Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 112:4 - Buku Lopatulika

Kuunika kutulukira oongoka mtima mumdima; Iye ndiye wachisomo, ndi wansoni ndi wolungama.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Kuunika kutulukira oongoka mtima mumdima; Iye ndiye wachisomo, ndi wansoni ndi wolungama.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Ngakhale nthaŵi ya mdima, munthu wochita chilungamo ayenda m'kuŵala, chifukwa ngwokoma mtima, wachifundo ndi woongoka.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ngakhale mu mdima kuwala kumatulukira olungama mtima; wokoma mtima, wachifundo ndi wowongoka mtima.

Onani mutuwo



Masalimo 112:4
26 Mawu Ofanana  

Ndipo moyo wako udzayera koposa usana; kungakhale kuli mdima kudzakhala ngati m'mawa.


Ukatsimikiza mtima kakuti, kadzakhazikikira iwe; ndi kuunika kudzawala panjira zako.


muja nyali yake inawala pamutu panga, ndipo ndi kuunika kwake ndinayenda mumdima;


Aleluya. Yamikani Yehova; pakuti Iye ndiye wabwino: Pakuti chifundo chake nchosatha.


Yehova ngwa chifundo ndi wolungama; ndi Mulungu wathu ngwa nsoni.


Yehova ali wolungama m'njira zake zonse, ndi wachifundo m'ntchito zake zonse.


Ndipo adzaonetsa chilungamo chako monga kuunika, ndi kuweruza kwako monga usana.


Kuunika kufesekera wolungama, ndi chikondwerero oongoka mtima.


Wolondola chilungamo ndi chifundo apeza moyo, ndi chilungamo, ndi ulemu.


Ndani ali mwa inu amene amaopa Yehova, amene amamvera mau a mtumiki wake? Iye amene ayenda mumdima, ndipo alibe kuunika, akhulupirire dzina la Yehova, ndi kutsamira Mulungu wake.


ndipo ngati upereka kwa wanjala chimene moyo wako umakhumba, ndi kukhutitsa moyo wovutidwa, pomwepo kuunika kwako kudzauka mumdima, ndipo usiku wako udzanga usana;


Pomwepo kuunika kwako kudzawalitsa monga m'mawa, ndi kuchira kwako kudzaonekera msangamsanga; ndipo chilungamo chako chidzakutsogolera; ulemerero wa Yehova udzakhala wotchinjiriza pambuyo pako.


Koma inu akuopa dzina langa, dzuwa la chilungamo lidzakutulukirani, muli kuchiritsa m'mapiko mwake; ndipo mudzatuluka ndi kutumphatumpha ngati anaang'ombe onenepa otuluka m'khola.


Khalani inu achifundo monga Atate wanu ali wachifundo. Ndipo musamaweruza, ndipo simudzaweruzidwa.


Ndadza Ine kuunika kudziko lapansi, kuti yense wokhulupirira Ine asakhale mumdima.


Koma mukhalirane okoma wina ndi mnzake, a mtima wachifundo, akukhululukirana nokha, monganso Mulungu mwa Khristu anakhululukira inu.


Potero, penyani bwino umo muyendera, si monga opanda nzeru, koma monga anzeru;


pakuti chipatso cha kuunika tichipeza mu ubwino wonse, ndi chilungamo, ndi choonadi,


Ngati mudziwa kuti ali wolungama, muzindikira kuti aliyensenso wakuchita chilungamo abadwa kuchokera mwa Iye.


M'menemo aoneka ana a Mulungu, ndi ana a mdierekezi: yense wosachita chilungamo siali wochokera mwa Mulungu; ndi iye wosakonda mbale wake.


Tiana, munthu asasokeretse inu; iye wakuchita cholungama ali wolungama, monga Iyeyu ali wolungama: