Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -

Masalimo 108 - Buku Lopatulika


Davide aimbira Mulungu womgonjetsera adani
( Mas. 57.7-11 ; 60.5-12 )
Nyimbo. Salimo la Davide.

1 Wakhazikika mtima wanga, Mulungu; ndidzaimba, inde ndidzaimba zolemekeza, ndiko ulemerero wanga.

2 Galamukani, chisakasa ndi zeze; ndidzauka ndekha mamawa.

3 Ndidzakuyamikani mwa mitundu ya anthu, Yehova: ndipo ndidzaimba zakukulemekezani mwa anthu.

4 Pakuti chifundo chanu nchachikulu kupitirira kumwamba, ndi choonadi chanu kufikira mitambo.

5 Kwezekani pamwamba pa thambo, Mulungu; ndi ulemerero wanu pamwamba padziko lonse lapansi,

6 kuti okondedwa anu alanditsidwe, pulumutsani ndi dzanja lanu lamanja ndipo mutivomereze.

7 Mulungu analankhula m'chiyero chake; ndidzakondwerera: ndidzagawa Sekemu; ndidzayesa muyeso chigwa cha Sukoti.

8 Giliyadi ndi wanga, Manase ndi wanga; ndi Efuremu ndiye mphamvu ya mutu wanga; Yuda ndiye wolamulira wanga.

9 Mowabu ndiye mkhate wanga; pa Edomu ndidzaponya nsapato yanga; ndidzafuulira Filistiya.

10 Adzandifikitsa ndani m'mzinda wa m'linga? Adzanditsogolera ndani ku Edomu?

11 Si ndinu Mulungu, amene mwatitaya osatuluka nao magulu athu?

12 Tithandizeni mumsauko; pakuti chipulumutso cha munthu ndi chabe.

13 Mwa Mulungu tidzachita molimbika mtima: Ndipo Iye adzapondereza otisautsa.

Bible Society of Malawi

Bible Society of Malawi
Titsatireni:



Zotsatsa