Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 140:5 - Buku Lopatulika

Odzikuza ananditchera msampha, nandibisira zingwe; anatcha ukonde m'mphepete mwa njira; ananditchera makwekwe.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Odzikuza ananditchera msampha, nandibisira zingwe; anatcha ukonde m'mphepete mwa njira; ananditchera makwekwe.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Anthu odzikuza anditchera msampha mobisika, atchera ukonde wa zingwe, anditchera misampha m'mbali mwa njira.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Anthu odzikuza anditchera msampha mobisika; iwo atchera zingwe za maukonde awo ndipo anditchera misampha pa njira yanga. Sela

Onani mutuwo



Masalimo 140:5
21 Mawu Ofanana  

Msampha udzamgwira kuchitendeni, ndi khwekhwe lidzamkola.


Oipa ananditchera msampha; koma sindinasokere m'malangizo anu.


Odzikuza anandipangira bodza: Ndidzasunga malangizo anu ndi mtima wanga wonse.


Odzikuza anandikumbira mbuna, ndiwo osasamalira chilamulo chanu.


Pamene mzimu wanga unakomoka m'kati mwanga, munadziwa njira yanga. M'njira ndiyendamo ananditchera msampha.


Mundionjole mu ukonde umene ananditchera mobisika. Pakuti Inu ndinu mphamvu yanga.


Pakuti ananditchera ukonde wao m'mbunamo kopanda chifukwa, anakumbira moyo wanga dzenje kopanda chifukwa.


Phazi la akudzikuza lisandifikire ine, ndi dzanja la oipa lisandichotse.


Mundiweruzire, Mulungu, ndipo mundinenere mlandu kwa anthu opanda chifundo. Mundilanditse kwa munthu wonyenga ndi wosalungama.


Ananditchera ukonde apo ndiyenda; moyo wanga wawerama. Anandikumbira mbuna patsogolo panga; anagwa m'kati mwake iwo okha.


Usabisalire, woipa iwe, pomanga wolungama; usapasule popuma iyepo.


Wosyasyalika mnzake atcherera mapazi ake ukonde.


Ndipo iwo anati, Tiyeni, tilingalire Yeremiya chomchitira choipa; pakuti chilamulo sichidzathera wansembe, kapena uphungu wanzeru, kapena mau mneneri. Tiyeni, timpande iye ndi lilime, tisamvere iye mau ake ali onse.


Kodi choipa chibwezedwe pa chabwino? Pakuti akumbira moyo wanga dzenje. Mukumbukire kuti ndinaima pamaso panu kuwanenera zabwino, kuwachotsera iwo ukali wanu.


Mfuu umvekedwe m'nyumba zao, pamene muwatengera khamu la nkhondo dzidzidzi; pakuti akumba dzenje lakundigwira ine, anabisira mapazi anga misampha.