Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -

Masalimo 148 - Buku Lopatulika


Zolengedwa zonse zilemekeze Mulungu

1 Aleluya. Lemekezani Yehova kochokera kumwamba; mlemekezeni m'misanje.

2 Mlemekezeni, angelo ake onse; mlemekezeni, makamu ake onse.

3 Mlemekezeni, dzuwa ndi mwezi; mlemekezeni, nyenyezi zonse zounikira.

4 Mlemekezeni, m'mwambamwamba, ndi madzi inu, a pamwamba pa thambo.

5 Alemekeze dzina la Yehova; popeza analamulira, ndipo zinalengedwa.

6 Anazikhazikanso kunthawi za nthawi; anazipatsa chilamulo chosatumphika.

7 Lemekezani Yehova kochokera ku dziko lapansi, zinsomba inu, ndi malo ozama onse;

8 moto ndi matalala, chipale chofewa ndi nkhungu; mphepo ya namondwe, yakuchita mau ake;

9 mapiri ndi zitunda zonse; mitengo yazipatso ndi yamikungudza yonse:

10 Nyama zakuthengo ndi zoweta zonse; zokwawa, ndi mbalame zakuuluka.

11 Mafumu a padziko ndi mitundu yonse ya anthu; zinduna ndi oweruza onse a padziko.

12 Anyamata ndiponso anamwali; okalamba pamodzi ndi ana.

13 Alemekeze dzina la Yehova; pakuti dzina lake lokha ndi lokwezeka; ulemerero wake uli pamwamba padziko lapansi ndi thambo.

14 Ndipo anakweza nyanga ya anthu ake, chilemekezo cha okondedwa ake onse; ndiwo ana a Israele, anthu a pafupi pa Iye. Aleluya.

Bible Society of Malawi

Bible Society of Malawi
Titsatireni:



Zotsatsa