Biblia Todo Logo
Mavesi a Baibulo

- Zotsatsa -


66 Mau a Mulungu Pa Nzeru ndi Luntha

66 Mau a Mulungu Pa Nzeru ndi Luntha

Mtima wanga ukukukumbutsa kuti nzeru zimachokera kwa Mulungu. Ngati ukufuna kukhala wanzeru, yandikila Iye.

Kuti tizikonda nzeru, choyamba tiyenera kukonda Atate wathu wakumwamba amene amatipatsa nzeruzo. Tsiku lililonse tipemphere nzeru zimene zimachokera kumwamba, kuti tizitha kusankha zinthu mwanzeru zimene zingatithandize kuyenda panjira yoyenera komanso zimene zingatipatse chimwemwe chenicheni mumtima mwathu.

Nzeru ziyenera kukhala nafe nthawi zonse. Tikatero, sitidzalakwitsa zambiri ndipo tidzayenda molimba mtima, chifukwa munthu wanzeru amatha kupeza njira yopitira patsogolo, bola ngati alola Mulungu kumutsogolera. Ngati wina wa inu akusowa nzeru, apemphe kwa Mulungu, ndipo adzazipatsidwa, chifukwa Mulungu amapereka mowolowa manja kwa onse, popanda kunyoza aliyense. Koma apemphe ndi chikhulupiriro, wopanda kukayika, chifukwa wokayika ali ngati mafunde a m’nyanja, amene amayendayenda ndi mphepo. (Yakobo 1:5-6)

Tifufuze nzeru za Mulungu ndi chikhulupiriro, ndipo tidzazipeza, ndipo tizikumbukira kuti chiyambi cha nzeru ndicho kuopa Yehova. Opa Mulungu, ndipo Iye adzatsogolera mapazi ako. Usalole kuti maganizo ako kapena zakukhosi kwako zikutsogolere, choka pa zoyipa, mvera mawu a Mulungu, mvere Iye, ndipo udzatchedwa wanzeru padziko lapansi.




Aroma 11:33

Ha! Kuya kwake kwa kulemera ndi kwa nzeru ndi kwa kudziwa kwake kwa Mulungu! Osasanthulikadi maweruzo ake, ndi njira zake nzosalondoleka!

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 23:15

Mwananga, mtima wako ukakhala wanzeru, mtima wanga wa inedi udzakondwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yobu 28:28

Koma kwa munthu anati, Taonani, kuopa Ambuye ndiko nzeru; ndi kupatukana nacho choipa ndiko luntha.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 13:20

Ukayenda ndi anzeru udzakhala wanzeru: koma mnzao wa opusa adzaphwetekedwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 1:25

Chifukwa kuti chopusa cha Mulungu chiposa anthu ndi nzeru zao; ndipo chofooka cha Mulungu chiposa anthu ndi mphamvu yao.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 2:6

Pakuti Yehova apatsa nzeru; kudziwa ndi kuzindikira kutuluka m'kamwa mwake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 16:16

Kodi kulandira nzeru sikupambana ndi golide, kulandira luntha ndi kusankhika koposa siliva?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 19:7

Malamulo a Yehova ali angwiro, akubwezera moyo; mboni za Yehova zili zokhazikika, zakuwapatsa opusa nzeru.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 15:33

Kuopa Yehova ndiko mwambo wanzeru; ndipo chifatso chitsogolera ulemu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 111:10

Kumuopa Yehova ndiko chiyambi cha nzeru; onse akuchita chotero ali nacho chidziwitso chokoma; chilemekezo chake chikhalitsa kosatha.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mlaliki 10:12

Mau a m'kamwa mwa munthu wanzeru nga chisomo; koma milomo ya chitsiru idzachimeza.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 24:14

Potero udzadziwa kuti nzeru ili yotero m'moyo wako; ngati waipeza padzakhala mphotho, ndipo chiyembekezo chako sichidzalephereka.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 12:1

Wokonda mwambo akonda kudziwa; koma wakuda chidzudzulo apulukira.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yakobo 3:17

Koma nzeru yochokera kumwamba iyamba kukhala yoyera, nikhalanso yamtendere, yaulere, yomvera bwino, yodzala chifundo ndi zipatso zabwino, yopanda tsankho, yosadzikometsera pamaso.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Danieli 2:23

Ndikuyamikani ndi kukulemekezani Inu, Mulungu wa makolo anga, pakuti mwandipatsa nzeru ndi mphamvu; ndipo mwandidziwitsa tsopano ichi tachifuna kwa Inu; pakuti mwatidziwitsa mlandu wa mfumu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 1:7

Kuopa Yehova ndiko chiyambi cha kudziwa; opusa anyoza nzeru ndi mwambo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 3:13

Wodala ndi wopeza nzeru, ndi woona luntha;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 9:10

Chiyambi cha nzeru ndicho kuopa Yehova; kudziwa Woyerayo ndiko luntha.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 4:7

Nzeru ipambana, tatenga nzeru; m'kutenga kwako konseko utenge luntha.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 10:8

Mwini mtima wanzeru amalandira malamulo; koma chitsiru cholongolola chidzagwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 10:1

Mwana wanzeru akondweretsa atate; koma mwana wopusa amvetsa amake chisoni.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 3:5-6

Khulupirira Yehova ndi mtima wako wonse, osachirikizika pa luntha lako; umlemekeze m'njira zako zonse, ndipo Iye adzaongola mayendedwe ako.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 29:3

Mwamuna wokonda nzeru akondweretsa atate wake; koma wotsagana ndi akazi adama amwaza chuma.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yakobo 3:13

Ndani ali wanzeru, ndi waluso mwa inu? Aonetsere ndi mayendedwe ake abwino ntchito zake mu nzeru yofatsa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 90:12

Mutidziwitse kuwerenga masiku athu motero, kuti tikhale nao mtima wanzeru.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Akolose 4:5-6

Muyendere munzeru ndi iwo akunja, kuchita machawi nthawi ingatayike. Mau anu akhale m'chisomo, okoleretsa, kuti mukadziwe inu mayankhidwe anu a kwa yense akatani.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aefeso 5:15-16

Potero, penyani bwino umo muyendera, si monga opanda nzeru, koma monga anzeru; akuchita machawi, popeza masiku ali oipa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Danieli 12:10

Ambiri adzadzitsuka ndi kudziyeretsa, nadzayesedwa ndi moto; koma oipa adzachita moipa; ndipo palibe mmodzi wa oipa adzazindikira; koma aphunzitsi ndiwo adzazindikira.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 12:16

Mkwiyo wa chitsiru udziwika posachedwa; koma wanzeru amabisa manyazi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 13:3

Wogwira pakamwa pake asunga moyo wake; koma woyasamula milomo yake adzaonongeka.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mlaliki 7:10

Usanene, Kodi bwanji masiku akale anapambana ano? Pakuti sulikufunsa mwanzeru pamenepo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mlaliki 1:18

Pakuti m'nzeru yambiri muli chisoni chambiri; ndi yemwe aenjezera chidziwitso aenjezera zowawa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 7:24

Chifukwa chimenechi yense amene akamva mau anga amenewa, ndi kuwachita, ndidzamfanizira iye ndi munthu wochenjera, amene anamanga nyumba yake pathanthwe;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 28:29

Ichinso chifumira kwa Yehova wa makamu, uphungu wake uzizwitsa ndi nzeru yake impambana.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yakobo 1:5

Koma wina wa inu ikamsowa nzeru, apemphe kwa Mulungu, amene apatsa kwa onse modzala manja, niwosatonza; ndipo adzampatsa iye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 4:5-6

Tenga nzeru, tenga luntha; usaiwale, usapatuke pa mau a m'kamwa mwanga; usasiye nzeru, ndipo idzakusunga; uikonde, idzakutchinjiriza.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mlaliki 7:12

Pakuti nzeru itchinjiriza monga ndalama zitchinjiriza; koma kudziwa kupambana, chifukwa nzeru isunga moyo wa eni ake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:130

Potsegulira mau anu paunikira; kuzindikiritsa opusa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 16:13

Milomo yolungama ikondweretsa mafumu; wonena zoongoka amkonda.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 3:13-14

Wodala ndi wopeza nzeru, ndi woona luntha; pakuti malonda a nzeru aposa malonda a siliva, phindu lake liposa golide woyengeka.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Akolose 1:9

Mwa ichi ifenso, kuyambira tsiku limene tidamva, sitileka kupembedzera ndi kupempherera inu, kuti mukadzazidwe ndi chizindikiritso cha chifuniro chake mu nzeru zonse ndi chidziwitso cha mzimu,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 14:29

Wosakwiya msanga apambana kumvetsa; koma wansontho akuza utsiru.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yobu 12:12

Kwa okalamba kuli nzeru, ndi kwa a masiku ochuluka luntha.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 1:30

Koma kwa Iye muli inu mwa Khristu Yesu, amene anayesedwa kwa ife nzeru ya kwa Mulungu, ndi chilungamo ndi chiyeretso ndi chiombolo;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 3:13-18

Wodala ndi wopeza nzeru, ndi woona luntha; pakuti malonda a nzeru aposa malonda a siliva, phindu lake liposa golide woyengeka. Mtengo wake uposa ngale; ndipo zonse zikukondweretsa sizilingana naye. Masiku ambiri ali m'dzanja lamanja lake; chuma ndi ulemu m'dzanja lake lamanzere. Njira zake zili zokondweretsa, mayendedwe ake onse ndiwo mtendere. Ndiyo mtengo wa moyo wa akuigwira; wakuiumirira ngwodala.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 37:30

Pakamwa pa wolungama palankhula zanzeru, ndi lilime lake linena chiweruzo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mlaliki 2:26

Pakuti yemwe Mulungu amuyesa wabwino ampatsa nzeru ndi chidziwitso ndi chimwemwe; koma wochimwa amlawitsa vuto la kusonkhanitsa ndi kukundika, kuti aperekere yemwe Mulungu amuyesa wabwino. Ichinso ndi chabe ndi kungosautsa mtima.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 19:8

