Mavesi a Baibulo

Zotsatsa


Gulu Laling'ono

MAVESI OKHUDZA CHItonthozo

Zimakhala zovuta kudziwa kuti simudzakumananso ndi munthu amene wamwalirayu, munthu amene mumamukonda kwambiri ndipo anali wofunika pa moyo wanu. Simudzakumananso naye kuti mucheze, museke, ndiponso mugawane nthawi zosaiwalika. Tonse timadutsamo m'nthawi yachisoni, nthawi yomvetsa chisoni. M'nthawi ngati imeneyi tingalire ndikumva kuwawa ndipo si tchimo. Yesu nayenso analira atamva kuti Lazaro, mnzake, wamwalira (Yohane 11:35). Ndikofunika kuulula zakukhosi kwanu m'nthawi yachisoni.

Koma ngakhale muli pachisoni, musalole kuti chisonicho chikulepheretseni kupitiriza ndi moyo. Mulungu ali nanu kuti apukute misozi yanu, atonthoze mtima wanu, ndikubwezeretsanso chimwemwe pa nkhope yanu. Ingomulolani Mulungu achite zimenezi. (2 Akorinto 1:3) Dalitsani Mulungu Atate wa Ambuye wathu Yesu Khristu, Atate wachifundo ndi Mulungu wa chitonthozo chonse.


Deuteronomo 6:5

ndipo muzikonda Yehova Mulungu wanu ndi mtima wanu wonse, ndi moyo wanu wonse, ndi mphamvu yanu yonse.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Yohane 5:3

Pakuti ichi ndi chikondi cha Mulungu, kuti tisunge malamulo ake: ndipo malamulo ake sali olemetsa.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 145:20

Yehova asunga onse akukondana naye; koma oipa onse adzawaononga.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 91:14

Popeza andikondadi ndidzampulumutsa; ndidzamkweza m'mwamba, popeza adziwa dzina langa.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 8:28

Ndipo tidziwa kuti amene akonda Mulungu zinthu zonse zithandizana kuwachitira ubwino, ndiwo amene aitanidwa monga mwa kutsimikiza kwa mtima wake.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Akorinto 8:3

Koma ngati wina akonda Mulungu, yemweyu adziwika ndi Iye.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Yohane 4:10

Umo muli chikondi, sikuti ife tinakonda Mulungu, koma kuti Iye anatikonda ife, ndipo anatuma Mwana wake akhale chiombolo chifukwa cha machimo athu.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 8:17

Akundikonda ndiwakonda; akundifunafuna adzandipeza.

Mutu    |  Mabaibulo
Marko 12:30

ndipo uzikonda Ambuye Mulungu wako ndi mtima wako wonse, ndi moyo wako wonse, ndi nzeru zako zonse, ndi mphamvu yako yonse.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 116:1-2

Ndimkonda, popeza Yehova amamva mau anga ndi kupemba kwanga.

Ndinakhulupirira, chifukwa chake ndinalankhula; ndinazunzika kwambiri.

Pofulumizidwa mtima ndinati ine, anthu onse nga mabodza.

Ndidzabwezera Yehova chiyani chifukwa cha zokoma zake zonse anandichitira?

Ndidzanyamula chikho cha chipulumutso, ndipo ndidzaitanira dzina la Yehova.

Ndidzachita zowinda zanga za kwa Yehova, tsopano, pamaso pa anthu ake onse.

Imfa ya okondedwa ake nja mtengo wake pamaso pa Yehova.

Ndiloleni, Yehova, indetu ndine mtumiki wanu; ndine mtumiki wanu, mwana wa mdzakazi wanu; mwandimasulira zondimanga.

Ndidzapereka kwa Inu nsembe yachiyamiko, ndipo ndidzaitanira dzina la Yehova.

Ndidzachita zowinda zanga za kwa Yehova, tsopano, pamaso pa anthu ake onse.

M'mabwalo a nyumba ya Yehova, pakati pa inu, Yerusalemu. Aleluya.

Popeza amanditcherera khutu lake, chifukwa chake ndidzaitanira Iye masiku anga onse.

Mutu    |  Mabaibulo
Yohane 14:23

Yesu anayankha nati kwa iye, Ngati wina akonda Ine, adzasunga mau anga; ndipo Atate wanga adzamkonda, ndipo tidzadza kwa iye, ndipo tidzayesa kwa iye mokhalamo.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Yohane 5:1

Yense wokhulupirira kuti Yesu ndiye Khristu wabadwa kuchokera kwa Mulungu; ndipo yense wakukonda Iye amene anabala akondanso iye amene anabadwa wochokera mwa Iye.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Yohane 4:7-8

Okondedwa, tikondane wina ndi mnzake: chifukwa kuti chikondi chichokera kwa Mulungu, ndipo yense amene akonda, abadwa kuchokera kwa Mulungu, namzindikira Mulungu.

Iye wosakonda sazindikira Mulungu; chifukwa Mulungu ndiye chikondi.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 22:37-38

Ndipo Yesu anati kwa iye, Uzikonda Ambuye Mulungu wako ndi mtima wako wonse, ndi moyo wako wonse, ndi nzeru zako zonse.

Ili ndilo lamulo lalikulu ndi loyamba.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 18:1

Ndikukondani, Yehova, mphamvu yanga.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 5:11

Koma akondwere onse amene athawira kwa Inu, afuule mokondwera kosaleka, popeza muwafungatira; nasekere mwa Inu iwo akukonda dzina lanu.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Yohane 4:19

Tikonda ife, chifukwa anayamba Iye kutikonda.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Yohane 4:20

Munthu akati, kuti, Ndikonda Mulungu, nadana naye mbale wake, ali wabodza: pakuti iye wosakonda mbale wake amene wamuona, sakhoza kukonda Mulungu amene sanamuona.

Mutu    |  Mabaibulo
Deuteronomo 7:9

Chifukwa chake dziwani kuti Yehova Mulungu wanu ndiye Mulungu; ndiye Mulungu wokhulupirika, wakusunga chipangano ndi chifundo ndi iwo akumkonda ndi kusunga malamulo ake, kufikira mibadwo zikwi.

Mutu    |  Mabaibulo
Aefeso 4:15

koma ndi kuchita zoona mwa chikondi tikakule m'zinthu zonse, kufikira Iye amene ali mutu ndiye Khristu;

Mutu    |  Mabaibulo
2 Atesalonika 3:5

Ndipo Ambuye atsogolere bwino mitima yanu ilowe m'chikondi cha mulungu ndi m'chipiriro cha Khristu.

Mutu    |  Mabaibulo
Deuteronomo 7:12

Ndipo kudzakhala, chifukwa cha kumvera inu maweruzo awa, ndi kuwasunga, ndi kuwachita, Yehova Mulungu wanu adzakusungirani chipangano ndi chifundo chimene analumbirira makolo anu;

Mutu    |  Mabaibulo
Deuteronomo 30:20

kukonda Yehova Mulungu wanu, kumvera mau ake, ndi kummamatira Iye, pakuti Iye ndiye moyo wanu, ndi masiku anu ochuluka; kuti mukhale m'dziko limene Yehova analumbirira makolo anu, Abrahamu, Isaki, ndi Yakobo, kuwapatsa ili.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Yohane 3:1

Taonani, chikondicho Atate watipatsa, kuti titchedwe ana a Mulungu; ndipo tili ife otere. Mwa ichi dziko lapansi silizindikira ife, popeza silimzindikira Iye.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 8:39

ngakhale utali, ngakhale kuya, ngakhale cholengedwa china chilichonse, sichingadzakhoze kutisiyanitsa ife ndi chikondi cha Mulungu, chimene chili mwa Khristu Yesu Ambuye wathu.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 5:5

ndipo chiyembekezo sichichititsa manyazi; chifukwa chikondi cha Mulungu chinatsanulidwa m'mitima mwathu mwa Mzimu Woyera, amene wapatsidwa kwa ife.

Mutu    |  Mabaibulo
Yohane 12:25

Iye wokonda moyo wake adzautaya; ndipo wodana ndi moyo wake m'dziko lino lapansi adzausungira kumoyo wosatha.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 27:4

Chinthu chimodzi ndinachipempha kwa Yehova, ndidzachilondola ichi, Kuti ndikhalitse m'nyumba ya Yehova masiku onse a moyo wanga, kupenya kukongola kwake kwa Yehova ndi kufunsitsa m'Kachisi wake.

Mutu    |  Mabaibulo
2 Akorinto 5:14-15

Pakuti chikondi cha Khristu chitikakamiza; popeza taweruza chotero, kuti mmodzi adafera onse, chifukwa chake onse adafa;

ndipo adafera onse kuti iwo akukhala ndi moyo asakhalenso ndi moyo kwa iwo okha, koma mwa Iye amene adawafera iwo, nauka.

Mutu    |  Mabaibulo
Eksodo 34:6

Ndipo Yehova anapita pamaso pake, nafuula, Yehova, Yehova, Mulungu wachifundo ndi wachisomo, wolekereza, ndi wa ukoma mtima wochuluka, ndi wachoonadi;

Mutu    |  Mabaibulo
1 Yohane 4:12

Palibe munthu adamuona Mulungu nthawi iliyonse; tikakondana wina ndi mnzake, Mulungu akhala mwa ife, ndi chikondi chake chikhala changwiro mwa ife;

Mutu    |  Mabaibulo
1 Yohane 4:18

Mulibe mantha m'chikondi; koma chikondi changwiro chitaya kunja mantha, popeza mantha ali nacho chilango, ndipo wamanthayo sakhala wangwiro m'chikondi.

Mutu    |  Mabaibulo
Deuteronomo 11:13

Ndipo kudzakhala mukasamalira chisamalire malamulo anga amene ndikuuzani lero lino, kukonda Yehova Mulungu wanu, ndi kumtumikira ndi mtima wanu wonse, ndi moyo wanu wonse,

Mutu    |  Mabaibulo
Deuteronomo 13:3

musamamvera mau a mneneri uyu, kapena wolota maloto uyu; popeza Yehova Mulungu wanu akuyesani, kuti adziwe ngati mukonda Yehova Mulungu wanu ndi mtima wanu wonse, ndi moyo wanu wonse.

Mutu    |  Mabaibulo
Deuteronomo 30:16

popeza ndikuuzani lero kukonda Yehova Mulungu wanu, kuyenda m'njira zake, ndi kusunga malamulo ake ndi malemba ake ndi maweruzo ake, kuti mukakhale ndi moyo ndi kuchuluka, ndi kuti Yehova Mulungu wanu akakudalitseni m'dziko limene mulowako kulilandira.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Akorinto 16:22

Ngati wina sakonda Ambuye, akhale wotembereredwa. Akudza Ambuye.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 31:23

Kondani Yehova, Inu nonse okondedwa ake, Yehova asunga okhulupirika, ndipo abwezera zochuluka iye wakuchita zodzitama.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 97:10

Inu okonda Yehova, danani nacho choipa: Iye asunga moyo wa okondedwa ake; awalanditsa m'manja mwa oipa.

Mutu    |  Mabaibulo
Yohane 15:9

Monga momwe Atate wandikonda Ine, Inenso ndakonda inu; khalani m'chikondi changa.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 116:1

Ndimkonda, popeza Yehova amamva mau anga ndi kupemba kwanga.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 10:37

Iye wakukonda atate wake, kapena amake koposa Ine, sayenera Ine, ndipo iye wakukonda mwana wake wamwamuna, kapena wamkazi koposa Ine, sayenera Ine.

Mutu    |  Mabaibulo
Aefeso 6:24

Akhale nacho chisomo onse akukonda Ambuye wathu Yesu Khristu m'chosaonongeka.

Mutu    |  Mabaibulo
Yakobo 4:8

Yandikirani kwa Mulungu, ndipo adzayandikira kwa inu. Sambani m'manja, ochimwa inu; yeretsani mitima, a mitima iwiri inu.

Mutu    |  Mabaibulo
Luka 10:27

Ndipo iye anayankha nati, Uzikonda Ambuye Mulungu wako ndi mtima wako wonse, ndi moyo wako wonse, ndi mphamvu yako yonse, ndi nzeru zako zonse, ndi mnansi wako monga iwe mwini.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Yohane 4:8

Iye wosakonda sazindikira Mulungu; chifukwa Mulungu ndiye chikondi.

Mutu    |  Mabaibulo
Yohane 14:15

Ngati mukonda Ine, sungani malamulo anga.

Mutu    |  Mabaibulo
Yohane 14:21

Iye wakukhala nao malamulo anga, ndi kuwasunga, iyeyu ndiye wondikonda Ine; koma wondikonda Ine adzakondedwa ndi Atate wanga, ndipo Ine ndidzamkonda, ndipo ndidzadzionetsa ndekha kwa iye.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 43:4

Pokhala iwe wa mtengo wapatali pamaso panga, ndi wolemekezeka, ndipo ndakukonda iwe; Ine ndidzakuombola ndi anthu, ndi kupereka anthu m'malo mwa moyo wako.

Mutu    |  Mabaibulo
Afilipi 1:9

Ndipo ichi ndipempha, kuti chikondi chanu chisefukire chionjezere, m'chidziwitso, ndi kuzindikira konse;

Mutu    |  Mabaibulo
Akolose 3:2

Lingalirani zakumwamba osati za padziko ai.

Mutu    |  Mabaibulo
Agalatiya 5:13

Pakuti adakuitanani inu, abale, mukhale mfulu; chokhacho musachite nao ufulu wanu chothandizira thupi, komatu mwachikondi chitiranani ukapolo.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 12:1

Chifukwa chake ndikupemphani inu, abale, mwa zifundo za Mulungu, kuti mupereke matupi anu nsembe yamoyo, yopatulika, yokondweretsa Mulungu, ndiko kupembedza kwanu koyenera.

