Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -

Mlaliki 1 - Buku Lopatulika


Za pansi pano nzachabe

1 Mau a Mlaliki, mwana wa Davide, mfumu ya mu Yerusalemu.

2 Zachabechabe, ati Mlaliki; zachabechabe zonse ndi chabe.

3 Kodi ntchito zake zonse munthu asauka nazo zimpindulira chiyani?

4 Mbadwo wina upita, mbadwo wina nufika; koma dziko lingokhalabe masiku onse.

5 Inde dzuwa lituluka, nililowa, nilifulumira komwe linatulukako.

6 Kulowa kumwera ndi kuzungulira kumpoto zungulirezungulire imaomba mphepo; ibweranso monga mwa mazunguliridwe ake.

7 Mitsinje yonse ithira m'nyanja, koma nyanja yosadzala; komwe imukira mitsinjeyo, komweko ibweranso.

8 Zinthu zonse zilemetsa; munthu sangathe kuzifotokoza; maso sakhuta m'kuona, ndi makutu sakhuta m'kumva.

9 Chomwe chinaoneka chidzaonekanso; ndi chomwe chinachitidwa chidzachitidwanso; ndipo palibe kanthu katsopano pansi pano.

10 Kodi pali kanthu unganene kuti, Taona katsopano aka? Kanalipo kale, kale lomwe tisanabadwe ife.

11 Zoyamba zija sizikumbukiridwa; ngakhale zomwe zilinkudzazo, omwe adzakhalabe m'tsogolomo, sadzazikumbukirai.

12 Ine Mlaliki ndinali mfumu ya Israele mu Yerusalemu.

13 Ndipo ndinapereka mtima kufunafuna ndi nzeru, ndi kulondetsa zonse zimachitidwa pansi pa thambo; ntchito yovuta imeneyi Mulungu apatsa ana a anthu akasauke nayo.

14 Ndaona ntchito zonse zipangidwa kunja kuno; ndipo zonsezo ndi chabe ndi kungosautsa mtima.

15 Chokhotakhota sichingaongokenso; ndipo choperewera sichingawerengedwe.

16 Ndinalankhula ndi mtima wanga, ndi kuti, Taona, ndakuza ndi kudzienjezera nzeru koposa onse anakhala mu Yerusalemu ndisanabadwe ine; inde mtima wanga wapenyera kwambiri nzeru ndi chidziwitso.

17 Ndipo ndinapereka mtima kudziwa nzeru ndi kudziwa misala ndi utsiru; ndinazindikira kuti ichinso chingosautsa mtima.

18 Pakuti m'nzeru yambiri muli chisoni chambiri; ndi yemwe aenjezera chidziwitso aenjezera zowawa.

Bible Society of Malawi

Bible Society of Malawi
Titsatireni:



Zotsatsa