Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 6:1 - Buku Lopatulika

Yehova, musandidzudzule mu mkwiyo wanu, ndipo musandilange muukali wanu.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Yehova, musandidzudzule mu mkwiyo wanu, ndipo musandilange m'kukali wanu.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Inu Chauta, musandikalipire ndi kundidzudzula, musapse mtima ndi kundilanga.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Inu Yehova, musandidzudzule mu mkwiyo wanu, kapena kundilanga mu ukali wanu.

Onani mutuwo



Masalimo 6:1
12 Mawu Ofanana  

ndi Zekariya, ndi Aziyele, ndi Semiramoti, ndi Yehiyele, ndi Uni, ndi Eliyabu, ndi Maaseiya, ndi Benaya, ndi zisakasa kuimbira mwa Alimoti;


ndi Matitiya, ndi Elifelehu, ndi Mikineya, ndi Obededomu, ndi Yeiyele, ndi Azaziya, ndi azeze akuimbira mwa Seminiti, kutsogolera maimbidwe.


Kulanga anandilangadi Yehova: koma sanandipereke kuimfa ai.


Pulumutsani, Yehova; pakuti wofatsa wasowa; pakuti okhulupirika achepa mwa ana a anthu.


Pomwepo adzalankhula nao mu mkwiyo wake, nadzawaopsa mu ukali wake.


Yehova, musandidzudzule ndi mkwiyo wanu, ndipo musandilange moopsa m'mtima mwanu.


Pakufuula ine mundiyankhe, Mulungu wa chilungamo changa; pondichepera mwandikulitsira malo. Ndichitireni chifundo, imvani pemphero langa.


Pakuti kumeneku kuli kwa Ine monga madzi a Nowa; pakuti monga ndinalumbira kuti madzi a Nowa sadzamizanso padziko lapansi, momwemo ndinalumbira kuti sindidzakukwiyira iwe, pena kukudzudzula.


Pakuti sindidzatsutsana kunthawi zonse, sindidzakwiya masiku onse; pakuti mzimu udzalefuka pamaso pa Ine, ndi miyoyo imene ndinailenga.


Yehova, mundilangize, koma ndi chiweruzo; si m'mkwiyo wanu, mungandithe psiti.


Usaope, iwe Yakobo mtumiki wanga, ati Yehova; pakuti Ine ndili ndi iwe; pakuti Ine ndidzathetsa mitundu yonse kumene ndinakuingitsirako iwe, koma sindidzakuthetsa iwe; koma ndidzakulangiza ndi chiweruziro, ndipo sindidzakusiya konse wosalangidwa.