Mutu    |  Mabaibulo
2 Timoteyo 1:7

Pakuti Mulungu sanatipatsa mzimu wa mantha; komatu wa mphamvu ndi chikondi ndi chidziletso.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Petro 1:8

amene mungakhale simunamuona mumkonda; amene mungakhale simumpenya tsopano, pokhulupirira, mukondwera naye ndi chimwemwe chosaneneka, ndi cha ulemerero:

Mutu    |  Mabaibulo
Ahebri 10:24-25

ndipo tiganizirane wina ndi mnzake kuti tifulumizane ku chikondano ndi ntchito zabwino,

osaleka kusonkhana kwathu pamodzi, monga amachita ena, komatu tidandaulirane, ndiko koposa monga momwe muona tsiku lilikuyandika.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:47

Ndipo ndidzadzikondweretsa nao malamulo anu, amene ndiwakonda.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 26:8

Yehova, ndikonda chikhalidwe cha nyumba yanu, ndi malo akukhalamo ulemerero wanu.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 22:39

Ndipo lachiwiri lolingana nalo ndili, Uzikonda mnzako monga udzikonda iwe mwini.

Mutu    |  Mabaibulo
Yohane 21:15-17

Ndipo pamene atafisula Yesu ananena kwa Simoni Petro, Simoni mwana wa Yona, kodi undikonda Ine koposa awa? Ananena ndi Iye, Inde, Ambuye; mudziwa kuti ndikukondani Inu. Ananena naye, Dyetsa anaankhosa anga.

Ananena nayenso kachiwiri, Simoni mwana wa Yona, ukonda Ine kodi? Ananena ndi Iye, Inde, Ambuye; mudziwa kuti ndikukondani Inu. Ananena naye, Weta nkhosa zanga.

Ananena naye kachitatu, Simoni mwana wa Yona, kodi undikonda Ine? Petro anamva chisoni kuti anati kwa iye kachitatu, Kodi undikonda Ine? Ndipo anati kwa iye, Ambuye, mudziwa Inu zonse; muzindikira kuti ndikukondani Inu. Yesu ananena naye, Dyetsa nkhosa zanga.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Yohane 2:15

Musakonde dziko lapansi, kapena za m'dziko lapansi. Ngati wina akonda dziko lapansi, chikondi cha Atate sichili mwa iye.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 13:10

Chikondano sichichitira mnzake choipa; chotero chikondanocho chili chokwanitsa lamulo.

Mutu    |  Mabaibulo
Deuteronomo 11:1

Chifukwa chake muzikonda Yehova Mulungu wanu, ndi kusunga chilangizo chake, ndi malemba ake, ndi maweruzo ake, ndi malamulo ake, masiku onse.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 3:5-6

Khulupirira Yehova ndi mtima wako wonse, osachirikizika pa luntha lako;

umlemekeze m'njira zako zonse, ndipo Iye adzaongola mayendedwe ako.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:165

Akukonda chilamulo chanu ali nao mtendere wambiri; ndipo alibe chokhumudwitsa.

Mutu    |  Mabaibulo

Pemphero kwa Mulungu

Zikomo Ambuye, chifukwa ndinu wochiritsa wanga, wopereka wanga, ndi wolinda wanga. Ndinu amene mumalungama nkhondo zanga, ndipo mumanditsogolera kuchoka mu ulemerero kupita mu ulemerero wina. Mu dzina lamphamvu la Yesu, ndikupempherani Mulungu wanga wamphamvu, kuti ndikuthokozani chifukwa pakati pa mavuto, mwakhala thandizo langa ndi mphamvu yanga. Pakati pa kusowa, mwandipatsa zonse zimene ndikufuna. Mundidzaze ndi kukhalapo kwanu ndi Mzimu Woyera wanu waulemerero. Mtendere wanu wopambana luntha lonse usunge mtima wanga ndi maganizo anga. Pakati pa mavuto, ndikhale ndi chikhulupiriro chonse kuti mukuwongolera zonse. Sungani mtima wanga ku zowawa zonse. Ndipo nthawi zovuta pamene ambiri anandisiya, inu munali nane. Zikomo chifukwa pakati pa mantha, Mzimu wanu Woyera wandipatsa mphamvu kuti ndithane ndi mavuto ndi mayesero, ndipo ndapeza chigonjetso mu dzina la Yesu. Ambuye, pakati pa chete ndi chikhulupiriro, ndadziwa kuti ndinu Mulungu amene mumalungama nkhondo zanga. Mawu anu amati: “Ngakhale nditayenda m’chigwa cha mthunzi wa imfa, sindidzaopa choipa; chifukwa inu muli ndi ine; ndodo yanu ndi chikwakwa chanu zinditonthoza.” Mu dzina lamphamvu la Yesu. Ameni.