Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -

Masalimo 140 - Buku Lopatulika


Davide apempha Mulungu amlanditse kwa mdani woipa wamphamvu
Kwa Mkulu wa Nyimbo: Salimo la Davide.

1 Ndilanditseni, Yehova, kwa munthu woipa; ndisungeni kwa munthu wachiwawa;

2 amene adzipanga zoipa mumtima mwao; masiku onse amemeza nkhondo.

3 Anola lilime lao ngati njoka; pansi pa milomo yao pali ululu wa mphiri.

4 Ndilindireni Yehova, ndisalowe m'manja mwa woipa; ndisungeni kwa munthu wachiwawa; kwa iwo akuti akankhe mapazi anga.

5 Odzikuza ananditchera msampha, nandibisira zingwe; anatcha ukonde m'mphepete mwa njira; ananditchera makwekwe.

6 Ndinati kwa Yehova, Inu ndinu Mulungu wanga; munditcherere khutu mau a kupemba kwanga, Yehova.

7 Yehova Ambuye, ndinu mphamvu ya chipulumutso changa, munandiphimba mutu wanga tsiku lakulimbana nkhondo.

8 Yehova, musampatse woipa zokhumba iye; musamthandize zodzipanga zake; angadzikuze.

9 Kunena za mutu wao wa iwo akundizinga, choipa cha milomo yao chiwaphimbe.

10 Makala amoto awagwere; aponyedwe kumoto; m'maenje ozama, kuti asaukenso.

11 Munthu wamlomo sadzakhazikika padziko lapansi; choipa chidzamsaka munthu wachiwawa kuti chimgwetse.

12 Ndidziwa kuti Yehova adzanenera wozunzika mlandu, ndi kuweruzira aumphawi.

13 Indedi, olungama adzayamika dzina lanu; oongoka mtima adzakhala pamaso panu.

Bible Society of Malawi

Bible Society of Malawi
Titsatireni:



Zotsatsa