Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Masalimo 59:10 - Buku Lopatulika

10 Mulungu wa chifundo changa adzandichingamira, adzandionetsa tsoka la adani anga.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

10 Mulungu wa chifundo changa adzandichingamira, adzandionetsa tsoka la adani anga.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

10 Mulungu wanga adzandichingamira chifukwa ndi wa chikondi chosasinthika. Mulungu wanga adzandilola kuti ndisangalale poona adani anga atagonja.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

10 Mulungu wanga wachikondi. Mulungu adzapita patsogolo panga ndipo adzandilola kunyada pa iwo amene amandinyoza.

Onani mutuwo Koperani




Masalimo 59:10
23 Mawu Ofanana  

Ndipo Davide analirira Saulo ndi Yonatani mwana wake ndi nyimbo iyi ya maliro;


Mtima wake ngwochirikizika, sadzachita mantha, kufikira ataona chofuna iye pa iwo omsautsa.


Pakuti mufika kwa iye ndi madalitso okoma; muika korona wa golide woyengetsa pamutu pake.


Idzani, penyani ntchito za Yehova, amene achita zopululutsa padziko lapansi.


Yehova, munditsogolere m'chilungamo chanu, chifukwa cha akundizondawo; mulungamitse njira yanu pamaso panga.


Adzabwezera choipa adani anga, aduleni m'choonadi chanu.


Pakuti anandilanditsa m'nsautso yonse; ndipo ndapenya ndi diso langa icho ndakhumbira pa adani anga.


Adani anga afuna kundimeza tsiku lonse, pakuti ambiri andithira nkhondo modzikuza.


Amemezana, alalira, atchereza mapazi anga, popeza alindira moyo wanga.


Ndidzaimbira zakukulemekezani Inu, mphamvu yanga; pakuti Mulungu ndiye msanje wanga, Mulungu wa chifundo changa.


Musakumbukire motitsutsa mphulupulu za makolo athu; nsoni zokoma zanu zitipeze msanga, pakuti tafooka kwambiri.


Koma udzapenya ndi maso ako, nudzaona kubwezera chilango oipa.


Diso langa lapenya chokhumba ine pa iwo ondilalira, m'makutu mwanga ndamva chokhumba ine pa iwo akuchita zoipa akundiukira.


Ndipo padzakhala kuti iwo asanaitane Ine, ndidzayankha; ndipo ali chilankhulire, Ine ndidzamva.


Koma ine, pokhala mbusa sindinafulumire kuchokerako kuti ndikutsateni Inu; sindinakhumbe tsiku la tsoka; Inu mudziwa, chimene chinatuluka pa milomo yanga chinali pamaso panu.


Wolemekezeka Mulungu ndi Atate wa Ambuye wathu Yesu Khristu, Atate wa zifundo ndi Mulungu wa chitonthozo chonse,


Pakuti ichi tinena kwa inu m'mau a Ambuye, kuti ife okhala ndi moyo, otsalira kufikira kufikanso kwa Ambuye, sitidzatsogolera ogonawo.


Ndipo Mulungu wa chisomo chonse, amene adakuitanani kulowa ulemerero wake wosatha mwa Khristu, mutamva zowawa kanthawi, adzafikitsa inu opanda chilema mwini wake, adzakhazikitsa, adzalimbikitsa inu.


Nati Davide, Pali Yehova, Yehova adzamkantha iye; kapena tsiku la imfa yake lidzafika; kapena adzatsikira kunkhondo, nadzafako.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa