Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 112:8 - Buku Lopatulika

Mtima wake ngwochirikizika, sadzachita mantha, kufikira ataona chofuna iye pa iwo omsautsa.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Mtima wake ngwochirikizika, sadzachita mantha, kufikira ataona chofuna iye pa iwo omsautsa.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Ali wolimba mtima, sadzachita mantha, potsiriza adzaona adani ake atagonja.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mtima wake ndi wotetezedwa, sadzakhala ndi mantha; potsiriza pake adzayangʼana adani ake mwachipambano.

Onani mutuwo



Masalimo 112:8
11 Mawu Ofanana  

Yehova ndi wanga; sindidzaopa; adzandichitanji munthu?


Yehova ndi wanga, mwa iwo akundithandiza; m'mwemo ndidzaona chofuna ine pa iwo akundida.


Yembekeza Yehova, limbika, ndipo Iye adzalimbitsa mtima wako; inde, yembekeza Yehova.


Limbikani ndipo Iye adzalimbitsa mtima wanu, inu nonse akuyembekeza Yehova.


Yembekeza Yehova, nusunge njira yake, ndipo Iye adzakukweza kuti ulandire dziko. Pakudulidwa oipa udzapenya.


Iwo akutama kulemera kwao; nadzitamandira pa kuchuluka kwa chuma chao;


Mulungu wa chifundo changa adzandichingamira, adzandionetsa tsoka la adani anga.


Koma udzapenya ndi maso ako, nudzaona kubwezera chilango oipa.


Diso langa lapenya chokhumba ine pa iwo ondilalira, m'makutu mwanga ndamva chokhumba ine pa iwo akuchita zoipa akundiukira.


Yehova atemberera za m'nyumba ya woipa; koma adalitsa mokhalamo olungama.


Musatengedwe ndi maphunzitso a mitundumitundu, ndi achilendo; pakuti nkokoma kuti mtima ukhazikike ndi chisomo; kosati ndi zakudya, zimene iwo adazitsata sanapindule nazo.