Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Masalimo 112:5 - Buku Lopatulika

5 Wodala munthu wakuchitira chifundo, nakongoletsa; adzalimbika nao mlandu wake poweruzidwa.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

5 Wodala munthu wakuchitira chifundo, nakongoletsa; adzalimbika nao mlandu wake poweruzidwa.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

5 Munthu amene amakongoza mosafuna phindu, amene amayendetsa ntchito zake mwachilungamo, zinthu zimamuyendera bwino.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

5 Zinthu zabwino zidzabwera kwa iye amene amapereka mowolowamanja ndi wokongoletsa mwaufulu, amene amachita ntchito yake mwachilungamo.

Onani mutuwo Koperani




Masalimo 112:5
22 Mawu Ofanana  

Chifukwa chake ndinawaika potera m'kati mwa linga, popenyeka; inde ndinaika anthu monga mwa mabanja ao, akhale nao malupanga ao, nthungo zao, ndi mauta ao.


Woipa akongola, wosabweza, koma wolungama achitira chifundo, napereka.


Yehova akomera mtima munthu wabwino; koma munthu wa ziwembu amtsutsa.


Munthu wosowa nzeru apangana kulipirira wina, napereka chikole pamaso pa mnzake.


Wogwira ntchito mwaulesi ndiye mbale wake wa wosakaza.


nzeru idzakuyendetsa m'njira ya anthu abwino, kuti usunge mayendedwe a olungama.


Longosola ntchito yako panjapo, nuikonzeretu kumunda; pambuyo pake ndi kumanga nyumba yako.


Ndipo taonani, munthu dzina lake Yosefe, ndiye mkulu wa milandu, munthu wabwino ndi wolungama


Koma takondanani nao adani anu, ndi kuwachitira zabwino, ndipo kongoletsani osayembekeza kanthu konse, ndipo mphotho yanu idzakhala yaikulu, ndipo inu mudzakhala ana a Wamkulukuluyo; chifukwa Iye achitira zokoma anthu osayamika ndi oipa.


Ndipo pamene adakhuta, Iye ananena kwa ophunzira ake, Sonkhanitsani makombo kuti kasatayike kanthu.


chifukwa anali munthu wabwino, ndi wodzala ndi Mzimu Woyera ndi chikhulupiriro: ndipo khamu lalikulu lidaonjezeka kwa Ambuye.


musakhale aulesi m'machitidwe anu; khalani achangu mumzimu, tumikirani Ambuye;


Pakuti ndi chivuto munthu adzafera wina wolungama; pakuti kapena wina adzalimbika mtima kufera munthu wabwino.


Potero, penyani bwino umo muyendera, si monga opanda nzeru, koma monga anzeru;


Ndipo ichi ndipempha, kuti chikondi chanu chisefukire chionjezere, m'chidziwitso, ndi kuzindikira konse;


Muyendere munzeru ndi iwo akunja, kuchita machawi nthawi ingatayike.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa