Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Masalimo 76:6 - Buku Lopatulika

6 Pa kudzudzula kwanu, Mulungu wa Yakobo, galeta ndi kavalo yemwe anagwa m'tulo.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

6 Pa kudzudzula kwanu, Mulungu wa Yakobo, galeta ndi kavalo yemwe anagwa m'tulo.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

6 Pamene mudaŵaopsa, Inu Mulungu wa Yakobe, onse okwera pa akavalo ndi akavalo ao omwe adagwa nangoti kakasi.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

6 Pa kudzudzula kwanu, Inu Mulungu wa Yakobo, kavalo pamodzi ndi galeta zimakhala chete zitagona pansi.

Onani mutuwo Koperani




Masalimo 76:6
20 Mawu Ofanana  

Ndipo Aaramu anathawa pamaso pa Israele; Davide naphapo Aaramu apamagaleta mazana asanu ndi awiri, ndi apakavalo zikwi makumi anai, nakantha Sobaki kazembe wa khamu lao, nafa iye pomwepo.


Ndipo kunali, usiku womwewo mthenga wa Yehova anatuluka, nakantha m'misasa ya Aasiriya zikwi zana limodzi mphambu makumi asanu ndi atatu kudza zisanu, ndipo pouka anthu mamawa, taonani, onsewo ndi mitembo.


Ndipo Yehova anatuma wamthenga amene anaononga ngwazi zamphamvu zonse, ndi atsogoleri, ndi akazembe, kuchigono cha mfumu ya Asiriya. Nabwerera iye ndi nkhope yamanyazi kudziko lake. Ndipo atalowa m'nyumba ya mulungu wake, iwo otuluka m'matumbo mwake anamupha ndi lupanga pomwepo.


Pa kudzudzula kwanu anathawa; anathawa msanga liu la bingu lanu;


Ndipo zidaoneka zoyendamo madzi, nafukuka maziko a dziko lapansi, mwa kudzudzula kwanu, Yehova, mwa mpumo wa mpweya wa m'mphuno mwanu.


Unapserera ndi moto, unadulidwa; aonongeka pa kudzudzula kwa nkhope yanu.


Pamenepo Mose ndi ana a Israele anaimbira Yehova nyimbo iyi, nanena, ndi kuti, Ndidzaimbira Yehova pakuti wapambanatu; kavalo ndi wokwera wake anawaponya m'nyanja.


Munaombetsa mphepo yanu, nyanja inawamiza; anamira m'madzi aakulu ngati mtovu.


Ndipo Miriyamu anawayankha, Imbirani Yehova, pakuti wapambanatu; kavalo ndi wokwera wake anawaponya m'nyanja.


Ndipo mthenga wa Yehova anatuluka, naphaipha m'zithando za Asiriya, zikwi zana ndi makumi asanu ndi atatu ndi zisanu, ndipo pamene anthu anauka mamawa, taonani, onse ndiwo mitembo.


Pamene atentha, ndidzakonza madyerero ao, ndidzawaledzeretsa, kuti asangalale, agone chigonere, asanyamuke, ati Yehova.


Ndipo ndidzaledzeretsa akulu ake ndi anzeru ake, akazembe ake ndi ziwanga zake, ndi anthu ake olimba; ndipo adzagona chigonere, sadzanyamuka, ati Mfumu, dzina lake ndi Yehova wa makamu.


Ndipo podyera panga mudzakhuta akavalo, ndi magaleta, ndi anthu amphamvu, ndi anthu onse a nkhondo, ati Ambuye Yehova.


Adzaima ndani pa kulunda kwake? Ndipo adzakhalitsa ndani pa mkwiyo wake wotentha? Ukali wake utsanulidwa ngati moto, ndi matanthwe asweka ndi Iye.


Taona, nditsutsana nawe, ati Yehova wa makamu, ndipo ndidzatentha magaleta ake mu utsi; ndi lupanga lidzadya misona yako ya mkango; ndipo ndidzachotsa zofunkha zako padziko lapansi, ndi mau a mithenga yako sadzamvekanso.


Abusa ako aodzera, mfumu ya ku Asiriya; omveka ako apumula; anthu ako amwazika pamapiri, ndipo palibe wakuwasonkhanitsa.


Tsiku ilo, ati Yehova, ndidzakantha kavalo aliyense ndi kumdabwitsa, ndi womkwera adzayaluka; ndipo ndidzatsegulira maso anga nyumba ya Yuda, ndi kukantha kavalo aliyense wa mitundu ya anthu akhale wakhungu.


Chomwecho Davide anatenga mkondowo, ndi chikho cha madzi ku mutu wa Saulo nachoka iwowa, osawaona munthu, kapena kuzidziwa, kapena kugalamuka; pakuti onse anali m'tulo; popeza tulo tatikulu tochokera kwa Yehova tinawagwira onse.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa