Moyoyo, ndikudziwa kuti nthawi zina zinthu zimavuta kwambiri. Timakumana ndi mavuto osiyanasiyana, nthawi zina timamva ngati titayika mtima. Koma dziwani izi, Mulungu watiitana kuti tikhale ngati mitengo yomera m’mphepete mwa mtsinje, yomwe imakhalabe yolimba ngakhale mvula ikugwa bwanji.
Ndikudziwa kuti nthawi zina ukhoza kumva ngati sudzatuluka m’mavuto amene ukukumana nawo. Koma Mulungu, m’chifundo chake chachikulu, nthawi zonse amatilankhula mawu olimbikitsa. Mawu ake ndiwo amene amatilimbitsa, amatipatsa mphamvu kuti tipitirize ulendo wathu. Chofunika ndicho kukhala ndi mtima wofunitsitsa kumvera Mulungu.
Dziwani kuti simuli nokha. Mulungu ali nanu nthawi zonse. Adzachiritsa mabala anu onse ndipo adzakudzazani ndi chimwemwe. Ndikupempherera kuti Mzimu Woyera akubweretsereni mtendere ndi mpumulo umene mukufuna. Mulungu alimbitse mtima wanu ndi kukupatsani mphamvu zatsopano.
M'zonse yamikani; pakuti ichi ndi chifuniro cha Mulungu cha kwa inu, mwa Khristu Yesu.
Yehova akudalitse iwe, nakusunge;
Yehova awalitse nkhope yake pa iwe, nakuchitire chisomo;
Yehova akweze nkhope yake pa iwe, nakupatse mtendere.
Ndiyamika Mulungu wanga pokumbukira inu ponse;
nthawi zonse m'pembedzero langa lonse la kwa inu nonse ndichita pembedzerolo ndi kukondwera,
Pakuti Inu munalenga impso zanga; munandiumba ndisanabadwe ine.
Ndikuyamikani chifukwa kuti chipangidwe changa nchoopsa ndi chodabwitsa; ntchito zanu nzodabwitsa; moyo wanga uchidziwa ichi bwino ndithu.
Ndiyamika Mulungu wanga nthawi yonse kaamba ka inu, chifukwa cha chisomo cha Mulungu chinapatsidwa kwa inu mwa Khristu Yesu;
Ndipo tidziwa kuti amene akonda Mulungu zinthu zonse zithandizana kuwachitira ubwino, ndiwo amene aitanidwa monga mwa kutsimikiza kwa mtima wake.
Chisomo kwa inu ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate wathu, ndi Ambuye Yesu Khristu.
Ndiyamika Mulungu wanga nthawi yonse kaamba ka inu, chifukwa cha chisomo cha Mulungu chinapatsidwa kwa inu mwa Khristu Yesu;
Mwananga, usaiwale malamulo anga, mtima wako usunge malangizo anga;
pakuti adzakuonjezera masiku ambiri, ndi zaka za moyo ndi mtendere.
Ndipo Mulungu wa chiyembekezo adzaze inu ndi chimwemwe chonse ndi mtendere m'kukhulupirira, kuti mukachuluke ndi chiyembekezo, mu mphamvu ya Mzimu Woyera.
Ndisanakulenge iwe m'mimba ndinakudziwa, ndipo usanabadwe ndinakupatula iwe; ndinakuika kuti ukhale mneneri wa mitundu ya anthu.
Koma tsopano atero Yehova, amene anakulenga iwe Yakobo, ndi Iye amene anakupanga iwe Israele, Usaope, chifukwa ndakuombola iwe, ndakutchula dzina lako, iwe uli wanga.
Pamene udulitsa pamadzi ndili pamodzi ndi iwe; ndi pooloka mitsinje sidzakukokolola; pakupyola pamoto sudzapsa; ngakhale lawi silidzakutentha.
Pakuti ndidziwa malingiriro amene ndilingiririra inu, ati Yehova, malingiriro a mtendere, si a choipa, akukupatsani inu adzukulu ndi chiyembekezero.
Iye asungira oongoka mtima nzeru yeniyeni; ndiye chikopa cha oyenda molunjika;
kuti atchinjirize njira za chiweruzo, nadikire khwalala la opatulidwa ake.
Yehova adzanditsirizira za kwa ine: Chifundo chanu, Yehova, chifikira kunthawi zonse: Musasiye ntchito za manja anu.
ngakhale mpaka mudzakalamba Ine ndine, ndipo ngakhale mpaka tsitsi laimvi, Ine ndidzakusenzani inu; ndalenga, ndipo ndidzanyamula; inde, ndidzasenza, ndipo ndidzapulumutsa.
pokhulupirira pamenepo, kuti Iye amene anayamba mwa inu ntchito yabwino, adzaitsiriza kufikira tsiku la Yesu Khristu;
Pakuti ife ndife chipango chake, olengedwa mwa Khristu Yesu, kuchita ntchito zabwino, zimene Mulungu anazipangiratu, kuti tikayende m'menemo.
Chifukwa chakusathedwa ife ndicho chifundo cha Yehova, pakuti chisoni chake sichileka,
chioneka chatsopano m'mawa ndi m'mawa; mukhulupirika ndithu.
Nkokoma kuyamika Yehova, ndi kuimbira nyimbo dzina lanu, Wam'mwambamwamba Inu.
Kuonetsera chifundo chanu mamawa, ndi chikhulupiriko chanu usiku uliwonse.
Tiyeni tiimbire Yehova mokondwera; tifuule kwa thanthwe la chipulumutso chathu.
Tidze nacho chiyamiko pamaso pake, timfuulire Iye mokondwera ndi nyimbo.
Ndikuyamikani chifukwa kuti chipangidwe changa nchoopsa ndi chodabwitsa; ntchito zanu nzodabwitsa; moyo wanga uchidziwa ichi bwino ndithu.
koma iwo amene alindira Yehova adzatenganso mphamvu; adzauluka pamwamba ndi mapiko monga ziombankhanga; adzathamanga koma osalema; adzayenda koma osalefuka.
Ndiyamika Mulungu wanga pokumbukira inu ponse;
nthawi zonse m'pembedzero langa lonse la kwa inu nonse ndichita pembedzerolo ndi kukondwera,
chifukwa cha chiyanjano chanu chakuthandizira Uthenga Wabwino, kuyambira tsiku loyambalo, kufikira tsopano lino;
pokhulupirira pamenepo, kuti Iye amene anayamba mwa inu ntchito yabwino, adzaitsiriza kufikira tsiku la Yesu Khristu;
Khulupirira Yehova ndi mtima wako wonse, osachirikizika pa luntha lako;
umlemekeze m'njira zako zonse, ndipo Iye adzaongola mayendedwe ako.
Pakuti Yehova Mulungu ndiye dzuwa ndi chikopa; Yehova adzapatsa chifundo ndi ulemerero; sadzakaniza chokoma iwo akuyenda angwiro.
Pokhala iwe wa mtengo wapatali pamaso panga, ndi wolemekezeka, ndipo ndakukonda iwe; Ine ndidzakuombola ndi anthu, ndi kupereka anthu m'malo mwa moyo wako.
usaope, pakuti Ine ndili pamodzi ndi iwe; usaopsedwe, pakuti Ine ndine Mulungu wako; ndidzakulimbitsa; inde, ndidzakuthangata; inde, ndidzakuchirikiza ndi dzanja langa lamanja la chilungamo.
Aleluya. Wodala munthu wakuopa Yehova, wakukondwera kwambiri ndi malamulo ake.
Mbeu yake idzakhala yamphamvu pa dziko lapansi; mbadwo wa oongoka mtima udzadalitsidwa.
Chifukwa chake ngati munthu aliyense ali mwa Khristu ali wolengedwa watsopano; zinthu zakale zapita, taonani, zakhala zatsopano.
Yehova ndiye mbusa wanga; sindidzasowa.
Andigonetsa kubusa lamsipu, anditsogolera kumadzi odikha.
Yehova ndiye mbusa wanga; sindidzasowa.
Andigonetsa kubusa lamsipu, anditsogolera kumadzi odikha.
Atsitsimutsa moyo wanga; anditsogolera m'mabande a chilungamo, chifukwa cha dzina lake.
monga yense walandira mphatso, mutumikirane nayo, ngati adindo okoma a chisomo cha mitundumitundu cha Mulungu;
Chinthu chimodzi ndinachipempha kwa Yehova, ndidzachilondola ichi, Kuti ndikhalitse m'nyumba ya Yehova masiku onse a moyo wanga, kupenya kukongola kwake kwa Yehova ndi kufunsitsa m'Kachisi wake.