang'ambika pakati kuloza kum'mawa ndi kumadzulo, ndipo padzakhala chigwa chachikulu; ndi gawo lina la phirilo lidzamuka kumpoto, ndi gawo lina kumwera.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Zekariya 14:5

Pamenepo mudzathawa kudzera chigwa cha mapiri anga; pakuti chigwa cha mapiri chidzafikira ku Azali; ndipo mudzathawa monga umo munathawira chivomezi, masiku a Uziya mfumu ya Yuda; ndipo Yehova Mulungu wanga adzadza, ndi opatulika onse pamodzi ndi Inu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 27:51-54

Ndipo onani, chinsalu chotchinga cha mu Kachisi chinang'ambika pakati, kuchokera kumwamba kufikira pansi; ndipo dziko linagwedezeka, ndi miyala inang'ambika; ndi manda anatseguka, ndi mitembo yambiri ya anthu oyera mtima, akugona kale, inauka; ndipo anatuluka m'manda mwao pambuyo pa kuuka kwake, nalowa m'mzinda woyera, naonekera kwa anthu ambiri. Ndipo anali naye akudikira Yesu, anaona chivomezi, ndi zinthu zimene zinachitidwa, anaopa kwambiri, nanena, Indedi Uyu ndiye Mwana wa Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 27:51

Ndipo onani, chinsalu chotchinga cha mu Kachisi chinang'ambika pakati, kuchokera kumwamba kufikira pansi; ndipo dziko linagwedezeka, ndi miyala inang'ambika;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 12:26

amene mau ake anagwedeza dziko pamenepo; koma tsopano adalonjeza, ndi kuti, Kamodzinso ndidzagwedeza, si dziko lokha, komanso m'mwamba.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Machitidwe a Atumwi 4:31

Ndipo m'mene adapemphera iwo, panagwedezeka pamalo pamene adasonkhanirapo; ndipo anadzazidwa onse ndi Mzimu Woyera, nalankhula mau a Mulungu molimbika mtima.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 104:32

amene apenyerera padziko lapansi, ndipo linjenjemera; akhudza mapiri, ndipo afuka.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 12:26-27

amene mau ake anagwedeza dziko pamenepo; koma tsopano adalonjeza, ndi kuti, Kamodzinso ndidzagwedeza, si dziko lokha, komanso m'mwamba. Ndipo ichi, chakuti kamodzinso, chilozera kusuntha kwake kwa zinthu zogwedezeka, monga kwa zinthu zolengedwa, kuti zinthu zosagwedezeka zikhale.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 37:2

Pakuti adzawamweta msanga monga udzu, ndipo adzafota monga msipu wauwisi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Chivumbulutso 8:5

Ndipo mngeloyo anatenga mbale ya zofukiza, naidzaza ndi moto wopala paguwa la nsembe, nauponya padziko lapansi; ndipo panakhala mabingu, ndi mau, ndi mphezi, ndi chivomezi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ezekieli 3:12

Pamenepo mzimu unandinyamula, ndipo ndinamva kumbuyo kwanga mau a mkokomo waukulu, ndi kuti, Wodala ulemerero wa Yehova m'malo mwake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mika 1:3

Pakuti, taonani, Yehova alikutuluka m'malo mwake, nadzatsika, nadzaponda pa misanje ya dziko lapansi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 68:8

Dziko lapansi linagwedezeka, inde thambo linakha pamaso pa Mulungu; Sinai lomwe linagwedezeka pamaso pa Mulungu, Mulungu wa Israele.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 17:26-30

Ndipo monga kunakhala masiku a Nowa, momwemo kudzakhalanso masiku a Mwana wa Munthu. Anadya, anamwa, anakwatira, anakwatiwa, kufikira tsiku lija Nowa analowa m'chingalawa, ndipo chinadza chigumula, nkuwaononga onsewo. Monga momwenso kunakhala masiku a Loti; anadya, anamwa, anagula, anagulitsa, anabzala, anamanga nyumba; koma tsiku limene Loti anatuluka mu Sodomu udavumba moto ndi sulufure zochokera kumwamba, ndipo zinawaononga onsewo; Kadzichenjerani nokha; akachimwa mbale wako umdzudzule, akalapa, umkhululukire. momwemo kudzakhala tsiku lakuvumbuluka Mwana wa Munthu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Mafumu 19:11

Ndipo Iye anati, Tuluka, nuime paphiri lino pamaso pa Yehova. Ndipo taonani, Yehova anapitapo, ndi mphepo yaikulu ndi yamphamvu inang'amba mapiri, niphwanya matanthwe pamaso pa Yehova; koma Yehova sanakhale m'mphepomo. Itapita mphepoyo kunali chivomezi; komanso Yehova sanali m'chivomezicho.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 75:3

Lasungunuka dziko lapansi, ndi onse okhalamo; ndinachirika mizati yake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 2:19

Anthu adzalowa m'mapanga a m'matanthwe, ndi m'maenje apansi, kuthawa kuopsa kwa Yehova, ndi ulemerero wachifumu wake, podzuka Iye kugwedeza dziko ndi mphamvu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 102:25-26

Munakhazika dziko lapansi kalelo; ndipo zakumwamba ndizo ntchito ya manja anu. Zidzatha izi, koma Inu mukhala: Inde, zidzatha zonse ngati chovala; mudzazisintha ngati malaya, ndipo zidzasinthika:

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 8:24-26

Ndipo onani, panauka namondwe wamkulu panyanja, kotero kuti ngalawa inafundidwa ndi mafunde: koma Iye anali m'tulo. Ndipo iwo anadza, namuutsa Iye, nanena, Ambuye, tipulumutseni, tilikutayika. Ndipo ananena Iye kwa iwo, Muli amantha bwanji, okhulupirira pang'ono inu? Pomwepo Iye anauka, nadzudzula mphepo ndi nyanja, ndipo panagwa bata lalikulu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani

Pemphero kwa Mulungu

Ambuye Mulungu wanga, Wamuyaya, wapamwamba koposa, m'dzina la Yesu ndikubwera kwa Inu, Inu nokha ndinu woyenera kutamandidwa ndi kupembedzedwa kwakukulu. Atate, nthawi ino yachisoni ndi masoka pomwe mabanja ambiri akhudzidwa ndi zivomezi ndi masoka achilengedwe, ndikupemphani kuti muchitire chifundo ndi kutambasula dzanja lanu lamphamvu pa miyoyo yawo ndipo chitetezo chanu chikhale pa iwo, kuti athe kuyang'ana kumwamba ndi kulira kwa Inu kuti amvetsetse kuti Inu ndinu thandizo lawo, chithandizo chawo chachangu m'mavuto, ndipo muli ndi mphamvu pa chilichonse chifukwa m'manja mwanu muli kuzama kwa dziko lapansi ndipo Inu nokha muli ndi mphamvu zolilimbitsa. Ndikupemphani kuti pakati pa kutaya mtima kwawo, mtendere ndi mphamvu zanu zilamulire mitima yawo. Sungani ndi kuteteza omwe avulala ndi omwe akhudzidwa m'maganizo, tambasulani dzanja lanu lochiritsira pa iwo, awapatse mankhwala, chakudya ndi pokhala kuti miyoyo yawo itetezedwe ku mantha ndi kutaya mtima. M'dzina la Yesu. Ameni.
Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa