Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 69:18 - Buku Lopatulika

Yandikizani moyo wanga, ndi kuuombola; ndipulumutseni chifukwa cha adani anga.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Yandikizani moyo wanga, ndi kuuombola; ndipulumutseni chifukwa cha adani anga.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Senderani pafupi, mundiwombole, mundipulumutse kwa adani anga.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Bwerani pafupi ndi kundilanditsa; ndiwomboleni chifukwa cha adani anga.

Onani mutuwo



Masalimo 69:18
15 Mawu Ofanana  

Kapena, Mundilanditse m'dzanja la mdani? Kapena, Mundiombole m'dzanja la oopsa?


Muimiranji patali, Yehova? Mubisaliranji m'nyengo za nsautso?


Anatumizira anthu ake chipulumutso; analamulira chipangano chake kosatha; dzina lake ndilo loyera ndi loopedwa.


Fulumirani ndiyankheni, Yehova; mzimu wanga ukutha. Musandibisire nkhope yanu; ndingafanane nao akutsikira kudzenje.


Mulungu wanga, Mulungu wanga, mwandisiyiranji ine? Mukhaliranji kutali kwa chipulumutso changa, ndi kwa mau a kubuula kwanga?


Ng'ombe zamphongo zambiri zandizinga; mphongo zolimba za ku Basani zandizungulira.


Koma Inu, Yehova, musakhale kutali; mphamvu yanga Inu, mufulumire kundithandiza.


Landitsani moyo wanga kulupanga; wokondedwa wanga kumphamvu ya galu,


Musandibisire ine nkhope yanu; musachotse kapolo wanu ndi kukwiya. Inu munakhala thandizo langa; musanditaye, ndipo musandisiye Mulungu wa chipulumutso changa.


Ndipereka mzimu wanga m'dzanja lanu; mwandiombola, Inu Yehova, Mulungu wa choonadi.


Koma Mulungu adzaombola moyo wanga kumphamvu ya manda. Pakuti adzandilandira ine.


Inu, chiyembekezo cha Israele, Mpulumutsi wake nthawi ya msauko, bwanji mukhala ngati mlendo m'dziko, ngati woyendayenda amene apatuka usiku?


Munayandikira tsiku la kukuitanani ine; munati, Usaope.


Ndikadapanda kuopa mkwiyo wa pa mdani, angayese molakwa outsana nao, anganene, Lakwezeka dzanja lathu, ndipo Yehova sanachite ichi chonse.


Akadzamva ichi Akanani ndi okhala m'dziko onse, adzatizinga ndi kuduliratu dzina lathu padziko lapansi; ndipo mudzachitiranji dzina lanu lalikulu?