Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 41:5 - Buku Lopatulika

Adani anga andinenera choipa, ndi kuti, adzafa liti, ndi kutayika dzina lake?

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Adani anga andinenera choipa, ndi kuti, adzafa liti, ndi kutayika dzina lake?

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Koma adani anga ondifunira zoipa, amati, “Kodi munthu ameneyu adzafa liti, kuti aiŵalike?”

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Adani anga mwankhwidzi amanena za ine kuti, “Kodi munthu ameneyu adzafa liti kuti ayiwalike?”

Onani mutuwo



Masalimo 41:5
13 Mawu Ofanana  

Chikumbukiro chake chidzatayika m'dziko, ndipo adzasowa dzina kukhwalala.


koma adzatayika kosatha ngati zonyansa zake; iwo amene adamuona adzati, Ali kuti iye?


Adani anga anditonza tsiku lonse; akundiyalukirawo alumbirira ine.


Ndipo anditchera misampha iwo akufuna moyo wanga; ndipo iwo akuyesa kundichitira choipa alankhula zoononga, nalingirira zonyenga tsiku lonse.


Chifukwa ndazindikira machimo anga; ndipo choipa changa chili pamaso panga chikhalire.


Onani, Inu mukondwera ndi zoonadi m'malo a m'katimo; ndipo m'malo a m'tseri mudzandidziwitsa nzeru.


Adani anga afuna kundimeza tsiku lonse, pakuti ambiri andithira nkhondo modzikuza.


Ndidzafuulira kwa Mulungu Wam'mwambamwamba; ndiye Mulungu wonditsirizira zonse.


kuti njira yanu idziwike padziko lapansi, chipulumutso chanu mwa amitundu onse.


Mundibwerere ine, ndi kundichitira chifundo; mpatseni mtumiki wanu mphamvu yanu, ndipo pulumutsani mwana wa mdzakazi wanu.


Mundichitire chifundo, Ambuye; pakuti tsiku lonse ndiitana Inu.


Amayesa wolungama wodala pomkumbukira; koma dzina la oipa lidzavunda.