Mavesi a Baibulo

Zotsatsa


Gulu Laling'ono

Mavesi odalitsa

Pali anthu apadera amene Mulungu waika pa moyo wako, ndi anthu odalitsidwa ndi okondedwa, amene tikuwadalitsa m'dzina la Yesu. M'Baibulo muli mavesi ambiri oti tithokoze ndi kudalitsa miyoyo imeneyi.

Sitimadalitsa anthu okhawo, koma mabanja athu, dziko lathu, ndi abale athu mwa Khristu. “Yehova akudalitse, nakusunge; Yehova akuunikire nkhope yake pa iwe, nakuchitire chifundo; Yehova akweze nkhope yake pa iwe, nakupatsenso mtendere.” (Numeri 6:24-26)

Timadalitsanso abusa athu amene Mulungu amawagwiritsa ntchito. “Pakuti Inu, Yehova, mudzadalitsa wolungama; Mudzam'zungulira ndi chiyanjo chanu ngati ndi chishango.” (Salimo 5:12)

Sitiyenera kudalitsa okhawo atichitira zabwino, chifukwa Mulungu watilamula kuti tizidalitsa ngakhale atichitira zoipa. “Dalitsani iwo akutikuzunzani; dalitsani, musatemberere.” (Aroma 12:14)


Masalimo 30:11-12

Munasanduliza kulira kwanga kukhale kusekera; munandivula chiguduli changa, ndipo munandiveka chikondwero,

kuti ulemu wanga uimbire Inu, wosakhala chete. Yehova Mulungu wanga, ndidzakuyamikani nthawi zonse.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 118:24

Tsiku ili ndilo adaliika Yehova; tidzasekera ndi kukondwera m'mwemo.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 68:3

Koma olungama akondwere; atumphe ndi chimwemwe pamaso pa Mulungu; ndipo asekere nacho chikondwerero.

Mutu    |  Mabaibulo
Eksodo 34:22

Ndipo uzichita chikondwerero cha Masabata, ndicho chikondwerero cha Zipatso zoyamba za Masika a tirigu, ndi chikondwerero cha Kututa pakutha pa chaka.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 101:1

Ndidzaimba zachifundo ndi chiweruzo; ndidzaimba zakukulemekezani Inu, Yehova.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 98:4-5

Fuulirani kwa Yehova, inu, dziko lonse lapansi; kuwitsani ndi kufuulira mokondwera; inde, imbirani zomlemekeza.

Muimbireni Yehova zomlemekeza ndi zeze; ndi zeze ndi mau a salimo.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 42:10

Imbirani Yehova nyimbo yatsopano, ndi matamando ake kuchokera ku malekezero a dziko lapansi; inu amene mutsikira kunyanja, ndi zonse zili m'menemo, zisumbu ndi okhala mommo.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Mbiri 16:9

Muimbireni, muimbireni zomlemekeza; fotokozerani zodabwitsa zake zonse.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 109:30

Ndidzayamika Yehova kwakukulu pakamwa panga; ndi pakati pa anthu aunyinji ndidzamlemekeza.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 47:1

Ombani m'manja, mitundu yonse ya anthu; fuulirani kwa Mulungu ndi liu la kuimbitsa.

Mutu    |  Mabaibulo
Deuteronomo 16:9-10

Mudziwerengere masabata asanu ndi awiri; muyambe kuwerenga masabata asanu ndi awiri poyambira kusenga tirigu wachilili.

Ndipo muchitire Yehova Mulungu wanu chikondwerero cha Masabata, ndiwo msonkho waufulu wa dzanja lanu, umene mupereke monga Yehova Mulungu wanu akudalitsani.

Mutu    |  Mabaibulo
Eksodo 12:14

Ndipo tsiku lino lidzakhala kwa inu chikumbutso, muzilisunga la chikondwerero cha Yehova; ku mibadwo yanu muzilisunga la chikondwerero, likhale lemba losatha.

Mutu    |  Mabaibulo
Numeri 9:2

Ana a Israele achite Paska pa nyengo yoikidwa.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 147:1

Aleluya; Pakuti kuimbira zomlemekeza Mulungu wathu nkokoma; pakuti chikondwetsa ichi, chilemekezo chiyenera.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 48:1

Yehova ndiye wamkulu, ayenera kulemekezekadi, m'mudzi wa Mulungu wathu, m'phiri lake loyera.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 66:8

Lemekezani Mulungu wathu, mitundu ya anthu inu, ndipo mumveketse liu la chilemekezo chake.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 30:29

Inu mudzakhala ndi nyimbo, monga usiku, podya phwando lopatulika; ndi mtima wokondwa, monga pomuka wina ndi chitoliro, kufikira kuphiri la Yehova, kuthanthwe la Israele.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 118:15

M'mahema a olungama muli liu lakufuula mokondwera Dzanja lamanja la Yehova ndi la chipulumutso:

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 100:1-2

Fuulirani kwa Yehova, inu, dziko lonse lapansi.

Tumikirani Yehova ndi chikondwerero: Idzani pamaso pake ndi kumuimbira mokondwera.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 148:13-14

Alemekeze dzina la Yehova; pakuti dzina lake lokha ndi lokwezeka; ulemerero wake uli pamwamba pa dziko lapansi ndi thambo.

Ndipo anakweza nyanga ya anthu ake, chilemekezo cha okondedwa ake onse; ndiwo ana a Israele, anthu a pafupi pa Iye. Aleluya.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 25:1

Yehova, Inu ndinu Mulungu wanga, ndidzakukuzani Inu, ndidzatamanda dzina lanu, chifukwa mwachita zinthu zodabwitsa, ngakhale zauphungu zakale, mokhulupirika ndi m'zoonadi.

Mutu    |  Mabaibulo
2 Samueli 22:4

Ndidzaitana kwa Yehova amene ayenera timtamande; chomwecho ndidzapulumutsidwa kwa adani anga.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 75:9

Koma ine ndidzalalikira kosalekeza, ndidzaimbira zomlemekeza Mulungu wa Yakobo.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 40:3

Ndipo anapatsa nyimbo yatsopano m'kamwa mwanga, chilemekezo cha kwa Mulungu wanga; ambiri adzachiona, nadzaopa, ndipo adzakhulupirira Yehova.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Mbiri 16:8

Yamikani Yehova, itanani dzina lake; bukitsani mwa mitundu ya anthu zochita Iye.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Mbiri 16:25

Pakuti Yehova ali wamkulu, nayenera kulemekezedwa kwakukulu; ayenera amuope koposa milungu yonse.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 7:17

Ndidzayamika Yehova monga mwa chilungamo chake; ndipo ndidzaimbira Yehova Wam'mwambamwamba.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 135:1-3

Aleluya; Lemekezani dzina la Yehova! Lemekezani inu atumiki a Yehova.

Inu akuimirira m'nyumba ya Yehova, m'mabwalo a nyumba ya Mulungu wathu.

Lemekezani Yehova; pakuti Yehova ndiye wabwino; muimbire zolemekeza dzina lake; pakuti nkokondweretsa kutero.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:171

Milomo yanga itulutse chilemekezo; popeza mundiphunzitsa malemba anu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 145:21

Pakamwa panga padzanena chilemekezo cha Yehova; ndi zinthu zonse zilemekeze dzina lake loyera kunthawi za nthawi.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 18:49

Chifukwa chake Yehova ndidzakuyamikani mwa amitundu, ndipo dzina lanu ndidzaliimbira.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 95:1-3

Tiyeni tiimbire Yehova mokondwera; tifuule kwa thanthwe la chipulumutso chathu.

Tidze nacho chiyamiko pamaso pake, timfuulire Iye mokondwera ndi nyimbo.

Pakuti Yehova ndiye Mulungu wamkulu; ndi mfumu yaikulu yoposa milungu yonse.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 69:30

Ndidzalemekeza dzina la Mulungu ndi kuliimbira, ndipo ndidzambukitsa ndi kumyamika.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 116:19

M'mabwalo a nyumba ya Yehova, pakati pa inu, Yerusalemu. Aleluya.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 145:7

Adzabukitsa chikumbukiro cha ubwino wanu waukulu, nadzaimbira chilungamo chanu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 81:1-3

Imbitsirani Mulungu ndiye mphamvu yathu; fuulirani kwa Mulungu wa Yakobo.

Utsani salimo, bwera nakoni kalingaka, zeze wokondwetsa pamodzi ndi chisakasa.

Ombani lipenga, pokhala mwezi, utakula mwezi, tsiku la phwando lathu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 47:6

Imbirani Mulungu, imbirani; imbirani mfumu yathu, imbirani.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 68:32

Imbirani Mulungu, maufumu a dziko lapansi inu; imbirani Ambuye zomlemekeza.

Mutu    |  Mabaibulo
Nehemiya 8:10

Nanena naonso, Mukani, mukadye zonona, mukamwe zozuna, nimumtumizire gawo lake iye amene sanamkonzeretu kanthu; chifukwa lero ndilo lopatulikira Ambuye wathu; ndipo musamachita chisoni; pakuti chimwemwe cha Yehova ndicho mphamvu yanu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 95:2

Tidze nacho chiyamiko pamaso pake, timfuulire Iye mokondwera ndi nyimbo.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 126:3

Yehova anatichitira ife zazikulu; potero tikhala okondwera.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 34:3

Bukitsani pamodzi ndine ukulu wa Yehova, ndipo tikweze dzina lake pamodzi.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 50:14

Pereka kwa Mulungu nsembe yachiyamiko; numchitire Wam'mwambamwamba chowinda chako.

Mutu    |  Mabaibulo
Nehemiya 12:27

Ndipo popereka linga la Yerusalemu anafunafuna Alevi m'malo mwao monse, kubwera nao ku Yerusalemu, kuti achite kuperekaku mokondwera, ndi mayamiko, ndi kuimbira, ndi nsanje, zisakasa, ndi azeze.

Mutu    |  Mabaibulo
Aefeso 5:19

ndi kudzilankhulira nokha ndi masalmo, ndi mayamiko, ndi nyimbo zauzimu, kuimbira ndi kuimba m'malimba Ambuye mumtima mwanu;

Mutu    |  Mabaibulo
Akolose 3:16

Mau a Khristu akhalitse mwa inu chichulukire mu nzeru yonse, ndi kuphunzitsa ndi kuyambirirana eni okha ndi masalmo, ndi mayamiko ndi nyimbo zauzimu, ndi kuimbira Mulungu ndi chisomo mumtima mwanu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 149:1-3

Aleluya, Muimbireni Yehova nyimbo yatsopano, ndi chilemekezo chake mu msonkhano wa okondedwa ake.

Akondwere Israele mwa Iye amene anamlenga; ana a Ziyoni asekere mwa mfumu yao.

Alemekeze dzina lake ndi kuthira mang'ombe; amuimbire zomlemekeza ndi lingaka ndi zeze.

Mutu    |  Mabaibulo
Zekariya 9:9

Kondwera kwambiri, mwana wamkazi wa Ziyoni; fuula mwana wamkazi wa Yerusalemu; taona, Mfumu yako ikudza kwa iwe; ndiye wolungama, ndi mwini chipulumutso; wofatsa ndi wokwera pa bulu, ndi mwana wamphongo wa bulu.

Mutu    |  Mabaibulo
Luka 19:37-40

Ndipo pakuyandikira Iye tsono potsetsereka pake pa phiri la Azitona, unyinji wonse wa ophunzira anayamba kukondwera ndi kuyamika Mulungu ndi mau akulu, chifukwa cha ntchito zonse zamphamvu anaziona;

nanena, Wolemekezeka Mfumuyo ikudza m'dzina la Ambuye; mtendere m'Mwamba, ndi ulemerero m'Mwambamwamba.

Ndipo Afarisi ena a m'khamu la anthu anati kwa Iye, Mphunzitsi, dzudzulani ophunzira anu.

Ndipo anayankha nati, Ndinena ndi inu, ngati awa khala chete miyala idzafuula.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 9:1-2

Ndidzayamika Yehova ndi mtima wanga wonse; ndidzawerengera zodabwitsa zanu zonse.

Ndidzakondwerera ndi kusekera mwa Inu; ndidzaimbira dzina lanu, Wam'mwambamwamba Inu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 34:1-3

Ndidzalemekeza Yehova nyengo zonse; kumlemekeza kwake kudzakhala m'kamwa mwanga kosalekeza.

Moyo wanga udzatamanda Yehova; ofatsa adzakumva nadzakondwera.

Bukitsani pamodzi ndine ukulu wa Yehova, ndipo tikweze dzina lake pamodzi.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 12:1-2

Chifukwa chake ndikupemphani inu, abale, mwa zifundo za Mulungu, kuti mupereke matupi anu nsembe yamoyo, yopatulika, yokondweretsa Mulungu, ndiko kupembedza kwanu koyenera.

Ndipo musafanizidwe ndi makhalidwe a pansi pano: koma mukhale osandulika, mwa kukonzanso kwa mtima wanu, kuti mukazindikire chimene chili chifuno cha Mulungu, chabwino, ndi chokondweretsa, ndi changwiro.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 42:4

Ndidzikumbukira izi ndipo nditsanulira moyo wanga m'kati mwa ine, pakuti ndidafopita ndi unyinji wa anthu, ndinawatsogolera kunyumba ya Mulungu, ndi mau akuimbitsa ndi kuyamika, ndi unyinji wakusunga dzuwa lokondwera.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 26:30

Ndipo pamene anaimba nyimbo, anatuluka kunka kuphiri la Azitona.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Petro 2:9

Koma inu ndinu mbadwa yosankhika, ansembe achifumu, mtundu woyera mtima, anthu a mwini wake, kotero kuti mukalalikire zoposazo za Iye amene anakuitanani mutuluke mumdima, mulowe kuunika kwake kodabwitsa;

Mutu    |  Mabaibulo
Ahebri 13:15

Potero mwa Iye tipereke chiperekere nsembe yakuyamika Mulungu, ndiyo chipatso cha milomo yovomereza dzina lake.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 66:1-4

Fuulirani kwa Mulungu, dziko lonse lapansi.

Imbirani ulemerero wa dzina lake; pomlemekeza mumchitire ulemerero.

Nenani kwa Mulungu, Ha, ntchito zanu nzoopsa nanga! Chifukwa cha mphamvu yanu yaikulu adani anu adzagonjera Inu.

Dziko lonse lapansi lidzakugwadirani, ndipo lidzakuimbirani; ndzaimbira dzina lanu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 96:1-3

Muimbireni Yehova nyimbo yatsopano; muimbireni Yehova, inu, dziko lonse lapansi.

Muimbireni Yehova, lemekezani dzina lake; lalikirani chipulumutso chake tsiku ndi tsiku.

Fotokozerani ulemerero wake mwa amitundu; zodabwitsa zake mwa mitundu yonse ya anthu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 71:23

Milomo yanga idzafuula mokondwera poimbira Inu nyimbo; inde, moyo wanga umene munaombola.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 103:1-2

Lemekeza Yehova, moyo wanga; ndi zonse za m'kati mwanga zilemekeze dzina lake loyera.

Lemekeza Yehova, moyo wanga, ndi kusaiwala zokoma zake zonse atichitirazi:

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 5:11

Koma akondwere onse amene athawira kwa Inu, afuule mokondwera kosaleka, popeza muwafungatira; nasekere mwa Inu iwo akukonda dzina lanu.

Mutu    |  Mabaibulo
Eksodo 15:1-2

Pamenepo Mose ndi ana a Israele anaimbira Yehova nyimbo iyi, nanena, ndi kuti, Ndidzaimbira Yehova pakuti wapambanatu; kavalo ndi wokwera wake anawaponya m'nyanja.

Yehova ndiye mphamvu yanga ndi nyimbo yanga, ndipo wakhala chipulumutso changa; ameneyo ndiye Mulungu wanga, ndidzamlemekeza; ndiye Mulungu wa kholo langa, ndidzamveketsa.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 147:7-9

Yamikani Yehova ndi kuthira mang'ombe; muimbireni Mulungu wathu zomlemekeza pazeze:

Amene aphimba thambo ndi mitambo, amene akonzera mvula nthaka, amene aphukitsa msipu pamapiri.

Amene apatsa zoweta chakudya chao, ana a khungubwi alikulira.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 84:1-2

Pokhala Inu mpotikonda ndithu, Yehova wa makamu!

Moyo wanga ulakalaka, inde ukomokanso ndi kufuna mabwalo a Yehova; mtima wanga ndi thupi langa zifuulira kwa Mulungu wamoyo.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 146:1-2

Aleluya; Ulemekeze Yehova, moyo wanga.

Ndidzalemekeza Yehova m'moyo mwanga; ndidzaimbira zomlemekeza Mulungu wanga pokhala ndi moyo ine.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 138:1-2

Ndidzakuyamikani ndi mtima wanga wonse; ndidzaimba zakukulemekezani patsogolo pa milungu.

Ndidzagwadira kuloza ku Kachisi wanu woyera, ndi kuyamika dzina lanu, chifukwa cha chifundo chanu ndi choonadi chanu; popeza munakuzitsa mau anu koposa dzina lanu lonse.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 9:11

Imbirani zoyamika Yehova, wokhala ku Ziyoni; lalikirani mwa anthu ntchito zake.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 145:5-7

Ndidzalingalira ulemerero waukulu wa ulemu wanu, ndi ntchito zanu zodabwitsa.

Ndipo adzanenera mphamvu za ntchito zanu zoopsa; ndi ukulu wanu ndidzaufotokozera.

Adzabukitsa chikumbukiro cha ubwino wanu waukulu, nadzaimbira chilungamo chanu.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 61:3

ndikakonzere iwo amene alira maliro m'Ziyoni, ndi kuwapatsa chovala kokometsa m'malo mwa phulusa, mafuta akukondwa m'malo mwa maliro, chovala cha matamando m'malo mwa mzimu wopsinjika; kuti iwo atchedwe mitengo ya chilungamo yakuioka Yehova, kuti Iye alemekezedwe.

Mutu    |  Mabaibulo
2 Mbiri 5:13-14

Ndipo kunali, pakuchita limodzi amalipenga ndi oimba, kumveketsa mau amodzi akulemekeza ndi kuyamika Yehova, ndi pakukweza mau ao pamodzi ndi malipenga, ndi nsanje, ndi zoimbira zina, ndi kulemekeza Yehova, ndi kuti, Pakuti Iye ndiye wabwino, pakuti chifundo chake chikhala chikhalire; pamenepo mtambo unadzaza nyumbayi, ndiyo nyumba ya Yehova;

ndipo ansembe sanakhoze kuimirira kutumikira chifukwa cha mtambowo; pakuti ulemerero wa Yehova unadzaza nyumba ya Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo

Pemphero kwa Mulungu

Ambuye, inu ndinu Alfa ndi Omega! Atate, Mlengi wa thambo ndi dziko lapansi, ndinu woyamba ndi wotsiriza, chiyambi ndi chitsiriziro. Ndikubwera kwa inu kudzera mwa Ambuye wanga Yesu Khristu, ndikupempha kuti muteteze ndi kulimbitsa moyo wa mnzanga, mupatseni nzeru ndi luntha kuti asankhe zinthu zabwino, kuti ayende m'cholinga chimene munamupangira. Mulimbitseni, mutsitsimutseni mphamvu zake ndipo molimbikira mulimbitse chikhulupiriro chake, kotero kuti kukhalapo kwa Mzimu Woyera wanu kukhale patsogolo pa moyo wake ndi banja lake. Mawu anu amati: "Pakuti adzatumiza angelo ake kukutetezani m'njira zako zonse." Ambuye, pitirizani kumupatsa zonse zomfunika, mupatseni nzeru ndi kulimba mtima kuti agonjetse mantha ake ndipo athe kupambana mavuto aliwonse omwe akukumana nawo. Ndikulengeza kuti mukupita patsogolo pake ngati chimphona champhamvu, mukulimbana nkhondo zake zonse. Mumuteteze ku ziwembu zonse ndi misampha ya mdani. Zikomo, Ambuye, ulemerero ndi ulemu zonse zikhale kwa inu. M'dzina la Yesu. Ameni!