Mavesi a Baibulo

Zotsatsa


Gulu Laling'ono

70 Mau a Mulungu Okhudza Kuzindikira Mizimu


1 Akorinto 12:10

ndi kwa wina machitidwe a mphamvu; ndi kwa wina chinenero; ndi kwa wina chizindikiro cha mizimu; kwa wina malilime a mitundumitundu; ndi kwa wina mamasulidwe a malilime.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Yohane 4:1

Okondedwa, musamakhulupirira mzimu uliwonse, koma yesani mizimu ngati ichokera mwa Mulungu: popeza aneneri onyenga ambiri anatuluka kulowa m'dziko lapansi.

Mutu    |  Mabaibulo
Ahebri 5:14

Koma chakudya chotafuna chili cha anthu akulu misinkhu, amene mwa kuchita nazo anazoloweretsa zizindikiritso zao kusiyanitsa chabwino ndi choipa.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Akorinto 2:14

Koma munthu wa chibadwidwe cha umunthu salandira za Mzimu wa Mulungu: pakuti aziyesa zopusa; ndipo sakhoza kuzizindikira, chifukwa ziyesedwa mwauzimu.

Mutu    |  Mabaibulo
Ahebri 4:12

Pakuti mau a Mulungu ali amoyo, ndi ochitachita, ndi akuthwa koposa lupanga lakuthwa konsekonse, napyoza kufikira kugawira moyo ndi mzimu, ndi zimfundo ndi mafuta a m'mafupa, nazindikiritsa zolingirira ndi zitsimikizo za mtima.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 7:15-16

Yang'anirani mupewe aneneri onyenga, amene adza kwa inu ndi zovala zankhosa, koma m'kati mwao ali mimbulu yolusa.

Mudzawazindikira ndi zipatso zao. Kodi atchera mphesa paminga, kapena nkhuyu pamtula?

Mutu    |  Mabaibulo
1 Atesalonika 5:21

Yesani zonse; sungani chokomacho,

Mutu    |  Mabaibulo
2 Akorinto 11:14

Ndipo kulibe kudabwa; pakuti Satana yemwe adzionetsa ngati mngelo wa kuunika.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Timoteyo 4:1

Koma Mzimu anena monenetsa, kuti m'masiku otsiriza ena adzataya chikhulupiriro, ndi kusamala mizimu yosocheretsa ndi maphunziro a ziwanda,

Mutu    |  Mabaibulo
1 Akorinto 12:1-11

Koma za mphatso zauzimu, abale, sindifuna kuti mukhale osadziwa.

ndi kwa wina machitidwe a mphamvu; ndi kwa wina chinenero; ndi kwa wina chizindikiro cha mizimu; kwa wina malilime a mitundumitundu; ndi kwa wina mamasulidwe a malilime.

Koma zonse izi achita Mzimu mmodzi yemweyo, nagawira yense pa yekha monga afuna.

Mutu    |  Mabaibulo
Yohane 7:24

Musaweruze monga maonekedwe, koma weruzani chiweruziro cholungama.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 15:14

Mtima wa wozindikira ufunitsa kudziwa; koma m'kamwa mwa opusa mudya utsiru.

Mutu    |  Mabaibulo
2 Akorinto 11:13-15

Pakuti otere ali atumwi onyenga, ochita ochenjerera, odzionetsa ngati atumwi a Khristu.

Ndipo kulibe kudabwa; pakuti Satana yemwe adzionetsa ngati mngelo wa kuunika.

Chifukwa chake sikuli kanthu kwakukulu ngatinso atumiki ake adzionetsa monga atumiki a chilungamo; amene chimaliziro chao chidzakhala monga ntchito zao.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:125

Ine ndine mtumiki wanu, ndizindikiritseni; kuti ndidziwe mboni zanu.

Mutu    |  Mabaibulo
Aefeso 5:6

Asakunyengeni inu munthu ndi mau opanda pake, pakuti chifukwa cha izi umadza mkwiyo wa Mulungu pa ana a kusamvera.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Mafumu 3:9

Patsani tsono kapolo wanu mtima womvera wakuweruza anthu anu; kuti ndizindikire pakati pa zabwino ndi zoipa; pakuti akutha ndani kuweruza anthu anu ambiri amene?

Mutu    |  Mabaibulo
Aefeso 6:12

Chifukwa kuti kulimbana kwathu sitilimbana nao mwazi ndi thupi, komatu nao maukulu, ndi maulamuliro, ndi akuchita zolimbika a dziko lapansi a mdima uno, ndi auzimu a choipa m'zakumwamba.

Mutu    |  Mabaibulo
Machitidwe a Atumwi 16:16-18

Ndipo panali, pamene tinali kunka kukapemphera, anakomana ndi ife mdzakazi wina amene anali ndi mzimu wambwebwe, amene anapindulira ambuye ake zambiri pakubwebweta pake.

Ameneyo anatsata Paulo ndi ife, nafuula, kuti, Anthu awa ndi akapolo a Mulungu wa Kumwambamwamba, amene akulalikirani inu njira ya chipulumutso.

Ndipo anachita chotero masiku ambiri. Koma Paulo anavutika mtima ndithu, nacheuka, nati kwa mzimuwo, Ndikulamulira iwe m'dzina la Yesu Khristu, tuluka mwa iye. Ndipo unatuluka nthawi yomweyo.

Mutu    |  Mabaibulo
Chivumbulutso 2:2

Ndidziwa ntchito zako, ndi chilemetso chako ndi chipiriro chako ndi kuti sukhoza kulola oipa, ndipo unayesa iwo amene adzitcha okha atumwi, osakhala atumwi, nuwapeza onama;

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 12:2

Ndipo musafanizidwe ndi makhalidwe a pansi pano: koma mukhale osandulika, mwa kukonzanso kwa mtima wanu, kuti mukazindikire chimene chili chifuno cha Mulungu, chabwino, ndi chokondweretsa, ndi changwiro.

Mutu    |  Mabaibulo
Akolose 2:8

Penyani kuti pasakhale wina wakulanda inu ngati chuma, mwa kukonda nzeru kwake, ndi chinyengo chopanda pake, potsata mwambo wa anthu, potsata zoyamba za dziko lapansi, osati potsata Khristu;

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 2:3-5

ukaitananso luntha, ndi kufuulira kuti ukazindikire;

ukaifunafuna ngati siliva, ndi kuipwaira ngati chuma chobisika;

pompo udzazindikira kuopa Yehova ndi kumdziwadi Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo
2 Timoteyo 3:16-17

Lemba lililonse adaliuzira Mulungu, ndipo lipindulitsa pa chiphunzitso, chitsutsano, chikonzero, chilangizo cha m'chilungamo:

kuti munthu wa Mulungu akhale woyenera, wokonzeka kuchita ntchito iliyonse yabwino.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 11:2-3

Ndipo mzimu wa Yehova udzambalira iye mzimu wanzeru ndi wakuzindikira, mzimu wa uphungu ndi mphamvu, mzimu wakudziwa ndi wakuopa Yehova;

ndipo adzakondwera nako kumuopa Yehova, ndipo sadzaweruza monga apenya maso, sadzadzudzula mwamphekesera:

Mutu    |  Mabaibulo
1 Akorinto 14:29

Ndipo aneneri alankhule awiri kapena atatu, ndi ena azindikire.

Mutu    |  Mabaibulo
2 Petro 2:1

Koma padakhalanso pakati pa anthuwo aneneri onama, monganso padzakhala aphunzitsi onama pakati pa inu, amene adzalowa nayo m'tseri mipatuko yotayikitsa, nadzakana Ambuye amene adawagula, nadzadzitengera iwo okha chitayiko chakudza msanga.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 16:3

Ndipo m'mawa, Lero nkwa mphepo: popeza thambo lili la cheza chodera. Mudziwa kuzindikira za pa nkhope ya thambo; koma zizindikiro za nyengo yino, simungathe kuzindikira.

Mutu    |  Mabaibulo
Yakobo 3:17

Koma nzeru yochokera kumwamba iyamba kukhala yoyera, nikhalanso yamtendere, yaulere, yomvera bwino, yodzala chifundo ndi zipatso zabwino, yopanda tsankho, yosadzikometsera pamaso.

Mutu    |  Mabaibulo
Machitidwe a Atumwi 5:3

Koma Petro anati, Ananiya, Satana anadzaza mtima wako chifukwa ninji kudzanyenga Mzimu Woyera, ndi kupatula pa mtengo wake wa mundawo?

Mutu    |  Mabaibulo
Agalatiya 1:8

Koma ngakhale ife, kapena mngelo wochokera Kumwamba, ngati akakulalikireni Uthenga Wabwino wosati umene tidakulalikirani ife, akhale wotembereredwa.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 16:17-18

Ndipo ndikudandaulirani, abale, yang'anirani iwo akuchita zopatutsana ndi zophunthwitsa, kosalingana ndi chiphunzitsocho munachiphunzira inu; ndipo potolokani pa iwo.

Pakuti otere satumikira Ambuye wathu Khristu, koma mimba yao; ndipo ndi mau osalaza ndi osyasyalika asocheretsa mitima ya osalakwa.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Yohane 2:26-27

Izi ndakulemberani za iwo akusokeretsa inu.

Ndipo inu, kudzoza kumene munalandira kuchokera kwa Iye, kukhala mwa inu, ndipo simusowa kuti wina akuphunzitseni; koma monga kudzoza kwake kukuphunzitsani za zinthu zonse, ndipo kuli koona, sikuli bodza ai, ndipo monga kudaphunzitsa inu, mukhale mwa Iye.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 28:11

Wolemera adziyesa wanzeru; koma wosauka wozindikira aululitsa zake.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 24:24

chifukwa Akhristu onama adzauka, ndi aneneri onama nadzaonetsa zizindikiro zazikulu ndi zozizwa: kotero kuti akanyenge, ngati nkotheka, osankhidwa omwe. Onani ndakuuziranitu pasadafike.

Mutu    |  Mabaibulo
Yohane 10:27

Nkhosa zanga zimva mau anga, ndipo Ine ndizizindikira, ndipo zinditsata Ine.

Mutu    |  Mabaibulo
Luka 12:11-12

Ndipo pamene paliponse adzamuka nanu kumlandu wa m'sunagoge ndi kwa akulu, ndi aulamuliro, musade nkhawa ndi kuti mukadzikanira bwanji, ndipo ndi mau otani, kapena mukanena chiyani;

pakuti Mzimu Woyera adzaphunzitsa inu nthawi yomweyo zimene muyenera kuzinena.

Mutu    |  Mabaibulo
2 Timoteyo 3:5

akukhala nao maonekedwe a chipembedzo, koma mphamvu yake adaikana; kwa iwonso udzipatule.

Mutu    |  Mabaibulo
Yohane 16:13

Koma atadza Iyeyo, Mzimu wa choonadi, adzatsogolera inu m'choonadi chonse; pakuti sadzalankhula za Iye mwini; koma zinthu zilizonse adzazimva, adzazilankhula; ndipo zinthu zilinkudza adzakulalikirani.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Akorinto 2:15

Koma iye amene ali wauzimu ayesa zonse, koma iye yekha sayesedwa ndi mmodzi yense.

Mutu    |  Mabaibulo
Agalatiya 5:22-23

Koma chipatso cha Mzimu ndicho chikondi, chimwemwe, mtendere, kuleza mtima, chifundo, kukoma mtima, chikhulupiriro,

chifatso, chiletso; pokana zimenezi palibe lamulo.

Mutu    |  Mabaibulo
Yakobo 1:5

Koma wina wa inu ikamsowa nzeru, apemphe kwa Mulungu, amene apatsa kwa onse modzala manja, niwosatonza; ndipo adzampatsa iye.

Mutu    |  Mabaibulo
Afilipi 1:3-5

Ndiyamika Mulungu wanga pokumbukira inu ponse;

ndi kukhala nacho inu chilimbano chomwechi mudachiona mwa ine, nimukumva tsopano chili mwa ine.

nthawi zonse m'pembedzero langa lonse la kwa inu nonse ndichita pembedzerolo ndi kukondwera,

chifukwa cha chiyanjano chanu chakuthandizira Uthenga Wabwino, kuyambira tsiku loyambalo, kufikira tsopano lino;

Mutu    |  Mabaibulo
1 Yohane 2:27

Ndipo inu, kudzoza kumene munalandira kuchokera kwa Iye, kukhala mwa inu, ndipo simusowa kuti wina akuphunzitseni; koma monga kudzoza kwake kukuphunzitsani za zinthu zonse, ndipo kuli koona, sikuli bodza ai, ndipo monga kudaphunzitsa inu, mukhale mwa Iye.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Akorinto 3:13-15

ntchito ya yense idzaonetsedwa; pakuti tsikulo lidzaisonyeza, chifukwa kuti yavumbululuka m'moto; ndipo moto wokha udzayesera ntchito ya yense ikhala yotani.

Ngati ntchito ya munthu aliyense ikhala imene anaimangako, adzalandira mphotho.

Ngati ntchito ya wina itenthedwa, zidzaonongeka zake; koma iye yekha adzapulumutsidwa; koma monga momwe mwa moto.

Mutu    |  Mabaibulo
Aefeso 4:14

Kuti tisakhalenso makanda, ogwedezekagwedezeka, natengekatengeka ndi mphepo yonse ya chiphunzitso, ndi tsenga la anthu, ndi kuchenjerera kukatsata chinyengo cha kusocheretsa;

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 139:23-24

Mundisanthule, Mulungu, nimudziwe mtima wanga; mundiyese nimudziwe zolingalira zanga.

