Dziko lauzimu lilipoli, ndipo mmenemo timayenera kuchita nkhondo ndi pemphero komanso ndi mawu a Mulungu. Nkhondo zazikulu zimamenyedwa m’dziko lauzimu limeneli. M’dziko lauzimuli ndi kumene mphamvu zodabwitsa za Mulungu zimaonekera. Si kumene timangomenyana ndi mizimu yoipa yokha ayi, komanso kumene umapezera zodabwitsa ndi chipambano m’moyo wako.
Pakuti nkhondo yathu si yolimbana ndi anthu, koma ndi olamulira, ndi akuluakulu, ndi mafumu a dziko la mdima lino, ndi makamu a mizimu yoipa m’malo akumwamba. (Aefeso 6:12) Apa Mulungu akutiuza za dziko lauzimu limeneli, kumene ukhoza kupambana pokhapokha wodzazidwa ndi mphamvu zake.
Ngakhale kuti timakhala m’dzikoli, sitimenya nkhondo monga mmene dziko limamenyera. Zida zathu za nkhondo si za dziko lino, koma zili ndi mphamvu ya Mulungu yogumula mipanda. (2 Akorinto 10:3-4)
Ndipo chilichonse mukachichita m'mau kapena muntchito, chitani zonse m'dzina la Ambuye Yesu, ndi kuyamika Mulungu Atate mwa Iye.
Ndikuyamikani ndi kukulemekezani Inu, Mulungu wa makolo anga, pakuti mwandipatsa nzeru ndi mphamvu; ndipo mwandidziwitsa tsopano ichi tachifuna kwa Inu; pakuti mwatidziwitsa mlandu wa mfumu.
Musadere nkhawa konse; komatu m'zonse ndi pemphero, ndi pembedzero, pamodzi ndi chiyamiko, zopempha zanu zidziwike kwa Mulungu.
Ndipo mtendere wa Mulungu wakupambana chidziwitso chonse, udzasunga mitima yanu ndi maganizo anu mwa Khristu Yesu.
M'zonse yamikani; pakuti ichi ndi chifuniro cha Mulungu cha kwa inu, mwa Khristu Yesu.
Tikuyamikani Inu, Mulungu; tiyamika, pakuti dzina lanu lili pafupi; afotokozera zodabwitsa zanu.
Lowani kuzipata zake ndi chiyamiko, ndi kumabwalo ake ndi chilemekezo: Myamikeni; lilemekezeni dzina lake.
polemeretsedwa inu m'zonse kukuolowa manja konse, kumene kuchita mwa ife chiyamiko cha kwa Mulungu.
Lemekezo langa lidzakhala la Inu mu msonkhano waukulu, zowinda zanga ndidzazichita pamaso pa iwo akumuopa Iye.
koma ayamikike Mulungu, amene atipatsa ife chigonjetso mwa Ambuye wathu Yesu Khristu.
Ndidzasamba manja anga mosalakwa; kuti ndizungulire guwa la nsembe lanu, Yehova;
kuti ndimveketse mau a chiyamiko, ndi kulalikira ntchito zanu zonse zozizwa.
Pakuti cholengedwa chonse cha Mulungu nchabwino, ndipo palibe kanthu kayenera kutayika, ngati kalandiridwa ndi chiyamiko;
pakuti kayeretsedwa ndi Mau a Mulungu ndi kupemphera.
Wopereka nsembe yachiyamiko andilemekeza Ine; ndipo kwa iye wosunga mayendedwe ake ndidzamuonetsa chipulumutso cha Mulungu.
Ndipo anathirirana mang'ombe, kulemekeza ndi kuyamika Yehova, ndi kuti, Pakuti ndiye wabwino, pakuti chifundo chake nchosalekeza pa Israele. Nafuula anthu onse ndi chimfuu chachikulu, pomlemekeza Yehova; popeza adamanga maziko a nyumba ya Yehova.
ndi kuyamika Mulungu Atate masiku onse, chifukwa cha zonse, m'dzina la Ambuye wathu Yesu Khristu;
Chifukwa chake monga momwe munalandira Khristu Yesu Ambuye, muyende mwa Iye,
ozika mizu ndi omangirika mwa Iye, ndi okhazikika m'chikhulupiriro, monga munaphunzitsidwa, ndi kuchulukitsa chiyamiko.
Kondwerani nthawi zonse;
Pempherani kosaleka;
M'zonse yamikani; pakuti ichi ndi chifuniro cha Mulungu cha kwa inu, mwa Khristu Yesu.
Yamikani Yehova, itanirani pa dzina lake; bukitsani mwa mitundu ya anthu zochita Iye.
ndipo anachiimikira Yakobo, chikhale malemba, chikhale chipangano chosatha kwa Israele.
Ndi kunena kuti, Ndidzakupatsa iwe dziko la Kanani, gawo la cholandira chako;
pokhala iwo anthu owerengeka, inde, anthu pang'ono, ndi alendo m'mwemo;
nayendayenda kuchokera mtundu wina kufikira mtundu wina, kuchokera ufumu wina kufikira anthu ena.
Sanalola munthu awasautse; ndipo anadzudzula mafumu chifukwa cha iwowa.
Ndi kuti, Musamakhudza odzozedwa anga, musamachitira choipa aneneri anga.
Ndipo anaitana njala igwere dziko; anathyola mchirikizo wonse wa mkate.
Anawatsogozeratu munthu; anamgulitsa Yosefe akhale kapolo:
Anapweteka miyendo yake ndi matangadza; anamgoneka m'unyolo;
kufikira nyengo yakuchitika maneno ake; mau a Yehova anamuyesa.
Muimbireni, muimbireni zomlemekeza; fotokozerani zodabwitsa zake zonse.
Ndiyamika Mulungu wanga nthawi yonse kaamba ka inu, chifukwa cha chisomo cha Mulungu chinapatsidwa kwa inu mwa Khristu Yesu;
Wolemekezeka Mulungu ndi Atate wa Ambuye wathu Yesu Khristu, amene anatidalitsa ife ndi dalitso lonse la mzimu m'zakumwamba mwa Khristu;
Ndipo mtendere wa Khristu uchite ufumu m'mitima yanu, kulingakonso munaitanidwa m'thupi limodzi; ndipo khalani akuyamika.
Mau a Khristu akhalitse mwa inu chichulukire mu nzeru yonse, ndi kuphunzitsa ndi kuyambirirana eni okha ndi masalmo, ndi mayamiko ndi nyimbo zauzimu, ndi kuimbira Mulungu ndi chisomo mumtima mwanu.
Ndipo chilichonse mukachichita m'mau kapena muntchito, chitani zonse m'dzina la Ambuye Yesu, ndi kuyamika Mulungu Atate mwa Iye.
Yehova ndiye mphamvu yanga, ndi chikopa changa; mtima wanga wakhulupirira Iye, ndipo anandithandiza, chifukwa chake mtima wanga ukondwera kwakukulu; ndipo ndidzamyamika nayo nyimbo yanga.
Pamenepo mitengo yonse ya kunkhalango idzafuula mokondwera pamaso pa Yehova; pakuti akudza kudzaweruza dziko lapansi.
Yamikani Yehova; pakuti Iye ndiye wabwino; pakuti chifundo chake nchosatha.
Musadere nkhawa konse; komatu m'zonse ndi pemphero, ndi pembedzero, pamodzi ndi chiyamiko, zopempha zanu zidziwike kwa Mulungu.
Kuti ndibukitse lemekezo lanu lonse; pa bwalo la mwana wamkazi wa Ziyoni, ndidzakondwera nacho chipulumutso chanu.
Ndidzalemekeza Yehova nyengo zonse; kumlemekeza kwake kudzakhala m'kamwa mwanga kosalekeza.
Mwa ichi polandira ufumu wosagwedezeka, tikhale nacho chisomo, chimene tikatumikire nacho Mulungu momkondweretsa, ndi kumchitira ulemu ndi mantha.
Ndidzakuyamikani, Ambuye, Mulungu wanga, ndi mtima wanga wonse; ndipo ndidzalemekeza dzina lanu nthawi zonse.
Lemekeza Yehova, moyo wanga; ndi zonse za m'kati mwanga zilemekeze dzina lake loyera.
Sanatichitira monga mwa zolakwa zathu, kapena kutibwezera monga mwa mphulupulu zathu.
Pakuti monga m'mwamba mutalikira ndi dziko lapansi, motero chifundo chake chikulira iwo akumuopa Iye.
Monga kum'mawa kutanimpha ndi kumadzulo, momwemo anatisiyanitsira kutali zolakwa zathu.
Monga atate achitira ana ake chifundo, Yehova achitira chifundo iwo akumuopa Iye.
Popeza adziwa mapangidwe athu; akumbukira kuti ife ndife fumbi.
Koma munthu, masiku ake akunga udzu; aphuka monga duwa la kuthengo.
Pakuti mphepo ikapitapo pakhala palibe: Ndi malo ake salidziwanso.
Koma chifundo cha Yehova ndicho choyambira nthawi yosayamba kufikira nthawi yosatha kwa iwo akumuopa Iye, ndi chilungamo chake kufikira kwa ana a ana;
kwa iwo akusunga chipangano chake, ndi kwa iwo akukumbukira malangizo ake kuwachita.
Yehova anakhazika mpando wachifumu wake Kumwamba; ndi ufumu wake uchita mphamvu ponsepo.
Lemekeza Yehova, moyo wanga, ndi kusaiwala zokoma zake zonse atichitirazi:
chifukwa kuti, ngakhale anadziwa Mulungu, sanamchitira ulemu wakuyenera Mulungu, ndipo sanamyamika; koma anakhala opanda pake m'maganizo ao, ndipo unada mtima wao wopulukira.
kuti ulemu wanga uimbire Inu, wosakhala chete. Yehova Mulungu wanga, ndidzakuyamikani nthawi zonse.
Chomwecho muwalitse inu kuunika kwanu pamaso pa anthu, kuti pakuona ntchito zanu zabwino, alemekeze Atate wanu wa Kumwamba.
Ntchito zanu zonse zidzakuyamikani, Yehova; ndi okondedwa anu adzakulemekezani.
Adzanenera ulemerero wa ufumu wanu, adzalankhulira mphamvu yanu.
Kudziwitsa ana a anthu zamphamvu zake, ndi ulemerero waukulu wa ufumu wake.
Khulupirira Yehova ndi mtima wako wonse, osachirikizika pa luntha lako;
umlemekeze m'njira zako zonse, ndipo Iye adzaongola mayendedwe ako.
Koma chipatso cha Mzimu ndicho chikondi, chimwemwe, mtendere, kuleza mtima, chifundo, kukoma mtima, chikhulupiriro,
Koma Inu, Mulungu, mudzawatsitsira kudzenje la chionongeko. Anthu okhetsa mwazi ndi achinyengo masiku ao sadzafikira nusu; koma ine ndidzakhulupirira Inu.
Tsiku lomwelo mudzati, Muyamikire Yehova, bukitsani dzina lake, mulalikire machitidwe ake mwa mitundu ya anthu, munene kuti dzina lake lakwezedwa.
Muimbire Yehova; pakuti wachita zaulemerero; chidziwike ichi m'dziko lonse.
Chifukwa chake ndikupemphani inu, abale, mwa zifundo za Mulungu, kuti mupereke matupi anu nsembe yamoyo, yopatulika, yokondweretsa Mulungu, ndiko kupembedza kwanu koyenera.
nati, Ndinatuluka m'mimba ya mai wanga wamaliseche, wamaliseche ndidzamukanso; Yehova anapatsa, Yehova watenga, lidalitsike dzina la Yehova.
Ndinamfuulira Iye pakamwa panga, ndipo ndinamkuza ndi lilime langa.
Ndikadasekera zopanda pake m'mtima mwanga, Ambuye sakadamvera.
Koma Mulungu anamvadi; anamvera mau a pemphero langa.
Imbirani ulemerero wa dzina lake; pomlemekeza mumchitire ulemerero.
Wolemekezeka Mulungu, amene sanandipatutsire ine pemphero langa, kapena chifundo chake.
Koma tiyenera ife tiziyamika Mulungu nthawi zonse chifukwa cha inu, abale okondedwa ndi Ambuye, kuti Mulungu anakusankhani inu kuyambira pachiyambi, mulandire chipulumutso mwa chiyeretso cha Mzimu ndi chikhulupiriro cha choonadi;
Aleluya, Muimbireni Yehova nyimbo yatsopano, ndi chilemekezo chake mu msonkhano wa okondedwa ake.
Ndipo pamene anatenga chikho, anayamika, napatsa iwo, nanena, Mumwere ichi inu nonse,
pakuti ichi ndi mwazi wanga wa pangano wothiridwa chifukwa cha anthu ambiri ku kuchotsa machimo.