Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Genesis 7:5 - Buku Lopatulika

Ndipo anachita Nowa monga mwa zonse anamlamulira iye Yehova.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndipo anachita Nowa monga mwa zonse anamlamulira iye Yehova.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Ndipo Nowa adachita zonse zimene Mulungu adamlamula.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ndipo Nowa anachita zonse zimene Yehova anamulamulira.

Onani mutuwo



Genesis 7:5
14 Mawu Ofanana  

Chotero anachita Nowa, monga mwa zonse anamlamulira iye Mulungu, momwemo anachita.


Zimene zinalowazo, zinalowa yamphongo ndi yaikazi zamoyo zonse, monga momwe Mulungu anamlamulira iye: ndipo Yehova anamtsekera iye.


Pamenepo sindidzachita manyazi, pakupenyerera malamulo anu onse.


Potero anatsiriza ntchito yonse ya Kachisi wa chihema chokomanako; ndipo ana a Israele adachita monga mwa zonse Yehova adamuuza Mose, anachita momwemo.


Anatero Mose; monga mwa zonse Yehova adamuuza, momwemo anachita.


Ndipo Mose ndi Aroni anachita monga Yehova anawalamulira, momwemo anachita.


Koma Yesu anayankha, nati kwa iye, Balola tsopano: pakuti kuyenera ife kukwaniritsa chilungamo chonse motero. Pamenepo anamlola Iye.


Koma Iye anayankha, nati kwa iwo, Amai wanga ndi abale anga ndiwo amene akumva mau a Mulungu, nawachita.


Ngati mudziwa izi, odala inu ngati muzichita.


Amake ananena kwa atumiki, Chimene chilichonse akanena kwa inu, chitani.


ndipo popezedwa m'maonekedwe ngati munthu, anadzichepetsa yekha, nakhala womvera kufikira imfa, ndiyo imfa ya pamtanda.


angakhale anali Mwana, anaphunzira kumvera ndi izi adamva kuwawa nazo;