Ndipo mupenye ngati ndili nao mayendedwe oipa, nimunditsogolere pa njira yosatha.

Mutu    |  Mabaibulo
Machitidwe a Atumwi 17:11

Amenewa anali mfulu koposa a m'Tesalonika, popeza analandira mau ndi kufunitsa kwa mtima wonse, nasanthula m'malembo masiku onse, ngati zinthu zinali zotero.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 3:21

Mwananga, zisachokere kumaso ako; sunga nzeru yeniyeni ndi kulingalira;

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 10:16

Taonani, Ine ndikutumizani inu monga nkhosa pakati pa mimbulu; chifukwa chake khalani ochenjera monga njoka, ndi oona mtima monga nkhunda.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:66

Mundiphunzitse chisiyanitso ndi nzeru; pakuti ndinakhulupirira malamulo anu.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Petro 5:8

Khalani odzisungira, dikirani; mdani wanu mdierekezi, monga mkango wobuma, ayendayenda ndi kufunafuna wina akamlikwire:

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 2:6-7

Pakuti Yehova apatsa nzeru; kudziwa ndi kuzindikira kutuluka m'kamwa mwake.

Iye asungira oongoka mtima nzeru yeniyeni; ndiye chikopa cha oyenda molunjika;

Mutu    |  Mabaibulo
Akolose 3:2

Lingalirani zakumwamba osati za padziko ai.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 16:17

Ndipo ndikudandaulirani, abale, yang'anirani iwo akuchita zopatutsana ndi zophunthwitsa, kosalingana ndi chiphunzitsocho munachiphunzira inu; ndipo potolokani pa iwo.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 4:7

Nzeru ipambana, tatenga nzeru; m'kutenga kwako konseko utenge luntha.

Mutu    |  Mabaibulo
Yakobo 3:13

Ndani ali wanzeru, ndi waluso mwa inu? Aonetsere ndi mayendedwe ake abwino ntchito zake mu nzeru yofatsa.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 25:9

Adzawatsogolera ofatsa m'chiweruzo; ndipo adzaphunzitsa ofatsa njira yake.

Mutu    |  Mabaibulo
Aefeso 1:17-18

kuti Mulungu wa Ambuye wathu Yesu Khristu, Atate wa ulemerero, akupatseni inu mzimu wa nzeru, ndi wa vumbulutso kuti mukamzindikire Iye;

ndiko kunena kuti maso a mitima yanu awalitsike, kuti mukadziwe inu chiyembekezo cha kuitana kwake nchiyani; chiyaninso chuma cha ulemerero wa cholowa chake mwa oyera mtima,

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:104

Malangizo anu andizindikiritsa; chifukwa chake ndidana nao mayendedwe onse achinyengo.

Mutu    |  Mabaibulo
2 Akorinto 13:5

Dziyeseni nokha, ngati muli m'chikhulupiriro, dzitsimikizeni nokha. Kapena simuzindikira kodi za inu nokha kuti Yesu Khristu ali mwa inu? Mukapanda kukhala osatsimikizidwa.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Akorinto 10:15

Ndinena monga kwa anzeru; lingirirani inu chimene ndinena.

Mutu    |  Mabaibulo
Luka 21:8

Ndipo Iye anati, Yang'anirani musasocheretsedwe; pakuti ambiri adzadza m'dzina langa, nadzanena, Ndine amene; ndipo, Nthawi yayandikira; musawatsate pambuyo pao.

Mutu    |  Mabaibulo
Ahebri 6:1

Mwa ichi, polekana nao mau a chiyambidwe cha Khristu, tipitirire kutsata ukulu msinkhu; osaikanso maziko a kutembenuka mtima kusiyana nazo ntchito zakufa, ndi a chikhulupiriro cha pa Mulungu,

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 14:15

Wachibwana akhulupirira mau onse; koma wochenjera asamalira mayendedwe ake.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 12:9

Chikondano chikhale chopanda chinyengo. Dana nacho choipa; gwirizana nacho chabwino.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 7:6

Musamapatsa chopatulikacho kwa agalu, ndipo musamaponya ngale zanu patsogolo pa nkhumba, kuti zingazipondereze ndi mapazi ao, ndi potembenuka zingang'ambe inu.

Mutu    |  Mabaibulo
Yohane 4:24

Mulungu ndiye mzimu; ndipo omlambira Iye ayenera kumlambira mumzimu ndi m'choonadi.

Mutu    |  Mabaibulo