Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -

Masalimo 76 - Buku Lopatulika


Ulemerero ndi mphamvu ya Mulungu
Kwa Mkulu wa Nyimbo: pa Neginoto. Salimo la Asafu. Nyimbo.

1 Mulungu adziwika mwa Yuda, dzina lake limveka mwa Israele.

2 Msasa wake unali mu Salemu, ndipo pokhala Iye mu Ziyoni.

3 Pomwepo anathyola mivi ya pauta; chikopa, ndi lupanga, ndi nkhondo.

4 Inu ndinu wakuunikira, ndi womveka wakuposa mapiri muli achifwamba.

5 Olimba mtima chifunkhidwa chuma chao, agona tulo tao; amuna onse amphamvu asowa manja ao.

6 Pa kudzudzula kwanu, Mulungu wa Yakobo, galeta ndi kavalo yemwe anagwa m'tulo.

7 Inu ndinu woopsa; ndipo utauka mkwiyo wanu adzakhala chilili ndani pamaso panu?

8 Mudamveketsa chiweruzo chochokera Kumwamba; dziko lapansi linachita mantha, nilinakhala chete,

9 pakuuka Mulungu kuti aweruze, kuti apulumutse ofatsa onse a padziko lapansi.

10 Indedi, kuzaza kwake kwa munthu kudzakulemekezani; chotsalira cha kuzazaku mudzachiletsa.

11 Windani ndipo chitirani Yehova Mulungu wanu zowindazo; onse akumzinga abwere nacho chopereka cha kwa Iye amene ayenera kumuopa.

12 Iye adzadula mzimu wa akulu; akhala woopsa kwa mafumu a padziko lapansi.

Bible Society of Malawi

Bible Society of Malawi
Titsatireni:



Zotsatsa