Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 2:6 - Buku Lopatulika

Koma Ine ndadzoza mfumu yanga Pa Ziyoni, phiri langa loyera.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Koma Ine ndadzoza mfumu yanga Pa Ziyoni, phiri langa loyera.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Adzati, “Ine ndakhazika kale mfumu yanga, ili pa phiri langa loyera la Ziyoni.”

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

“Ine ndakhazikitsa mfumu yanga pa Ziyoni, phiri langa loyera.”

Onani mutuwo



Masalimo 2:6
21 Mawu Ofanana  

Mpando wachifumu wanu, Mulungu, ukhala nthawi zonse zomka muyaya. Ndodo yachifumu ya ufumu wanu ndiyo ndodo yolunjika.


Mulungu awalira mu Ziyoni, mokongola mwangwiro.


koma anasankha fuko la Yuda, Phiri la Ziyoni limene analikonda.


Inde ndidzamuyesa mwana wanga woyamba, womveka wa mafumu a padziko lapansi.


Taonani, ndampereka iye akhale mboni ya anthu, wotsogolera ndi wolamulira anthu.


Atero Ambuye Yehova, Ndidzatenganso nsonga ya mkungudza wautali ndi kuiika; ndidzabudula nsonga yosomphoka ya nthambi zake zanthete, ndi kuioka paphiri lalitali lothuvuka;


Ndipo masiku a mafumu aja Mulungu wa Kumwamba adzaika ufumu woti sudzaonongeka kunthawi zonse, ndi ulamuliro wake sudzasiyidwira mtundu wina wa anthu, koma udzaphwanya ndi kutha maufumu ao onse, nudzakhala chikhalire.


Atero Yehova: Ndabwerera kudza ku Ziyoni, ndidzakhala pakati pa Yerusalemu; ndi Yerusalemu adzatchedwa, Mzinda wa choonadi; ndi phiri la Yehova wa makamu, Phiri lopatulika.


Ndipo Yesu anadza nalankhula nao, nanena, Mphamvu zonse zapatsidwa kwa Ine Kumwamba ndi padziko lapansi.


ndipo anakonza zonse pansi pa mapazi ake, nampatsa Iye akhale mutu pamutu pa zonse, kwa Mpingo


Komatu mwayandikira kuphiri la Ziyoni, ndi mzinda wa Mulungu wamoyo, Yerusalemu wa Kumwamba, ndi kwa unyinji wochuluka wa angelo,


Ndipo ndinapenya, taonani, Mwanawankhosayo alikuimirira paphiri la Ziyoni, ndipo pamodzi ndi Iye zikwi zana mphambu makumi anai kudza anai, akukhala nalo dzina lake ndi dzina la Atate wake lolembedwa pamphumi pao.