Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 13:4 - Buku Lopatulika

kuti anganene mdani wanga, Ndamgonjetsa; ndipo angakondwere otsutsana nane posunthika ine.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

kuti anganene mdani wanga, Ndamlaka; ndipo angakondwere otsutsana nane posunthika ine.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Mdani wanga asati, “Ndampambana,” adani anga onse asakondwere poona kuti ndagwa.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

mdani wanga adzati, “Ndamugonjetsa,” ndipo adani anga adzakondwera pamene ine ndagwa.

Onani mutuwo



Masalimo 13:4
17 Mawu Ofanana  

Ndipo tsopano, kamphindi, Yehova Mulungu wathu wationetsa chisomo, kutisiyira chipulumutso, ndi kutipatsa chichiri m'malo mwake mopatulika; kuti Mulungu wathu atipenyetse m'maso mwathu, ndi kutitsitsimutsa pang'ono mu ukapolo wathu.


Anena m'mtima mwake, Mulungu waiwala; wabisa nkhope yake; sapenya nthawi zonse.


Popeza sadzagwedezeka nthawi zonse; wolungama adzakumbukika ku nthawi yosatha.


Mulungu wanga, ndakhulupirira Inu, ndisachite manyazi; adani anga asandiseke ine.


Adani anga asandikondwerere ine monyenga; okwiya nane kopanda chifukwa asanditsinzinire.


Asanene mumtima mwao, Hede, momwemo! Asanene, Tammeza iye.


Pakuti ndinati, Asakondwerere ine; pakuterereka phazi langa, asadzikuze pa ine.


Umsenze Yehova nkhawa zako, ndipo Iye adzakugwiriziza, nthawi zonse sadzalola wolungama agwedezeke.


Iye yekhayo ndiye thanthwe langa ndi chipulumutso changa; msanje wanga, sindidzagwedezeka kwakukulu.


Iye yekhayo ndiye thanthwe langa ndi chipulumutso changa, msanje wanga, sindidzagwedezeka.


Ukani, Yehova, asalimbike munthu; amitundu aweruzidwe pankhope panu.


Munthu sadzakhazikika ndi udyo, muzu wa olungama sudzasunthidwa.


Ndipo adzamenyana ndi iwe; koma sadzakuposa; chifukwa Ine ndili ndi iwe, ati Yehova, kukulanditsa.


Chifukwa cha zimenezi ndilira; diso langa, diso langatu likudza madzi: Pakuti wonditonthoza, wotsitsimutsa moyo wanga, anditalikira; ana anga asungulumwa, pakuti adaniwo apambana.


Akadzamva ichi Akanani ndi okhala m'dziko onse, adzatizinga ndi kuduliratu dzina lathu padziko lapansi; ndipo mudzachitiranji dzina lanu lalikulu?