Wolandira nzeru akonda moyo wake; wosunga luntha adzapeza zabwino.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 2:10-11

Pakuti nzeru idzalowa m'mtima mwako, moyo wako udzakondwera ndi kudziwa, kulingalira kudzakudikira, kuzindikira kudzakutchinjiriza;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:66

Mundiphunzitse chisiyanitso ndi nzeru; pakuti ndinakhulupirira malamulo anu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 10:14

Anzeru akundika zomwe adziwa; koma m'kamwa mwa chitsiru muononga tsopano lino.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 25:4-5

Mundidziwitse njira zanu, Yehova; Mundiphunzitse mayendedwe anu. Munditsogolere m'choonadi chanu, ndipo mundiphunzitse; pakuti Inu ndinu Mulungu wa chipulumutso changa; Inu ndikuyembekezerani tsiku lonseli.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 12:15

Njira ya chitsiru njolungama pamaso pakepake; koma wanzeru amamvera uphungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 11:2

Ndipo mzimu wa Yehova udzambalira iye mzimu wanzeru ndi wakuzindikira, mzimu wa uphungu ndi mphamvu, mzimu wakudziwa ndi wakuopa Yehova;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aefeso 5:15-17

Potero, penyani bwino umo muyendera, si monga opanda nzeru, koma monga anzeru; akuchita machawi, popeza masiku ali oipa. Chifukwa chake musakhale opusa, koma dziwitsani chifuniro cha Ambuye nchiyani.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Akolose 2:2-3

kuti itonthozeke mitima yao, nalumikizike pamodzi iwo m'chikondi, kufikira chuma chonse cha chidzalo cha chidziwitso, kuti akazindikire iwo chinsinsi cha Mulungu, ndiye Khristu, Ngati munafa pamodzi ndi Khristu kusiyana nazo zoyamba za dziko lapansi, mugonjeranji kuzoikikazo, monga ngati moyo wanu mukhala nao m'dziko lapansi, usaikapo dzanja, usalawa, usakhudza, (ndizo zonse zakuonongedwa pochita nazo), monga mwa malangizo ndi maphunziro a anthu? Zimene zili naotu manenedwe a nzeru m'kutumikira kwa chifuniro cha mwini wake, ndi kudzichepetsa, ndi kusalabadira thupi; koma zilibe mphamvu konse yakuletsa chikhutitso cha thupi. amene zolemera zonse za nzeru ndi chidziwitso zibisika mwa Iye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 19:7-8

Malamulo a Yehova ali angwiro, akubwezera moyo; mboni za Yehova zili zokhazikika, zakuwapatsa opusa nzeru. Malangizo a Yehova ali olungama, akukondweretsa mtima; malamulo a Yehova ali oyera, akupenyetsa maso.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 13:14

Malamulo a wanzeru ndiwo kasupe wa moyo, apatutsa kumisampha ya imfa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 21:30

Kulibe nzeru ngakhale luntha ngakhale uphungu wotsutsana ndi Yehova.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 18:15

Mtima wa wozindikira umaphunzira; khutu la anzeru lifunitsa kudziwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 4:5

Tenga nzeru, tenga luntha; usaiwale, usapatuke pa mau a m'kamwa mwanga;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 51:6

Onani, Inu mukondwera ndi zoonadi m'malo a m'katimo; ndipo m'malo a m'tseri mudzandidziwitsa nzeru.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:104

Malangizo anu andizindikiritsa; chifukwa chake ndidana nao mayendedwe onse achinyengo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 22:17-18

Tchera makutu ako, numvere mau a anzeru, nulozetse mtima wako kukadziwa zanga. Pakuti mauwo akondweretsa ngati uwasunga m'kati mwako, ngati akhazikika pamodzi pa milomo yako.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 24:5

Mwamuna wanzeru ngwamphamvu; munthu wodziwa ankabe nalimba.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani

Pemphero kwa Mulungu

Atate wanga wakumwamba, Wokondedwa! Inu nokha ndinu woyenera ulemerero ndi ulemu. Zikomo chifukwa chondisonyeza chikondi chanu chosatha ndi chisamaliro chanu. Zikomo chifukwa chondithandiza ndi kundichirikiza nthawi zonse. Ndikupemphani kuti mundipatse nzeru ndipo ndizifune kuposa golide ndi siliva. Mundithandize kuti ndisachite zinthu monga ine ndikufunira, koma monga momwe inu mukufunira. Mawu anu amati: "Kuopa Yehova ndiko nzeru; ndipo kudziwa Woyera ndiwo luntha." Ambuye, sindikufuna kudzidalira ndekha kapena kutsatira nzeru zanga zokha. Nditsogolereni, khalani kapitawo wa boti langa, mundipatse nzeru, mtima womvetsa, ndi mzimu wofunitsitsa kukonzedwa, kuti ndikupatseni chiwongolero cha moyo wanga, chifukwa ndiko chitsimikizo cha chipambano changa chenicheni. M'dzina la Yesu. Amene.
Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa