Zekariya 8:3 - Buku Lopatulika3 Atero Yehova: Ndabwerera kudza ku Ziyoni, ndidzakhala pakati pa Yerusalemu; ndi Yerusalemu adzatchedwa, Mzinda wa choonadi; ndi phiri la Yehova wa makamu, Phiri lopatulika. Onani mutuwoChichewa Buku Lopatulika Bible 20143 Atero Yehova: Ndabwerera kudza ku Ziyoni, ndidzakhala pakati pa Yerusalemu; ndi Yerusalemu adzatchedwa, Mudzi wa choonadi; ndi phiri la Yehova wa makamu, Phiri lopatulika. Onani mutuwoBuku Loyera Catholic Edition - Chichewa3 Ine Chauta Wamphamvuzonse mau anga ndi aŵa: Tsopano ndidzabweranso ku phiri la Ziyoni, ndidzakhalanso ku Yerusalemu. Yerusalemuyo adzatchedwa Mzinda Wokhulupirika. Phiri la Ine Chauta Wamphamvuzonse lidzatchedwa Phiri Loyera. Onani mutuwoMawu a Mulungu mu Chichewa Chalero3 Yehova akuti, “Ndidzabwerera ku Ziyoni ndi kukakhala ku Yerusalemu. Pamenepo Yerusalemu adzatchedwa Mzinda wa Choonadi ndipo phiri la Yehova Wamphamvuzonse lidzatchedwa Phiri Lopatulika.” Onani mutuwo |
Ndipo iwo adzatenga abale anu onse mwa amitundu onse akhale nsembe ya kwa Yehova; adzabwera nao pa akavalo, ndi m'magaleta, ndi m'machila, ndi pa nyuru, ndi pa ngamira, kudza kuphiri langa lopatulika ku Yerusalemu, ati Yehova, monga ana a Israele abwera nazo nsembe zao m'chotengera chokonzeka kunyumba ya Yehova.
Dziko lonse lidzasandulika, lidzanga chidikha, kuyambira ku Geba kufikira ku Rimoni, kumwera kwa Yerusalemu; ndipo pali uwupo padzakhala ponyamuka, ndipo udzakhala m'malo mwake, kuyambira ku Chipata cha Benjamini kufikira ku malo a chipata choyamba, kufikira ku Chipata cha Kungodya, ndi kuyambira Nsanja ya Hananele kufikira ku zoponderamo mphesa za mfumu.