Mavesi a Baibulo

Zotsatsa


Gulu Laling'ono

MAVESI OLIMBIKITSA

Moyoyo, ndikudziwa kuti nthawi zina zinthu zimavuta kwambiri. Timakumana ndi mavuto osiyanasiyana, nthawi zina timamva ngati titayika mtima. Koma dziwani izi, Mulungu watiitana kuti tikhale ngati mitengo yomera m’mphepete mwa mtsinje, yomwe imakhalabe yolimba ngakhale mvula ikugwa bwanji.

Ndikudziwa kuti nthawi zina ukhoza kumva ngati sudzatuluka m’mavuto amene ukukumana nawo. Koma Mulungu, m’chifundo chake chachikulu, nthawi zonse amatilankhula mawu olimbikitsa. Mawu ake ndiwo amene amatilimbitsa, amatipatsa mphamvu kuti tipitirize ulendo wathu. Chofunika ndicho kukhala ndi mtima wofunitsitsa kumvera Mulungu.

Dziwani kuti simuli nokha. Mulungu ali nanu nthawi zonse. Adzachiritsa mabala anu onse ndipo adzakudzazani ndi chimwemwe. Ndikupempherera kuti Mzimu Woyera akubweretsereni mtendere ndi mpumulo umene mukufuna. Mulungu alimbitse mtima wanu ndi kukupatsani mphamvu zatsopano.


1 Atesalonika 5:18

M'zonse yamikani; pakuti ichi ndi chifuniro cha Mulungu cha kwa inu, mwa Khristu Yesu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 20:4

likupatse cha mtima wako, ndipo likwaniritse upo wako wonse.

Mutu    |  Mabaibulo
Numeri 6:24-26

Yehova akudalitse iwe, nakusunge;

Yehova awalitse nkhope yake pa iwe, nakuchitire chisomo;

Yehova akweze nkhope yake pa iwe, nakupatse mtendere.

Mutu    |  Mabaibulo
Afilipi 1:3-4

Ndiyamika Mulungu wanga pokumbukira inu ponse;

ndi kukhala nacho inu chilimbano chomwechi mudachiona mwa ine, nimukumva tsopano chili mwa ine.

nthawi zonse m'pembedzero langa lonse la kwa inu nonse ndichita pembedzerolo ndi kukondwera,

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 90:12

Mutidziwitse kuwerenga masiku athu motero, kuti tikhale nao mtima wanzeru.

Mutu    |  Mabaibulo
Yuda 1:2

Chifundo ndi mtendere ndi chikondi zikuchulukireni.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 118:24

Tsiku ili ndilo adaliika Yehova; tidzasekera ndi kukondwera m'mwemo.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 139:13-14

Pakuti Inu munalenga impso zanga; munandiumba ndisanabadwe ine.

Ndikuyamikani chifukwa kuti chipangidwe changa nchoopsa ndi chodabwitsa; ntchito zanu nzodabwitsa; moyo wanga uchidziwa ichi bwino ndithu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 139:13

Pakuti Inu munalenga impso zanga; munandiumba ndisanabadwe ine.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 65:11

Muveka chakachi ndi ukoma wanu; ndipo mabande anu akukha zakucha.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Akorinto 1:4

Ndiyamika Mulungu wanga nthawi yonse kaamba ka inu, chifukwa cha chisomo cha Mulungu chinapatsidwa kwa inu mwa Khristu Yesu;

Mutu    |  Mabaibulo
1 Akorinto 1:3-4

Chisomo kwa inu ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate wathu, ndi Ambuye Yesu Khristu.

Koma kwa Iye muli inu mwa Khristu Yesu, amene anayesedwa kwa ife nzeru ya kwa Mulungu, ndi chilungamo ndi chiyeretso ndi chiombolo;

kuti monga mwalembedwa, Iye amene adzitamanda, adzitamande mwa Ambuye.

Ndiyamika Mulungu wanga nthawi yonse kaamba ka inu, chifukwa cha chisomo cha Mulungu chinapatsidwa kwa inu mwa Khristu Yesu;

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 4:10

Tamvera mwananga, nulandire mau anga; ndipo zaka za moyo wako zidzachuluka.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 8:28

Ndipo tidziwa kuti amene akonda Mulungu zinthu zonse zithandizana kuwachitira ubwino, ndiwo amene aitanidwa monga mwa kutsimikiza kwa mtima wake.

Mutu    |  Mabaibulo
3 Yohane 1:2

Wokondedwa, ndipemphera kuti pa zonse ulemere, nukhale bwino, monga mzimu wako ulemera.

Mutu    |  Mabaibulo
Yeremiya 1:5

Ndisanakulenge iwe m'mimba ndinakudziwa, ndipo usanabadwe ndinakupatula iwe; ndinakuika kuti ukhale mneneri wa mitundu ya anthu.

Mutu    |  Mabaibulo
Yeremiya 29:11

Pakuti ndidziwa malingiriro amene ndilingiririra inu, ati Yehova, malingiriro a mtendere, si a choipa, akukupatsani inu adzukulu ndi chiyembekezero.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 9:11

Pakuti mwa ine masiku ako adzachuluka, zaka za moyo wako zidzaonjezedwa.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 43:1-2

Koma tsopano atero Yehova, amene anakulenga iwe Yakobo, ndi Iye amene anakupanga iwe Israele, Usaope, chifukwa ndakuombola iwe, ndakutchula dzina lako, iwe uli wanga.

Inu ndinu mboni zanga, ati Yehova, ndi mtumiki wanga, amene ndakusankha; kuti mundidziwe, ndi kundikhulupirira Ine, ndi kuzindikira, kuti Ine ndine; ndisanakhale Ine, panalibe Mulungu wolengedwa, ngakhale pambuyo panga sipadzakhala wina.

Ine, Inetu ndine Yehova; ndipo palibe Mpulumutsi, koma Ine ndekha.

Ine ndalalikira, ndipo ndikupulumutsa ndi kumvetsa, ndipo panalibe Mulungu wachilendo pakati pa inu; chifukwa chake inu ndinu mboni zanga, ati Yehova, ndipo Ine ndine Mulungu.

Inde chiyambire nthawi Ine ndine, ndipo palibe wina wopulumutsa m'dzanja langa; ndidzagwira ntchito, ndipo ndani adzaletsa?

Atero Yehova, Mombolo wanu, Woyera wa Israele: Chifukwa cha inu ndatumiza ku Babiloni, ndipo ndidzatsitsira iwo onse monga othawa, ngakhale Ababiloni m'ngalawa za kukondwa kwao.

Ine ndine Yehova Woyera wanu, Mlengi wa Israele, Mfumu yanu.

Atero Yehova, amene akonza njira panyanja, ndi popita m'madzi amphamvu;

amene atulutsa galeta ndi kavalo, nkhondo ndi mphamvu; iwo agona pansi pamodzi sadzaukai; iwo atha, azimidwa ngati lawi.

Musakumbukire zidapitazo, ngakhale kulingalira zinthu zakale.

Taonani, Ine ndidzachita chinthu chatsopano; tsopano chidzaoneka; kodi simudzachidziwa? Ndidzakonzadi njira m'chipululu, ndi mitsinje m'zidalala.

Pamene udulitsa pamadzi ndili pamodzi ndi iwe; ndi pooloka mitsinje sidzakukokolola; pakupyola pamoto sudzapsa; ngakhale lawi silidzakutentha.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 3:1-2

Mwananga, usaiwale malamulo anga, mtima wako usunge malangizo anga;

motero nkhokwe zako zidzangoti thee, mbiya zako zidzasefuka vinyo.

Mwananga, usapeputse mwambo wa Yehova, ngakhale kutopa ndi kudzudzula kwake;

pakuti Yehova adzudzula omwe awakonda; monga atate mwana amene akondwera naye.

Wodala ndi wopeza nzeru, ndi woona luntha;

pakuti malonda a nzeru aposa malonda a siliva, phindu lake liposa golide woyengeka.

Mtengo wake uposa ngale; ndipo zonse zikukondweretsa sizilingana naye.

Masiku ambiri ali m'dzanja lamanja lake; chuma ndi ulemu m'dzanja lake lamanzere.

Njira zake zili zokondweretsa, mayendedwe ake onse ndiwo mtendere.

Ndiyo mtengo wa moyo wa akuigwira; wakuiumirira ngwodala.

Yehova anakhazika dziko ndi nzeru; naika zamwamba ndi luntha.

pakuti adzakuonjezera masiku ambiri, ndi zaka za moyo ndi mtendere.

Mutu    |  Mabaibulo
2 Akorinto 9:15

Ayamikike Mulungu chifukwa cha mphatso yakeyake yosatheka kuneneka.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 15:13

Ndipo Mulungu wa chiyembekezo adzaze inu ndi chimwemwe chonse ndi mtendere m'kukhulupirira, kuti mukachuluke ndi chiyembekezo, mu mphamvu ya Mzimu Woyera.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 2:7-8

Iye asungira oongoka mtima nzeru yeniyeni; ndiye chikopa cha oyenda molunjika;

kuti atchinjirize njira za chiweruzo, nadikire khwalala la opatulidwa ake.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 46:4

ngakhale mpaka mudzakalamba Ine ndine, ndipo ngakhale mpaka tsitsi laimvi, Ine ndidzakusenzani inu; ndalenga, ndipo ndidzanyamula; inde, ndidzasenza, ndipo ndidzapulumutsa.

Mutu    |  Mabaibulo
Afilipi 4:4

Kondwerani mwa Ambuye nthawi zonse: ndibwerezanso kutero, kondwerani.

Mutu    |  Mabaibulo
Afilipi 1:6

pokhulupirira pamenepo, kuti Iye amene anayamba mwa inu ntchito yabwino, adzaitsiriza kufikira tsiku la Yesu Khristu;

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 138:8

Yehova adzanditsirizira za kwa ine: Chifundo chanu, Yehova, chifikira kunthawi zonse: Musasiye ntchito za manja anu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 9:7

Koma Yehova akhala chikhalire, anakonzeratu mpando wachifumu wake kuti aweruze.

Mutu    |  Mabaibulo
Maliro 3:22-23

Chifukwa chakusathedwa ife ndicho chifundo cha Yehova, pakuti chisoni chake sichileka,

chioneka chatsopano m'mawa ndi m'mawa; mukhulupirika ndithu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 92:1-2

Nkokoma kuyamika Yehova, ndi kuimbira nyimbo dzina lanu, Wam'mwambamwamba Inu.

Koma munakweza nyanga yanga ngati ya njati; anandidzoza mafuta atsopano.

Diso langa lapenya chokhumba ine pa iwo ondilalira, m'makutu mwanga ndamva chokhumba ine pa iwo akuchita zoipa akundiukira.

Wolungama adzaphuka ngati mgwalangwa; adzakula ngati mkungudza wa ku Lebanoni.

Iwo ookedwa m'nyumba ya Yehova, adzaphuka m'mabwalo a Mulungu wathu.

Atakalamba adzapatsanso zipatso; adzadzazidwa ndi madzi nadzakhala abiriwiri,

kulalikira kuti Yehova ngwolunjika; Iye ndiye thanthwe langa, ndipo mwa Iye mulibe chosalungama.

Kuonetsera chifundo chanu mamawa, ndi chikhulupiriko chanu usiku uliwonse.

Mutu    |  Mabaibulo
Aefeso 2:10

Pakuti ife ndife chipango chake, olengedwa mwa Khristu Yesu, kuchita ntchito zabwino, zimene Mulungu anazipangiratu, kuti tikayende m'menemo.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 139:14

Ndikuyamikani chifukwa kuti chipangidwe changa nchoopsa ndi chodabwitsa; ntchito zanu nzodabwitsa; moyo wanga uchidziwa ichi bwino ndithu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 95:1-2

Tiyeni tiimbire Yehova mokondwera; tifuule kwa thanthwe la chipulumutso chathu.

Zaka makumi anai mbadwo uwu unandimvetsa chisoni, ndipo ndinati, Iwo ndiwo anthu osokerera mtima, ndipo sadziwa njira zanga.

Chifukwa chake ndinalumbira mu mkwiyo wanga, ngati adzalowa mpumulo wanga.

Tidze nacho chiyamiko pamaso pake, timfuulire Iye mokondwera ndi nyimbo.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 21:4

Anakupemphani moyo, mwampatsa iye; mwamtalikitsira masiku kunthawi za nthawi.

Mutu    |  Mabaibulo
Mlaliki 3:1

Kanthu kalikonse kali ndi nthawi yake ndi chofuna chilichonse cha pansi pa thambo chili ndi mphindi yake;

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 40:31

koma iwo amene alindira Yehova adzatenganso mphamvu; adzauluka pamwamba ndi mapiko monga ziombankhanga; adzathamanga koma osalema; adzayenda koma osalefuka.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 126:3

Yehova anatichitira ife zazikulu; potero tikhala okondwera.

Mutu    |  Mabaibulo
Afilipi 1:3-6

Ndiyamika Mulungu wanga pokumbukira inu ponse;

ndi kukhala nacho inu chilimbano chomwechi mudachiona mwa ine, nimukumva tsopano chili mwa ine.

nthawi zonse m'pembedzero langa lonse la kwa inu nonse ndichita pembedzerolo ndi kukondwera,

chifukwa cha chiyanjano chanu chakuthandizira Uthenga Wabwino, kuyambira tsiku loyambalo, kufikira tsopano lino;

pokhulupirira pamenepo, kuti Iye amene anayamba mwa inu ntchito yabwino, adzaitsiriza kufikira tsiku la Yesu Khristu;

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 3:5-6

Khulupirira Yehova ndi mtima wako wonse, osachirikizika pa luntha lako;

umlemekeze m'njira zako zonse, ndipo Iye adzaongola mayendedwe ako.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 12:12

kondwerani m'chiyembekezo, pirirani m'masautso; limbikani chilimbikire m'kupemphera.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 91:16

Ndidzamkhutitsa ndi masiku ambiri, ndi kumuonetsera chipulumutso changa.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 37:4

Udzikondweretsenso mwa Yehova; ndipo Iye adzakupatsa zokhumba mtima wako.

Mutu    |  Mabaibulo
Agalatiya 6:9

Koma tisaleme pakuchita zabwino; pakuti pa nyengo yake tidzatuta tikapanda kufooka.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 4:7

Nzeru ipambana, tatenga nzeru; m'kutenga kwako konseko utenge luntha.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 84:11

Pakuti Yehova Mulungu ndiye dzuwa ndi chikopa; Yehova adzapatsa chifundo ndi ulemerero; sadzakaniza chokoma iwo akuyenda angwiro.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 43:4

Pokhala iwe wa mtengo wapatali pamaso panga, ndi wolemekezeka, ndipo ndakukonda iwe; Ine ndidzakuombola ndi anthu, ndi kupereka anthu m'malo mwa moyo wako.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 112:1-2

Aleluya. Wodala munthu wakuopa Yehova, wakukondwera kwambiri ndi malamulo ake.

Woipa adzaziona, nadzapsa mtima; adzakukuta mano, nadzasungunuka; chokhumba oipa chidzatayika.

Mbeu yake idzakhala yamphamvu pa dziko lapansi; mbadwo wa oongoka mtima udzadalitsidwa.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 41:10

usaope, pakuti Ine ndili pamodzi ndi iwe; usaopsedwe, pakuti Ine ndine Mulungu wako; ndidzakulimbitsa; inde, ndidzakuthangata; inde, ndidzakuchirikiza ndi dzanja langa lamanja la chilungamo.

Mutu    |  Mabaibulo
2 Akorinto 5:17

Chifukwa chake ngati munthu aliyense ali mwa Khristu ali wolengedwa watsopano; zinthu zakale zapita, taonani, zakhala zatsopano.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 23:1-2

Yehova ndiye mbusa wanga; sindidzasowa.

Andigonetsa kubusa lamsipu, anditsogolera kumadzi odikha.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 23:1-3

Yehova ndiye mbusa wanga; sindidzasowa.

Andigonetsa kubusa lamsipu, anditsogolera kumadzi odikha.

Atsitsimutsa moyo wanga; anditsogolera m'mabande a chilungamo, chifukwa cha dzina lake.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Petro 4:10

monga yense walandira mphatso, mutumikirane nayo, ngati adindo okoma a chisomo cha mitundumitundu cha Mulungu;

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 27:4

Chinthu chimodzi ndinachipempha kwa Yehova, ndidzachilondola ichi, Kuti ndikhalitse m'nyumba ya Yehova masiku onse a moyo wanga, kupenya kukongola kwake kwa Yehova ndi kufunsitsa m'Kachisi wake.

Mutu    |  Mabaibulo

Pemphero kwa Mulungu

Ambuye Wamphamvuzonse! Inu nokha ndinu woyenera kutambasula ulemu wonse ndi kulambira. Ndikukupemphani kudzera mwa Ambuye wathu Yesu Khristu kuti mundipatse mphamvu zatsopano, ndatopa ndipo ndataya mtima wopitirira. Nthawi zina ndimamva ngati ndiyenera kusiya zonse, ndichifukwa chake ndikupempha kuti munditsanulire chisomo ndi chifundo pa moyo wanga kuti ndipitirire ku cholinga changa popanda kuima. Mawu anu amati: "Chifundo changa ndi linga langa, mphamvu yanga ndi wopulumutsa wanga, chishango changa, amene ndimakhulitsa; amene aweramitsa anthu pansi panga." Ngakhale mavuto a kuntchito ndi kunyumba akufuna kundigwetsa, ndidzakutambasulani Ambuye ndipo ndidzakhala ndikuyembekezera thandizo lanu. Nditsogolereni Mzimu Woyera kuti ndithamangire kwa Yesu popanda kutopa kapena kudandaula. Ndikufuna kukhala wolimba mtima ndi wamphamvu, koma ndikufunika thandizo lanu ndi mphamvu zanu Ambuye. Lero ndikulengeza kuti Mulungu ndiye chishango changa ndi Ambuye wanga, inu ndinu thanthwe langa, wochirikiza wanga, wopulumutsa wanga, inu ndinu mphamvu yanga ndi chishango changa, chipulumutso changa champhamvu, pothawirapo panga, ndipo chifukwa chake sindidzagwa kapena kusunthika pa thanthwe lomwe ndi Khristu. Munditsuke ndi kundikonza Ambuye, lamulirani maganizo anga, malingaliro anga ndi mbali zonse za moyo wanga, mundipatse chimwemwe chanu ndi mtendere wanu. M'dzina la Yesu. Ameni.